Eden Malawi

Eden Malawi broadcasting company

congratulations Adad
25/09/2025

congratulations Adad

24/09/2025

A pro tudikilasotu ka live Mr Jefu tiseke comedy Louy Cee TV

Omwe amaima limodzi ndi mtsogoleri wa Malawi Congress party ngati wachiwili pa chisankho Cha dziko pa 16 September Vitum...
21/09/2025

Omwe amaima limodzi ndi mtsogoleri wa Malawi Congress party ngati wachiwili pa chisankho Cha dziko pa 16 September Vitumbiko Mumba achititsa Msonkhano wa atola nkhani mu mzinda wa Lilongwe.

Zina mwa zomwe Iwo alankhula pa msonkhanowu ndikusalongosoka kwa manambala omwe Ali pa ma pepala olembapo zotsatila za mavoti mmadera ena kummwera kwa dziko lino.

Mmawu awo amumba ati apeleka kale ena mwa madandaulo kubungwe la MEC

Mobwereza bwereza Iwo ayankhu muchingerezi kuti MCP got iti zomwe zikutanthauza kuti mbali yawo yawayendera kunkhani yazitstila zachisankho

Pomaliza Iwo anenaso kuti chipani chawo chimalemekeza malamulo ndipo akudikila kuti bungwe la MEC likoze zotsatila ndikuulutsa.


  #  #Mtsogoleri wachipani Cha UDF Atupele Muluzi ati ndiokhumudwa kuti dimokalase ya dziko lamalawi chili pa opsyezo.Iw...
20/09/2025

#
#
Mtsogoleri wachipani Cha UDF Atupele Muluzi ati ndiokhumudwa kuti dimokalase ya dziko lamalawi chili pa opsyezo.

Iwo ayankhula izi mu mzinda wa Lilongwe loweluka pa 20 September 2025

Malinga a Muluzi zotsatila zosatsimikizika zachisankho zikuonetsa zolakwika zambili.

Iwo ati zolakwika zambili zapezeka m'maboma ena kummwera ndiku m'mawa kwa dziko lamalawi.

Chipani Cha UDF chapeleka madandaulo ake ndi umboni ku bungwe loyendetsa chisankho la MEC "Muluzi".

pomaliza Iwo apemha amalawi kuti adekhe pomwe aliyese akudikilira zotsatila za chisankho chomwe chimaponyedwa pa 16 September chaka chino.

Bungwe la MEC lili mkati molandula zotsatila za chisankho kuchokela mdera osiyanasiyana mdziko muno.

Thomas Phiri- Lilongwe

Yemwe amaima ngati Mtsogoleli wadziko ngati oimanpayekha Adil James Chilungo wati avomereza kugonja kwawo pachisankho ch...
20/09/2025

Yemwe amaima ngati Mtsogoleli wadziko ngati oimanpayekha Adil James Chilungo wati avomereza kugonja kwawo pachisankho chachaka chino.

Iwo alankhula izi pamsonkhano wanayola nkhani mumzinda wa Lilongwe.

Mmawu Iwo ati ngakhale bungwe loyendetsa zisankho la MEC silinalengeze zotsatila zotsimikizika za chisankhochi koma Iwo ati ndiokozeka kugwila ntchito ndi yemwe apambane.

Ngakhale izi zili chomwechi iwowa alonjeza kuti ndondomeko ngakhaleso mfundo zawo sizintha koma kuti ziwatengera chitsogolo kuti zaka zikubwerazi akwanitse maso mphenya awo autsogoleri.

Thomas phiri -Lilongwe

26/08/2025

Bwalo lalikulu la milandu mu mzinda wa Lilongwe, lakana pempho la yemwe anali bwanamkubwa wa banki ya Reserve komanso woyimira mtsogoleri wa chipani cha UTM a Dalitso Kabambe ndi mnzake, loti aimitse mlandu wawo wachinyengo pa ngongole ya K13.6 biliyoni kuti amupatse mwayi wochita kampeni pachisankho cha pa 16 September.

Popereka chigamulo Lachisanu pa 22 August, 2025, Justice Anneline Kantambi adati pempholi linalibe tanthauzo ndipo likadasokoneza kuchitiridwa nkhanza pamaso pa malamulo.

Kabambe, pamodzi ndi Henry Mathanga, Leston Ted Mulli, Felton Mulli, Joseph Khupe, Mulli Brothers Limited, ndi Web Commercials Limited, akuimbidwa mlandu wotsogolera ngongole ku Mulli Brothers ndi ena kuti agule feteleza wa Affordable Inputs Programme (AIP) yemwe sanapezeke, ndipo ngongoleyo sanabweze.

Director of Public Prosecutions (DPP) Masauko Chamkakala alandila chigamulochi ponena kuti ndale sizingagwiritsidwe ntchito kuchedwetsa milandu.

Mlanduwu uli poyambirira, ndipo pempho silinatengedwe.

Boma lanenetsa kuti kupezeka kwa Kabambe sikofunikira pakadali pano, chifukwa choyimira pamilandu chilipo, ndipo milandu sikuphwanya ufulu wake wopikisana nawo pazisankho.

Nkhaniyi yadza patatha sabata imodzi kuchokera pamene khoti lina lidaloleza mtsogoleri wakale wa dziko lino Peter Mutharika kuti ayimitse kukaonekera pamlandu wa Cement Gate mpaka chisankho chitatha kuti chikwaniritse ndondomeko yake ya kampeni.

Address

Area 27, Mchezi
Lilongwe
207227

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Eden Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Eden Malawi:

Share