10/05/2022
Mateyu 9:12
Ndipo mmene Yesu ananva anati, olimba safuna sing'anga ai, koma odwala.
Okondedwa dziwani Yesu akulankhula mau awa pa nthawi yomwe akuitana Mateyu mkulu yemwe anali mwa mmodzi okhometsa misonkho,
Yesu kuti afike polankhula mau amenewa ndichifukwa chakuti anthu ankamunena kuti bwanji akukhala pamodzi ndi anthu ochimwa?
Nthawi imeneyi anamuuza Mateyu kuti nyamuka ndipo amutsate, Mateyu anasiya zonse namutsata Yesu mosanyinyirika,
Yesu akulankhula monveka bwino kuti amene sakudwala safuna sing'anga, koma yekhayo amene akudwala ndiye amafuna sing'anga,
Lero lino ambirife tikudwala nthenda zosiyana siyana zakuuzimu, koma tsoka ifeyo sitikudziwa, zilipo nthenda zina umadwala koma usakudziwa, zina zilipo umadziwa ndithu kuti ukudwala koma kunyala nyaza,
Machimo tichitawa dziwani ndi nthenda zimene Yesu akulankhula, zofunika tikumane ndi sing'anga Yesu kuti atichilitse,
Tikhoza kumapemphera bwino bwino, koma nthenda ikuononga moyo wauzimu, zofunika tifune funeYesu kuti atichilitse,
Ukhoza kumaoneka ngati zilibwino pamaso pa wanthu pomwe mkatimo nthenda inadya moyo wako wauzimu, Sizikutengera kuti umapemphera kapena ayi, nthenda yakuuzimu imagwira aliyense,
Mukufunika mukumane ndi Yesu, mumutsate Yesu, Mateyu akunyamuka kumutsata Yesu kuti achilitsidwe, nanga inu muchedweranji?
Musachite manyazi, nthendayo ndiyanu, nthenda imeneyi ochiza wake ndi Yesu yekha kulibeso sing'anga wina yemwe angachize kuposa Yesu, lapani, batizidwani mdzina la Yesu kuloza ku chikhululukiro cha machimo anu, pamenepo mudzachiritsidwa, Amen.