25/04/2026
ZAKA CHIKWI- KUONONGEDWA KWA DZIKO LAPANSI
Nthawi yobwera Khristu, akufa olungama adzauka, pamodzi ndi olungama amoyo adzakwatulidwa kukakumana naye mu mlengalenga. Pamenepo oyipa adzafa poona ulemelero wake (1 Atesalonika 4:16,17; 2 Atesalonika 2:8).
Kwa zaka chikwi dziko lapansi lidzakhala bwinja (Yeremiya 4:23-26)
Satana adzayendayenda pa dziko lowonongeka, kulingalira za zotsatira za kupanduka kwake. Adzavutika atalandidwa mphamvu ndipo sipadzapezeka oti amunyenge (Chivumbulutso 20: 1-3)
Mu zaka chikwi'zi, olungama adzalamulira ndi Khristu kumwamba ndikuchita ntchito yakuweruza. Adzaweruza oyipa ndi angelo akugwa, kuyerekeza zochita zawo ndi lamulo la Mulungu ndi kutsimikizira chilango choyenera pa mlandu uliwonse. ( Chivumbulutso 20:4; 1 Akorinto 6:3)
Kumapeto kwa zaka chikwi, mzinda Woyerawo udzatsika kuchokera kumwamba (Chivumbulutso 21:2), anthu oyipa adzaukitsidwa mu mdzukiro wachiwiri, ndipo Satana adzamasulidwa.
Woyipayo adzamemeza anthu ochimwa kuti azinge mzindawo ndi kuuthira nkhondo, koma moto udzatsika kwa Mulungu ndikunyeketsa satana ndi omutsatira ake (Chivumbulutso 20:5,7-9, 14)
Kenako dziko lapansi lidzakonzedwanso mwatsopano (Chivumbulutso 21:1,4), ndipo anthu a Mulungu adzalandira ufumu wosatha. Ichi ndi choonadi cha m’Baibulo chokhudza zaka chikwi—nthawi ya bwinja, chiweruzo, ndi kubwezeretsanso komaliza, osati mwayi wachiwiri kapena ufumu wapadziko lapansi wabwino.
Mpaka Babulo agwe.....