27/10/2022
NYAMATA WINA YEMWE ANAMWALIRA ZAKA 20 ZAPITAZO WAPEZEKA WAMOYO.
Nyamata wina yemwe anamwalira zaka makumi awili zapitazo ku Thekelani mudzi mwa Ndongo T/A Nsabwe wapezeka wa moyo ku Zalewa muboma la Blantyre.
Mfumu yayikulu Ndongo yasikimiza zankhaniyi kuti nyamatayi yemwe dzina lake ndi Paulo Phaiva anamwalira muchaka cha 2002 nthawi yomwe anali ndizaka 10 zakubadwa.
Nyamatayi atamwalira anthu analira maliro ndikukamiyika m'manda.
Masiku apitawa mzimayi wina wokhala ku Zalewa muboma la Blantyre atapita kotunga madzi anakumana ndinyamatayi ali chogonele ndinso akuwoneka ofowoka. Ngakhale ankalephela kuyankhula zomveka nyamatayi anakwanisa kutchula mudzi wakwawo ndi dzina la mayi ake.
Mzimayiyu atapita ndinyamatayi kumudzi komwe amatchula mayi ake ndi achibale anali odabwa kuwona kuti mwana wawo yemwe anamwalira ndikuyikidwa m'manda zaka 20 zapitazo wapezeka wamoyo.
Atamuyang'anisisa mayi ake anakhulupilira zamwanayo kamba kachipewa chomwe anamugulira ali ndi zaka 10 ndipo mosakhalisa anamulandila ndikumufusa zakomwe anali.
Asing'anga ena anawuza achibale kuti mwanayo anasandusidwa chabe ndondotcha ndimpondamatiki wina koma wabwelelaso ku umoyo wake kamba koti zizimba zomwe mpondamatikiyo anagwilitsa ntchito zasuluka.
Pakanali pano nyamatayi ali ndizaka 30 ndipo watha zaka 20 makolo ake akuyesa kuti anamwalira osaziwa kuti anangophedwa mumasenga ndipo thupi lake linachosedwa kumakagwilitsidwa ntchito ngati ndondotcha
Follow Page Mr Screenshot Mw 🙏🏽