PortHerald Press

  • Home
  • PortHerald Press

PortHerald Press Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from PortHerald Press, Media Agency, Chikwawa, .

Registered Media House
best online publication that provides catchy and tangible breaking news.

provide top-notch media consultancy and advertisements

/Whatsapp +265 889 35 35 57
✉️ [email protected]
#"The Truth Uncovered"

 ATHOKOZA MAKOLO CHIFUKWA CHOTUMIZA ANA KU SUKULU ZA OPEN DOOR PRIVATE      Mwini sukulu za pulayimale ndi nursey za Ope...
30/09/2025


ATHOKOZA MAKOLO CHIFUKWA CHOTUMIZA ANA KU SUKULU ZA OPEN DOOR PRIVATE



Mwini sukulu za pulayimale ndi nursey za Open Door Private Bishop ku Bangula m'boma la Nsanje Lyson Bendicto wati akuthoza makolo chifukwa chotumiza ana ambiri potsatira kulengezetsa kuti sukuluzi zikhale zaulere.

Bishop Bendicto aulula izi Lachiwiri polankhula ndi PortHerald Press.

Iye wati ku nursey okha kuli ana mazana atatu (300).

"Pano ndili pachilingaliro chofuna kulemba aphunzitsi ena,' watero mkuluyu.

M'modzi mwa wa makalo a Zione Masamba wati ganizo ladza nthawi yabwino pomwe makolo amalephera kutumiza ana awo ku sukuluzi.

"Chosangalatsa china ophunzira amalandira chakudya ku sukuluku," watero Masamba.

30/09/2025


ACHITANSO ZISANKHO ZINA

SOURCE: BBC

Dziko la Seychelles likhalaso ndi zisankho zina zosankha mtsogoleri wadziko pamene gawo loyamba losankha mtsogoleri yemwe ayendetse dziko lo sanafike theka la mavoti.

Izi zikutero pamene mtsogoleri wotsutsa boma m'dziko mo Patrick Herminie wapeza 48.8% mwa mavoti omwe anthu anaponya kugonjetsa yemwe ndi mtsogoleri wadziko lo a Wavel Ramkalawan omwe apeza 46.4%, pamene bungwe loyendetsa zisankho m'dzikomo lalengezera.

 BESENI YA CHIMANGA YAFIKA PA 5000 KWACHA    Chimanga chayamba kutsika  mtengo pa Misewufolo Trading Center m'boma la Ch...
29/09/2025


BESENI YA CHIMANGA YAFIKA PA 5000 KWACHA



Chimanga chayamba kutsika mtengo pa Misewufolo Trading Center m'boma la Chikwawa pomwe beseni yolemera 5 Kgs ikugulitsidwa pa mtengo wa 5 000 kwacha.

"Tinadyambo ntchima ya mkonora pepa thangwi yache chatchitha chimangachi" a Chrisy Moffolo auza PortHerald Press.

Nyumba yosindikiza nkhani ino yapezanso kuti anthu ochuluka ochita malonda pa msika wa Misewufolo anagula chimanga chochuluka kuti agulitse mokwera njala ikafika pa mnanu.

 BAMBO AMWALIRA PA NGOZI YA PAMSEU KU PHALOMBE     Ku Phalombe,  bambo wa zaka makumi asanu a Jalawanda Nambazo  amwalir...
29/09/2025


BAMBO AMWALIRA PA NGOZI YA PAMSEU KU PHALOMBE



Ku Phalombe, bambo wa zaka makumi asanu a Jalawanda Nambazo amwalira pa ngozi ya pamseu m'bandakucha wa lero Lolemba pa 29th September 2025.

Wofalitsa nkhani za apolisi m'bomali Sergeant Jimmy Kapanja watsimikiza za ngoziyi yomwe yachitika pa mudzi wa Nambazo.

Iye wati galimoto ya lorry ya mtundu wa Mercedes Benz nambala yake MJ 3740 yomwe imayendetsedwa ndi Justin Binali imachokera ku malo azamalonda a Malinguni kulowera ku mudzi wa Nambazo mu mseu wa fumbi wa Malinguni-Nambazo itanyamula njerwa za simenti ndi anthu anayi.

"Itafika pa mudzi wa Nambazo pafupi ndi Transformer malemu Jalawanda mosazindikira anadumpha kuchokera m'galimoto yikuyenda," watero Kapanja.

Iye watinso potsatira kugwa kuchokera pa mwamba pa galimoto a Jawalanda avulala m'mutu chifukwa chopondedwa ndi tayala ya m'mbuyo.

Iwo anatengeredwa pa chipatala chaching'ono cha Nambazo komwe anatsimikiza za imfa yawo atangofika kumene.

Apolisi m'bomali akumema anthu ogwiritsa mseu kuti adzitsatira malamulo apa mseu pofuna kupewa ngozi ngati zimenezi.

Jalawanda Nambazo amachokera pa mudzi wa Mwakuwamwatha m'dera la Mfumu yaikulu Chiwalo m'boma la Phalombe.

 SENIOR CHIEF KWATAINE YAMWALIRA    Mfumu yaikulu Kwataine ya m'boma la Ntcheu yamwalira lero Lolemba pa 29th September,...
29/09/2025


SENIOR CHIEF KWATAINE YAMWALIRA



Mfumu yaikulu Kwataine ya m'boma la Ntcheu yamwalira lero Lolemba pa 29th September,2025.

Mneneri wa maboma ang'ono Anjoya Mwanza watsimikiza za imfa ya malemu Mfumu yaikulu Kwataine yomwe yamwalilira pa chipatala cha Lilongwe Private mu mzinda wa Lilongwe komwe amalandira chithandizo cha mankhwala.

Iye wati malemu Mfumu yaikulu Kwataine omwe dzina lawo lenileni ndi MacJulio Kasiteni Kwataine anabadwa pa 30th June,1966.

"Analongedwa ufumu ngati Traditional Authority Kwataine pa 30th December,1999 ndipo anakwezedwa kukhala Senior Chief Kwataine pa 27th October,2012," watero Mwanza.

Mneneri wati mafumu ngofunika kuno ku Malawi chifukwa amapangitsa anthu alemekezeke miyambo, mitundu ya anthu idzilekezedwa komanso anthu adzikhala a mwambo.

Iye wapitiliza kunena kuti mafumu amakhala mamembala a khonsolo amene amakhala ali kupanga ntchito za zitukuko za madera mwawo.

Pa za malemu Mfumu yaikulu Kwataine, mneneriyu wati inali mfumu ya kasu yomwe yakhala paudindo kwa zaka zopanda 26 ndipo imatsogolera dera lake mwachidwi ndi chikondi.

Malemu Mfumu yaikulu Kwataine yasiya mkazi ndi ana anayi (4).

 APM ALUMBILITSIDWA LOWERUKALI    Mtsogoleri wongosankhidwa Arthur Peter Mutharika akuyembekezera kulumbilitsidwa Loweru...
29/09/2025


APM ALUMBILITSIDWA LOWERUKALI



Mtsogoleri wongosankhidwa Arthur Peter Mutharika akuyembekezera kulumbilitsidwa Loweruka sabata ino pa 4th October,2025.

Mneneri wa chipani cha DPP yemwenso ndi mneneri mtsogoleri wa chipanichi Shadrick Namalomba watsimikiza za nkhaniyi ponena kuti mwambo udzachitikira pa bwalo la Kamuzu mu mzinda wa Blantyre.

Namalomba sapapereke ndondomeko ya mwambo wa Lowerukali.

Mutharika adasankhidwa ndi aMalawi pa 16th September chaka chino kuti awatsogolere kwa zaka zisanu zikubwerazi.

 . Yankhani molondola. Kodi ndi page iti ku Shire Valley yomwe ili ndi more followers? Then tag it.Winners will...
28/09/2025

. Yankhani molondola. Kodi ndi page iti ku Shire Valley yomwe ili ndi more followers? Then tag it.

Winners will be announced on this platform. NB: Only 3 are needed

Ife yathu ndi 12K followers is not qualifying. Musamkhe ena and tag not PortHerald Press

 CHITIPA UTD YAKWAPULA ASILIKALI     Timu ya mpira wa miyendo ya Chitipa United yatenga mapointi atatu itakwapula Moyale...
28/09/2025


CHITIPA UTD YAKWAPULA ASILIKALI



Timu ya mpira wa miyendo ya Chitipa United yatenga mapointi atatu itakwapula Moyale Barracks ndi zigoli ziwiri kwa chilowere.

Matimuwa amasewera bwalo Chitipa pomwe eni bwalo anatengerapo mwayi kwa asilikari aku mzinda wa Mzuzu.

Osewera a Chitipa United Zenga Manda ndi Peter Barry ndi omwe anapereka chipambano cha eni nthaka.

Blue Eagles ndi Creck Sporting Club apindirana ndevu mkamwa pogoletsana chigoli chimodzi kwa chimodzi.

Frank Phiri anagoletsa chigoli cha Creck Sporting Club ndipo Lanken Mwale anabweza chigoli.

Eagles ndi Creck apeza pointi iliyonse.

Timu ya Songwe Border United ikupitilira kuona malodza pomwe yakwapulidwa ndi Karonga United ndi chigoli chimodzi kwa duu.

 MAMBEMBALA ENA A MCP AKANA MUMBA KUKHALA MTSOGOLERI WOTSUTSA KU PARLIAMENT   Mamembala ochuluka achipani cha Malawi Con...
28/09/2025


MAMBEMBALA ENA A MCP AKANA MUMBA KUKHALA MTSOGOLERI WOTSUTSA KU PARLIAMENT



Mamembala ochuluka achipani cha Malawi Congress Party (MCP) akana kuti Vitumbiko Mumba kuti akhale mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma ku Nyumba ya Malamulo.

Izi zatumphuka muzokambirana zomwe mamembalawa anali nazo posachedwapa.

Membala wina yemwe wati tisamutchule dzina wauza PortHerald Press kuti pakadalipano kuli mpungwepungwe ku chipani ku pa yemwe asankhidwe udindowu.

"Mumba asankhidwa ngati phungu woima payekha pa chisankho chapitachi ngati woima payekha osati ngati wa MCP " watero.

Membala yu anaonjezeranso kuti Mumba sakukwanira pa udindowu.

 NDAYISIRATU NDALE-Chiumya   A Jamestar Chiumya omwe ndi m'modzi mwa  anthu omwe anapikitsana nawo pa  mpando wa khansal...
28/09/2025


NDAYISIRATU NDALE-Chiumya



A Jamestar Chiumya omwe ndi m'modzi mwa anthu omwe anapikitsana nawo pa mpando wa khansala ku ward ya Bangwe-Namiyango pa chisankho chapitachi ati sazaimilanso mpandowu kusogoloku ndikuti asiyiratu ndale sopano.

Poyankhula nafe kudzera pa lamya a chiumya ati sanapange chiganizochi kamba kokhumudwa koma ati nthawi yakwana yakuti aone zina kupita Chitsogolo.

Aka mkachiwiri kugonja pa Chisankho ku delari komwe a Joseph Makwinja a chipani cha DPP ndi omwe anapambana ngati khansala wa Bangwe-Namiyango ward .

28/09/2025

Big shout out to my newest top fans! Ñêlsøñ Ñèø Kåñzîmbî, Akimu Wa Ngalu, Senior Merchant Pheto, NA Chaukah, Dizzol Kopitathi, Zacharia K Kumbukan, Cnyangulu Post, Martin Gundani, Ishmael Bwanali, Kennedy Hez Malola, Mìçkëy Dãdå Khūmbīdzì, Auswizzy Kameme, Paul Wahiye Master, Ganizani Muleso Brighton, Benson Malinki, Yasin Juma, Sibu Felix, Mwai Kay, Moses Steshy, Manase George Bandah, Stewart Gama, Kennedy Makwiza, Happy Half, Ephraim Stanly Ndongo, Grace Kapelenganya, Symon Kabayo, John Nkhabebve Malemba, Cashmore Charlie Williams, Paul Mlongoti, Wezi WA Chiuta, Ben Mazengo SC, Stephen Biasi, Thokozani Mwakulamwatha, Mtsogoli Ganamba, Isaac P Kuyeli, Charles Chisada, Dan Busyman Henry Manyera

  Tikugulireni? Muli kuti?Uwu upose ulemelero wa pa dziko pano?Pitani ku Max & Sherry Dine and Lounge kuti mukadye zimen...
28/09/2025

Tikugulireni? Muli kuti?

Uwu upose ulemelero wa pa dziko pano?

Pitani ku Max & Sherry Dine and Lounge kuti mukadye zimenezi. For more visit their page ASAP.

Address

Chikwawa

Telephone

+265990485072

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when PortHerald Press posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share