Radio Lilanguka Online

Radio Lilanguka Online Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Radio Lilanguka Online, Radio Station, Fort Johnston.

ANTHU AYEMBEKEZERE MPIKISANO WAPAMWAMBA (MDFA).Komiti yoyendetsa masewero ampira wamiyendo m'boma la Mangochi ya Mangoch...
04/08/2025

ANTHU AYEMBEKEZERE MPIKISANO WAPAMWAMBA (MDFA).

Komiti yoyendetsa masewero ampira wamiyendo m'boma la Mangochi ya Mangochi District Football Association (MDFA) yatulutsa ndandanda wamasewero amumpikisano wa Castel Cup wa chaka chino.

Izi ndi malinga ndi mayere omwe komitiyi pamodzi ndi matimu omwe akutenga nawo gawo mu mpikisanawu anali nawo loweruka pa bwalo la zamasewero la Mangochi

Poyankhula ndi Lilanguka Sports Desk mlembi wamkulu wa komitiyi Islamu Rajabu wati anthu ayembekezere mpikisano wa Castel wapamwamba chaka chino.

Apa iwe wati alengezabe malo komanso masiku omwe mpikisanowu uyambe koma wapempha matimu kuti akhale okonzeka.

Ndipo ndandawu uli motere:

1-Kalonga Stars 🆚 Majuni Super Market
2-Chiponde Hammers 🆚 Namwera United
3-Philirongwe United 🆚 Black Jack
4-Namias United 🆚 Chipoka Rangers
5-Chawe Bullets 🆚 MMF Marines Reserve
6-Galaxy 🆚 Madelco Super Stars
7-Tech 🆚 Kondwan Mbumba
8-Makawa Young Navy 🆚 Chimbende united.

Timu ya Chipoka united inafika mu ndime ya national level chaka chatha pomwe inatuluka mumpikisanowu itagonja ndi timu ya Mighty Wandereres ndi zigoli 10 kwa chimodzi masewero omwe anachitika pa bwalo la Kamuzu mu nzinda wa Blantyre.

Kampani ya yopanga ndikugulitsa mowa ya Castel ndi yomwe imathandiza mpikisanowu ndi ndalama zokwana k450 million , ndipo timu ya Mighty wanderers ndiyomwe inakhala akaswiri ampikisanowu.

Wolemba : Patrick Makweza

Mtsogoleri wa chipani cha People’s (PP) Dr. Joyce Banda wati akadzapambana pa chisankho chapa 16 September, azayamba ndi...
01/08/2025

Mtsogoleri wa chipani cha People’s (PP) Dr. Joyce Banda wati akadzapambana pa chisankho chapa 16 September, azayamba ndi kuwonetsetsa kuti wathana ndi mavuto a zachuma omwe anthu mdziko muno akukumana nawo.

Dr. Banda ayankhula izi pa msonkhano wokhazikitsa mfundo za chipanichi pa bwalo la zamasewero la sukulu ya pulaimale ya st. Augustine 3 m’boma la Mangochi.

Iwo ati ali ndi kuthekera kothana ndi mavuto wa potengera ukadaulo omwe ali nawo pa utsogoleri monga momwe adachitira pa nthawi yomwe anali mtsogoleri wa dziko lino.

Mwazina a Banda ati azayamba ndi kuthana ndi vuto la kusowa kwa mafuta a galimoto, azakhazikitsa ntchito ya ‘cash for work’ kuti anthu azizapeza ndalama mosavuta, komanso azakhazikitsa ndindomeko zowonetsetsa kuti chakudya chikupezeka mosavuta.

Iwo atinso azagawa njinga za kabaza Kwa achinyamata komanso azizapereka ngongole zoyambira bizinesi Kwa amayi ngati njira zolimbikitsa kuti akhale ozidalira pa chuma.

Kupatula izi iwo ati chidwi chawo chizagonanso popititsa patsogolo ntchito za migodi, za ulimi, za misewu, za magetsi komanso zokopa alendo.

Olemba : Alackie Chakwana

  Khwimbi la anthu otsatira chipani cha Peoples lasonkhana pa bwalo la sukulu ya pulaimale ya St. Augustine 3 m’boma la ...
01/08/2025




Khwimbi la anthu otsatira chipani cha Peoples lasonkhana pa bwalo la sukulu ya pulaimale ya St. Augustine 3 m’boma la Mangochi pomwe mtsogoleri wa chipanichi mayi Dr. Joyce Banda akhale akuyankhula masanawa.

Mwazina pa msonkhanowu Dr. Joyce Banda akhala akukhazikitsa manifesto omwe chipanichi chikhale chikugwiritsa ntchito pa chisankho chapa 16 September.

Wolemba : Alackie Chakwana

    A Isaac Ramsy Khan omwe akuyimira ngati phungu wa chipani cha MCP kudera la Mangochi Nkungulu, ati anthu akuderali a...
31/07/2025




A Isaac Ramsy Khan omwe akuyimira ngati phungu wa chipani cha MCP kudera la Mangochi Nkungulu, ati anthu akuderali akonzekere zitukuko zochuluka akasankhidwa pa udindowu pa 16 September chaka chino.

A Khan ayankhula izi lachitatu pomwe amakasiya makalata awo owayenereza kuyimila pa udindowu pa sukulu ya pulayimale ya Chimwala ku bungwe loyendetsa chisakho la MEC.

M'mawu awo a Khan ati akazapambana azaonetsetsa kuti ntchito za chitukuko monga za ulimi, za maphunziro komaso za masewero ndi za achinyamata zikupita patsogolo.

"Ndizaonetsetsa kuti dera la Mangochi Nkungulu ndi lotukuka ndipo silili lotsalila ku nkhani za zitukuko. Ndikhumbo langa kuti derali likhale ndi zipangizo zamakono za ulimi wa mbewu komaso wa nsomba ndipo kumbali ya achinyamata ndizaonetsetsa kuti ndawamangila bwalo la za masewero lamakono"

Pa ulendowu a Khan anakasiya makalatawa limodzi ndi mankasala a MCP omwe akuimila ma owodi amu derali.

Wolemba: Geoffrey Abba

  A Rodrick Clement Chiyawa a Chipani cha DPP abwerezanso kunena kuti akufunitsitsa kuti atukure miyoyo ya anthu akudera...
30/07/2025




A Rodrick Clement Chiyawa a Chipani cha DPP abwerezanso kunena kuti akufunitsitsa kuti atukure miyoyo ya anthu akudera la Mangochi Municipality ngati anthu atawasankhe pa chisankho cha pa 16 September.

Iwo ayankhula izi lero pambuyo popereka kalata zosonyeza chidwi chopikisana nawo ngati phungu pa chisankhochi ku dera la Mangochi Municipality ku St Augustine 3

A Chiwaya ati kupatula kutukula chuma cha anthu m'derali, Iwo akufunamso kukonza misewu yamakono komanso kumanga zipatala zing'onozing'ono m'derali pofuna kupititsa patsogolo ntchito za mtengatenga ndi Umoyo.

Iwo awuzanso Lilanguka Online kuti khwimbi lomwe linawaperekeza kosiya kalata zawo ndi chizindikiro choti anthu akufuna zinthu zisinthe kuderali

A Chiwaya anaperekezedwa ndi makhansala khumi a Chipani cha DPP komanso anthu ena otsatira Chipani cha AFORD.

Sabata yatha, Iwo anakhazikitsa ntchito yophunzitsa anthu kupanga Sopo, mafuta ophikira komanso yogati kuderali yomwe akuitchula kuti Mbedza ndipo ifikira anthu opitirira 10 000

Padakali pano, bungwe la MEC latsiliza kulandira kalata kuchokera kwa omwe akufuna kupikisana nawo pa mipando ya mtsogoleri wa dziko, phungu ndi makhansala ndipo litsimikizira mayinawa pa 16 mwezi wamawa.

Wolemba : Patrick Makweza

  Bungwe lowona ndi kuteteza ufulu wa anthu achikulire m'dziko muno la Malawi Network of Older Persons' Organizations(MA...
30/07/2025




Bungwe lowona ndi kuteteza ufulu wa anthu achikulire m'dziko muno la Malawi Network of Older Persons' Organizations(MANEPO) lati kusamusidwa kwa ogwira ntchito za umoyo m'madera ena m'boma la Zomba kukusokoneza ntchito za bungweli maka kumbali yosamalira anthu achikulire m'bomali.

Mkulu wa bungweli, Andrew Kavala ndiye wanena izi pa mkumano omwe bungweli linali nawo ndi akuluakulu a khonsolo ya boma la Zomba.

Malinga ndi Kavala, kusamusidwa kwa ogwira ntchito za umoyowa kwkhudza kwambiri bungweli pa ntchito zake kamba koti likuvutika kupeza ndalama zochititsira maphunziro okhudza chisamaliro cha anthu achikulire kwa ogwira ntchito za umoyo atsopano kudera.

M'mau ake, mkulu owona za mapulani ndi chitukuko ku khonsolo ya boma la Zomba, Precious Kamtsitsi wavomereza za vutoli ndipo m'malo mwake watsimikizira bungweli kuti monga khonsolo akhale akupeza njira zatsopano zomwe zizithandizira kubwezeretsa mwachangu ogwira ntchito za umoyo omwe asamusidwa kudera ndicholinga choti ntchito za chisamaliro cha anthu achikulire zisamakhudzidwe

Wolemba: Laston Idana, Zomba

    Yemwe akuyimila pa udindo wa mphungu ku dera la Mangochi Municipality, Vincent Makda wati ndiwokonzeka kutumikila de...
30/07/2025




Yemwe akuyimila pa udindo wa mphungu ku dera la Mangochi Municipality, Vincent Makda wati ndiwokonzeka kutumikila derali ku zitukuko zosiyanasiyana zomwe delali likusowekela.

Makda wayankhula izi lachiwiri pa sukulu ya St. Augastine 3 komwe amakapereka makalata awo owayeneraza kupikisana pa mpandowu ku bungwe la chisankho la MEC.

Mwazina Makda wanena kuti azamanga sukulu za sekondale zoyendera zomwe zizatukule ntchito za mamphunziro mu Manicipality-yi.

Iwo anatiso azaonetsetsa kuti nthambi ya chitetezo komanso umuyo m'bomali zakwezedwa ndi cholinga chopititsa patsogolo ntchito za nthambizi.

Pa ulendowu a Makda anakasiya makalatawa pamodzi ndi mankasala khumi a MCP omwe akuimila ma wodi osiyana siyana a Municipality-yi.

Wolemba: Geoffrey Abba

  Yemwe akupikisana nawo pa udindo wa phungu wakunyumba ya malamulo  ngati oyima payekha kudera la Kumpoto cha Kumawa kw...
29/07/2025




Yemwe akupikisana nawo pa udindo wa phungu wakunyumba ya malamulo ngati oyima payekha kudera la Kumpoto cha Kumawa kwa boma la Mangochi Charles Makwenda, wati akazasankhidwa ngati phungu wa derali, pa 16 September azaonesetsa kuti ntchito za zaumoyo, ulimi wanthilira komanso zamaphunziro zapita patsogolo.

Makwenda wayankhula izi lero pa sukulu ya Primary ya Chimbende atamaliza kuperela kalata zake ku bungwe la Malawi Electrol Commission(MEC), zowonetsa chidwi chozayima ngati phungu wa derali.

Makwenda wati cholinga chake ndikufuna kulisintha derali kukhala lotukuka pobweletsa chitukuko m'magawo osiyanasiyana.

Kumbali ya achinyamata komanso amayi wati azaonesetsa kuti wapezera zochita kuti akhale ozidalira pa chuma powapezera zochita zokhazikika.

Pa ulendowu iye analinso ndi mansakhala awiri Aisha Chikoloni yemwe akuimira ward ya Mikongo komanso Jafali Piyasi yemwe akuimira ward ya Malindi.

Wolemba : Patrick Makweza

SINDINATHAWE  KU MALINDI- KALOSI A Idi Kalosi a Chipani cha UDF ati sanathawe kudera la kumpoto cha ku m'mawa kwa boma l...
29/07/2025

SINDINATHAWE KU MALINDI- KALOSI

A Idi Kalosi a Chipani cha UDF ati sanathawe kudera la kumpoto cha ku m'mawa kwa boma la Mangochi, komwe iwo anali phungu ngati momwe anthu ena akunenera.

A Kalosi ayankhula izi pambuyo pa Msonkhano womwe anachititsa pa bwalo la St Augustine 3 ku dera la Mangochi Municipality komwe Iwo tsopano awonetsa chidwi chopikisana ngati phungu.

Malinga ndi a Kalosi, kubwera kwawo ku dera la tsopanoli ndi chifukwa choti bungwe la MEC linadulanso malire a madera a aphungu zomwe zachititsa kuti Iwo tsopano asamukire dera la Municipalityli

Iwo ati achita zitukuko zosiyanasiyana kudera lakumpoto cha Kum'mawa kwa bomali komwe anali phungu ndipo akukonza zomanga zipatala zing'onozing'ono mu ma wodi a makhansala ku dera latsopanoli, kutukula moyo wa Amayi ndi achinyanata powaphunzitsa kuyendetsa galimoto komanso ayesetsa kuti ana asukulu adzapeze yunifolomu za sukulu zawo mosavuta.

Asanayankhule a Kalosi Mkulu wokonza zinthu mchipanichi a Abubakar M'baya anapempha anthu kuderali kudzavotera a Kalosi ponena kuti ndi mbadwa yeniyeni ya derali komanso boma la Mangochi, yemwe ikudziwa mavuto a anthu.

A Kalosi apereka Kalata zawo zoonetsa chidwi chopikisana ku dera latsopanoli ku Bungwe lachisankho la Malawi Electoral Commission MEC pa sukulu ya Saint Augustine 3, lolemba masana

Iwo akupikisana nawo kachitatu ngati phungu, atapambana kawiri konse ku dera la kumpoto cha Kum'mawa kwa boma la Mangochi kuyambira mchaka cha 2014.

Wolemba : Chancy Maulana

28/07/2025

Ali wawojo mpaka atende uli?

   A Kalosi ayamba kuyankhula kwa anthu amene asonkhana pa bwalo la St Augustine 3Iwo ati akufuna kukweza amayi komanso ...
28/07/2025




A Kalosi ayamba kuyankhula kwa anthu amene asonkhana pa bwalo la St Augustine 3

Iwo ati akufuna kukweza amayi komanso anyamata

" I urge everyone here to be behind us. I am here to save the people of Mangochi Minicipal"

Anaonjezera motero mu chingerezi

Iwo ati anthu akadzawasankha ayesetsa kubweretsa zipatala m'mawodi onse

Wolemba : Chancy Maulana

    Yemwe akuimira ngati phungu wa chipani cha UTM kudera la Mangochi Malombe Dalaban Chibwana Wati wakonzeka kudzutsa d...
28/07/2025




Yemwe akuimira ngati phungu wa chipani cha UTM kudera la Mangochi Malombe Dalaban Chibwana Wati wakonzeka kudzutsa derali lomwe lakhala lakufa Kwa nthawi yaitali ku mbali ya chitukuko.

Chibwana wayankhula izi lolemba pomwe amapereka ma pepala omuvomereza kuimira nawo pa chisankho chapa 16 September ku bungwe la zisankho la MEC pa Malombe TDC.

Mwazina Chibwana wati azaonetsetsa kuti misewu yonse yakuderali yakonzedwa bwino Komanso kubweretsa magesi pofuna kupititsa patsogolo ntchito za malonda.

Iye watinso azapititsa patsogolo ntchito zamaphunziro komanso wati azalimbikitsa ulimi wanthilira kuti anthu akuderali azikhala ndi chakudya chokwanira.

Chibwana anakapereka kalata zake pamodzi ndi ma khansala omwe akuimira chipani cha UTM kuderali, omwe ndi Zakaliya Yuma yemwe akuimira ku Wodi ya Maiwa komanso Cassim Missi yemwe akuimira Wodi ya Masanje.

Wolemba: Alack Chakwana

Address

Fort Johnston

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Radio Lilanguka Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Radio Lilanguka Online:

Share

Category