EDEN FM RADIO

EDEN FM RADIO Media,manufacturing and entertainment company

Phungu wa dera la ntcheu Bwanje souhth Alexander Mwisho chilikumtima ati sanakhutile ndi yankho la nduna mu unduna wa za...
21/02/2025

Phungu wa dera la ntcheu Bwanje souhth Alexander Mwisho chilikumtima ati sanakhutile ndi yankho la nduna mu unduna wa za chitetezo cha mdziko Ezeckiel Ching'oma pa pempho lawo lokhudza mayendedwe pa polisi ya bilira lomwe analipereka kunyumba ya Malamulo.

Phunguyu wati polisi ya Bilira imayenda mitunda itali itali kuti ikagwile ntchito zake pomwe mayendedwe palibepo.

Iwo ati madera otalika kuposa ma kilomita makumi atatu(30) imadila polisi yomweyi zomwe zimapangitsa iwo kugwilitsa ntchito ndalama za mthumba mwawo

Pepmholi akahala akulipereka mu nyumbayi kwanthawi yaitali koma palibepo yankho logwilika,pomwe undunawu wati ukukoza za vutoli.

Thomas Nakali Phiri -Lilongwe

20/02/2025
20/02/2025

Phungu wa dera la kummwera kwa bwanje,Mwisho alexender chilikumtima auza unduna wa za chitetezo cha mdziko kuti athandizilepo pa nkhani zokhudza polisi ya Bilira m'bomali.

Chilikuntima ati nkhani ya mayendedwe ndiyomwe yavuta kwambili maka kuti apolisi amayenda mtunda wautali kuti akagwile ntchito zawo.

Nduna mu undunawu Ezeckiel ching'oma yati unduna wawo uyesesa kuti ukoze zavutoli.

18/02/2025

Gulu la anthu otchedwa mbadwa zokhudzidwa motsogozedwa ndi a gape khombe ati lachinayi sabata ino apita kunyumba ya malamulo kukamizamiza aphungu kuti akambilane ndi kukhazikitsa lamulo lokhudza zaka zokhudzaa yemwe akuyenera kukhala mtsogoleri wa dziko (President)
Mu kanema Ali mmusiyu akhombe akufotokoza ko komanso mneneri wa chipani cha Dpp a shadrick namalomba akuyankhapo kumbali yawo.

Zokambilana za lero mnyumba ya Malamulo zachedwerapo kuyamba kamba koti aphungu ambili sadapezeke mnyumbayi zomwe zapang...
18/02/2025

Zokambilana za lero mnyumba ya Malamulo zachedwerapo kuyamba kamba koti aphungu ambili sadapezeke mnyumbayi zomwe zapangitsa kuyamba kuitana maina aphungu kuti adziwe uyo sanabwere kuzokambilana za lero mnyumbayi

Mchitidwe onga uwu umuchukila kwambili Maka kuzokambilana za nthawi yomwe yayandikana ndizokozekela misonkhano yokopa anthu

Aphungu omwe apezeka mnyumbayi kummawaku ndi 51 mwa aphungu 193 onse omwe alipo mdziko muno .

18/02/2025

With Gerald Chavez Kampanikiza – I just made it onto their weekly engagement list by being one of their top engagers!

Mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma ku nyumba ya Malamulo ati zomwe anayankhula a Chakwera m'mawu awo potsekulira nyumba ...
17/02/2025

Mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma ku nyumba ya Malamulo ati zomwe anayankhula a Chakwera m'mawu awo potsekulira nyumba ya Malamulo ndikungofuna kudzichekenila chabe ponena kuti ulamuliro wawo ndiolephera

Achaponda ayankhula izi lolemba masana kunyumba ya malamulo pomwe amayankhapo pa zomwe achakwera anayankhula nthawi yomwe amatsekulira zokambilana zanyumbayi lachisanu sabata Latha

Popitilira kuyankhula Iwo ati dziko lino likukunana ndi mavuto ochuluka zomwe zikupangitsa amalawi ambili kulephera kukwanilitsa zokhumba zawo.

Iwo akhudzanso zinthu zingapo zomwe pakadali pano ngati dziko likudutsamo monga kusowa kwa ndalama zakunja ngakhaleso kukwera mitengo ya katundu ofunikila pa moyo wamunthu.

Phungu wadera la pakati m'boma la ntcheu Dr Albert Mbawala ati zomwe wachita president Chakwera mzogometsa.Iwo ati dziko...
17/02/2025

Phungu wadera la pakati m'boma la ntcheu Dr Albert Mbawala ati zomwe wachita president Chakwera mzogometsa.

Iwo ati dziko lino lasintha mu ngodya za mbili kamba ka ulamuliro wa maso mphenya womwe achakwera alinawo.

Mbawala ayankhula izi lolemba masana kunyumba ya malamulo pomwe amayankhapo pa zomwe achekwera anayankhula nthawi yomwe amatsekulira zokambilana zanyumbayi lachisanu sabata Latha

Izi zili chomwechi pomwe anthu ochuluka akulankhulapo zokhudzana ndi zomwe achakwera anayankhula.

Zokambilana za aphungu akunyumba ya malamulo zayamba mu mzinda wa Lilongwe.Nyumba ya Malamulo anatsekulira lachisanu pa ...
17/02/2025

Zokambilana za aphungu akunyumba ya malamulo zayamba mu mzinda wa Lilongwe.
Nyumba ya Malamulo anatsekulira lachisanu pa 14 February 2025 pomwe mtsogoleri wa dziko la Malawi Dr Lazarus McCarthy Chakwera anapeleka ndandanda wa momwe chitukuko chilili mdziko muno.

17/02/2025

With Gerald Chavez Kampanikiza – I just got recognized as one of their top fans!

Your trusted partner Entertainment,News and talk
17/02/2025

Your trusted partner
Entertainment,News and talk

Alibe mulandu munthuyu
17/02/2025

Alibe mulandu munthuyu

Odya zake uja alibedi mulandu
13/02/2025

Odya zake uja alibedi mulandu

13/02/2025

Nkhondo iyiyi eeee

13/02/2025

Anthu akuti amavina ngati nyimbo iyi

13/02/2025

Address

Area 27, Mchezi
Lilongwe
207227

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when EDEN FM RADIO posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to EDEN FM RADIO:

Videos

Share