23/04/2025
Anthu ena avulala pa chipwirikiti chomwe chinabuka dera la phungu la kumpoto kwa boma la Chikwawa komwe chipani cha DPP chimafuna kuchititsa chisankho cha chipulula lero.
Nthumwi zonse ku chisankhochi zinalowa kuti ziyambe kuvota koma anthu ena omwe sakudziwika anayamba kugenda.
Izi zinachititsa kuti onse omwe amafuna kupikisana nawo pa chisankhochi athawe pamalowa.
Izitu zimachitika pomwe apolisi omwe anabwera kuti akhazikitsa bata atabwezedwa pa malowa cha ku mmawa.
Wolemba: Esmy Kamba Kamanga