Boma Lathu

Boma Lathu Boma Lathu is published by the publications section of the Ministry of Information.

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wadziko lino Dr Jane Ansah lachinayi anakayendera koparetive ya Tiafikile kwa a gulupu Chimwala...
12/03/2026

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wadziko lino Dr Jane Ansah lachinayi anakayendera koparetive ya Tiafikile kwa a gulupu Chimwala ku Mitundu m’boma la Lilongwe, komwe anakaona ntchito zaulimi zomwe anthu pa koparetiviyi akuchita.

Kudzera mu bungwe lawo lomwe akulitchula kuti Jane Ansah Foundation, Wachiwiri kwa Mtsogoleriyu anaperekanso zinthu zosiyanasiyana kwa achikulire, anthu akhungu lachi albino komanso aulumali.

Katundu yemwe anaperekedwayu ndi monga zakudya komanso zinthu zina zomwe amagwiritsa ntchito anthu a khungu lachi albino monga mafuta odzola otchinjiriza ku dzuwa, magalasi komanso zipewa mwa zina.

Pulezidenti  wadziko lino Pulofesa Arthur Peter Mutharika wafika mdziko muno lero kuchokera mdziko la South Africa komwe...
12/03/2026

Pulezidenti wadziko lino Pulofesa Arthur Peter Mutharika wafika mdziko muno lero kuchokera mdziko la South Africa komwe anapita paulendo wapadera.

Ndege yomwe anakwera Pulezidenti Mutharika inafika pa bwalo la ndege la Kamuzu nthawi itangodutsa kumene 5 koloko madzulo.

Mmene amafika mdziko muno, Pulezidenti Mutharika yemwe anatsagana ndi Madame Gertrude Mutharika paulendowu, analandiridwa ndi Mlembi wamkulu wa Boma, Dr. Justin Saidi.

A Mutharika ananyamuka mdziko muno pa 1 March, 2026, kupita mdziko la South Africa.

  Pofuna kulimbikitsa lamulo limene mtsogoleri wa dziko lino a Pulofesa Arthur Peter Mutharika apereka pa nkhani yolimbi...
09/03/2026



Pofuna kulimbikitsa lamulo limene mtsogoleri wa dziko lino a Pulofesa Arthur Peter Mutharika apereka pa nkhani yolimbikitsa ukhondo mmalo opezeka anthu ambiri, nduna yazaumoyo a Madalitso Baloyi pamodzi ndi nduna yoyang'anira maboma ang'ono ndi chitukuko cha m'midzi a Ben Phiri, masana a lero anakayendera msika waukulu wa Lilongwe, msika wa msungwi komanso chipatala cha area 25.

Polankhula atayendera malowa, a Phiri ati cholinga choyendera malowa ndi kuonetsetsa kuti anthu komanso adindo akutsatira lamulo limene linaperekedwali kuti madera ambiri akhale aukhondo.

Iwo apempha anthu amene amapezeka mmalowa kuonetsetsa kuti akutsatira njira zabwino zotayira zinyalala, mwa zina zolimbikitsa ukhondo.

Mmau awo, a Baloyi ati unduna wawo upitiliza kupititsa patsogolo ntchito zolimbikitsa ukhondo mdziko muno.

A Baloyi apemphanso anthu mdziko muno kutenga udindo osamalira malo owazungulira ponena kuti izi zithandiza kuchepetsa matenda amene amafala chifukwa cha kusatsatira bwino njira za ukhondo.


Malawi Government

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Jane Ansah, ayamikira boma la dziko la Zambia posunga chikhalidwe, ndipo anat...
01/03/2026

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino, Dr Jane Ansah, ayamikira boma la dziko la Zambia posunga chikhalidwe, ndipo anati izi simsangulutso chabe koma kulimbikitsa umodzi pakati pa anthu.

Iwo ananena izi loweruka pamene anali mlendo olemekezeka wapadera pa mwambo wa a Ngoni a mtundu wa Mpezeni otchedwa Nc’wala ku Chipata, mdziko la Zambia, moyitanidwa ndi Inkosi Ya Makhosi Mpezeni IV.

Wachiwiwri kwa Mtsogoleriyu, anati chikhalidwe ndi ufulu komanso chimatsamira pa mfundo zitatu zimene ndi; chilankhulo, zakudya ndi kavalidwe, zimene anati ndi zofanana mmayiko ozungulira dziko la Malawi.

“Mukaona pakati pathu, tikuoneka ofanana ndipo stingasiyanitse komwe tikuchokera. Ndife anthu amodzi, sitinafunsidwe pamene amatigawa kukhala maiko awiri,” iwo anatero.

A Ansah anayamikiranso boma la dziko la Zambia povomera kuchita mgwirizano pa malonda a chimanga ndi dziko la Malawi pamene limafunika chakudya cha maanja omwe anali ndi njala.

Polankhulaponso pa mwambowu, Pulezidenti wa dziko la Zambia, a Hakainde Hichilema, omwe anali mlendo olemekezeka, anati boma lawo lipitiriza kupititsa patsogolo zachikhalidwe chifukwa ndi zoyenera kutero.

Mtsogoleri wa dziko la Zambiayu anayamikira dziko la Malawi, kudzera kwa Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino, poonetsetsa kuti ana akuphunzira zachikhalidwe kuti zipitilire, malingana ndi mmene magule a a Ngoni analiri poyamba pa mwambowu.

“Pamene a Ngoni aku Malawi amavina, ndinaona ana pakati pawo, tiyeni tiombere mmanja Malawi popeza izi zikuonetsera kuti chikhalidwechi chikhala chikupitilira mpaka kale,” anatero a Hichilema.

Dr Ansah anafunira mafuno abwino Inkosi Ya Makhosi Mpezeni IV pa mwambowu ndipo anapereka mphatso zosiyanasiyana kwa mfumuyi.

Kuchokera ku Malawi, Inkosi Ya Makhosi V, Inkosi Gomani V, komanso Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino wa kale, a Khumbo Kachali ndi omwe anali nawo pa mwambo wa Nc’walawu mwa ena.


Bungwe la Beautify Malawi (BEAM) Trust madzulo ano likhazikitsa ndondomeko ya zaka zisanu ya kagwiridwe kake ka ntchito ...
27/02/2026

Bungwe la Beautify Malawi (BEAM) Trust madzulo ano likhazikitsa ndondomeko ya zaka zisanu ya kagwiridwe kake ka ntchito kuyambira chaka cha 2026 mpaka 2030.

Mtsogoleri wa dziko lino, Professor Arthur Peter Mutharika, ndi yemwe akhale mlendo olemekezeka pamwambowu.

Bungwe la BEAM likukhazikitsa ndondomekoyi kutsatira kutha kwa ndondomeko yomwe inkagwiritsa ntchito zaka zisanu zapitazo.



  Boma layamba kugwiritsa ntchito makina ngati ndondomeko yolipirira ndalama ku boma pofuna kuchepetsa  kugwiritsa ntchi...
27/02/2026



Boma layamba kugwiritsa ntchito makina ngati ndondomeko yolipirira ndalama ku boma pofuna kuchepetsa kugwiritsa ntchito ndalama zapepala mmaunduna komaso mnthambi za boma.

Kulipira ndalama komanso chindapusa ku polisi tsopano kuzichitika pogwiritsa ntchito njira zotumizira ndalama pa lamya.

Boma lati lazindikira kuti mdziko muno mukulowa zakumwa zina zimenezikupereka chiopsezo ku miyoyo ya aMalawi.Pachifukwa ...
27/02/2026

Boma lati lazindikira kuti mdziko muno mukulowa zakumwa zina zimenezikupereka chiopsezo ku miyoyo ya aMalawi.

Pachifukwa ichi boma lakhazikitsa msokho wa 20 kwacha pa 100 kwacha iliyonse.


A Mwanamveka ati njira yolembera anthu ntchito mmaudindo  okhazikika ndi osakhazikika m'boma tsopano yaimitsidwa kaye.Iw...
27/02/2026

A Mwanamveka ati njira yolembera anthu ntchito mmaudindo okhazikika ndi osakhazikika m'boma tsopano yaimitsidwa kaye.

Iwo ati kukwezedwa kwa maofesala a giredi F ndi magiredi ena otsika mmusi kuziyenera chirolezo chochokera ku nthambi yosunga chuma komanso ku nthambi ya olemba ntchito za boma kuti atsimikizire kaye za kupezeka kwa ndalama.

A Mwanamvekha alengeza kuti makampani akunja amene alibe ma ofesi ku Malawi kuno koma akupindula ndi anthu a mdziko muno...
27/02/2026

A Mwanamvekha alengeza kuti makampani akunja amene alibe ma ofesi ku Malawi kuno koma akupindula ndi anthu a mdziko muno tsopano adzipereka msonkho.

Ma kampaniwa ndi monga Netflix, YouTube mwa ena.

Ndunayi yati ipereka tsatane tsatane wa momwe ndondomeko yotolera msonkho oterewu iziyendera mtsogolomu.


  Boma lakweza thandizo limene limapereka kwa anthu osowa mu chaka cha 2026 kufikira 2027, kuphatikizaponso ndalama  yok...
27/02/2026



Boma lakweza thandizo limene limapereka kwa anthu osowa mu chaka cha 2026 kufikira 2027, kuphatikizaponso ndalama yokwana K7 biliyoni ku ndondomeko ya Mtukula Pakhomo, imene yakwera mopitirira theka posiyanitsa ndi ndalama imene inaperekedwa mchaka cha 2025 ndi 2026, malingana ndi nduna ya zachuma, mapulani a zachuma ndi mphamvu ku anthu, a Joseph Mwanamveka.

Iwo anaonjezera kuti ndalama zoonjezera zokwana K2 biliyoni zapita ku thandizo loona za anthu a ulumali ndi ndondomeko zoona za chisamaliro cha ana pofuna kuchepetsa mavuto a zachuma ndi njala ku maanja ochepekedwa.

Amwanamveka ati kuyambila pa 1 April chaka chino, ma office aboma akuyenela azigwilitsa ntchito makina (Malawi Electroni...
27/02/2026

Amwanamveka ati kuyambila pa 1 April chaka chino, ma office aboma akuyenela azigwilitsa ntchito makina (Malawi Electronic System) akafuna kugula katundu.


  Kumbali ya maphunziro,a Mwanamveka ati boma layika ndalama zokwana K1.8 thililiyoni ku ntchito zotukula maphunziro mdz...
27/02/2026



Kumbali ya maphunziro,a Mwanamveka ati boma layika ndalama zokwana K1.8 thililiyoni ku ntchito zotukula maphunziro mdziko muno.

Pa ndalamazi, ndalama zokwana K47 biliyoni zayikidwa ku sukulu ya ulere.

Address

Department Of Information
Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Boma Lathu posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share