28/05/2026
Nthambi ya Airtel Money yomwe ili pansi pa kampani ya Airtel Malawi, yati ndikhumbo lawo kuwona miyoyo ya a Malawi ikupita patsogolo kumbali ya zachuma.
Mkulu wa zamalonda ku nthambi ya Airtel Money, Virginia Jere, ndiye wayankhula izi pomwe amachititsa mayere a anthu omwe apambana mpikisano wa Airtel Money Tola Promotion mu sabata yake yachiwiri.
"Tinali okondwa sabata yatha kumva zomwe opambana anatiuzila mmene ndalamazi zisinthire miyoyo yawo ndipo lero tili pano kuchitira umboni opambana ena, omwe analowa mu mpikisanowu potumiza ndalama komaso kulipira ma bilu kudzera pa Airtel Money" anatero a Jere.
Pamayerewa, anthu atatu apambana 5 miliyoni kwacha aliyense, pomwe ena 300 apata ma 50,000 kwacha, kutanthauza kuti 30 miliyoni kwacha ndiyomwe yagawidwa.
A Willack Ndala aku Chiradzulu, omwe amachita bizinesi yogula ndikugulitsa mbuzi, ati 5 miliyoni kwacha yomwe apata iwathandiza kuti amangire nyumba.
Ena omwe apambana mphoto za 5 miliyoni kwacha ndi a John Bamusi omwe ndi phungu wa nyumba yamalamulo ku dera la Balaka Ngwangwa, ndipo ati ndalamayi ayigwiritsa ntchito popereka kwa amayi ku dera lawo kuti ayambire ma bizinesi.
Omaliza omwe apambana 5 miliyoni kwacha ndi mphunzitsi wa sukulu ya purayimare ya Monkebay, a Stephano Mandimba omwe ati ndalamayi ithandizira maphunziro a ana awo omwe wina ali fomu 4 pomwe wina ali ku College of Medicine.
Mayere oyamba anachitika sabata yatha pomwe mphoto ngati zomwezi zinagawidwa kwa anthu opambana.