Eden Broadcasting station

Eden Broadcasting station broadcasting company

Nkhani yoopsa kwambiri yachitika lero  ku Mponela m’boma la Dowa, pamene bambo wina yemwe sakudziwika wadzipha podzipony...
05/07/2025

Nkhani yoopsa kwambiri yachitika lero ku Mponela m’boma la Dowa, pamene bambo wina yemwe sakudziwika wadzipha podziponya kutsogolo kwa galimoto yomwe imayenda.

Malinga ndi mboni yowona ndi maso,yati bamboyo mmene amayenda mumsewu waukulu wa M1, adadziponya dala m’matayala akumbuyo kwa galimotoyo.

Apolisi sananenepobe kanthu za nkhaniyi.

05/07/2025
04/07/2025

Unduna wa za malo, nyumba ndi chitukuko, wakhazikitsa khonsolo yomwe idzayang’anire kukhazikitsidwa kwa lamulo latsopano la Land and Housing Act.

Cholinga chachikulu cha khonsoloyi, ndi kubweretsa bata munthambi ya za nthaka ndi nyumba pakayendetsedwe ka malo, kusiya makhalidwe oipa, komanso kuteteza nzika ku zachinyengo.

Lamulo la Land Act, lomwe linakhazikitsidwa mu 2024, limapereka ndondomeko yoyendetsera malo ndi nyumba m’Malawi.

Stella Nthengu-Blantyre.

Bwalo lalikulu la milandu ku Blantyre, lagamula m’bale wina wa zaka 22 ochokera m’dziko la Zimbabwe, Daryl Edwards, kuti...
04/07/2025

Bwalo lalikulu la milandu ku Blantyre, lagamula m’bale wina wa zaka 22 ochokera m’dziko la Zimbabwe, Daryl Edwards, kuti alipire chindapusa cha K130,000 chifukwa chofuna kugula chitupa cha dziko la Malawi mwachinyengo.

Edwards, yemwe adalandira chiphaso cha Malawi mchaka cha 2010 pogwiritsa ntchito zinthu zabodza, adamugwira atapita ku maofesi a Immigration ku Likulu la dziko lino kuti akakonzenso chikalatacho.

Edwards, wagwidwa pa nthawi yomwe amafunsidwa mafunso ndipo atapereka chindapusa, Edwards wagamulidwa kuti adapezekenso mdziko muno mwanjira iliyonse.

Kulangidwa kwa Edward, ndi chenjezo kwa ena omwe angayese kugwiritsa ntchito dongosololi.

Stella Nthengu-Blantyre.

03/07/2025

Apolisi a ku Ndirande agwira bambo wina wa zaka 43, yemwe dzina lake ndi Steven Chisale, kamba koba ndalama zokwana K4.2 miliyoni za mpingo wawo.

Malinga ndi malipoti, Chisale ndi amene adapatsidwa udindo woyang’anira chuma cha mpingowu pomwe msungichuma wampingowu atapita ku tchuthi .

Chisale yemwe adamupatsa udindo woyika ndalama zachikhumi mu akaunti yakubanki ya mpingowu, akuti adalephera kuyika ndalamazo ndicholinga choti azigwiritsa ntchito.

A Chisale avomera kuti adagwiritsa ntchito ndalamazo molakwika ponena kuti amafuna kuzibweza koma sanazibweze.

Padakali pano munthuyu ali m’manja mwa apolisi, ndipo kufufuza kwina kuli mkati.

Mamembala ampingo akuoneka kuti apumira m’mwamba ndi kumangidwako, koma zomwe zachitikazi zikudzetsa nkhawa pa nkhani ya zachuma pakati pa utsogoleri wa mpingowu.

Stella Nthengu-Blantyre.

Wachiwiri kwa Purezidenti wakale wa South Africa David Dabede Mabuza wamwalira. Mabuza anabadwira ku Phola Trust, m’chig...
03/07/2025

Wachiwiri kwa Purezidenti wakale wa South Africa David Dabede Mabuza wamwalira.

Mabuza anabadwira ku Phola Trust, m’chigawo cha Mpumalanga, pa 25 August 1960. Analandira Bachelor of Arts Degree in Psychology ku yunivesite ya South Africa mu 1989, kutsatira kupambana kwake pa National Teacher’s Certificate kuchokera ku Mgwenya College of Education mu 1985.

Anali mphunzitsi wa Masamu wophunzitsidwa mwaluso ndipo adakhala Mphunzitsi Wasukulu asanalowe ndale. Chikhumbo chake chinali pa maphunziro ndipo adakhazikitsa DD Mabuza Foundation mu 2014, akuyang'ana kwambiri za maphunziro ndi kulimbikitsa anthu omwe ali pachiopsezo monga ana, mabanja otsogozedwa ndi ana, okalamba ndi anthu olumala.

Walapisiwa ka 17 ku tshama ku va Mupuresidennde wa Riphabliki ya Afrika-Dzonga hi ti 27 Febuluwa 2018, naswona hi Lachinayi, 30 May 2019 eka Utawala wa Demokrasi wa 6 ku landzela ku thwasiwa kakwe eka ntirho lowu hi Phuresidente Cyril Ramaphosa.

Wachiwiri kwa Purezidenti Mabuza adapatsidwa ntchito ndi Purezidenti Ramaphosa ndi Maudindo Otumidwa atsopano mu nthawi ya Boma ya 2019-2024.

Stella Nthengu-Blantyre

Pulezidenti Lazarus Chakwera wanenetsa kuti kupita patsogolo kwa dziko la Malawi sikungatheke ndi ndalama, mphamvu, mape...
03/07/2025

Pulezidenti Lazarus Chakwera wanenetsa kuti kupita patsogolo kwa dziko la Malawi sikungatheke ndi ndalama, mphamvu, mapemphero kapena anthu opereka ndalama zakunja, koma chifukwa cha kukhulupirika kwa nzika zodzipereka ku dziko lawo.

A Chakwera anena izi lero pamwambo wolumbiritsa mkulu wa aphungu watsopano ku Kamuzu Palace mumzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi a Chakwera, adagwiritsa ntchito zinthu zitatu zomwe ndi kukhulupirika, kukhulupirika ndi luso posankha maloya 12 kuphatikiza awiri omwe adapatsidwa ulemu atamwalira.

Anthuwa ndi monga veteran lawyer Kamudoni Nyasulu, Ralph Mhone , Maziko Phiri , James Masumbu, Innocentia Ottober, Emily Makuta, Minister of Justice Titus Mvalo ,Pempho Likongwe , Attorney General Thabo Chakaka Nyirenda, Marshal Chilenga ,Garton Kainja (awarded) .

Nduna ya zofalitsa nkhani ndi kasamalidwe ka digito, Moses Kunkuyu, walengeza kuti chikondwelero cha chaka chino chokumb...
03/07/2025

Nduna ya zofalitsa nkhani ndi kasamalidwe ka digito, Moses Kunkuyu, walengeza kuti chikondwelero cha chaka chino chokumbukira zaka 61 za ufulu wa dziko la Malawi chichitika mu mzinda wa Lilongwe.

Polankhulapo pamsonkhano wa atolankhani, a Kunkuyu adati mwambowu uyamba ndi mwambo wa National Service of Worship womwe udzachitike pa 5 July ku Bingu International Convention Centre (BICC), komwe mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera adzatsogolere a Malawi pa mwambo wopembedzera, wosonkhanitsa magulu achipembedzo osiyanasiyana.

Ndunayi idaonjezanso kuti zikondwererozi zipitilira ndi mwambo waukulu wa pa 6 July womwe udzachitikire pa bwalo la Bingu National Stadium (BNS), pomwe Purezidenti Lazarus Chakwera ndi mlendo wolemekezeka, Duma Boko, Purezidenti wa Republic of Botswana, adzakomera mwambowu.

Kunkuyu adatinso pachikondwerero cha tsiku la ufulu wodzilamulira mudzakhala ndi zochitika zosiyanasiyana, monga gulu lankhondo la Malawi Defence Force, kukamba nkhani, masewero a mpira, kuvina kwa chikhalidwe, nyimbo ndi zina zosangalatsa.

Timu ya Silver Strikers FC, yapambana pamasewero ampira wamiyendo womwe imamenya  ndi CRECK Sporting Club ndi zigoli ziw...
02/07/2025

Timu ya Silver Strikers FC, yapambana pamasewero ampira wamiyendo womwe imamenya ndi CRECK Sporting Club ndi zigoli ziwiri kwa chimodzi.

Innocent Shema ndiye wasankhidwa kukhala Man of the Match chifukwa chakuchita bwino kwambiri pamasewerowa.

Kupambanaku kwalimbikitsa kwambiri timu ya Silver Strikers FC yomwe ikuwoneka yamphamvu mu ligi ndipo Otsatira a timuyi ndi osangalala kwambiri kaamba kachipambanochi.

Address

Area 27, Mchezi
Lilongwe
207227

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Eden Broadcasting station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Eden Broadcasting station:

Share