Nkhani Za M'maboma

Nkhani Za M'maboma 🌍THIS IS THE LATEST & FASTEST GROWING PAGE FOR BREAKING NEWS🌏 . Welcome 😎kuing'alura osaopa😎💪💪

10/07/2025

Nkhan yoopsa

Moto watentha ndi kupha ana amapasa achaka chimodzi pomwe nyumba yomwe mayi wawo anawasiyamo yapsa m'boma la Kasungu.

Mfumu yaikulu Chisinga yatsimikizira Times 360 Malawi za nkhaniyi.

Malinga ndi a Henz Kamanga omwe anathamangira pa malo angoziwa, mayi wa anawa, a Monica Kenkere anasiya anawa mnyumba kandulo akuyaka ulendo wa kunsika kuti akagule ma pampa.

"Moto wa kanduloyu, unayatsa zovala mpaka kufika pomwe anawa anali ndikuwatentha modetsa nkhawa mpaka kufera pomwepo," atero a Kamanga.

Pakadali pano, apolisi m'bomali, sanayankhulepo za nkhaniyi.

Wolemba: Nelson Gonjani.

Breaking News 🤣Russia - Ukraine Russia yayamba kutumiza zimabomba zazikulu zikulu zowala ngati mwezi ku Ukraine .Chikama...
09/07/2025

Breaking News 🤣

Russia - Ukraine

Russia yayamba kutumiza zimabomba zazikulu zikulu zowala ngati mwezi ku Ukraine .
Chikamabwera Mzinda ukumawala ngati kukucha kumene ili nyambalo

Will update
Wolemba kondwani kachamba ✍️
Pangani sha

NKHANI YOCHITIKA 👇Wolemba kondwani kachamba ✍️Malawi Tiyambe ndi nkhani Ya kumalawi.Ma tchalichi akulu akulu mudziko mun...
09/07/2025

NKHANI YOCHITIKA 👇

Wolemba kondwani kachamba ✍️
Malawi
Tiyambe ndi nkhani Ya kumalawi.

Ma tchalichi akulu akulu mudziko muno monga Mpingo wachikatolila , Bungwe loimila Asilamu onse la Muslims Association of Malawi ndi mpingo yoziwika bwino Yakana kuti palibe olo modzi mwa abusa ao alandilako ndalama pa 8 Billion anatchula Abusa a Kamwendo😅.

Iwo ati aaaaaaaa sanampenyepo olo wani mbusa wao analandila ndiye sakuziwa kuti 5 thousand azibusa amakamba Iwo ndi ati ati.

Chazutsa Mau akulu akoma akagonera kapena kuti Nkhuku zodya akulu zipota mwana ndi choti pa 6 July Abusa anathokoza a President a Dziko Lino kuti Ndalama 8 Billion Ku NEEF zapalekedwa Kwa azibusa 5 sauzande

Pangani follow page Yi apa Mwachangu 👉Nkhani Za M'maboma

 Bungwe la MEC lati, chiwerengero cha anthu omwe atenga kalata zowavomereza kuyima nawo pa chisankho chikudzachi pa mpan...
08/07/2025



Bungwe la MEC lati, chiwerengero cha anthu omwe atenga kalata zowavomereza kuyima nawo pa chisankho chikudzachi pa mpando wa mtsogoleri wa dziko chinakali pa 15.

M'neneri wa bungweli a Sangwani Mwafuriwa wati, tsiku loti anthu omwe akuyima nawo pa chisankhochi ayambe kupereka zikalatazi ku MEC ndi pa 24 July kufika pa 30 July.

Iwo atinso pa 14 July ndi pomwe atsekulire movomerezeka kuti anthu atha kuyamba kuchita misonkhano yokopa anthu kuti adzawavotere.

MEC yatolera 150 miliyoni kwacha kwa atsogoleri 15 wa, komanso ndalama za nkhani nkhani kwa omwe akuyimira ngati a phungu ndi ma khansala mdziko muno.

(by Chikondi Mphande-Blantyre:07/08/25)

08/07/2025



Apolisi ku Liwonde amanga anthu atatu omwe akuwaganizira kuti akukhudzidwa ndikubedwa kwa makina omwe amatchedwa kuti (Genexpert) pachingerezi omwe amagwiritsidwa ntchito
popimira nthenda ya chifuwa chachikulu ( TB) ndi matenda ena.

Ofalitsa nkhani za polisi ya Liwonde a Ngwashape Msume atsimikiza za nkhaniyi ngakhale sadapereke tsatanetsatane wa omangidwawa koma ati pakadali pano apolisi akuchitabe kafukufuku pomwe makinawa sadapezekebe.

Koma Times 360 Malawi yamvetsedwa kuti omangidwawa ndi ogwira ntchito pachipatala chachikulu chabomali.

Makinawa omwe alipo awiri akuganiziridwa kuti asowa kucha kwa lero lachiwiri ndipo ndiandalama pafupifupi 60 million kwacha.

Germany - China Tensions Dziko la Germany laitanisa  ambassador wa China pompano kuti afotokoze bwino cholinga chaoLero ...
08/07/2025

Germany - China Tensions

Dziko la Germany laitanisa ambassador wa China pompano kuti afotokoze bwino cholinga chao

Lero masanawa Ndege za nkhondo za German zimauluka kudela kwako osati Ku space ya China . Koma China inawaunika ndi chi torch chachikulu Kumaso chotchedwa Lazer pogwiritsa Ndege yao

Izizi zimapangisa kuti Pilot asaone ndi kusokoneza pa dashboard nkuchita Ngozi .

Germany ifuna kuziwa nchifukwa chani China imafuna kuti Ndege ya German ichite Ngozi .
China sinayankhe Kaye.

Chithunzi ndi laser jet tangoika kuti wina amvesese nkhaniyi. Zofilazo ndi kuwala kofila kumene anawunikila Ndege ya German kuti asaone.

Germany yalusa kwambiri ndipo yanena kuti Iyoyo simaopa munthu. Imaswa

Wolemba :kondwani kachamba ✍️

From kachambaIsrael - Iran update Israel inapereka warning Ku Gulu la iran kuti anthu asamuke Ku yemenPamene amasamuka i...
08/07/2025

From kachamba

Israel - Iran update
Israel inapereka warning Ku Gulu la iran kuti anthu asamuke Ku yemen

Pamene amasamuka iyo inanyamuka ndikupita Ku Dziko Lina Lebanon kumene Gulu Lina la Iran lotchedwa Hezbollah limapanga plan yophulisa Israel.

Kumeneko achotsa Miyoyo ya ma Commander onse , office ndi barracks yao

08/07/2025

Nkhani yongotipeza kumene 😭

Makina awiri oyezera chifuwa chachikulu (TB) komanso matenda a HIV (GeneXpert) asowa pachipatala chachikulu cha Machinga.

Mneneri wa chipatalachi a Wongani Nyirenda atsimikiza zankhaniyi ponena kuti izi zachitika kucha kwa lero ndipo kuti makinawa onse pamodzi ndi a ndalama za pafupifupi 60 million kwacha.

Iwo ati, ngakhale izi zachitika, ntchito yoyeza matendawa siidakhudzidwe kwenikweni kaamba koti chipatalachi chatsala ndi makina amodzi kutsatira kubedwa kwa awiriwa ndipo pakadali pano nkhaniyi ayitula kale ku polisi ndipo kafukufuku ali mkati.

Pakadali pano apolisi sanayankhulepo kanthu pa nkhaniyi koma wapampando wa mgwirozano wamabungwe omwe siaboma ku Machinga a Belinda Somanje Chimombo adzudzula za mchitidwewu ndipo ati ngati mabungwe atengapo gawo pokomana ndiadindo achipatalachi komanso kuonetsetsa kuti lamulo ligwire ntchito kwa amene akukhudzidwa ndikusowa kwa makinawa.

Wolemba Blessings Tambala.

🐓Apresindent chakwera akuti👇👇Kumasekelera munthu owononga kuti apitilile kuwononga ndi chimodzi chomwe chawononga dziko ...
07/07/2025

🐓Apresindent chakwera akuti👇👇

Kumasekelera munthu owononga kuti apitilile kuwononga ndi chimodzi chomwe chawononga dziko lino - Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera wati dziko la Malawi likuyenera kumangidwanso pa maziko a mphamvu ndipo kusekelera anthu owononga ndi zina zomwe zasakaza maziko a dziko lino.

Chakwera wati dziko la Malawi palibe chomwe lingaphule ngati lingamapitilire kutaya maziko a chikhalidwe posekelera anthu owononga omwe akhazikika pa kudya za ulele, kulalata, kunyoza, chinyengo, kutukwana, ziwawa, kumenyana ndi zikwanje ndi zina pomwe dziko likuwadziwa koma kumawasekelera kuti azipitiliza.

Pangani follow page Yi apa 👉NkhaNkhani Za M'maboma muzikwanisa kuona nkhan iliyonse YOCHITIKA

😊AWANJATA 😊Apolisi ya Kanengo ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe amanga anthu asanu ndi atatu powaganizira kuti akhala aku...
07/07/2025

😊AWANJATA 😊

Apolisi ya Kanengo ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe amanga anthu asanu ndi atatu powaganizira kuti akhala akuchita za umbanda.

Anthuwa ndi Robert Petro wa zaka 30, Leonard Kamphale 48, komanso Patrick Mtengula wazaka 36, onse oti ndi akabwelebwele ku ndende. Pomwe ena anayi ndi Thokozani Henry wazaka 32, Madalitso Chidzanja 28, Richard Moyo 33, Andrew Zimba 30 komanso Henry Ebele wazaka 44.

Malingana ndi mneneri wa apolisi ya Kanengo a Gresham Ngwira anthuwa akuwaganizira kuti ndi gulu la anthu ambanda omwe lakhala likuyenda ndi zida zoopsa kudera la Area 25 ndikumachitira anthu ziwembu.

Iwo ati mwazina akuwaganizira anthuwa ndi umbanda waku Area 25 C komwe anabako 35 million Kwacha komanso akatundu ena andalama zoposa 40 million Kwacha.

A Ngwira ati gululi akuliganiziranso kuti linachitira za uchifwamba anthu ena atatu chaku Spama. Apolisi ati poyamba anagwira m'modzi mwa oganizilidwawa (Andrew Zimba wazaka 30), ndipo kenaka anakagwira oganizilidwa enawa kumalo ena ogona alendo komwe amakonzekera kukachita za umbanda zina.
(by InnocentKumchedwa-Lilongwe;07/06/25)

😭😭😭 WAZIPHA POZIPONYERA KUTEYARA LA GALIMOTO😭Munthu wina yemwe sakudziwika ku Mponela m'boma la Dowa, wafa atadziponya k...
05/07/2025

😭😭😭 WAZIPHA POZIPONYERA KUTEYARA LA GALIMOTO😭

Munthu wina yemwe sakudziwika ku Mponela m'boma la Dowa, wafa atadziponya ku galimoto lonyamula katundu lomwe limayenda.

A James Katema, womwe awona izi zikuchitika, ati bamboyo amayenda m'mbali mwa msewu wa M1, ndipo atawona galimotolo likubwera, anayima m'mbali kenako mkudziponya mkati mwa mateyara akumbuyo.

Mu nkhani ngati yomweyi, mtsikana wina yemwe pano sakudziwika wapezeka atafa pafupi ndi manda a Mponela 1 m'bomali. Pakadali pano, apolisi sadayankhulepo pa zomwe zachitikazi.

(by Wilson Henry-Dowa: 07/05/25)

Nkhan zangazi zizikupexani Mosavuta ngat mwapanga follow page Yi apa 👉Nkhani Za M'maboma

Nkhani mwachiduleMtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ati sakondwela akamaona aMalawi akungonyoza zovuta za mdzik...
04/07/2025

Nkhani mwachidule

Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera ati sakondwela akamaona aMalawi akungonyoza zovuta za mdziko muno malo momatengapo gawo lokonza zinthuzo.

Iwo ati mzika yabwino mdziko ndi yomwe imati ikaona zovuta pa malo sidikila kuti wina amuuze kuti achitepo kanthu kapena kumangoloza zala ayi koma ndi yomwe imakhala patsogolo kukonza zolakwikazo.

A Chakwera ati aMalawi azindikile kuti dziko lino ndi la aliyense ndipo pamodzi mzika iliyonse ingathe kukonza dzikoli.

Ndipo iwo awonjezeraso kuti anthu asamadikile kuti potengapo gawo lokonza zitukuko zosiyanasiya za mdziko azidikila kuti boma liwalipire kanthu kapena kufuna kutchukilapo koma makamaka azigwira ndi mtima olikonda dzikoli

Wolemba Brenda Kayo

Address

Lilongwe
INVITESOTHERSTOLIKETHISPAGEOF

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nkhani Za M'maboma posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share