30/09/2025
ATHOKOZA MAKOLO CHIFUKWA CHOTUMIZA ANA KU SUKULU ZA OPEN DOOR PRIVATE
Mwini sukulu za pulayimale ndi nursey za Open Door Private Bishop ku Bangula m'boma la Nsanje Lyson Bendicto wati akuthoza makolo chifukwa chotumiza ana ambiri potsatira kulengezetsa kuti sukuluzi zikhale zaulere.
Bishop Bendicto aulula izi Lachiwiri polankhula ndi PortHerald Press.
Iye wati ku nursey okha kuli ana mazana atatu (300).
"Pano ndili pachilingaliro chofuna kulemba aphunzitsi ena,' watero mkuluyu.
M'modzi mwa wa makalo a Zione Masamba wati ganizo ladza nthawi yabwino pomwe makolo amalephera kutumiza ana awo ku sukuluzi.
"Chosangalatsa china ophunzira amalandira chakudya ku sukuluku," watero Masamba.