Al Haqq Magazine

Al Haqq Magazine Registered at GPO as a Newspaper
THE TRUTH - AUTHENTIC ISLAMIC INFORMATION FOR ALL

Kuchokera mmawa pa 4 mpaka pa 8 mwezi uno wa June, Asilamu mazanamazana padziko lonse akhala akuchita Hajj, kukwaniritsa...
03/06/2025

Kuchokera mmawa pa 4 mpaka pa 8 mwezi uno wa June, Asilamu mazanamazana padziko lonse akhala akuchita Hajj, kukwaniritsa msichi ya chisanu yofunikira kwambiri kwa Msilamu wina aliyense.

Ulendo umenewu umasonyeza kutsatira mwachindunji machitidwe a Atumiki a mbuyo komanso kuzichepetsa kwawo ndikuzipereka pamaso pa Allah.

Kulowa Ihram
----------------
Asanayambe Hajj, anthu ochita Hajj-wa amayenera kuziyeretsa kaye paokha. Abambo amavala nsalu ziwiri zoyera zosasokedwa, pomwe amayi amavala zovala zoyenera ngati momwe amayenera kuvalira nthawi zonse. Kachitidwe kameneka kamaonetsa anthu kukhala ofanana pamaso pa Allah komanso kugonjera. Ndondomeko imeneyi imatchedwa Ihram.

Tsiku loyamba: Kufika ku Mecca komanso Ulendo wopita ku Mina
------------------------------------------------------------------------
Akafika ku Mecca, ma Hujjaj amayamba ulendo wawo ndi Tawaf, kumeneku ndi kuizungulira Kaaba kasanu ndi kawiri. Izi zikuwonetsa umodzi wa opembedza Mulungu mwa choonadi. Kenako amachita Sa’i, kumeneku ndi kuyenda kasanu ndi kawiri (7) pakati pa mapiri a Safa ndi Marwa, pokumbukira mayi Hajara panthawi imene ankafunafuna madzi kuti mwana wake Ismail amwe atathodwa ndi ludzu.

Kenako, akachoka kumeneku amayenda kupita ku Mina, mtunda wa makilomita 8 kuchokera ku Kaaba. Ndipo amadzagonapo usiku mu msasa waukulu, kupemphera ndikuchita ma Ibadah osiyanasiyana.

Tsiku lachiwiri: Tsiku la Arafah
---------------------------------
Madzulo ake, amayenda kupita ku phiri la Arafat, mtunda wa makilomita 15. Malo amenewa amachita pemphero la Wuquf, komwe ndi kuyimirira pomwe amachita mapemphero osiyanasiyana ndi kupempha chikhululukiro kwa Allah. Limeneli ndi gawo lofunika kwambiri la Hajj.

Usiku wake amayenda kupita ku Muzdalifah, kumeneku amakachita mapemphero a Maghrib ndi Isha. Pamenepa, amasonkhanitsa miyala yomwe adzagwiritse ntchito pa Ramy al-Jamarat (yogendera Satana) ndipo usiku onse amakhala ali pa malo amenewa kuchita ma Ibadah osiyanasiyana.

Tsiku lachitatu:Tsiku la Eid al-Adha ndi Kugenda Miyala
--------------------------------------------------------------
Ku Mina, ma Hujjaj amagenda miyala isanu ndi iwiri (7) kwa Satana, chimene chili chizindikiro chokana zinthu zoipa ndi machimo.
Kenako amazinga nyama ndi kupereka nsembe, pokumbukira chikhulupiriro cha Abraham pamene ankafuna kupereka nsembe mwana wake pofunitsitsa kutsatira lamulo la Mulungu. Nyama imeneyi imaperekedwa kwa osowa.

Ndipo kenako abambo amameta tsitsi lawo, ndipo amayi amapungula pang’ono tsitsi lawo, chizindikiro cha kuyambiranso moyo wauzimu.

Kenako amayenda kubwerera ku Mecca kuchita Tawaf al-Ifadah, kuzungulira Kaaba kachiwiri, kumene kumasonyeza kumaliza magawo akuluakulu a Hajj.

Tsiku lachinayi ndi lachisanu: Kugenda Miyala ndi Tawaf Yomaliza
------------------------------------------------------------------------
Kwa masiku awiriwa, ma Hujjaj amapitiriza kugenda miyala ku zipilala zitatu zonse zimene zili pa Mina. Akamaliza, amachita Tawaf al-Wada, kuzungulira Kaaba komaliza.

Ulendo uwu si umangokwaniritsa lamulo la chipembedzo chokha ayi, koma umabweretsa mtendere wauzimu, umodzi ndi chikondi pakati pa anthu ochokera m'mayiko osiyanasiyana. Tipemphe Allah kuti atipatse kuthekera kuti tsiku lina nafe tidzachite Hajj. Aameen!

Zithunzi: AP Photo, Getty Images

From June 4 to June 8, 2025, millions of Muslims worldwide will undertake the Hajj pilgrimage to Mecca, fulfilling a onc...
03/06/2025

From June 4 to June 8, 2025, millions of Muslims worldwide will undertake the Hajj pilgrimage to Mecca, fulfilling a once-in-a-lifetime religious obligation. This journey encompasses a series of spiritual rites that trace the footsteps of prophets and symbolize unity, humility, and devotion.

Pre-Hajj: Entering the State of Ihram
----------------------------------------
Before commencing Hajj, pilgrims enter a state of spiritual purity known as Ihram. Men don two unstitched white cloths, while women wear modest attire. This uniformity eliminates distinctions of class, wealth, and nationality, emphasizing equality before Allah.

Day 1: Arrival in Mecca and Journey to Mina
-------------------------------------------------
• Tawaf and Sa’i: Upon arrival in Mecca, pilgrims perform Tawaf, circling the Kaaba seven times anti-clockwise, symbolizing the unity of believers in the worship of the One God - Allah. Following this, they perform Sa’i, walking seven times between the hills of Safa and Marwa, commemorating Hagar's (Hajrah) search for water for her son Ishmael.

• Travel to Mina: Pilgrims proceed to Mina, approximately 8 kilometers east of the Kaaba, where they spend the night in prayer and reflection within a vast tent city designed to accommodate the multitude of worshippers.

Day 2: The Day of Arafah
----------------------------
• Stand at Arafat: Pilgrims travel to the plains of Arafat, about 15 kilometers from Mina, to perform the pivotal rite of Wuquf, standing in prayer and contemplation from midday to sunset. This act symbolizes the climax of Hajj and is considered a preview of the Day of Judgment.

• Evening at Muzdalifah: After sunset, pilgrims journey to Muzdalifah, where they perform the Maghrib and Isha prayers and collect pebbles for the upcoming ritual of stoning the devil. They spend the night under the open sky, engaging in prayer and rest.

Day 3: Eid al-Adha and the Stoning Ritual
-----------------------------------------------
• Stoning of the Devil: At Mina, pilgrims perform the Ramy al-Jamarat, throwing seven pebbles at the largest of three pillars, symbolizing the rejection of evil.

• Animal Sacrifice: Pilgrims partake in the ritual sacrifice of an animal, commemorating Prophet Abraham's willingness to sacrifice his son in obedience to God. The meat is distributed among the needy, reflecting the spirit of charity.

• Hair Cutting/Shaving: Men shave their heads or cut their hair, and women cut a small portion of their hair, signifying spiritual renewal.

• Return to Mecca: Pilgrims return to Mecca to perform another Tawaf around the Kaaba, known as the Tawaf al-Ifadah, marking the completion of the major rites of Hajj.

Days 4-5: Continued Stoning and Farewell
-----------------------------------------------
• Stoning Rituals: Over the next two days, pilgrims continue the stoning ritual by throwing pebbles at all three pillars in Mina, reaffirming their commitment to resisting temptation.

• Farewell Tawaf: Before departing Mecca, pilgrims perform the Tawaf al-Wada, a farewell circumambulation of the Kaaba, bidding goodbye to the sacred city.

Photos courtesy of AP Photo and Getty Images

Question-----------What is legislated for whoever wants to perform Hajj and Umrah?Answer----------Whoever decides to und...
03/06/2025

Question
-----------
What is legislated for whoever wants to perform Hajj and Umrah?

Answer
----------
Whoever decides to undertake a long journey for Hajj or anything else, it is legislated for him to pay off his current debts or to seek the permission of those to whom he owes debts if he knows that they are eager and anxious in requesting their payment. Then, he should write down his bequests and whatever he is responsible for and his wealth or whatever he owes. Then, he should offer the prayer of Al-Istikharah, seeking from his Lord that He chooses for him what is most beneficial and correct. Then he should go ahead with whatever his heart feels comfortable with. He should choose righteous companions from the people of knowledge and the religion (to travel with) and he should bring books of knowledge with him that he can benefit from concerning the acts of Hajj and other things, and that will benefit his brothers. He should
gather an abundance of wealth, money and provisions so that he can take care of himself or his brothers if there is a need.

Read more:

Click to download Al-Haqq May 2025

Funso-------Mwamuna wanga sakundilola kupita kochita Hajj ngakhale tili ndi kuthekera kutero. Iyeyo wachita Hajj kasanu ...
02/06/2025

Funso
-------
Mwamuna wanga sakundilola kupita kochita Hajj ngakhale tili ndi kuthekera kutero. Iyeyo wachita Hajj kasanu m’moyo mwake ndipo samafuna kunditenga kuti tikachite limodzi Hajj-yo. Kodi ndizovomerezeka kupita ku Hajj-ko ndi Mahram wanga ngakhale mwamunayo atakana kutero?

Yankho
--------
Ngati mmene mukufotokozeramu ndi mmene zinthu zanu zilili ndi mwamuna wanu, inu muli ndi ufulu wopita ku Hajj limodzi ndi Mahram (wachibale amene simungathe kukwatirana naye), ngakhale mwamuna wanu atapanda kuvomereza kutero, ndipo zili chomwechi ngati inuyo simunachitepo Hajj iliyonse mu moyo mwanu. Izi ndi kamba kakuti kusiya Hajj yoyamba pamene munthu ali ndi kuthekera kuchita ndi zoletsedwa. Msilamu sayenera kumvera munthu wina pakuchita chinthu chomwe chili chosamvera malamulo a Allah ngakhale atakhala wokondeka anu.

Werengani zambiri apa:

Click to download Al-Haqq May 2025

This month's edition of Al-Haqq covers pressing issues around Hajj, Qurban and general Islamic issues. Follow the link b...
02/06/2025

This month's edition of Al-Haqq covers pressing issues around Hajj, Qurban and general Islamic issues. Follow the link below to read what's in store for you.
https://bit.ly/43szmac

Eid Mubarak!May Allah accept our fasting and grant us his mercy and blessings 🙌 🙏
30/03/2025

Eid Mubarak!
May Allah accept our fasting and grant us his mercy and blessings 🙌 🙏

Funso 𝐊𝐮 𝐧𝐭𝐜𝐡𝐢𝐭𝐨 𝐤𝐰𝐚𝐭𝐡𝐮 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢 𝐮𝐤𝐚𝐭𝐡𝐚 𝐭𝐢𝐦𝐚𝐬𝐨𝐧𝐤𝐡𝐞𝐫𝐚𝐧𝐚 𝐧𝐝𝐚𝐥𝐚𝐦𝐚 𝐧𝐝𝐢𝐤𝐮𝐦𝐩𝐚𝐭𝐬𝐚 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐦𝐦𝐨𝐝𝐳𝐢. 𝐌𝐰𝐞𝐳𝐢 𝐰𝐢𝐧𝐚𝐰𝐨 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐰𝐢𝐧𝐚 𝐦𝐩𝐚𝐤𝐚 𝐚𝐥...
04/03/2025

Funso

𝐊𝐮 𝐧𝐭𝐜𝐡𝐢𝐭𝐨 𝐤𝐰𝐚𝐭𝐡𝐮 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢 𝐮𝐤𝐚𝐭𝐡𝐚 𝐭𝐢𝐦𝐚𝐬𝐨𝐧𝐤𝐡𝐞𝐫𝐚𝐧𝐚 𝐧𝐝𝐚𝐥𝐚𝐦𝐚 𝐧𝐝𝐢𝐤𝐮𝐦𝐩𝐚𝐭𝐬𝐚 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐦𝐦𝐨𝐝𝐳𝐢. 𝐌𝐰𝐞𝐳𝐢 𝐰𝐢𝐧𝐚𝐰𝐨 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐰𝐢𝐧𝐚 𝐦𝐩𝐚𝐤𝐚 𝐚𝐥𝐢𝐲𝐞𝐧𝐬𝐞 𝐚𝐝𝐳𝐚𝐥𝐚𝐧𝐝𝐢𝐫𝐞. 𝐍𝐝𝐨𝐧𝐝𝐨𝐦𝐞𝐤𝐨 𝐢𝐦𝐞𝐧𝐞𝐲𝐢 𝐭𝐢𝐦𝐚𝐢𝐭𝐜𝐡𝐚 𝐂𝐡𝐢𝐩𝐞𝐥𝐞𝐠𝐚𝐧𝐲𝐮. 𝐊𝐨𝐝𝐢 𝐂𝐡𝐢𝐬𝐢𝐥𝐚𝐦𝐮 𝐜𝐡𝐢𝐤𝐮𝐭𝐢 𝐜𝐡𝐢𝐲𝐚𝐧𝐢 𝐩𝐚 𝐧𝐤𝐡𝐚𝐧𝐢 𝐢𝐦𝐞𝐧𝐞𝐲𝐢?

Yankho

Palibe vuto ndi mchitidwe oterewu kamba koti imeneyi singongole imene imakhala ndi ndalama yowonjezera pamwamba pake. Choncho mchitidwe umenewu ndi ololedwa mu Chisilamu.

𝐅𝐮𝐧𝐬𝐨𝐏𝐚𝐦𝐞𝐧𝐞 𝐚𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐞𝐧𝐚 𝐚𝐤𝐮𝐬𝐚𝐥𝐚 𝐩𝐨𝐭𝐞𝐧𝐠𝐞𝐫𝐚 𝐤𝐮𝐨𝐧𝐞𝐤𝐚 𝐤𝐰𝐚 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢, 𝐤𝐨𝐝𝐢 𝐩𝐚𝐥𝐢 𝐯𝐮𝐭𝐨 𝐥𝐚𝐧𝐣𝐢 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐤𝐮𝐝𝐢𝐤𝐢𝐥𝐢𝐫𝐚 𝐤𝐮𝐭𝐢 𝐮𝐝𝐳𝐚𝐬𝐚𝐥𝐞 𝐮𝐤𝐚𝐝𝐳𝐚𝐮𝐨...
04/03/2025

𝐅𝐮𝐧𝐬𝐨

𝐏𝐚𝐦𝐞𝐧𝐞 𝐚𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐞𝐧𝐚 𝐚𝐤𝐮𝐬𝐚𝐥𝐚 𝐩𝐨𝐭𝐞𝐧𝐠𝐞𝐫𝐚 𝐤𝐮𝐨𝐧𝐞𝐤𝐚 𝐤𝐰𝐚 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢, 𝐤𝐨𝐝𝐢 𝐩𝐚𝐥𝐢 𝐯𝐮𝐭𝐨 𝐥𝐚𝐧𝐣𝐢 𝐦𝐮𝐧𝐭𝐡𝐮 𝐤𝐮𝐝𝐢𝐤𝐢𝐥𝐢𝐫𝐚 𝐤𝐮𝐭𝐢 𝐮𝐝𝐳𝐚𝐬𝐚𝐥𝐞 𝐮𝐤𝐚𝐝𝐳𝐚𝐮𝐨𝐧𝐚 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢𝐰𝐨 𝐧𝐝𝐢 𝐦𝐚𝐬𝐨 𝐚𝐤𝐨 𝐩𝐨𝐭𝐞𝐧𝐠𝐞𝐫𝐚 𝐇𝐚𝐝𝐢𝐭𝐡 𝐲𝐨𝐧𝐞𝐧𝐚 𝐤𝐮𝐭𝐢: ‘𝐒𝐚𝐥𝐚𝐧𝐢
𝐦𝐮𝐤𝐚𝐮𝐰𝐨𝐧𝐚 𝐧𝐝𝐢𝐩𝐨 𝐦𝐚𝐬𝐮𝐥𝐚𝐧𝐢 𝐦𝐮𝐤𝐚𝐮𝐰𝐨𝐧𝐚 𝐦𝐰𝐞𝐳𝐢𝐰𝐨’.

𝐘𝐚𝐧𝐤𝐡𝐨

Ndizokakamizika kwa Msilamu aliyense kusala pamene zatsimikizika ku deralo kuti mwezi wawoneka ngakhale munthu wauwonayo atakhala munthu mmodzi Msilamu okhulupilira komanso wanzeru zake. Kutanthauzira kwanu kwa Hadith imeneyi ndikolakwika chifukwa Mtumiki (Sallallahu Alayhi Wasallam) amapereka uthengawu kwa Asilamu onse. Mtumiki (Sallallahu Alayhi Wasallam) analamulapo maSwahaba ake (Radhiyallahu Anhum) kuti ayambe kusala munthu mmodzi okhala mu chipululu atatsimikiza zoti wauwona mwezi. Choncho zikatsimikizika kuti mwezi waoneka tiyeni tonse Asilamu tisale osatengera zoti munthuwe pawekha siunauwone mweziwo ndiye siusala.

Exciting! The Al-Haqq Magazine February 2025 Edition covers various issues regarding the Holy month of Ramadhan. Read Al...
04/03/2025

Exciting!

The Al-Haqq Magazine February 2025 Edition covers various issues regarding the Holy month of Ramadhan.

Read Al-Haqq Magazine by following this link https://bit.ly/41iMjkq

🌙 Something Special is Coming Soon! 📖✨  As we prepare for the holy month of Ramadhan, the upcoming edition of Al-Haqq Ma...
10/02/2025

🌙 Something Special is Coming Soon! 📖✨

As we prepare for the holy month of Ramadhan, the upcoming edition of Al-Haqq Magazine is packed with intuitive articles, answers to your burning questions, and spiritual guidance to help you make the most of this blessed season.

We have in the upcoming edition:
🔹 Essential Ramadhan preparation tips
🔹 Fiqh rulings on fasting, moon sighting & Zakaah
🔹 Motivational reflections to strengthen your faith
🔹 Thought-provoking Q&A on daily Islamic matters

📖 Stay tuned for the full release on 29th Shaban | 28th February 2025, Inshaa Allah!

What are you looking forward to in this issue? Drop a comment below!

Address

Globe Chambers
Blantyre
BOX497,BLANTYRE

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Al Haqq Magazine posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Al Haqq Magazine:

Share