28/05/2026
Abulazala khumi ndi awiri adzodzedwa kukhala adikoni
Kunali chimwemwe chodzadza tsaya ku seminale yaikulu ya St Peters mu Dayosizi ya Zomba pamene abulazala khumi ndi awiri amadzodzedwa kukhala a dikoni masiku apitawa. A dikoniwa khumi ndi m’modzi anali achibadwiri ndipo awiri anali a chipani cha Capuchins Missionaries.
Mwambo wokomawu unatsogoleredwa ndi Episkopi wa Dayosizi ya Mzuzu, a Yohane Suzgo Nyirenda, omwe anatsogolera mwambo wa nsembe ya Misa.
Episkopiyu analangiza abulazalawa kuti akuyenera kukatumikira Mulungu modzipereka ndi kukhala okonda mpingo wao. Iwo analangiza achinyamatawa kuti akatumikire mpingo monga ngati atumwi aja ankachitira.
Ambuye Nyirenda anati: “Mukapita m’maparishi anu mukatsogolere mpingo monga sinodi ikutiphunzitsira. Osati inu nomwe mukakhale asungichuma, inu nomwe akwaya, inu nomwe owona za ku kitchini ayi. Musakaike ndalama za parishi ku ma akaunti anu. Kasankheni anthu oyendetsa ntchito zosiyanasiyana pa parishi monga momwe anachitira atumwi aja posankha adikoni aja kuti adzigwira tchito zina pomwe atumwi anali akutumikira Mulungu.”
Ambuye Nyirenda analimbikitsa abulazalawa kuti akumbukire ntchito zawo zimene aphunzitsidwa ku seminale. Iwo anawalimbikitsa adikoniwa kuti ali ndi ma udindo atatu amene apatsidwa.
“Muli ndi maudindo atatu awa: udindo wogwira tchito, udindo wotumikira akhristu mu mpingo, komanso kuchita ntchito zachifundo. Osaiwala kupemphera, kupempherera mpingo ndi anthu onse. Kumbukirani kuti izi mwaphunzitsidwa kale.”
Woimilira makolo, Bambo Felensio McTear Phiri, anati iwo ndi okondwa ngati makolo kuona ana awo akulowa udikoni.
A Phiri anati: “Inu ana athu amene mwadzodzedwa udikoni lero kumbukirani kuti maitanidwe ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. Choncho, muyenera kuisamalira ndi mtima wonse.
Mwavomera nokha ntchitoyi popanda wina kukukakamizani. Choncho kumbukirani kusunga malonjezo onse amene mwachita lero pamaso pampingo. Ife makolo tikulonjeza kuti tidzapitiriza kukupemphererani ndikukuthandizani maitanidwe anu kuti tchito yabwino imene Mulungu anaiyamba mwa inu, Iye yemweyo ayitsirize.”
M’modzi oimilira kalasi ya adikoni atsopanowa, amenenso ndi mkulu wa kalasi imeneyi, Dikoni Pater Wandale, achipani cha abadwiri kuchokera kwa Nkhwayi Parishi mu Arkidayosizi ya Blantyre, anati iwo anayamba ulendowu ku seminale yaing'ono ku Pius Xii. Iwo anati moyo wa kuseminale siwophweka komabe zimangofunika kudalira Mulungu ndinso kulimba mtima. Iwo anati kalasi yawo munali anyamata khumi limodzi mphambu zisanu ndi ziwiri koma lero amene alandira udikoni ndi anthu khumi ndi atatu.
“Ulendowu amatitsogolera ndi Mulungu chifukwa sumadziwa kuti ukafika kapena ayi. Ifeyo timakhaka ndi nthawi yokhala ndi mibindikiro yomwe imatithandiza kuti tisinkhesinkhe za moyo wathu pakati pa ife ndi Mulungu wathu kuti tidziwe chenicheni chimene ife tili pamaso pa Mulungu wathu.
“Mau anga ndi owalimbikitsa abale athu amene aimitsidwa kuti asataye mtima. Iwo akhale ndi chikhulupiriro pa Mulungu kuti Mulungu amakhala ndi njira zina pamoyo wako kuti udzamutumikire mwanjira ina – kapenanso kumutumikira Mulungu ngati wansembe, asataye mtima. Ngati maitanidwe, akuyenera kusamalira maitanidwe awo, asataye chikhulupiliro,” anatero dikoni Wandale.
Dikoni Mayamiko Zangalama, a chipani cha Capuchins, wochokera ku St Louis Montfort Parishi, mu Mangochi Dayosizi, anati iwo ndi wokondwa kuti Mulungu walora kuti afike apa ngakhale kuti mkati mwa ulendo wawo munali zinthu zina zowabwezeretsa m'mbuyo.
Iwo anati: “Moyo wathu umakhala wovuta ndi mmene dziko likuyendera masiku ano. Anzathu ena achinyamata amakhala akuyenda ndi dziko pamene ife timakhaka ngati tikuyenda zosemphana ndi m’mene dziko likuyendera.”
WOLEMBA: Monique Vyahnorah Marco, Mtolankhani Wapadera