27/05/2026
Apolisi ku Lilongwe agwira abambo awiri omwe kale anali kundende chifukwa chogwidwa ali ndi mfuti ya mtundu wa pistol ndi zipolopolo zopanda chilolezo.
Malinga ndi m'neneri wa Polisi ya Lilongwe, Hastings Chigalu, awiriwa ndi Steven Kanongola Kambwiri wa zaka 54 ndi Philip Lazaro wa zaka 51. Mzawo wawo wina, Jack Semu Kapilikitsa, adathawa apolisi asanawagwire.
Chigalu adati chochitikacho chidachitika pa 26 May 2026 ku Bwalolanjovu mumzinda wa Lilongwe. Apolisi adachita chipikisheni mgalimoto yomwe anthuwa anali kuyendamo ndipo ndipamene adapeza mfutiyo.
Iye adanenanso kuti Kambwiri ndi Kapilikitsa amene wathawayu adangotuluka kumene pa belo pa mlandu wakuba. Komanso awiriwa akuganiziridwa kuti kale adachita chiwembu ndi nzika ya ku India. Akuti adaphwetsa matayala agalimoto yake, kenako nambera chikwama chokhala ndi ndalama.
Pakadali pano Kambwiri ndi Lazaro adzaonekera kubwalo la milandu kuti ayankhe mlandu wokhala ndi mfuti yopanda kalata yovomerezeka.
Wolemba John Bruce Jonathan