1Life that matter

1Life that matter Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from 1Life that matter, Digital creator, Headquarter Ching'oma Mission.

08/01/2026

Do you know what God did for me?
He broke my chains and set me free.
He pulled my heart from Mystery
He washed my sins in Calvary stream
He gave me life where death has been.
Now I stand redeemed and clean
Good morning and win forever 馃寗

"RIP Servant of God!!! Rev. Chibisa Banda!!A Christian does not consider death to be his end but the end of his trouble,...
24/12/2025

"RIP Servant of God!!! Rev. Chibisa Banda!!
A Christian does not consider death to be his end but the end of his trouble, tribulation. Whether you die young or old, no matter the nature of death, death is sure to come. What matters is the grace to continue living hereafter". ..

we praying for your family and the church in this difficult time..

09/09/2025

Prayer is a master key.
Jesus started with a prayer and ended with a prayer!!

20/02/2025

The level at which satan attacks us seems to be equal to the level of our commitment to God.
If we're truly committed to God almighty, he will take up Satan's challenge against us

01/06/2022

Aroma 13:11-14
Ndipo citani ici, podziwa inu nyengo, kuti tsopano ndiyo nthawi yabwino yakuuka kutulo; pakuti tsopano cipulumutso cathu ciri pafupi koposa pamene tinayamba kukhulupira. Usiku wapita, ndi dzuwa layandikira; cifukwa cace tibvule nchito za mdima, ntibvale camuna ca kuunika. Tiyendeyende koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'cigololo ndi conyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai. Koma bvalani inu Ambuye Yesu-Kristu, ndipo musaganizire za thupi kucita zofuna zace.

Mulinazo zambiri zimene mukuziwona zokondweretsa moyo wanu inu nkumati apa nde chinyamata chikuyenda bwino, koma ziwani kuti zonsezo ndizachabe ngati mwainu mulibe Yesu. Chopambana zonse kuti tizanjoye ndi moyo uno unkukhala ndi Yesu Amen.

25/05/2022

Deuteronomo 28:1-13 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi. Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu: Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za m始dziko lanu, ng始ombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse. Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika. Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu. Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri. Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m始dziko limene akukupatsani. Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda m始njira zake. Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani. Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, m始dziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani. Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula m始dziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense. Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi. Amen.

20/05/2022

Aroma 8:28,35,39 Ndipo tidziwa kuti amene akonda Mulungu zinthu zonse zithandizana kuwacitira ubwino, ndiwo amene aitanidwa monga mwa kutsimikiza kwa mtima wace. Adzatisiyanitsa ndani ndi cikondi ca Kristu? nsautso kodi, kapena kupsinjika mtima, kapena kuzunza, kapena njala, kapena usiwa, kapena zoopsya kapena lupanga kodi? ngakhale utali, ngakhale kuya, ngakhale colengedwa cina ciri conse, sicingadzakhoze kutisiyanitsa ife ndi cikondi ca Mulungu, cimene ciri mwa Kristu Yesu Ambuye wathu.

Amayi ndi Abambo, Nyamata ndi Nsikanda
Kondani Mulungu wanu kuti naye akukonde
Sangakukondeni ngati inu simumkonda
Sangakukondeni ngati inu simamvela
Sangakukondeni ngati simamutumikira
Kutelo khalani ake a Mulungu kuti naye akhale mwainu ndikulamulira moyo wanu Amen.

10/05/2022

Mateyu 9:12
Ndipo mmene Yesu ananva anati, olimba safuna sing'anga ai, koma odwala.

Okondedwa dziwani Yesu akulankhula mau awa pa nthawi yomwe akuitana Mateyu mkulu yemwe anali mwa mmodzi okhometsa misonkho,

Yesu kuti afike polankhula mau amenewa ndichifukwa chakuti anthu ankamunena kuti bwanji akukhala pamodzi ndi anthu ochimwa?

Nthawi imeneyi anamuuza Mateyu kuti nyamuka ndipo amutsate, Mateyu anasiya zonse namutsata Yesu mosanyinyirika,

Yesu akulankhula monveka bwino kuti amene sakudwala safuna sing'anga, koma yekhayo amene akudwala ndiye amafuna sing'anga,

Lero lino ambirife tikudwala nthenda zosiyana siyana zakuuzimu, koma tsoka ifeyo sitikudziwa, zilipo nthenda zina umadwala koma usakudziwa, zina zilipo umadziwa ndithu kuti ukudwala koma kunyala nyaza,

Machimo tichitawa dziwani ndi nthenda zimene Yesu akulankhula, zofunika tikumane ndi sing'anga Yesu kuti atichilitse,

Tikhoza kumapemphera bwino bwino, koma nthenda ikuononga moyo wauzimu, zofunika tifune funeYesu kuti atichilitse,

Ukhoza kumaoneka ngati zilibwino pamaso pa wanthu pomwe mkatimo nthenda inadya moyo wako wauzimu, Sizikutengera kuti umapemphera kapena ayi, nthenda yakuuzimu imagwira aliyense,

Mukufunika mukumane ndi Yesu, mumutsate Yesu, Mateyu akunyamuka kumutsata Yesu kuti achilitsidwe, nanga inu muchedweranji?

Musachite manyazi, nthendayo ndiyanu, nthenda imeneyi ochiza wake ndi Yesu yekha kulibeso sing'anga wina yemwe angachize kuposa Yesu, lapani, batizidwani mdzina la Yesu kuloza ku chikhululukiro cha machimo anu, pamenepo mudzachiritsidwa, Amen.

07/05/2022

Yobu 9:29
Mlandu udzanditsutsa, potero ndigwire ntchito cabe kodi cifukwa ninji?

Okondedwa Yobu akulankhula mau awa akudzinvera chisoni kuti zoona ntchito ya Mulungu yonse ndagwira ija zoona ndigwire pachabe?

Ambiri timagwira ntchito ya Mulungu koma pomwe mitima yathu ili kutari ndi Mulungu,

Timapemphera inde,
Timaimba,
Timalalika,
Timadya mgonero,
Timapanga nawo chirichonse kumpingo koma kodi timachita zomwe Mulungu amafuna?

Kukhala mkhristu sizisonyeza kuti ndiwe olungama ayi, ukhoza kukhala mkhristu koma ukuyendabe muuchimo, dziwa pakutha pa moyo ndiwakugahena,

Yobu akufusa kuti ndigwire ntchito ya Mulungu pachabe kodi?

Kodi ndi mlandu wanji omwe inuyo udzakutsutseni? Nthawi ndiyomwe ino pomwe muli ndimoyo, lapani, sungani chiyero, yendani mmau a Mulungu, kuti pakutha pa moyo uno mukalandire moyo osatha kumwamba,

Munthu ukagwira ntchito umalandira malipiro, ndimalipiro anji omwe mudzalandire pakutha pa moyo wanu? Ndi mlandu wanji omwe udzakutsutseni?

Mulungu akufuna timpembedze mu Mzimu ndi mchoonadi, kuti mlandu usadzatitsutse, ndi mlandu wanji omwe tapalamula kwa Mulungu? Zidzakhala zonvetsa chisoni kuti takhala tikupemphera nthawi yaitari, koma pakutha pa moyo ndikukalowa Ku gahena, Ambuye chitirani chifundo ana anu kuti tsiku la mlandu usadzatitsutse, tiphunzitseni, tikonzeni kuti tichite monga mmene mufunira, mdzina la Yesu, Amen.

Address

Headquarter Ching'oma Mission

Telephone

+27730941452

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when 1Life that matter posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to 1Life that matter:

Share