PortHerald Press

  • Home
  • PortHerald Press

PortHerald Press Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from PortHerald Press, Media Agency, Chikwawa, .

Registered Media House
best online publication that provides catchy and tangible breaking news.

provide top-notch media consultancy and advertisements
✉️ [email protected]
#"TheTruthUncovered"

29/12/2025



ANTHU OKWANA ATATU AFA NDIPO MAKUMI ANAYI NDI CHIMODZI ( 41 ) AVULALA.

✍️Wolemba_Kupatsa_Manyozo

Anthu okwana atatu amwalira ndipo anthu 41 avulala kaamba ka mvula yamphanvu yomwe inagwetsa zipupa kuyambira pa 22 December mpaka pa 28 December.

Izi ndimalingana ndi kalata yomwe mkulu wa bungwe la DODMA Wilson Moleni wasayinira yomwe ikufotokoza nso kuti anthu pafupi fupi 32,422 ochokera maanja okwana 7,205 akhudzidwa ndi ngozi yi m'maboma okwana 13.

Moleni wati pakadali pano Nthambi ya DODMA ikupereka thandizo loyenerera kwa anthu okhudzidwa -wa monga chakudya, mapepala ofolera nyumba, komanso zofunda mwazina.

Iwo atinso ngati nthambi akugwira ntchito limodzi ndi gulu lomwe limathandiza kupulumutsa anthu panthawi yomwe ngozi ikuchitika, nthambi yopeleka chitetezo mdziko muno ya MDF nthambi ya polisi a Malawi Red Cross komanso nthambi yoona zanyengo kungotchulapo ochepa.

Press

  press  CHIDZIWITSO PANKHANI YAKUSUTA FODYA CHIKISOWABE    _Zakeyu_Mamba_{Lilongwe)Ngakhale kuti anthu ochepa amasuta f...
29/12/2025

press

CHIDZIWITSO PANKHANI YAKUSUTA FODYA CHIKISOWABE


_Zakeyu_Mamba_{Lilongwe)

Ngakhale kuti anthu ochepa amasuta fodya mdziko muno, akatswiri azaumoyo ati chidziwitso cha kuoopsa kosuta fodya chikadali chochepa.

Kafukufuku akusonyeza kuti amuna 3 peresenti ndi akazi 3 peresenti amasuta, pomwe ena ambiri amakhudzidwa ndi utsi wa fodya m’malo osiyanasiya.

Nelson Zakeyo, mphunzitsi wa chikhalidwe komanso wolimbikitsa zaumoyo, wati anthu ayenera kudziwa kuti kusuta kumabweretsa matenda ena.

“Ngati munthu akusankha kusuta, ayenera kudziwa zoopsa zake,” anatero.

Womenyera ufulu wa zaumoyo Maziko Matemba wati kufunika kwa kulimbikitsa maphunziro m’madera n’kofunika kwambiri, makamaka chifukwa fodya ndi chuma chachikulu cha dziko.

Bungwe la WHO lati anthu oposera 120 miliyoni anasiya kusuta fodya pa dziko lonse kuyambira 2010.

Press

  PressOYIMBA NYIMBO ZA CHAMBA CHALOKOLO (LOCAL) FRED MW WATULUTSA YATSOPANO. ✍️Wolemba_Praise_EddingsOyimba nyimbo za c...
29/12/2025

Press

OYIMBA NYIMBO ZA CHAMBA CHALOKOLO (LOCAL) FRED MW WATULUTSA YATSOPANO.


✍️Wolemba_Praise_Eddings

Oyimba nyimbo za chamba cha local Fred Mw watulutsa nyimbo yatsopano yomwe akupempha Mulungu kuti amuchotsere mkwiyo kuopa wina kumugwila pa khosi .

Mkati mwa nyimboyi Fred Mw akukamba zambiri za mkazi amene anamukonda koma ali olakwika ndipo wayima poyera ndikulengeza kuti vuto ndi iyeyo ANAKONDA CHITSIRU zambiri mu link iyi 👇

https://youtu.be/PB_iGL0LMiM?si=VvptjxLz1XwQ5QPI

Press

A New Song by titled "Ndinakonda Chitsilu" Enjoy it ✨✨✨🎉🎉🎉 ...

  PressNJIRA ZOLIMBAN A NDI M'MAVUTO A CHUMA ZIKUSOWABE — Kapito.    _Mamba (Lilongwe)Mkulu wa bungwe la Consumers Assoc...
29/12/2025

Press

NJIRA ZOLIMBAN A NDI M'MAVUTO A CHUMA ZIKUSOWABE — Kapito.

_Mamba (Lilongwe)

Mkulu wa bungwe la Consumers Association of Malawi (CAMA), a John Kapito, ati dziko lino likupitirila kuvutika chifukwa chosowa zochita zenizeni zothana ndi mavuto a zachuma.

Kapito wati ngakhale pakhala zokambirana zambiri zokhudza kukonza chuma, palibe zomwe zikuwoneka pagalaundi zomwe zikuthandiza anthu wamba.

“Palibe chomwe chikuchitika kwenikweni cholimbana ndi mavuto a chuma,” atero a Kapito, ponena kuti kusachitapo kanthu kukukulitsa mavuto komanso kuchepetsa chidaliro cha anthu.

Iye wachenjeza kuti ngati sipakhala njira zomveka komanso zogwirizana,a Malawia asayembekezere kusintha kulikose.

Kapito ananenanso kuti chiyembekezo chokha sichokwanira.

“Tiyenera kuchita kuchitapo kanthu, osangoyembekezera,” anatero a Kapito.

A kapito akumema boma ndi okhudzidwa onse kuti ayambe kugwiritsa ntchito njira zenizeni zokhazikitsa chuma ndi kuthandiza miyoyo ya anthu.

Goal keeper uyu akuyenera kulandiratu ulemu 😀
29/12/2025

Goal keeper uyu akuyenera kulandiratu ulemu 😀

 SADAPEZEBE THANDIZO LOGWIRA MTIMA PA MAPHUNZIRO A MWANA WAKE    (Mulanje)Grace Mangalusa, mayi uja wa ku Mulanje yemwe ...
29/12/2025


SADAPEZEBE THANDIZO LOGWIRA MTIMA PA MAPHUNZIRO A MWANA WAKE

(Mulanje)

Grace Mangalusa, mayi uja wa ku Mulanje yemwe akhala akusakasaka thandizo la school fees la mwana wake Hopeson, wophunzira wa form 2 ku sekondare ya St. Patrick's wati anangolandira 100 000 kwacha kwa munthu m'modzi yemwe ndi phungu wadera lomwe amakhala kwa Mkando, Patricia Kaliat ngati thandizo.

Mayi Mangalusa, wati amafunikira ndalama yokwana 770 000 ngati ndalama yomwe amayenera kukalipira ku sukulu koma ndalama yomwe amafuna kukaipereka ku sukulu ko yochokera kwa Kaliati anamubweza akuluakulu apa sukuluyi ponena kuti ndiyochepa.

Apa, mayi yu wati wagwira njakata chifukwa Hopeson alibe komwe angapeze thandizo kwa achibale kamba kosowa.

Poyankhula ndi PortHerald Press Lolemba, Mangalusa wati atapita ku ofesi yoona za chisamaliro chawanthu m'boma la Mulanje sadapeze thandizo chifukwa anamuuza kuti makhansala omwe angowasankha kumene sadayambe kugwira ntchito bwino bwino.

Iye apempha ofuna kuthandizapo kuti akhonza kugwiritsa ntchito njira izi!

Nambala yake 0884825791/0884914095

Ya St.Patrick's secondary school 0888584018

Account number ya St. Patrick's secondary school
National Bank 2699257


&Hopeson.

 KOLERA YABUKA KU NENO, KASUNGU   (Lilongwe)Boma la Malawi lakhazikitsa njira zolimba zothana ndi matenda a kolera kutsa...
29/12/2025


KOLERA YABUKA KU NENO, KASUNGU

(Lilongwe)

Boma la Malawi lakhazikitsa njira zolimba zothana ndi matenda a kolera kutsatira kupezeka kwa matendewa m’maboma a Kasungu ndi Neno.

Unduna wa Zaumoyo wati pakadali pano anthu 11 apezeka ndi kolera.

Ku Kasungu anthu asanu ndiomwe apezeka ndi nthendayi pamene ku Neno kwapezeka anthu atatu, ndipo a zaumoyo ayamba kale ntchito yowunika, kuyesa ndi kulondoloza anthu onse omwe anakumana ndi odwalawa.

Polankhula pansonkhano wa atolankhani ku Lilongwe, nduna ya zaumoyo, Madalitso Waloi, yanena kuti boma lakhazikitsa ndondomeko zothana ndivutoli m'dziko muno, makamaka m'madera omwe ali pachiwopsezo.

Iye watsindika kufunikira kwa kugwiritsa ntchito madzi aukhondo, kusamba m'manja ndi kusamalira chilengedwe.

Waloi anapitiliza kunena kuti Boma likugwiranso ntchito limodzi ndi bungwe la WHO ndi othandizana nawo ena, pamodzi ndi kulumikizana ndi mayiko oyandikana nawo kuti alimbikitse kuwunika matenda m'malire.

Pakadali pano, boma layika ndalama zokwana K600 miliyoni pa ndondomeko yolimbana ndi kolera, ngakhale likuti likufunikabe ndalama zina zokwana K5.2 biliyoni.

Boma lapempha nzika zonse kuti zizitsatira malangizo a zaumoyo.

 ASANU APHEDWA, ENA AVULALA NDI ZIGAWENGA    (Blantyre)ku Syria, anthu asanu ndi m'modzi aphedwa pa chiwembu chomwe ziga...
29/12/2025


ASANU APHEDWA, ENA AVULALA NDI ZIGAWENGA

(Blantyre)

ku Syria, anthu asanu ndi m'modzi aphedwa pa chiwembu chomwe zigawenga zaphulitsa bomba mu mzikiti wa Iman Ali kudera la Wadi al-Zahab ku Homs.

Chiwembuchi chachitidwa ndi gulu lomwe linachoka ku Hayat Tahri al-Sham chaka chatha, malingana ndi a chitetezo ku Syria.

Gulu-li ndilomwenso lidakukhudzidwa kuti lidaphulitsa bomba ku mzikiti wa Mar Elias ku Damascus.

Pakadalipano, asilikali a nkhondo mdzikolo alimbitsa chitetezo m'malo onse opembedzera ndipo kafukufuku akupitilira kufuna kudziwa zambiri zokhudza gulu-li ndi zolinga zake.

 MVULA YASOKONEZA MALONDA KU MZIMBA    (Mzimba)Ntchito za malonda zasokonekera m'boma la Mzimba kutsatira mvula yomwe ya...
28/12/2025


MVULA YASOKONEZA MALONDA KU MZIMBA

(Mzimba)

Ntchito za malonda zasokonekera m'boma la Mzimba kutsatira mvula yomwe yakhala ikugwa kuchokera Lachisanu mpaka Lamulungu lero.

Elizabeth Lupeska, wochita malonda pa msika wa pa boma wati kwakhala kovuta mayendedwe kukagulitsa malonda ake.

Malingana ndi mtolankhani wathu, amalonda ochuluka angobindikira mma shop mwawo kudikilira mvulayi kuti ikate.

 MALO ENA OMWETSERA MAFUTA ALIBE MAFUTA KU BALAKA    (Balaka)Pali chiopsyezo chakuti mafuta a galimoto  a petulo ayambas...
28/12/2025


MALO ENA OMWETSERA MAFUTA ALIBE MAFUTA KU BALAKA

(Balaka)

Pali chiopsyezo chakuti mafuta a galimoto a petulo ayambaso kusowa kumalawi.

Uku ndiku Balaka komwe galimoto zili pa mzere kuti zithire mafuta.

PortHerald Press itayendera yapeza kuti mafuta akupezeka pa malo omwetsera mafuta a Simso basi pomwe malo ena omwetsera mafuta mulibe mafuta a galimoto a petulo.

kusowa kwa mafuta a galimoto ndi vuto lalikulu lomwe dziko la Malawi limakumana nalo chaka ndi chaka.

Izi zili chomwechi ngakhale boma likuyesesa kuika njira zosiyanasiyana kuti lithane ndivutoli.

Boma linasitha njira yakagulidwe ka mafuta yakale ya open tender kupita ku government to government (G2G) chaka chino.

Mafuta a galimoto a petulo akasowa khani zambiri za malonda zimasonekera mudziko muno pomwe zinthu zimakwera mitengo komaso kusowa kumene.

 NSANJE MEDICALS NDI AKATSWIRI A NATIONAL BANK LEAGUE   (Nsanje)Team ya Nsanje Medicals yakhala akatswiri a league ya Na...
28/12/2025


NSANJE MEDICALS NDI AKATSWIRI A NATIONAL BANK LEAGUE


(Nsanje)

Team ya Nsanje Medicals yakhala akatswiri a league ya National Bank lero pa 28 December itagonjetsa team ya Zion FC pa bwalo ya Youth Center .

Nsanje Medicals yagonjetsa team ya Zion FC ndi zigoli zinayi kwa chimodzi ( 5-1 ) mu mphindi 90+ .

Katswiri otchedwa Charity Charles ndi yemwe wagoletsa zigoli zokwana zinayi ndipo chimodzi chokwanitsa zisanu wagoletsa ndi Yohane.

Charity Charles ndi osewera amene asankhidwa ngati osewera bwino muja muchingelezi timati man of the Match .

 SOULS ON FIRE!!    (Blantyre)Showers of Blessings Church will officially relaunch its One Million Soul Winning Campaign...
28/12/2025


SOULS ON FIRE!!

(Blantyre)

Showers of Blessings Church will officially relaunch its One Million Soul Winning Campaign on January 4, 2026, at its headquarters in Blantyre, Chileka.

The evangelistic initiative aims to spread the message of hope, faith, and salvation to communities across the nation and beyond.

The campaign, which originally began as a vision to reach one million souls for Christ, is being revived with fresh passion, strategic outreach programs, and increased member involvement.

Senior Apostle and Founder of the church, Dr. Joshua Jamali Milanzi, emphasized the importance of personal and collective responsibility in soul winning. "This campaign is not just a program; it is a calling. Every believer has a role to play in sharing God's love and bringing hope to the lost," he said.

The One Million Soul Winning Campaign is expected to run throughout 2026, with special outreach weeks and revival services.


: Left_Milanzie, Right_Ndovi

Address

Chikwawa

Telephone

+265990485072

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when PortHerald Press posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share