09/10/2025
Nkhan
Apolisi m'boma la Ntchisi atsimikiza za imfa ya mwana wa miyezi inayi, Alexander Chimpeni, wa m'mudzi mwa Chiwembu m'bomalo yemwe wamwalira mayi ake atamugwera pomwe amamenyana ndi munthu wina.
Malingana ndi m'neneri wa polisi m'bomali Salomy Zgambo wati patsikuli mayiyu amakangana ndi nzawo atamubeleka Alexander kunsana ndipo ali mkati mokangana ndewu inabuka pakati pa awiriwa ndipo mwatsoka mayiyu anagwa ndikutsamila mwanayu.
Zgambo wati zitatero anathamangila naye ku chipatala cha Ntchisi komwe achipatala anatsimikiza kuti mwanayu wamwalira.
Zotsatira za chipatala zawonetsa kuti mwanayu wamwalira kaamba kovulala kwambiri m'mutu.
Wolemba: Maureen Kanyundo