The Radar

The Radar The Radar media advances uncensored truth through in-depth, analytical, credible and independent news

23/04/2025

Anthu ena avulala pa chipwirikiti chomwe chinabuka dera la phungu la kumpoto kwa boma la Chikwawa komwe chipani cha DPP chimafuna kuchititsa chisankho cha chipulula lero.

Nthumwi zonse ku chisankhochi zinalowa kuti ziyambe kuvota koma anthu ena omwe sakudziwika anayamba kugenda.

Izi zinachititsa kuti onse omwe amafuna kupikisana nawo pa chisankhochi athawe pamalowa.

Izitu zimachitika pomwe apolisi omwe anabwera kuti akhazikitsa bata atabwezedwa pa malowa cha ku mmawa.

Wolemba: Esmy Kamba Kamanga

Chisankho cha chipulula cha chipani cha DPP ku mpoto kwa boma la Chikwawa chili mkati lero. Pomwe chisankhochi chimayene...
23/04/2025

Chisankho cha chipulula cha chipani cha DPP ku mpoto kwa boma la Chikwawa chili mkati lero.

Pomwe chisankhochi chimayenera kuyamba, zosamiwtsa zingapo zawoneka ndipo zadzetsa chipwilikiti.

Mwazina mmodzi mwa omwe akuima nawo pa chisankhochi dzina lake linasowa mkaundula mwawo ndinso pomwe akuluakulu ochokera ku likulu la chipanichi anati aliyense ayenela kukhala ndi chiphatso cha unzika.

Omwe akupikisana ku mpoto kwa Chikwawa ndi Angamile Ngosi, Wyson Bush, Grace Masamba komanso Linda khembo.

Wolemba: Esmy Kamba Kamanga, Chikwawa

21/04/2025

Mtsogoleri wakale wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleri wa chipani cha Democtratic Progressive (DPP) Peter Mutharika wati ndiokhumudwa komanso akulira limodzi ndi anthu onse a mpingo wa chiKatolika pa imfa ya mtsogoleri wa mpingowu Papa Francis.

Izi zili mu kalata yomwe mtsogoleri wakale wa dziko linoyu watulutsa yomwe wasaina ndi ofalitsa nkhani wake Shadric Namalomba kutsatira imfayi.

A Mutharika ati Papa Francis anali mtsogoleri wapaderadera maka pa utsogoleri wake ozichepetsa, opititsa patsogolo mtendere komanso wachifundo kwa onse.

Iwo ati Papa Francis adachirimika kwambiri polimbikitsa chilungamo, chifundo mwazina zomwe ati zidachitira ubwino miyanda miyanda ya anthu pa dziko lonse la pansi.

Anthu pa dziko la pansi akukhuza maliro a mtsogoleri wa mpingo wa Katolika pa dziko lonse, Papa Francis. Papa Francis wa...
21/04/2025

Anthu pa dziko la pansi akukhuza maliro a mtsogoleri wa mpingo wa Katolika pa dziko lonse, Papa Francis.

Papa Francis wamwalira lero ku m'mawaku atadwala kwa nthawi yayitali.

Pakadali pano, mtsogoleri wa dziko lino, Lazarus Chakwera komanso mtsogoleri opuma, Peter Mutharika, mwa anthu ena, ati ali ndi chisoni ndi imfayi.

Mighty Wanderers FC technical director Yasin Osman has died.Wanderers FC board secretary, Chancy Gondwe, has confirmed t...
21/04/2025

Mighty Wanderers FC technical director Yasin Osman has died.

Wanderers FC board secretary, Chancy Gondwe, has confirmed the development.

Reports gathered by this publication show that Osman has died after a short illness.

Osman was the first player in Malawian football history to be bought from Wanderers to FCB Nyasa Big Bullets FC at about £100 in 1970.

More updates to follow as they unfold.

By Vincent Poya

It is Good Friday
18/04/2025

It is Good Friday

18/04/2025

Mtsogoleri wa dziko lino, Lazarus Chakwera lero akuyenda nawo pa Njira ya Mtanda, ulendo omwe uyambikire pa Botanic Garden mu mzinda wa Lilongwe.

Njira ya mtanda imakhala chifaniziro cha mazunzo omwe Ambuye Yesu, yemwe akhiristu amakhulupilira kuti ndi mtumiki wawo, anakumana nawo asanapachikidwe pa mtanda ndi kufa.

Kampani yopanga magesi mdziko muno ya EGENCO yalengeza kuti ikhala ikukonza makina ake ku Nkula A ndi B zomwe zidzetse k...
17/04/2025

Kampani yopanga magesi mdziko muno ya EGENCO yalengeza kuti ikhala ikukonza makina ake ku Nkula A ndi B zomwe zidzetse kuzimazima kwa magetsi.

Ntchitoyi iyamba lero lachinayi ndipo itha lolemba.

Mwa zina, ntchitoyi ikhudza kuchotsa zinyalala ku makinawa.

Pakadali pano, ena mwa ochita malonda mu mzinda wa Blantyre ati ngakhale kuti ntchitoyi ndi yofunika koma yabwera nthawi yolakwika.

Pali chiopsezo kuti maboma angapo mchigawo chakumwera kwadziko lino kugwa mvula yamphamvu komanso kukhudzidwa ndi mphenz...
17/04/2025

Pali chiopsezo kuti maboma angapo mchigawo chakumwera kwadziko lino kugwa mvula yamphamvu komanso kukhudzidwa ndi mphenzi.

Malingana ndi nthambi yoona za nyengo mdziko muno, maboma monga Blantyre, Phalombe, Thyolo, Mangochi komanso Mwanza ndi omwe akuyembekezera kukhudzidwa ndi nyengoyi.

Pakadali pano nthambiyi yapempha anthu kuti apewe kubisala pansi pa mitengo komanso mnyumba zomwe sizolimba.

Phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Mzimba a Yeremia Chihana awatulutsa pa belo la bwalo la milandu atamangidwa lachiw...
17/04/2025

Phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Mzimba a Yeremia Chihana awatulutsa pa belo la bwalo la milandu atamangidwa lachiwiri lapitali.

Oweruza milandu ku bwalo lamilandu la Mzuzu a Clemence Chamwenda ndi omwe apereka beloyi.

Mwazina a Chihana alamulidwa kupereka ndalama yokwana K1 miliyoni komanso chikole cha ndalama zokwana K10 miliyoni ndikumakaonekera Ku ma ofesi a bungwe lothana ndi ziphuphu mdziko muno sabata ziwiri zilizonse.

A Chihana anamangidwa lachiwiri powaganizira kuti anasakaza ndalama za chitukuko cha kudera komanso kugwiritsa ntchito udindo wawo molakwika.

Chithunzi: Times 360 Malawi

President Dr. Lazarus McCarthy Chakwera will tomorrow, Thursday, 17 April, preside over the launch of the Coca-Cola Beve...
16/04/2025

President Dr. Lazarus McCarthy Chakwera will tomorrow, Thursday, 17 April, preside over the launch of the Coca-Cola Beverages Terelytheylene (PET) line in Lilongwe.

TNM Super league log table
16/04/2025

TNM Super league log table

Address

P. O. Box 3539
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when The Radar posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to The Radar:

Share