Mr bronne kumayamika

Mr bronne kumayamika truth telling and gospel singers

25/08/2026

sungamuzembe mulungu, maso ake ndi makutu ake zimafikila palipose ngati anakanika yona kumuthawa mulungu, lwe ndiyine ndindani? chikufunika ndikuvomeleza kuti ndine ambuye wochimwane ndili pano udzawona ukulu wamulungu ukudza payiwe monga nthawi yakutembenuka mtima kwa saulo mkukhala pawulo

21/08/2026

mateyo 10 verse 33
Koma lye amene andikana lne pa maso pa anthu, lneso ndidzamukana pamaso pa atate anga akumwamba

Munthu amene uthenga wabwino ukumufikila azichitcha chamwayi, koma mmalo mwake ambili tikumayesa ngati pamene kunjaku ku...
21/08/2026

Munthu amene uthenga wabwino ukumufikila azichitcha chamwayi, koma mmalo mwake ambili tikumayesa ngati pamene kunjaku kukumada mkumacha tikuganiza kuti kudzikhala choncho mpaka kale , pamene sichoncho ayi, koma ndi nthawi yimene mulungu wayipeleka mphamvu yamkwiyo wake lsanatuluke chifukwa mphamvu yamkwiyo wake lkatuluka zowona zake ndizakuti sikudzakhalaso mwayi kwa Wochota zoyipa, nde tawonani mawu awa 👇

aroma 2 verse 4 Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirila kwake? Kodi sukuzindikila kuti kukoma mtima kwakeko, mkofuna kuti lweyo ulape machimo ako?

tisapeputse dala nthawi yamulungu yomwe wapeleka kwayife kuti titembenuke mtima tilape tingadzayilile kutsogolo kuno, tiyeni tigwilitse ntchito mwayi wumenewu odzuka ndi moyowu sikuti akatidzutsa ndi moyo ndekuti amafuna kuti tidzichita zofuna thupi ndi mwazi ayi koma kuti tizindikile zolakwa zathu ndikumupemphampha kuti atikhululukile ,kenako tikalapa tiyambe kuwonetsa zipatso zotidi munthuyu anatembenuka mtima zimene zili ntchito zabwino ndi chikhulupililo, ambuye akutsogoleleni anthu lnu

kodi mukudziwa kuti kubwela kwake kwa ambuye kuli ngati nsampha kulibe wodi ndipo mwini wake yesu anapeleka chitsazo yic...
18/08/2026

kodi mukudziwa kuti kubwela kwake kwa ambuye kuli ngati nsampha kulibe wodi ndipo mwini wake yesu anapeleka chitsazo yichi zamomwe zidzakhalila 👇

Mateyo 24 verse 38

pakuti mmasiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene nowa analowa mchombo; 39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndikuwamiza onse ,

tamvani akuti sanadziwe ose chimene mulungu amkafuna kuchita chifukwa kunali koti nowa akuwalalikila koma sanafune kumuvela ndikusiya zoyipa zawo, nde yesu mwini akuti nthiwi ngati yomweyi kudzakhalaso kubwera kwake, kodi nanga poti nthawi ya yesuyi ndiyanthu Kodi tikusintha pamene tikumva uthenga wabwino kapena tikunyalanyaza ngati nthawi ya nowa? Koma zindikilani kuti za nthawi ndi nyego sadziwa aliye angakhale angelo akumwamba koma atate okha , chomcho mulungu akadzangoti kwatha kudzakha kwatha basi, kulibe zopeleka chenjezo kuti ayi mawa ndikuwononga dziko lapani ayi nthawi yovela uthenga wabwino ndikutembenuka ndiyomweyi kulibe yina, ambuye akutsogoleleni muzose

wonani mawu awa lnu abale anga amantha mtima ,Luka 12 verse 4 lne ndikuwuzani, abwezi anga musachite mantha ndi amene am...
15/08/2026

wonani mawu awa lnu abale anga amantha mtima ,

Luka 12 verse 4

lne ndikuwuzani, abwezi anga musachite mantha ndi amene amapha thupi chifukwa akatelo sangachiteso kanthu,5 koma lne ndidzakuwonetsani amene muyenela kumuwopa wopani yiye, amene pambuyo pakupha thupi ali ndi mphamvu yakuponya ku gahena. lnde, lne ndikukuwuzani muwopeni lye

lye oponya ku gahena nde mulungu ameneyo ndamene malemba akutitsimikizila kuti tiyenela kumuwopa lye posunga chilungamo chake,
mkutheka munaphonyetsapo chilungamo chifukwa Cha kuwopa ena ake ,namati ndikayankhula chilungamo moyo wanga ukhala pa chiwopsezo ,kapena ntchito yanga ltha kapena zinthu zisokonekela pa moyo wanga ,osawopa aliyese amene afuna kuti mupange zinthu zosemphana ndi mulungu lnu mkumugonjela ,mpaka kumuchimwila mulungu chifukwa Chochiya Naye mantha ,ayi tichotse mantha ndi manyazi pofuna kutambasula chilungamo palipose pamene tingakhale ,munthu wamantha malemba amatuwuza kuti sadzalowa ufumu wa mulungu, ambuye akutsogoleleni muzose

lmvani lzi lnu ana amulungu, osayiwala Pali pose pamene tikhala kuti tili pa ulendo umene nthawi  yonyamukila sidziwika,...
13/08/2026

lmvani lzi lnu ana amulungu, osayiwala Pali pose pamene tikhala kuti tili pa ulendo umene nthawi yonyamukila sidziwika, tsono poti nthawi yonyamukila sidziwika tikungo yenela kukhala odzikozekeletsa ,kuzikozekeletsa kwake sikupakila dzovala mu bag ayi ,koma kukhazikika m'mawu amulungu nthawi zonse, lelo tiphuzileko ndikuchenjezana pa phuzilo lli monga lfe apawulendo👇

aroma 13 verse 8
Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyese kupatula ngongole yakukondana wina ndi mzake

apapa sikuti akuletsa kubweleka kanthu ayi ,koma zikutanthawuza kuti pamene tatenga kanthu kamunthu munjila yangongole tidzikwanitsa kubweza, tisafike popanga udani ndi mwini katundu chifukwa chakuti sitinamubwezele ayi pakuti tikatelo tikulakwitsa ndekuti ndi ulendo wathu sizikugwilizana, choncho ngati uli ndi ngongole ya mwini yofunika utabweza kabwezeleni ngati muli nayo, kaya ndiyakale kale mwini wake anayiwala kabwezeni chifukwa Cha ambuye ngati tilibe tikayipeza tikabweze lzi ndizofunika kwambili pozikozekeletsa pa ulendo umene tinyamuke munthawi yosadziwika , ambuye athandizile kuyendetsa bwino nyengo zako kuti ukwanitse kubwezela ngongole yamwini

anthu lnu muyenela kudziwa  kuti mawu amulungu samango kambapo ,koma kuti mawuwa anthu ambili tikapanda kumvera munthawi...
09/08/2026

anthu lnu muyenela kudziwa kuti mawu amulungu samango kambapo ,koma kuti mawuwa anthu ambili tikapanda kumvera munthawi yino tidzawamvetsa mutsogolo koma titagwa kale muzopweteka zosaleletseka, komabe mulungu ndiwa chifundo ndipo ndiwabwino wakupatsaso moyo mutsiku larelo ndicholinga chakuti mawu ake akufukileso kuti ukhale munthu osinthika kuti nthawi ya lmfa lkamakufikila udzatchedwe odala akufa akumwalila mwa ambuye ,pakuti mawu akutelo kuti 👇

aheberi 9 verse popeza kunayikika kwa munthu kufa kamodzi ndipo kenako kuweluzidwa

Chivumbulutso 13 verse 14 kenaka ndinamva mawu kuchokela kumwamba akuti lemba ,kuti odala anthu amene akufa ali mwa ambuye kuyambila tsopano mpaka mtsogolo

ndipo ndikutsimikizileni kuti wofa mwa yesu khirist saweluzidwa, koma yese womwalila asali mwa yesu amaweluzidwa ,ndikatitu kufa mwa yesu ndikutanthawu kuti unalapadi mowona mtima, chifukwa tikati kulapa ndikusiya choyipa chimene umachipanga kale uli osakhulupilila ambuye ,osati kukhulupilila ambuye mkuyamba kupemphela,koma mkumapitilizabe zoyipa zakale zija dziwani kuti kumeneko sikulapa ,koma kusiya zoyipa mkumatumikila ambuye mowona mtima, ndiwe wamwayi lelo lino kumawelenga nawo uthenga wuwu koma azako ena amalakalaka atabwelelaso kudziko kuno kuti adzamveso uthenga ngati umenewu mkuwugwilitsila ntchito koma tsoka ndilakuti mwayi umenewo sunapatsidwe kwayiwo,pakuti ukafa kamodzi kudziko kuno supatsidwaso mwayi odzawonekelaso ku wanth kachiwili,ambuye akutsogoleleni muzose

aheberi 2 verse 1 chifukwa chake lfe tiyenela kusamalila kwambili zimene tinamva, kuwopa kuti pang,Ono ndi pang,Ono ting...
08/08/2026

aheberi 2 verse 1 chifukwa chake lfe tiyenela kusamalila kwambili zimene tinamva, kuwopa kuti pang,Ono ndi pang,Ono tingazitaye

onani tiyenela kusunga zimene tidakhulupilila maka za uthenga wabwino ndikuwonetsetsa kuti mmoyo wathu wa tsiku ndi tsiku tikukhala m'mawu ake, kuwopa kuti tingazitaye ndikulowa muzina, choncho tizizindikila kuti kumene munthu wayikako chiyembekezo mkumene kumakhala kuli mtima wako ndipo zimakhala zopweteka ukakhala kuti waphonyana ndi chiyembekezocho, lfe tidayika chiyembekezo chathu pa ambuye kuti akamazabwela tikapulumuke nde mkudzasiyidwa zitha kudzakhala zopweteka kwambili ,nde tisamale kuti tisazitaye ambuye akutsogoleleni muzose

onani chofunika kugwilitsitsa kwambili,sichuma ayi kapena ntchito ayi kapena business ayi, chofunika kugwilitsitsa kwamb...
07/08/2026

onani chofunika kugwilitsitsa kwambili,sichuma ayi kapena ntchito ayi kapena business ayi, chofunika kugwilitsitsa kwambili ndi mawu amulungu osalola kupindula china Chake koma mkutaya mawu amulungu ayi ,onani chifukwa chake 👇

Luka 21 verse 33

Kumwamba ndi dziko lapasi zidzatha, koma mawu anga sadzatha

onani zonse tikuziwona lelozi zidzatha nthawi lkubwela ndipo palibe chidzatsale koma mawu amulungu amene lnu mutawasunge sadzatha mpaka muyaya ngakhale mufumu wake tidzakhala ndi mawu amwewa ambuye ukuthandizeni kugwilitsitsa mawu ake kuposa zose, ndiposo ambuye akutsogoleleni muzose

nthawi zonse pamene tikukhala tidzikhalaso ndi chikondi pozindikila kuti anayamba kutichitila chikondi ndi mulungu,  Pal...
06/08/2026

nthawi zonse pamene tikukhala tidzikhalaso ndi chikondi pozindikila kuti anayamba kutichitila chikondi ndi mulungu, Pali anthu wena pakati pathu azathu akalakwitsa timayankhula modutsa mulingo, sitisamala za azathu poganiza ngati zathu zose zili bwino ,Koma sitizindikila kuti palibe amene zake zili 100% tonse tili ndizofoka zimene zikufunika mulungu kuti adzitikhululukila kufikila kubwela kwa ambuye ,onani verse lli👇

Luka 8 verse7 aphuzitsi amalamulo ndi afalisi anabweletsa mkaz amene anagwidwa akuchita chigololo. lwo anamuyimililitsa patsogolo pa wanthu 4 ndipo anati kwa yesu," aphuzitsi , mkazi uyu tinamugwila akuchita chigololo.4 mmalamulo amose anatilamulila kuti akazi otele tiwagende miyala. tsonopano lnu mukutipo kuti chani?
pamene lwo anapitilila kumufusa, lye anawelamuka ndipo amawuza kuti , ngati wina wayinu alipo opanda tchimo ,ayambe lye kumugenda miyala mkaziyu,"lye anawelamaso pasi ndikulemba padothi, 8 lwo atamva lzi anayamba kuchoka mmodzi mmpdzi

mateyo 7 verse 1 musamaweluze wena ,kuti nanuso mungadzaweluzidwe.2 pakuti momwemo lnu muweluzila wena ,lnuso mudzaweluzidwa chimodzimodzi

tawonani amene anabweletsa mkazi wachigololowo pamene yesu adawawuza kuti ngati alipo mmodzi wayinu amene alibe tchimo lye ayambe kumugenda miyala mkazi yu, koma atamva lzi anayamba kuchoka okha chifukwa chani anayamba kuchoka chifukwa zinalipo zina zimene zimawoneka ngati zing,Ono zing,Ono koma zimakhalabe kuti ndi tchimo pamaso pa mulungu, choncho pamene tawona kuti wina wake walakwila kaya dziko kaya lnuyo tiyeni tisamale kalankhulidwe kathu ndikachitidwe kathu pozindikila kuti nafe tili nazo zofoka zimene kumaso kumaso kwa dziko lapasi ndizosawonekela koma pamaso pa mulungu ndizowoneka, palibe salakwitsa choncho chikondi patsogolo ambuye akutsogoleleni muzonse muzonse

Address

Mikundi
Lilongwe
1637

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mr bronne kumayamika posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share