Malawi Breaking News BNL

Malawi Breaking News BNL Kukupatsilani Nkhani momvekabwino komanso mofufuzidwa ndi akadawulo pa Nkhani zosiyanasiyana.

 KAJOKE ALAMULIDWA KUBWEZA NDALAMA KU MA BANKERBungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo mdziko muno la Football Ass...
25/05/2023



KAJOKE ALAMULIDWA KUBWEZA NDALAMA KU MA BANKER

Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo mdziko muno la Football Association of Malawi (FAM) lagamula kuti katswiri osewera kutsogolo kwa timu ya Nyasa Big Bullets Hassan Kajoke abweze ndalama zokwana 3.9 million kwacha ku timu ya Silver Strikers.

Malingana ndi chigamulochi, katswiriyu akuyenera kuchita izi pasanathe masiku asanu ndipo kuti kupanda kutero ndalamayi adzaipereka ndi chiongola dzanja.

Bungweli latinso Kajoke sakuyenera kusewera masewero aliwonse kuno pokhapokha atabweza ndalamayi komanso ina yomwe adapatsidwa ngati malipiro ake a January ndi February ku ma bankers.

Kumbali ina, ma bankers awapezaso olakwa posatsata malamulo ndipo agamulidwa kupereka ndalama yokwana 900 000.

Omuyimilira Kajoke , Ken Mvula nayeso akuyenera kupereka 500 000 atapezekanso olakwa pa nkhaniyi, ndalamazi malingana ndi FAM, zikuyenera kuperekedwa pasanathe masiku asanuso.

Pomaliza chigamulochi chati yemwe sakukhutira ndi izi atha kumang'ala kuti chiwunikidweso, koma akuyenera kugwapo ndi dipo lokwana 800 000.

Wolemba: Brenda kamowa

13/02/2023

Anthu omwe asonkhana pa bwalo la masewera a mpira wa miyendo la mgona ku area 25 mu mzinda wa Lilongwe akuwa monyazitsa Senior Chief Chitukula yomwe imawuza mtsogoleri wa dziko Dr Lazarus Chakwera kuti ndondomeko ya AIP idayenda bwino.

Mfumuyi imayankhula izi polandila anthu omwe asonkhana pa msonkhano wokhazikitsa kampeni yothetsa Kolera mdziko muno.

"Tithokoze a President kamba koti ndondomeko ya AIP Idayenda bwino,"inatelo mfumu yi kwinaku ikukanda chibwano.

Koma atangolakhula izi,anthu anayamba kukuwa ndi kunyoza mfumuyi kuti; "Iwe Iwe Iwe !!!!!!mutu wako sukugwira.

Ndipo ena amati ; "Mulandeni chi nkuza mawu."

Pakadali pano mwambo uli nkati.
Kampeni yothetsa kolela yi ikukhazikitsidwa pansi pa Mutu wakuti 'Tiyambe ndife kuthetsa Kolera.'
-Herbert Katanda-

Mkulu wa bungwe lothana ndi katangale a Martha Chizuma ayimitsidwa ntchito kuyambira pa 31 January 2023.
01/02/2023

Mkulu wa bungwe lothana ndi katangale a Martha Chizuma ayimitsidwa ntchito kuyambira pa 31 January 2023.

NDUNA ZA TSOPANOPresident Lazarus Chakwera kumawa kwa pa 01-02-2022 wasankha nduna zatsopano Mogwilizana ndi mphamvu za ...
01/02/2023

NDUNA ZA TSOPANO

President Lazarus Chakwera kumawa kwa pa 01-02-2022 wasankha nduna zatsopano Mogwilizana ndi mphamvu za mamulo oyendesera dziko lino lapa gawo (94)01 ndipo mayina andunawa Ali motere:

1. President of the Republic of Malawi, Commander-in-Chief of the Malawi
Defence Force, His Excellency Dr. Lazarus McCarthy Chakwera.
2. Vice President of the Republic of Malawi, Right Honourable Dr. Saulos Klaus
Chilima.
3. Minister of Finance and Economic Affairs, Hon. Sosten Gwengwe, MP.
4. Minister of Foreign Affairs – Hon. Nancy Tembo, MP.
5. Minister of Agriculture – Hon. Sam Kawale, MP.
6. Minister of Natural Resources and Climate Change – Hon. Michael Usi.
7. Minister of Local Government, Unity, and Culture – Hon. Richard
Chimwendo Banda, MP.
8. Minister of Justice – Hon. Titus Mvalo.
9. Minister of Homeland Security – Hon. Dr. Ken Zikhale Ng’oma, MP.
10.Minister of Health – Hon. Khumbize Kandodo Chiponda, MP.
11.Minister of Trade and Industry – Hon. Simplex Chithyola, MP.
12.Minister of Youth and Sports – Hon. Uchizi Mkandawire, MP.
13.Minister of Education – Hon. Madalitso Wirima Kambauwa, MP.
14.Minister of Transport and Public Works – Hon. Jacob Hara, MP.
15.Minister of Mining – Hon. Monica Chang’anamuno, MP.
16.Minister of Tourism – Hon. Vera Kamtukule.
17.Minister of Gender – Hon Jean Muonaowauza Sendeza, MP.
18.Minister of Labour – Hon. Agnes Makonda Nyalonje.
19.Minister of Defence – Hon. Harry Mkandawire.
20.Minister of Water and Sanitation – Hon. Abida Mia, MP.
21.Minister of Energy – Hon. Ibrahim Matola.
22.Minister of Lands – Hon. Deus Gumba, MP.
23.Minister of Information – Hon. Moses Kumkuyu.
24.Deputy Minister of Local Government, Unity, and Culture – Hon. Owen
Chomanika, MP.
25.Deputy Minister of Health – Hon. Halima Alima Daud, MP.
26.Deputy Minister of Education – Hon. Nancy Chaola Mdooko, MP.
27.Deputy Minister of Water and Sanitation – Hon. Liana Kakhobwe Chapota,
MP.
The appointments are with effect from 31st January 2023

1. Ndip

Kabinenti yasopano mulibe a Kazako komanso a Mkaka ndipo a kumkuyu ndiomwe Ali pamalo pa akazako.
01/02/2023

Kabinenti yasopano mulibe a Kazako komanso a Mkaka ndipo a kumkuyu ndiomwe Ali pamalo pa akazako.

A Malawian musician known as Walycris who trended with the song "Achalume" has died in an accident involving a Matours b...
23/12/2022

A Malawian musician known as Walycris who trended with the song "Achalume" has died in an accident involving a Matours bus and a truck.

The bus was coming from Johannesburg to Malawi and was hit by a truck trailer on the drivers side, injuring several passengers, the driver and killing one passenger, a musician Walycris Wanyengo.

According to Matours, the bus was brand-new, and had clocked 1 month since it arrived.

Lero ku St Augustine Ku Mangochi
17/12/2022

Lero ku St Augustine Ku Mangochi

CHAKWERA WAKHULULUKIRA MAI KUNJENduna za za chitetezo cha m'dziko, Jean Sendeza yawuza komishonala wa ndende za dziko li...
07/12/2022

CHAKWERA WAKHULULUKIRA MAI KUNJE

Nduna za za chitetezo cha m'dziko, Jean Sendeza yawuza komishonala wa ndende za dziko lino kuti atulutse yemwe anali komishonala wa bungwe la zisankho la MEC, Linda Kunje.

M'mwezi wa August chaka chino, aKunje anagamulidwa kukhala ku ndende atapezeka olakwa pa mlandu omwe iwo anapalamula pamodzi ndi dalavayilala wawo, John Tewesa, osokoneza mdipiti wa galimoto za President Lazarus Chakwera.

Kalata yomwe aSendeza alembera mkulu wa ndendeyu, Wandka Phiri yati mayi Kunje ali pa mndandanda wa anthu okhululukilidwa ndi a Chakwera, pomwe tikusendera nyengo ya zisangalalo za khilisimasi ndi chaka cha tsopano.

Zomba Chief Resident Magistrate Austin Banda adagamula aKunje kukakhala ku ndende miyezi 18.

07/12/2022

“CHOTSANI NTCHITO MVALO, SENDEZA KOMANSO YOLAMU"

Bungwe la akatswiri pa ndale la Political Science Association lauza President Lazarus Chakwera kuti achotse ntchito nduna yaza chilungamo, Titus Mvalo, yaza chitetezo cha m’dziko, Jean Sendeza komanso mkulu wa polisi Merlyne Yolamu ati kaamba kachibwana pa nkhani ya kumangidwa kwa mkulu wa ACB, Martha Chizuma.

Mu kalata yomwe atulutsa, mlembi wa bungweli, Makhumbo Munthali wati kusemphana Chichewa kuchokera kwa akuluakulu a boma pa nkhani-yi kukuotseratu poyera kuti palibe utsogoleri komanso pali kufuna kubisa a ndale ena a m’maundindo omwe m’ngachinyengo.

Apa, bungweli lauza aMalawi kuti adzuke ku tulo tawo pano ndikuchitapo kanthu pothana ndi magulu a anthu omwe alimba mtima kusakaza chuma cha boma mopanda mantha komanso chisoni.

Munthali wati bungweli likudziwa bwino kuti kuwamanga a Chizuma ndikufuna kuwapatsa mantha kuti alephere kugwira ntchito yawo momasuka.

CAREN Mudibo wins the ironfit classic and fitness expo, women's figure... Pongezi kwake!
05/12/2022

CAREN Mudibo wins the ironfit classic and fitness expo, women's figure... Pongezi kwake!

BREAKING NEWS: President of South Africa Cyril Ramaphosa has a case to answer, according to Section 89 Panel report.
30/11/2022

BREAKING NEWS: President of South Africa Cyril Ramaphosa has a case to answer, according to Section 89 Panel report.

29/11/2022

DNA by Sasoka🤝

Address

Blantyre
1103

Telephone

+27736372877

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Breaking News BNL posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Malawi Breaking News BNL:

Share