Radio Lilanguka Online

Radio Lilanguka Online Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Radio Lilanguka Online, Radio Station, Fort Johnston.

TIYEMBEKEZERE MVULA YAMBIRIRadio Lilanguka Online Nthambi yoona za nyengo ndi kusintha kwa nyengo m'dziko muno yati anth...
14/11/2025

TIYEMBEKEZERE MVULA YAMBIRI

Radio Lilanguka Online

Nthambi yoona za nyengo ndi kusintha kwa nyengo m'dziko muno yati anthu ayembekezere mvula m'madera amzigawo zonse za dziko muno.

Izi ndi malingana ndi kalata ya ulosi yomwe nthambiyi yatulutsa yomwe yati mvulayi idzigwa yamphanvu maka m'madera ena apakati komanso kumpoto kwa dziko lino mpaka lamulungu likudzali.

Padakali pano pali chiyembekezo kuti lolemba pa 17 November m'madera ambiri akuchigawo cha kummwera adzalandila mvula yochuluka.

Pamenepa nthambiyi yati pali chiwopsezo chakusefukira kwa madzi m'madera omwe mukhale mukugwa mvulayi.

Wolemba: Patrick Makweza

NDIGWIRA NTCHITO NDI ALIYENSE KUTI TITUKULE DERARadio Lilanguka Online Khansala wa wodi ya Mwansa kudera la Mangochi Mun...
14/11/2025

NDIGWIRA NTCHITO NDI ALIYENSE KUTI TITUKULE DERA

Radio Lilanguka Online

Khansala wa wodi ya Mwansa kudera la Mangochi Municipal Kida Adamu wati ndi ozipereka kugwira ntchito ndi aliyense kuti ntchito zachitukuko zipite patsogolo.

Iye wati kusowa kwa mgwilizano wabwino mbuyomu pakati pa khansala yemwe analipo ndi mafumu , komanso ma komiti a ADC, ndi VDC ndi komwe kwachititsa kuti wodiyi ikhale yotsalira pankhani ya chitukuko.

Kida yemwe ndi khansala wachipani cha UDF wayankhula izi kudzera ku wailesi ino , patangodutsa masiku ochepa atalumbilisidwa pa udindowu atambana pachisankho chomwe chachitika mdziko muno posachedwapa.

Pamenepa iye wapempha adindo onse okhuzidwa pankhani zachitukuko kuti agwire ntchito limodzi ndi khansalayi kuti mavuto omwe anthu akukumana nawo ikhale mbiri yakale.

Kwa achinyamata wati podziwa kuti achinyamata ndi atsogoleri alero ndipo ayesetsa kuika njira zokhazikika pofuna kuthana ndi mavuto omwe achinyamata akuderali akukumana nawo.

Wolemba: Patrick Makweza

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yalengeza kuti  Fischer Kondowe yemwe anali wachiwiri wina kwa mphunzitsi  wachoka kutimuy...
12/11/2025

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yalengeza kuti Fischer Kondowe yemwe anali wachiwiri wina kwa mphunzitsi wachoka kutimuyi.

Malinga ndi timuyi, Kondowe wachoka mbali ziwirizi zitamvana kutero ngakhale sanafotokoze chomwe wachokera.

Asanakhale mphunzitsi, Kondowe anali osewera wa timuyi ndipo anasiya kusewera mpira mu chaka cha 2022 ,kenako anasankhidwa kukhala Fitness Trainer pansi pa mphunzitsi wakale wa timuyi Kalisto Pasuwa.

Timu ya FCB Nyasa Big Bullets yamufunika mafuno abwino Kondowe ponena kuti kuyambira nthawi yomwe anali osewera wa timuyi kufikira pano pomwe wachoka ndi m'modzi mwa aphunzitsi odzipereka kwambiri.

Wolemba : Patrick Makweza

MAPHUNZIRO AYAMBA KUYENDA BWINO TSOPANORadio Lilanguka Online Kumangidwa kwa zipinda zophunzilira zokwana zisanu ndi chi...
11/11/2025

MAPHUNZIRO AYAMBA KUYENDA BWINO TSOPANO

Radio Lilanguka Online

Kumangidwa kwa zipinda zophunzilira zokwana zisanu ndi chimodzi pa Sukulu ya pulayimale ya Chiusi kwa mfumu yaikulu Chowe ku Mangochi, ati kuthandizira kukweza maphunziro pa sukuluyi.

Mphunzitsi wamkulu wapasukuluyi a George Nambuzi, auza Radio Lilanguka Online pamene sukuluyi yalandira zipindazi kudzera ku ntchito yotchedwa Malawi Education Reform Programme-MERP.

A Nambuzi, ati m'mbuyomu maphunziro pasukuluyi samayenda bwino maka munyengo ya mvula kamba koti ophunzira ambiri amaphunzira pamsi pa mtengo zomwe zimapangisa kuti ophunzira azithawa mkalasi mosavuta.

Pamenepa iwo ati ali ndi chikhulupiliro kuti zipindazi zisamalika bwino, kamba koti pali mgwirizano wabwino pa sukuluyi ndi anthu amidzi yozungulira.

Sukulu ya pulaimale ya Chiusi inayamba mchaka cha 1998 ndipo ili ndi ophunzira pafupifupi 1,400.

Wolemba: Chikondi Makungwa

MAKHANSALA ALUMBIRA POSACHEDWAPARadio Lilanguka Online Bwana mkubwa wa boma la mangochi Davie Chigwenebe wati ma khansal...
10/11/2025

MAKHANSALA ALUMBIRA POSACHEDWAPA

Radio Lilanguka Online

Bwana mkubwa wa boma la mangochi Davie Chigwenebe wati ma khansala omwe asankhidwa alandira maphunziro a momwe angagwilile ntchito ya ukhansala posachedwapa.

Iwo ayankhula izi pa mwambo olumbilitsa makhansala komanso kusankha wa pa mpandapo wa khonsolo ya bomali.

Iliyasa Sauzande wa dera la masongola wa chipani cha Democratic Progressive-DPP ndiyemwe wapambana pachisankhochi popeza ma vote okwana 12 pa ma vote 23 omwe makhansala anaponya, Mushe James ndiye wachiwiri kwa wapampando wa khosoloyi.

Sauzande wati ndi khumbo lake kuti boma la Mangochi likhale lotukuka komanso awonetsetsa kuti ntchito za maphunziro m'bomali zikupita patsogolo.

Makhansala 23 ndiomwe adasankhidwa m'bomali kumadera okwana 12.

Wolemba: Ernest Chitete

CHIWONETSERO CHAYAMBA BWINORadio Lilanguka Online Bwana mkubwa wa boma la mangochi a Davie Chigwenebe,  ati chionetsero ...
08/11/2025

CHIWONETSERO CHAYAMBA BWINO

Radio Lilanguka Online

Bwana mkubwa wa boma la mangochi a Davie Chigwenebe, ati chionetsero cha zaulimi chomwe chayamba lachisanu ku bwalo lazamasewero la Mangochi ndi njira imodzi yofuna kugulitsa malonda azaulimiwa komanso kufuna kukopa anthu ena ndi cholinga chofuna kuwathandiza.

Iwo ayankhula izi pomwe amatsegulira Chionetserochi ndipo apempha alimi kuti azitha kuchita ulimi, ngati bizines ndicholinga choti katundu wazaulimiyu athe kupita patsogolo komanso kupeza phindu ochuluka.

Rashid Mpinganjira, yemwe ndi modzi mwa anthu omwe ali mu komiti yokonza za Chionetserochi wati chayamba bwino ndipo alimi akhala ndi nthawi yofusa mafuso a momwe angathe kupitisira patsogolo ntchito za ulimi ndicholinga choti athekupitisa patsogolo ulimi wawo.

Ena mwa magulu omwe akutenga nawo gawo pa Chionetserochi a Jeyie Foods, Ziweto Agrovest, Islamic Relief Malawi, ADMARC Limited, kungotchulapo ochepa chabe.

Mutu wa ulendo uno ndi kupereka chikoka pa katundu wazaulimi komanso kupititsa ulimi patsogolo ngati business.

Wolemba: Ernest Chitete

NDINAGONJA KOMA SINDISIYA KUCHITA CHITUKUKORadio Lilanguka Online A Grace Gonani  omwe anakapikitsana nawo pa mpando wa ...
07/11/2025

NDINAGONJA KOMA SINDISIYA KUCHITA CHITUKUKO

Radio Lilanguka Online

A Grace Gonani omwe anakapikitsana nawo pa mpando wa phungu ku dera la kumpoto chakum'mawa kwa boma la Mangochi, ati apitilira kuchita ntchito za chitukuko mdelari ngakhale adangonja pachisakho.

Iwo auza Radio Lilanguka Online m'mawa wa lachisanu pomwe amafotokoza za chidwi chawo chozayimanso ngati phungu waderali.

A Gonani omwe anayima ngati phungu wachipani cha UTM ati ngakhale sadapambane pa chisakho cha pa 16 September, iwo sangasiye kugwira ntchito za chitukuko kamba koti amakhulupilira kuti kuthandizana wina ndi nzake kungathandize kuti dziko lino lipite patsogolo.

Iwo apempha amayi omwe analephera pachisankhochi kuti ayambe zokonzekera zachisankho cha mchaka cha 2030 ndicholinga choti amayi ambiri azachite bwino pachisankhochi.

Amayi atatu okha ndi omwe adapambana pa mpando waphungu wakunyumba yamalamulo pachisankho chapitachi m'boma la Mangochi.

Wolemba: Patrick Makweza

ZONSE ZILI MCHIMAKERadio Lilanguka OnlineZokonzekera  za mwambo wa chionetsero cha zaulimi m'boma la Mangochi ati zikuye...
03/11/2025

ZONSE ZILI MCHIMAKE

Radio Lilanguka Online

Zokonzekera za mwambo wa chionetsero cha zaulimi m'boma la Mangochi ati zikuyenda bwino.

M’modzi mwa akulu akulu omwe akuyendetsa zokonzekera za mwambowu Rashid Mpinganjira, wauza wailesi ya Lilanguka pamenepo wailesiyi imafuna kudziwa m’mene zokonzera za chionetserochi chomwe chikuyembekezeka kuchitika pa 7 mpaka 8 November 2025 pa bwalo la zamasewero la Mangochi.

Malinga ndi Mpinganjira pachioneselochi alimi eni ndi mabungwe ena omwe amathandizilapo nkhani ulimi azatenga nawo mbali patsikuli.

Wolemba: Francis Kamoto

MALO OMWE ANAWONONGEKA PA MLATHO AJA AYAMBA KUKONZEDWARadio Lilanguka Online Potsatira nkhani yomwe tinalemba pa 17 Octo...
03/11/2025

MALO OMWE ANAWONONGEKA PA MLATHO AJA AYAMBA KUKONZEDWA

Radio Lilanguka Online

Potsatira nkhani yomwe tinalemba pa 17 October chaka chino yokhudza kuwonongeka kwa malo ena pa Mlatho wa Bakili Muluzi ku Mangochi, bungwe la Roads Authority Malawi tsopano layamba ntchito yokonza malowa monga momwe mukuwonera nzithunzimo.

Wolemba: Sinthani M'baluku

Big shout out to my newest top fans! 💎 Simba Damson, Joncyna Phiri, Æñdrëw Køssæmü, Ulemu Yohane Banda, Sinthani Kay-Pie...
02/11/2025

Big shout out to my newest top fans! 💎 Simba Damson, Joncyna Phiri, Æñdrëw Køssæmü, Ulemu Yohane Banda, Sinthani Kay-Piece M'baluku, Ibraxy Mw, Austin Hon Chikopa, Patrick Makweza, Trigger Wisiki, Martin Michael, Bertha Njaliwe Makalande, Bravo Wellington Thengo, Iqra Adan, Shareefah Nokuthula Magomboh, Shareef Musah, Daniel Witness Pwetete, Francis Kamoto, Aliseni Sabili, Naps Dan, Yusuf Bwanali Chabwera, Fayaz Rashid, Allie Gerald, Rahamani Alfred, Maria Makina, Florence Fufu Chilanga, Kenny Zikhale

Drop a comment to welcome them to our community,

02/11/2025

ITENDO YACHIWANJA CHA AYAO YA 2025 ILEPELECHE


1-Nov-2025

Likuga lya Chiwanja cha Ayao lalikusajendesya itendo yapachaka yakusengwela mbili ni ndamo sya wandu wa mtundu wachiyao litite lilepele kutendesya itendoyi chaka achino ligongo lya chisausyo cha chipanje.

Nlembela jwamkulungwa jwa likugali, Smith Kamwana, ajisalile wailesi ja Lilanguka kuti yeleyi ili yiyi ligongo lyakuti komiti jijasagulidwe mwesi wa May 2025 kuti jijendesye yakosechela ya itendoyi nganijikola ndawi jakwanila jakusosa mbiya syakwendechesya itendoyi nipo m' malo mwakwe ichitendekwa chaka cha malawi.

Itendo yakumalisya ya Chiwanja cha Ayao yatendekwe pa 28 October 2023 m'boma ja Mangochi.

Wakulemba: Nancy Makalande

MWAMBO WA CHIWANJA CHA AYAO WA 2025 WALEPHEREKARadioLilangukaOnline Sat, 1-Nov-2025Gulu la Chiwanja Cha Ayao lomwe limay...
01/11/2025

MWAMBO WA CHIWANJA CHA AYAO WA 2025 WALEPHEREKA

RadioLilangukaOnline
Sat, 1-Nov-2025

Gulu la Chiwanja Cha Ayao lomwe limayendetsa mwambo wa pa chaka wokondwerera mbiri ndi chikhalidwe cha anthu a mtundu wachiyao lati lalephera kuchititsa mwambowu chaka chino kaamba ka vuto la zachuma.

Mlembi wamkulu wa gululi, Smith Kamwana, wauza wayilesi ya Lilanguka kuti izi zili chomwechi kaamba koti komiti yomwe idasankhidwa m'mwezi wa May 2025 kuti iyendetse zokonzekera za mwambowu inalibe nthawi yokwanira yosakasaka ndalama zoyendetsera mwambowu ndipo m'malo mwake udzachitika chaka cha mawa.

Mwambo wotsiriza wa Chiwanja Cha Ayao udachitika pa 28 October 2023 m'boma la Mangochi.

Wolemba: Nancy Makalande

Address

Fort Johnston

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Radio Lilanguka Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Radio Lilanguka Online:

Share

Category