Montfort Media

  • Home
  • Montfort Media

Montfort Media A print and publishing house

19/07/2025



Lions march on

An all Zomba-based battle between Red Lions and Changalume Barracks in the FDH Bank Cup has ended in favour of the lions who have triumphed 2-1 at Balaka Stadium today.

Changalume was the first to score through Emmanuel Sikelo Jnr in the 15th minute but the lions pressed on until they equalized through Mphatso Magaleta at the stroke of first half (45').

The result means Changalume Barracks are out of the race.

By Precious Msosa

Lilongwe iyaka moto n'kukhazikitsidwa kwa kampeni ya MCPMzinda wa Lilongwe unapentedwa ndi makaka ofiira ku mamawaku ndi...
19/07/2025

Lilongwe iyaka moto n'kukhazikitsidwa kwa kampeni ya MCP

Mzinda wa Lilongwe unapentedwa ndi makaka ofiira ku mamawaku ndi ulendo wa ndawala wa achinyamata a chipani cha Malawi Congress (MCP) omwe anayenda kuchokera ku Area 18 komanso bwalo la Lilongwe Community kukafika ku bwalo la Bingu komwe kuli kamuthemuthe wa kukhazikitsa kampeni ya chipanichi.

Pakadali pano anthu ochuluka osonkhana ku bwalo la masewero la Bingu komwe akufuna kumva mfundo zokopera anthu za chipanichi pa chisankho chomwe chichitike pa 16 seputembala.

Pakadali pano zoyankhula zili mkati ku mwambowu komwe woimba wotchuka Skeffa Chimoto anasangalatsa anthu ndi nyimbo zake.

Rose Chipumphula CHALIRA
Zinthunzi wojambula a MANA

19/07/2025

Sulom iyimba mlandu Silver, Elias Missi ndi Ekhaya

Bungwe loyendetsa ligi ya mpira wa miyendo mdziko muno la Super League of Malawi (Sulom) layimba mlandu timu ya Silver Strikers, goloboyi wa timu ya Ekhaya Elias Missi komanso timu yake ya Ekhaya.

Malingana ndi chikalata chomwe bungweli latulutsa lero pa 19 Julaye, Sulom yayitanitsa timu ya Silver Strikers kuti ikawonekere ku komiti yosungitsa mwambo chifukwa cholephera kudekhesa ochemere ake omwe anathira zinthu za madzi madzi kwa goloboyi wa timu ya Mafco mu masewero awo a mu ligi masiku apitawa.

Timu ya Mafco inadandaula kuti otsatira ena a Silver anathira mkodzo goloboyi wawo Christopher Mikuwa.

Sulom yayimbanso mlandu Silver chifukwa cholekerera ochemereraake kulowa mu bwalo la za masewero zomwe zinapereka chiopsezo kwa osewera ndi akuluakulu a matimu.

Iyo yayimbanso mlandu timuyi kaamba konyazitsa masewerowa a mpira.

Sulom yayimbanso mlandu wotchinga pa golo wa timu ya Ekhaya Elias Missi chifukwa cha mchitidwe wa uchigawenga wokonyonga pa khosi womwetsa zigoli ku timu ya FCB Nyasa Big Bullets Babatunde Adepoju mu masewero awo ku Blantyre.

Bungwe la FAM linapeza kale olakwa awiri mwa amene ankayimbira masewerowa ndipo linawagamula kuti asayimbirenso mpira mu ligi yayikulu kwa miyezi ingapo.

Wolemba Precious Msosa


NAYORG yakangalika kutukula miyoyo ya achinyamataBungwe la Nkhandze Youth Organization (NAYORG), lati ndalama zomwe alan...
18/07/2025

NAYORG yakangalika kutukula miyoyo ya achinyamata

Bungwe la Nkhandze Youth Organization (NAYORG), lati ndalama zomwe alandira kuchokera ku Non-Govermental Organizations Regulatory Authority (NGORA), zithandiza kupititsa patsogolo ntchito za achinyamata zomwe iwo amagwira mboma la Balaka.

Milton Sukasuka, yemwe amawona ntchito zofalitsa nkhani ku bungweli, wati maphunziro omwe anapanga okhudza kayendetsedwe ka ntchito ka ndalama, athandiza kukonza zolakwika zomwe zinalipo mmbuyomu.

“Maphunzirowa athandiza pa magwiridwe athu a ntchito kuti apite patsogolo. Zambiri zomwe taphunzira zokhudza kayendetsedwe ka ndalama ku bungwe lathu sitimazidziwa,” anatero Sukasuka.

Sukasuka anati ndi zofunika kuti mabungwe azidziwa nkhani zokhudza zachuma chifukwa zimathandiza kagwiridwe kawo ka ntchito ndi mabungwe ena. Iye anati koma ngati anthuwa alibe upangiriwu, zimakhala zovuta kuti apange ndondomeko ya chuma ya mmene angayendetsere mabungwe awo.

Bungwe la NAYORG lalandira ndalama kudzera ku bungwe la NGORA zomwe azipereka mmagulu a achinyamata omwe ali ndimaluso osiyanasiyana komanso kuthandiza kupitsa umoyo wa achinyamata patsogolo pozidalira pachuma.

Rose Chipumphula CHALIRA


Sukasuka: Maphunziro atsitsegula mmaso

Chimulirenji alowa UTMA Everton Chimulirenji, womwe amafuna kuyima ngati phungu woyima paokha ku dera la kumpoto m’boma ...
17/07/2025

Chimulirenji alowa UTM

A Everton Chimulirenji, womwe amafuna kuyima ngati phungu woyima paokha ku dera la kumpoto m’boma la Ntcheu, kutsatira kusakhutitsidwa ndi mmene masankho a chipulula anayendera – atuluka mu chipani cha DPP ndikulowa chipani cha UTM.

A Chimulirenji awalandira lero ku chipani cha UTM ku Mphepo Zinayi m’boma la Ntcheu.

Pa chisankho cha chipulula, a Chimulirenji, omwe mwa ena anapikisana ndi yemwe anali wapampando wa bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission, a Jane Ansah, ndi omwe anapambana. Koma a Ansah atakamang’ala ku chipani kuti chisankhocho sichinayende bwino, a DPP analengeza kuti adzayimire ndi mayi Ansah.

Mchaka cha 2019, Pulezidenti Peter Mutharika anasankha a Chimulirenji kukhala wachiwiri wawo ndipo atapambana pa chisankho chachikulu anakhala wachiwiri wa pulezidenti kufikira pomwe khoti linagamula kuti chisankhochi chichitikenso kaamba koti panali zolakwika.

Rose Chipumphula Chalira

Ali mchitokosi poganiziridwa kuti anapha mchemwali wawoApolisi ku Lilongwe amanga Egnat Katengeza wa zaka 51, yemwe ndi ...
16/07/2025

Ali mchitokosi poganiziridwa kuti anapha mchemwali wawo

Apolisi ku Lilongwe amanga Egnat Katengeza wa zaka 51, yemwe ndi mchemwali wawo yekhayo wa mayi m’modzi ndi bambo amodzi wa a Agnes Katengeza, omwe anali mkulu woona za netiweki ku banki yayikulu ya Reserve Bank of Malawi –
powaganizira kuti akukhudzidwa ndi kuphedwa kwa mchemwali wawoyu mchaka cha 2023.

Agnes anapezeka atafa kuseli kwa Gateway Mall mu mwezi wa Seputembala ku Lilongwe, 2023, ndipo apolisi anamanga mchimwene wawo a Amos Katengeza.

Malingana ndi mneneri wa polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, Amos yemwe ndi mchimwene wawo wa malemuwa ndi yemwe anawatchula Egnat kuti anatengapo gawo lalikulu pa imfa ya a mchemwali wawo.

A Chigalu ati apolisi anayitanitsa Egnat kuti akamufunse mafunso ndipo kumangidwa kwake kukutsatira kafukufuku yemwe apolisi akhala akuchita.

Iwo atinso Egnat ndi amene anali munthu woyamba kukachita lipoti za kusowa kwa mchemwali wawo tsiku lomwe Agnes anapezeka ku Gateway Mall atamwalira.

Egnat yemwe amakhala ku dera la Area 25 amutsegulira mlandu wakupha. Iye amachokera m’mudzi mwa Kalembo, Mfumu yayikulu Chiwere m’boma la Dowa.

Rose Chipumphula CHALIRA


Chinthunzi/ Chigalu

Apolisi ku  Chitipi ku Lilongwe,  amanga abambo awiri omwe anaba njinga yamoto ya kabaza yomwe iwo anakwera pa 4 Julayi ...
09/07/2025

Apolisi ku Chitipi ku Lilongwe, amanga abambo awiri omwe anaba njinga yamoto ya kabaza yomwe iwo anakwera pa 4 Julayi 2025, nthawi ya 9 koloko usiku kufupi ndi Admarc komwe mwini njingayi anamenyedwa.

Malingana ndi mneneri wa polisi ya Lilongwe, a Hastings Chigalu, abambowa ndi Vincent Phiri wa zaka 20 ndi Smart Banda wa zaka 30 ndipo onse amakhala ku Area 36.

Iwo ati patsikuli awiriwa anakwera njingayi ku Area 36 atamuwuza mwini njingayu kuti akupita ku depoti ya Lilongwe.

Koma atafika pa Admarc abambo awiriwa anamumenya wa njingayu ndi kuthawa ndi njingayo.

Patapita masiku awiri apolisi a kafukufuku ku Chitipi, anamva mphekesera kuti abambo awiriwa ali ndi njinga. Atachita kafukufuku wawo, apolisi anamanga awiriwa komanso njingayi inapezeka.

Oganiziridwawa akawonekera ku bwalo la milandu posachedwapa komwe akayankhe mlandu wakuba.

Phiri amachokera m’mudzi mwa Swayibu , Mfumu yayikulu Msanama, m’boma la Machinga, pamene Banda amachokera m’mudzi mwa Nameta Mfumu yayikulu Chimaliro, m'boma la Thyolo.

Wolemba: Rose Chipumphula CHALIRA


Wojambula chinthunzi cha oganiziridwa – Lilongwe Polisi

'Palibe angatukuke ndi AIP'Nduna ya zaulimi a Sam Kawale awuza nthumwi za achinyamata ku mkumano wawo wa pa chaka (Natio...
04/07/2025

'Palibe angatukuke ndi AIP'

Nduna ya zaulimi a Sam Kawale awuza nthumwi za achinyamata ku mkumano wawo wa pa chaka (National Youth Summit) lero ku Lilongwe kuti asiye kudalira zipangizo zaulimi zotsika mtengo (AIP) akamapanga kapena kuganiza zoyamba ulimi.

A Kawale ati ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengo ndi ya thandizo la kanthawi kochepa ndipo palibe yemwe angatukuke ndi thandizoli.

"Musataye nthawi ndi kumadikira AIP, chifukwa ndondomekoyi ndi yothandiza kwa ka nthawi kochepa. Lero kakhale komaliza kumaganiza za AIP chifukwa palibe amene angatukuke," atero a Kawale.

Iwo ati achinyamata omwe akufuna kupindula ndi ulimi akuyenera kulumikizana ndi mabungwe obwereketsa ndalama monga (NEEF) komanso pulojekiti ya AGCOM, mwa ena.

Koma malingana ndi achinyamata omwe amayankhula pa mkumanowu, iwo anati ngakhale ndunazi zatsimikizira achinyamatawa pa kuchuluka kwa mwayi yomwe ilipo popeza thandizo la ndalama zopangira mabizinesi osiyanasiyana, achinyamatawa akukumana ndizokhoma.

Iwo anati akapita ku ma ofesi a boma kapena maunduna monga a zamalonda, ulimi ndi mabungwe obwereketsa ndalamawa, akuluakulu ambiri amawakhomerera posawapatsa upangiri pomwe ku mabungwe kukumakhala zikole zochuluka.

Mkumanowu ukutha lero ndipo unali wa masiku atatu.

Precious Msosa

Youths decry favouritism in economic opportunitiesSome youths in the country have expressed concern on the continued fav...
03/07/2025

Youths decry favouritism in economic opportunities

Some youths in the country have expressed concern on the continued favouritism and sexual exploitation in employment and economic opportunities.

Presenting the concerns at the on-going National Youth Summit at Bingu International Convention Conference (BICC) today in Lilongwe, the youths say this practice has contributed to having more youths who are idle.

Ruth Kumwenda, a University of Livingstonia Public Health student said it's unfortunate that most bosses ask for sexual favours in order to offer them employment or other economic opportunities.

She said it's high time the bosses in many institutions started to take girls as they own daughters.

"They forget that they also have daughters and you wonder whether that is how they would wish their daughters to be treated," said Kumwenda amid loud applause in the auditorium.

Another speaker Dr. Precious Makiyi said when government comes up with financial opportunities, it's the sons and daughters of top government officials who are prioritized.

He cited the Israel Job Exchange program which he said most deserving youths are being left out in favour of the government and politicians connected youths.

Precious Msosa


Picture: Ruth making a point
Source: Alfred Maida

Buy a copy of Together Magazine and enjoy the story of Hope Mezuwa Banda and more other stories so that you can be inspi...
03/07/2025

Buy a copy of Together Magazine and enjoy the story of Hope Mezuwa Banda and more other stories so that you can be inspired by a story of drive, vision, and meaningful impact.
Let’s rise TOGETHER — for a better Malawi!!

Explore heartfelt stories, critical analysis, and bold reflections in this non-partisan magazine focused on Christians, ...
03/07/2025

Explore heartfelt stories, critical analysis, and bold reflections in this non-partisan magazine focused on Christians, politics, and culture.

'Kanani kugwiritsidwa ntchito'Wamkulu wa bungwe la United Nations Development Fund (UNDP) kuno ku Malawi  a Rebecca Adda...
03/07/2025

'Kanani kugwiritsidwa ntchito'

Wamkulu wa bungwe la United Nations Development Fund (UNDP) kuno ku Malawi a Rebecca Addah Donto apempha achinyamata kuti asalole kugwiritsidwa ntchito poyambitsa ziwawa.

A Donto ati ndiwokhudzidwa kwambiri ndi za chipolowe zomwe zinachitika masiku apitawa pamene a Silverster Namiwa omwe amatsogolera zionetsero anamenyedwa ndi anthu achifwamba mu mzinda Lilongwe.

Poyankhula izi dzulo pa mwambo wotsegulira mkumano wa achinyamata wokonzedwa ndi bungwe la National Youth Council of Malawi (NYCOM), a Donto anatsindika "refuse to be used" (kanani kugwiritsidwa ntchito).

Mu mau ake, mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera anavomerezana ndi a Donto kuti pamene dziko lino likuyandikira chisankho pa 16 Seputembala, achinyamata asagwiritsidwe ntchito pokolezera ziwawa.

Poyankhulapo pa za thumba la K2 biliyoni lomwe lakhazikitsidwa ndi bungwe la NYCOM, a Chakwera anati thumbali ndi mwayi waukulu kwa achinyamata kuti liwathandize kutukula miyoyo yawo.

Iwo anati chaka cha mawa ali ndi malingaliro wodzakweza ndalama za thumbali kufika pa K10 biliyoni.

Choncho iwo anapempha achinyamata kuti pamene akupitiriza zokambirana ku nkumanowu womwe uthe mawa, iwo akambirane zinthu zomwe zikuwakhudza ndipo abwere ndi mayankho omwe akufuna adindo awathandize.

Precious Msosa


Zithunzi: Alfred Maida

Address


Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Montfort Media posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Montfort Media:

Shortcuts

  • Address
  • Telephone
  • Alerts
  • Contact The Business
  • Claim ownership or report listing
  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share