01/03/2026
Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Jane Ansah, ayamikira boma la dziko la Zambia posunga chikhalidwe, ndipo anati izi simsangulutso chabe koma kulimbikitsa umodzi pakati pa anthu.
Iwo ananena izi loweruka pamene anali mlendo olemekezeka wapadera pa mwambo wa a Ngoni a mtundu wa Mpezeni otchedwa Nc’wala ku Chipata, mdziko la Zambia, moyitanidwa ndi Inkosi Ya Makhosi Mpezeni IV.
Wachiwiwri kwa Mtsogoleriyu, anati chikhalidwe ndi ufulu komanso chimatsamira pa mfundo zitatu zimene ndi; chilankhulo, zakudya ndi kavalidwe, zimene anati ndi zofanana mmayiko ozungulira dziko la Malawi.
“Mukaona pakati pathu, tikuoneka ofanana ndipo stingasiyanitse komwe tikuchokera. Ndife anthu amodzi, sitinafunsidwe pamene amatigawa kukhala maiko awiri,” iwo anatero.
A Ansah anayamikiranso boma la dziko la Zambia povomera kuchita mgwirizano pa malonda a chimanga ndi dziko la Malawi pamene limafunika chakudya cha maanja omwe anali ndi njala.
Polankhulaponso pa mwambowu, Pulezidenti wa dziko la Zambia, a Hakainde Hichilema, omwe anali mlendo olemekezeka, anati boma lawo lipitiriza kupititsa patsogolo zachikhalidwe chifukwa ndi zoyenera kutero.
Mtsogoleri wa dziko la Zambiayu anayamikira dziko la Malawi, kudzera kwa Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino, poonetsetsa kuti ana akuphunzira zachikhalidwe kuti zipitilire, malingana ndi mmene magule a a Ngoni analiri poyamba pa mwambowu.
“Pamene a Ngoni aku Malawi amavina, ndinaona ana pakati pawo, tiyeni tiombere mmanja Malawi popeza izi zikuonetsera kuti chikhalidwechi chikhala chikupitilira mpaka kale,” anatero a Hichilema.
Dr Ansah anafunira mafuno abwino Inkosi Ya Makhosi Mpezeni IV pa mwambowu ndipo anapereka mphatso zosiyanasiyana kwa mfumuyi.
Kuchokera ku Malawi, Inkosi Ya Makhosi V, Inkosi Gomani V, komanso Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino wa kale, a Khumbo Kachali ndi omwe anali nawo pa mwambo wa Nc’walawu mwa ena.