Boma Lathu

Boma Lathu Boma Lathu is published by the publications section of the Ministry of Information.

01/06/2026

Boma latsutsa mphekesera zokhudzana ndi mkumano wa Nduna

Ofesi ya Mtsogoleri wa dziko lino ndi Nduna ya OPC yatsutsa
mphekesera zimene zikuyenda mmasamba a mchezo zonena kuti Mtsogoleri wa dziko lino Pulofesa Arthur Peter Mutharika sanatsogolere mkumano wa nduna umene unachitika sabata yathayi, ndikutsindika kuti iwo akhala akutsogolera mkumanowu chiyambireni ntchito yawo.

Malingana ndi chikalata chimene ofesiyi yatulutsa ndipo chasayinidwa ndi Mlembi wa Mkulu wa boma, a Justin Saidi, a Mutharika amatsogolera misonkhano yonse chikhalireni pa mpando pa 16 Sepitembala chaka cha 2025.

“A Pulezidenti amatsogolera mkumanowu mogwirizana ndi mphamvu zimene anapatsidwa kwa iwo mu Malamulo a Dziko lino komanso malingana ndi udindo wawo,” chatero chikalatachi.

Ofesiyi yapempha Amalawi kugwiritsa ntchito ufulu wa kayankhulidwe moyenera ndikupewa kufalitsa nkhani zosatsimikizika zimene zimachotsa chikhulupiriro cha anthu mu nthambi za boma.

Address

Department Of Information
Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Boma Lathu posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share