Sautul-Huda

Sautul-Huda Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Sautul-Huda, Digital creator, Blantyre.

01/08/2025

Kodi Mukudziwa ?

Nkhumba ndiyoletsedwa kudya osati kwa asilamu okha koma ngakhalenso kwa akhristu, koma kuti chabe Mulungu akayankhula chinthu Mu Quran asilamu amanvetsera, kutsatira ndikukhanzikika pa malemba, nchifukwa chake zimaoneka ngati kusadya nkhumba nzachisilamu, koma ayi ndi chilengedwe kuti munthu asamadye nkhumba.

Qur'an: 2 v 173...nkhumba ndiyoletsedwa
Qur'an: 5 v 3.... Nkhumba ndiyoletsedwa
Qur'an : 6 v 145.... Nkhumba ndiyoletsedwa
Qur'an : 16 v 115..... Nkhumba ndiyoletsedwa

Mulungu analetsa ndipo asilamu anamvera ndikutsatira...

Bible: Leviticus11 v 7-8 ...Nkhumba ndiyoletsedwa
Bible: Deuteronomy 14:8... Nkhumba ndiyoletsedwa

Mulungu analetsa ndipo akhristu sanamvere ndipo sanatsatire..

Quran: 2 v 85.... Akukhulupilira gawo Lina la buku ndikusakhulupilira gawo Lina, Ndiye anthu a mchitidwe uwu, malipiro awo, ndi kunyozeka pa Dziko lapansi, ndipo pa kiyama adzabwenzeretsedwa ku chilango chowawa.

Mtendere ndi Madalitso a Mulungu apite kwa Abraham Mose Yesu ndi Muhammad..

Sautul-Huda

01/08/2025

kuswali swala za sunnah kumanyumba

27/07/2025

Science:
Kafukufuku wa Science wapeza kuti Dzuwa Lili kutali kwambiri ndi planet earth kuposa mwezi exactly 405 times, Komanso ndi lalikulu kwambiri koti mwezi utha kulowamo ka 405 times.

Distance pakati pa Mwezi ndi Planet Earth ndi 370 000 km

Distance pakati pa Dzuwa ndi Mwezi ndi 150 000 000 km.

Ichi nchifukwa chake Dzuwa ndi Mwezi zimaoneka size yofanana ku planet Earth kuno.

chifukwa Dzuwa ndi lalikulu koma Lili kutali, Mwezi ndi waung'ono koma uli pafupi.

Qur'an:
(Mulungu wachifundo analenga) Dzuwa ndi Mwezi, zikuyenda mwachiwerengero. (ar-Rahman 55:5)

Izi zinalembedwa kale M'buku la Korani zaka 1400 zapitazo..

Sautul-Huda

Science:KUZAMA KWA OCEANMtunda otalika mamita 200 kupita pansi mnyanja(Ocean), ndi 20% yokha ya kuzama kwake.  Nyanja ya...
24/07/2025

Science:
KUZAMA KWA OCEAN
Mtunda otalika mamita 200 kupita pansi mnyanja(Ocean), ndi 20% yokha ya kuzama kwake. Nyanja ya Ocean ndiyozama kwambiri kuposa apa.

Ukazama mu Ocean pa mtunda ma kilomita awiri kapena mamita 200, kupitilira apa umayamba kukumana ndi zolengedwa zodabwitsa kwambiri, chifukwa pansi pa nyanja dzuwa limasiya kuoneka pa mtunda wa mamita 200, kupita pansi kuposera apa kuli mdima okha okha.

Ukapitira apa umayamba kuona zolengedwa zomwe zimakhala ndi kuwala mkati mwake, apa umakhala kuti wafika mu zone ya bloluminescent (komwe kumakhala zolengedwa zokhala ndi nyali mkati mwake), chifukwa pafupifupi 90% ya moyo wa Mkati mwa nyanja kumeneko umakhala M'dima okha okha

Kafukufuku winanao wa science amati mafunde timawaona pamwamba pa nyanja aja, mkati Kati mwakenso mmadutsanso mafunde Ena oti atha kukukankhanso uli mkati mwa madzi.

Qur'an:
Kapena ngati M'dima mkati mwa nyanja ya madzi Ochuluka (Ocean), yomwe yaphimbidwa ndi mafunde, ndipo pamwamba pa mafundepo palinso mafunde ndipo pamwamba pa mafundepo Pali mitambo, ndipo M'dima uwu pamwamba pa M'dima uwu, ndipo atati atulutse mkono wake sangathe kuona (kamba ka mdima). (An-Nur24:40)

Anthu amatha kufikira pa 20 miters, ndani uyu analemba za 2km kuzama mnyanja zaka1400 zapitazo?

Izi zinalembedwa kale M'buku la Korani zaka 1400 zapitazo.

Sautul-Huda

MBIRI YA CHITSULOScience:Kale kale kunali nyenyezi za mtundu Wina Wina,  Solar system yathuyi kulibe, kudzela mma Nuclea...
23/07/2025

MBIRI YA CHITSULO

Science:
Kale kale kunali nyenyezi za mtundu Wina Wina, Solar system yathuyi kulibe, kudzela mma Nuclear Fusion, nyenyezizi, mma core mwake zinapanga ma elements olemera kwambiri, Zina mwa izo ndi chitsulo. Tsopano pomwe miyoyo ya nyenyezizi inafika kumapeto ndi kuphulika ngati ma supernova, zinatulutsa chitsulo ndi ma elements ena zomwe zinagwera ku space, ma materials amenewa anakhala gawo limodzi la ma Nebulas zomwe zinakhonza solar system yathuyi, Komanso planet yathuyi.

Mwachidule:
Chilichonse chimene timachiona mu planet yathuyi zinalipo ndi kale kupatula chitsulo, ichi chinachita kugwa kuchokera ku space komwe nyenyezi zimene zinafa kalero, zinasanduka ma nebulas.

Nyenyezi ikafa imasanduka nebula, nebula ndi chinthu chomwe nyenyezi yakufa imasanduka, zimatha kukhala mitambo, koma panali nyenyezi zomwe zinafa kale zomwe zinasanduka chitsulo, ndipo zinabwela mu planet yathuyi, kafukufuku winanao wa science, amati planet yathuyi kunalibe ndipo inapezeka Kamba ka ma nebulas ochokera ku nyenyezi, ndie chitsulo ndi chinthu chochita kubwera kuchokera kunja kwa Solar system yathu.

Qur'an:
Ndipo tidatsitsa Chitsulo momwe muli mphamvu zochuluka Komanso phindu kwa anthu. (57:25)

Mu vesiyi Mulungu akunena kuti chitsulo ndi chochita kubwera kuchoka kumwamba, kale kunalibeko, chinatumizidwa kudzapindulira anthu.

Izi zinalembedwa kale M'buku la Korani zaka 1400 zapitazo

Sautul-Huda

19/07/2025

Qur'an & Science

Ena kuseliku akuti chisilamu amachiopera Shariya...

Ndati ndiwaunikire Kuti Shariya ndi chani.

Kudyetsa anthu Osauka - 107:1-3...imeneyi ndiyo Shariya

Kumwetulira nzako - Sahih al-Bukhari 78-131...imeneyi ndiyo Shariya

Kukhala bwino ndi aneba - 4:36... imeneyi ndiyo Shariya

Maphunziro kwa mwana aliyense. Ibn Majah 224. Imeneyi ndiyo Shariya

Ufulu wa mayi pa ntchito. Sunan Abu Dawood 3404. Imeneyi ndiyo Shariya

Kulemekeza makolo 17:23-24. Imeneyi ndiyo Shariya

Kukaniza ngongole za katapira kuti pasafale umphawi.. (Korani 2:275-279) imeneyi ndiyo Shariya

System ya makhoti yalero anakopera mu Shariya (Sunan Ibn Majah 2360) imeneyi ndiyo Shariya

Democracy ndi Shariya. (Sahih al-Bukhari 3700)

Zipatala zinamangidwa kamba ka Malamulo a Shariya (the hospitals of the Islamic world by Ahmed Isa)

Mwachidule tili kale pansi pa Ulamukiro wa Shariya

Ndiye ndi chani kwenikwenichomwe mukuopa ?

Sautul-Huda

19/07/2025

Qur'an & Science

Chiyambi Cha Science..

Panali nthawi yomwe Maphunziro a science anabuka ku East..

Nthawi yomwe asilamu anatsogolera dziko pa nkhani ya Science, medicine and wisdom.

Izi zinatheka bwanji ? Asilamu amene ndi anthu a simple anakhala bwanji atsogoleri a Maphunziro ndi kafukufuku mu Science ?

Izi zinayambira mzaka za 18th century mu nzinda wa Baghdad ku Iraq, pansi pa Ulamuliro
Wa Abbas (Abbasid Caliph)

Iwo anamanga malo otchedwa Bait al- Hikmah kutanthauza nyumba ya Nzeru za kuya.

Kumeneko Asilamu anali pa mission zosiyanasiyana m'maphunziro kuphatikizapo kumasulira mabuku kuchokera ku Greek, Persian komanso ziyankhuro za India kupita ku Arabic..

Kumeneko Asilamu ophunzira kwambiri ngati al- khawarizmi anayambitsa masamu a algebra,

Ophunzira akulu akulu ngati Ibn Sina analemba mabuku a mankhwala ndi udotolo zomwe zinagwiritsidwa ntchito ku Ulaya kwa zaka 600.

Asilamu ngati alRazi anapanga discover new treatments ya odwala.

Anthu ngati al-Tusi anaphunzitsa nyenyezi ndikumanga ma observatories ndikusintha mmene timaonera nyenyezi.

Izizi sanapangire Ndalama koma anapangira Mulungu, chifukwa kuphunzira mchisilamu ndi Ibadah (mapemphero)

Sautul-Huda

Qur'an vs ScienceUmu ndi mmene atsogoleri omwe si asilamu amamuonera Mtumiki Muhammad.1. Pop Francis (papa, ntsogoleri w...
16/07/2025

Qur'an vs Science

Umu ndi mmene atsogoleri omwe si asilamu amamuonera Mtumiki Muhammad.

1. Pop Francis (papa, ntsogoleri wa Chikhristu): Mtumiki Muhammad anali Munthu wamtendere komanso otumikira Mulungu (Check Vatican News)
2. King Charles wa ku England (mfumu yaikulu ku England): Mtumiki Muhammad anali ntsogoleri Wina Wina emwe Nzeru zake ndi kudzichepetsa kwake kunakhonza mbiri ya anthu a Dziko lapansi, yemwe Uthenga wake unadutsa mu nthawi ndi ma border kudzatiphunzitsa Ife makhalidwe a moyo komanso Mtendere. (Oxford Center for Islamic studies 1993)
3. Mahatma Gandhi: Chiphunzitso Cha Mtumiki Muhammad (Quran & Hadith) ndi Mgodi wa Luntha osati kwa asilamu okha koma kwa anthu onse, ndikamawerenga Bukhu la Korani ndinaphunzira kuti Chisilamu chimaphunzitsa Za nzeru komanso ufulu.
4. Napolian (Mmodzi mwa ma commander akulu akulu akale achikhristu): Mtumiki Muhammad analetsa kupha azimayi ndi Ana pa nkhondo, analamula kukhala wabwino kwa amasiye,komanso anati anthu onse ndi chimodzimodzi pamaso pa Mulungu, zinthu zomwe mu Gospel mwathu mulibemo. (Memorial de sainte-Helene 1816)
5. Michael Tyson: Mbiri (sira) ya Mtumiki Muhammad inapulumutsa moyo wanga.
6. Kanye west: siine msilamu koma ndikuphunzira Korani, ndipo Discipline mchisilamu ili bwino kwambiri, no alcohol no fornication. (Drink champs podcast 2023)
7. Michael Heart: Mlembi uja analemba bukhu the 100, mmenemo anaikamo anthu 100 otchuka ndi ukadaulo osiyanasiyana mu mbiri ya anthu adziko lapansi mwandondomeko kuyambira amene Ali No 1 ukadaulo mpaka No 100 ndipo pa No1 panali Mtumiki Muhammad ndipo anati abwana alibe opikisana naye. (The Hundred)
8. Barack Obama: Mtumiki Muhammad anaphunzitsa Chilungamo komanso Chisoni (President of the United States)
9. Dalai Lama(Mkulu wachibudha): ndili ndi Ulemu kwambiri kwa Mtumiki Muhammad, abwanawa anali Ntsogoleri opambana yemwe anaphunzitsa Chilungamo Bata komanso Mtendere (towards a true kinship of faith, 2010)

Mtendere ndi madalitso a Mulungu zipite kwa Abraham

15/07/2025

📢 *Ndindani mwa ife amene wayedzamira mwa Allāh?*

Alhamdulillāh lero kwatichera mu Ulamuliro wa Allāh. Ndipo palibe tsiku limene limatichera kupatula kuti kumacha tili mu Ulamuliro wa Allāh.

Yemwe amapembedza Allāh, azindikira kuti amene wabwenzeretsa mzimu wake mthupi lake ndi Allāh. Choncho, tsiku lake alisiya kuti litsogoleredwe ndi Mwini zonse zili kumwamba ndi dziko lapansi.

Mumupeza akuyedzamira mwa Allāh mu zochita zake za tsiku limeneli.

🤦🏽‍♂️ Okhawo odziona anzeru, chuma, mphamvu, kudziwika komanso kukhalitsa; muwapeza asakuyedzamira mwa Allāh. Muwapeza akuyedzamira mu zinthu zina.

حسبنا الله

Watikwanire ife Allāh.

Sautul-Huda

13/07/2025
09/07/2025

Follow us on page Sautul-Huda and on tiktok Mujaweed12

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Sautul-Huda posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share