10/07/2025
Nkhan yoopsa
Moto watentha ndi kupha ana amapasa achaka chimodzi pomwe nyumba yomwe mayi wawo anawasiyamo yapsa m'boma la Kasungu.
Mfumu yaikulu Chisinga yatsimikizira Times 360 Malawi za nkhaniyi.
Malinga ndi a Henz Kamanga omwe anathamangira pa malo angoziwa, mayi wa anawa, a Monica Kenkere anasiya anawa mnyumba kandulo akuyaka ulendo wa kunsika kuti akagule ma pampa.
"Moto wa kanduloyu, unayatsa zovala mpaka kufika pomwe anawa anali ndikuwatentha modetsa nkhawa mpaka kufera pomwepo," atero a Kamanga.
Pakadali pano, apolisi m'bomali, sanayankhulepo za nkhaniyi.
Wolemba: Nelson Gonjani.