23/07/2025
MBIRI YA CHITSULO
Science:
Kale kale kunali nyenyezi za mtundu Wina Wina, Solar system yathuyi kulibe, kudzela mma Nuclear Fusion, nyenyezizi, mma core mwake zinapanga ma elements olemera kwambiri, Zina mwa izo ndi chitsulo. Tsopano pomwe miyoyo ya nyenyezizi inafika kumapeto ndi kuphulika ngati ma supernova, zinatulutsa chitsulo ndi ma elements ena zomwe zinagwera ku space, ma materials amenewa anakhala gawo limodzi la ma Nebulas zomwe zinakhonza solar system yathuyi, Komanso planet yathuyi.
Mwachidule:
Chilichonse chimene timachiona mu planet yathuyi zinalipo ndi kale kupatula chitsulo, ichi chinachita kugwa kuchokera ku space komwe nyenyezi zimene zinafa kalero, zinasanduka ma nebulas.
Nyenyezi ikafa imasanduka nebula, nebula ndi chinthu chomwe nyenyezi yakufa imasanduka, zimatha kukhala mitambo, koma panali nyenyezi zomwe zinafa kale zomwe zinasanduka chitsulo, ndipo zinabwela mu planet yathuyi, kafukufuku winanao wa science, amati planet yathuyi kunalibe ndipo inapezeka Kamba ka ma nebulas ochokera ku nyenyezi, ndie chitsulo ndi chinthu chochita kubwera kuchokera kunja kwa Solar system yathu.
Qur'an:
Ndipo tidatsitsa Chitsulo momwe muli mphamvu zochuluka Komanso phindu kwa anthu. (57:25)
Mu vesiyi Mulungu akunena kuti chitsulo ndi chochita kubwera kuchoka kumwamba, kale kunalibeko, chinatumizidwa kudzapindulira anthu.
Izi zinalembedwa kale M'buku la Korani zaka 1400 zapitazo
Sautul-Huda