08/10/2025
“Anjateni amenewo” – akhwithima a Malawi
Kuiwala kuti ntchentche inati mtsogolo moyo mbuyo moyo, anthu ena omwe amagwira ntchito ku nyumba za chifumu pansi pa utsogoleri wa a Lazarus Chakwera, achokako atawononga pomwe amasamuka potsatira kusankhidwa kwa mtsogoleri wa tsopano a Peter Mutharika.
M'masamba amchezo mwakhala mukuyenda mphekesera yoti posamuka kunyumba zachifumuzi makamaka ku Kamuzu munzinda wa Lilongwe, ogwira ntchito ena adawonongako, mpaka kufika potenga chimbudzi ndikupakapaka khoma la nyumba zina kumeneku.
Nyuzipepala za lero zatsimikizaso za nkhaniyi. Mwachitsanzo, Daily Times yati ku nyumba yachifumu ya Kamuzu kwabedwa zinthu zina monga ma television, mipando, ma fridge makina opangira gym, ma bulb ndi zina zambiri, komaso magalasi ena oswedwa
Nkhaniyi yakwiyitsa anthu ambiri omwe ati nkofunika kuti anthu omwe achita izi anjatidwe. “Koma izizi ngati zili zoona apolisi nde mukuchedwatu, awawa onse anjatidwe, ukunkuchititsa manyazi dziko,” watelo Ephias Matebule poikira ndemanga za nkhaniyi pa tsamba lina pa fesibuku.
Ndemanga zambiri com we taona zikulimbikitsa atsogoleri kuti achitepo kanthu kuphatikizapo kumanga onse okhudzidwa ndi khalidweli.
Zithuzi: za pa masamba amchezo