18/08/2026
Apolisi ku Mponela m'boma la Dowa alanda njinga zamoto makumi awiri ndi zinayi(24)chifukwa chomphwanya malamulo apa msewu.
Malingana ndi Ofalitsa nkhani ku polisi ya Mponela Macpatson Msadala,izi zachitika lero pomwe alanda njingazi Malo osiyana siyana ochitira malonda,kusatira ntchito yapadera yoyendera ndi kuwunika oyendetsa njinga zamoto yomwe inatsogoleredwa ndi inspector Leston Masambo amene ndi owona za malamulo apa msewu.
Pa ntchitoyi , apolisi amayang,ana kwambiri njinga zamoto zomwe zimamphwanya malamulo monga kuyendesa njinga zamoto zomwe sizinalembesedwe,kuyendesa popanda inshuwaransi yovomelezeka komanso kugwiritsa ntchito matayala ok*tha kapena owonongeka.
M'mawu ake Masambo wati ntchitoyi yayenda bwino ,ndipo apolisi ku Mponela apitiliza ntchitoyi m'masiku akubwerawa pofuna kuchepesa ngozi zapamsewu,choncho wapempha eni njinga zamoto komanso oyendetsa njingazi k*ti azitsatira malamulo onse okhudza pamseu.