Montfort Media

Montfort Media A print and publishing house

Jun.—Jul. 2026 Issue (N. 135) of TOGETHER Magazine is officially out!
01/06/2026

Jun.—Jul. 2026 Issue (N. 135) of TOGETHER Magazine is officially out!

Mwambo wa buku la Pemphero la Mpingo wadza mu ZombaDayosizi ya Zomba lero yadala pomwe kampani ya Montfort Media ikukhad...
31/05/2026

Mwambo wa buku la Pemphero la Mpingo wadza mu Zomba

Dayosizi ya Zomba lero yadala pomwe kampani ya Montfort Media ikukhadzikitsa buku la Pemphero la Mpingo mu mpingo wa Katolika.

Zochitikachitika zili mkati lero pa tchalitchi cha St. Charles Lwanga. Mlendo wolemekezeka ku mwambowu ndi nthumwi ya Ambuye Alfred Chaima, Bambo Bernard Chipole.

Wolemba ndi kujambula Precious Msosa

It's Today
31/05/2026

It's Today

Abulazala khumi ndi awiri adzodzedwa kukhala adikoni Kunali chimwemwe chodzadza tsaya ku seminale yaikulu ya St Peters m...
28/05/2026

Abulazala khumi ndi awiri adzodzedwa kukhala adikoni

Kunali chimwemwe chodzadza tsaya ku seminale yaikulu ya St Peters mu Dayosizi ya Zomba pamene abulazala khumi ndi awiri amadzodzedwa kukhala a dikoni masiku apitawa. A dikoniwa khumi ndi m’modzi anali achibadwiri ndipo awiri anali a chipani cha Capuchins Missionaries.

Mwambo wokomawu unatsogoleredwa ndi Episkopi wa Dayosizi ya Mzuzu, a Yohane Suzgo Nyirenda, omwe anatsogolera mwambo wa nsembe ya Misa.

Episkopiyu analangiza abulazalawa kuti akuyenera kukatumikira Mulungu modzipereka ndi kukhala okonda mpingo wao. Iwo analangiza achinyamatawa kuti akatumikire mpingo monga ngati atumwi aja ankachitira.

Ambuye Nyirenda anati: “Mukapita m’maparishi anu mukatsogolere mpingo monga sinodi ikutiphunzitsira. Osati inu nomwe mukakhale asungichuma, inu nomwe akwaya, inu nomwe owona za ku kitchini ayi. Musakaike ndalama za parishi ku ma akaunti anu. Kasankheni anthu oyendetsa ntchito zosiyanasiyana pa parishi monga momwe anachitira atumwi aja posankha adikoni aja kuti adzigwira tchito zina pomwe atumwi anali akutumikira Mulungu.”

Ambuye Nyirenda analimbikitsa abulazalawa kuti akumbukire ntchito zawo zimene aphunzitsidwa ku seminale. Iwo anawalimbikitsa adikoniwa kuti ali ndi ma udindo atatu amene apatsidwa.

“Muli ndi maudindo atatu awa: udindo wogwira tchito, udindo wotumikira akhristu mu mpingo, komanso kuchita ntchito zachifundo. Osaiwala kupemphera, kupempherera mpingo ndi anthu onse. Kumbukirani kuti izi mwaphunzitsidwa kale.”
Woimilira makolo, Bambo Felensio McTear Phiri, anati iwo ndi okondwa ngati makolo kuona ana awo akulowa udikoni.

A Phiri anati: “Inu ana athu amene mwadzodzedwa udikoni lero kumbukirani kuti maitanidwe ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. Choncho, muyenera kuisamalira ndi mtima wonse.
Mwavomera nokha ntchitoyi popanda wina kukukakamizani. Choncho kumbukirani kusunga malonjezo onse amene mwachita lero pamaso pampingo. Ife makolo tikulonjeza kuti tidzapitiriza kukupemphererani ndikukuthandizani maitanidwe anu kuti tchito yabwino imene Mulungu anaiyamba mwa inu, Iye yemweyo ayitsirize.”

M’modzi oimilira kalasi ya adikoni atsopanowa, amenenso ndi mkulu wa kalasi imeneyi, Dikoni Pater Wandale, achipani cha abadwiri kuchokera kwa Nkhwayi Parishi mu Arkidayosizi ya Blantyre, anati iwo anayamba ulendowu ku seminale yaing'ono ku Pius Xii. Iwo anati moyo wa kuseminale siwophweka komabe zimangofunika kudalira Mulungu ndinso kulimba mtima. Iwo anati kalasi yawo munali anyamata khumi limodzi mphambu zisanu ndi ziwiri koma lero amene alandira udikoni ndi anthu khumi ndi atatu.

“Ulendowu amatitsogolera ndi Mulungu chifukwa sumadziwa kuti ukafika kapena ayi. Ifeyo timakhaka ndi nthawi yokhala ndi mibindikiro yomwe imatithandiza kuti tisinkhesinkhe za moyo wathu pakati pa ife ndi Mulungu wathu kuti tidziwe chenicheni chimene ife tili pamaso pa Mulungu wathu.

“Mau anga ndi owalimbikitsa abale athu amene aimitsidwa kuti asataye mtima. Iwo akhale ndi chikhulupiriro pa Mulungu kuti Mulungu amakhala ndi njira zina pamoyo wako kuti udzamutumikire mwanjira ina – kapenanso kumutumikira Mulungu ngati wansembe, asataye mtima. Ngati maitanidwe, akuyenera kusamalira maitanidwe awo, asataye chikhulupiliro,” anatero dikoni Wandale.

Dikoni Mayamiko Zangalama, a chipani cha Capuchins, wochokera ku St Louis Montfort Parishi, mu Mangochi Dayosizi, anati iwo ndi wokondwa kuti Mulungu walora kuti afike apa ngakhale kuti mkati mwa ulendo wawo munali zinthu zina zowabwezeretsa m'mbuyo.

Iwo anati: “Moyo wathu umakhala wovuta ndi mmene dziko likuyendera masiku ano. Anzathu ena achinyamata amakhala akuyenda ndi dziko pamene ife timakhaka ngati tikuyenda zosemphana ndi m’mene dziko likuyendera.”

WOLEMBA: Monique Vyahnorah Marco, Mtolankhani Wapadera

Ukhondo wa msambo wa amayi ndi atsikana ndi wofunikaPamene dziko la Malawi komanso maiko ena pa dziko lonse lapansi lero...
28/05/2026

Ukhondo wa msambo wa amayi ndi atsikana ndi wofunika

Pamene dziko la Malawi komanso maiko ena pa dziko lonse lapansi lero akukumbukira ukhondo wa msambo, “World Menstrual Hygiene Day”, Unduna wa zaumoyo ndi ukhondo wati pali kusintha kwakukulu chiyambireni kukumbukira tsikuli mchaka cha 2013.

Malingana ndi uthenga womwe undunawu watulutsa ndipo wasayinidwa ndi mlembi wamkulu ku undunawu, Dr. Dan Namarika, zipangizo zogwiritsa ntchito nthawi ya msambo zayamba kupezeka mmalo ofunikira monga m’misika, masukulu ndi malo ena ambiri m’dziko muno.

“Tsikuli linakhazikitsidwa pofuna kupititsa patsogolo ntchito za ukhondo pa nthawi ya msambo ndikuonetsetsa kuti amayi ndi asungwana akukhala ndi mwayi wopeza zipangizo zogwiritsa ntchito pa nthawi ya msambo mosavuta, komanso kuthetsa miyambo ndi zikhulupiriro zomwe zimawaphinja pa nthawiyi,” gawo la uthengawu latero.

Ngakhale izi zili chomwechi, undunawu wati mavuto akadalipobe, makamaka kwa amayi ndi atsikana a m’madera a kumudzi chifukwa choti akukunamanabe ndi mavuto pakapezedwe ka zipangizo zogwiritsa ntchito pa nthawi ya msambo kaamba ka umphawi komanso chinsinsi ndi kusakambirana mwatchutchutchu nkhani za ukhondo okhudza msambo. Izi zimapangitsa kuti amayi ndi atsikana aziphinjika kumbali ya maphunziro ndi chitukuko.

Choncho undunawu wati pali kufunika kolimbikitsa ntchito zomanga zipinda zomwe amayi ndi atsikana angathe kumagwiritsa ntchito momasuka nthawi ya msambo – makamaka malo a ntchito, m’masukulu, m’misika, malo okwerera ma basi ndi malo ena onse amene anthu ambiri amakumaniranako.

Boma likupepha anthu komanso mabungwe kuti azionetsetsa kuti amayi ndi atsikana akupeza zipangizo zoyenera, kulimbikitsa komanso kuphunzitsa anthu zakufunika kopititsa patsogolo ntchito za msambo ndi ukhondo, kuthetsa m’nyozo komanso kusalana polimbikitsa mauthenga ndiinso kukambirana poyera, kulimbikitsa mgwirizanzo pakati pa mabungwe ndi opanga malonda potukula ntchito zokhudza ukhondo wa msambo.

Chaka chino tsikuli likukumbukiridwa pa mutu oti ‘Together for a period-friendly world’ kutanthauza kuti tonse tiyenera kuyendera limodzi poonetsetsa kuti aliyense wazindikira kuti msambo ndi chilengedwe komanso mbali imodzi ya moyo osati chinthu chamanyazi kwa amayi ndi atsikana.

Wolemba: Faith Kaisi MATHOTHO

28/05/2026
 Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo m'dziko muno lalengeza tsatanetsatane wa mpikisano wa chikho cha Airtel T...
27/05/2026



Bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo m'dziko muno lalengeza tsatanetsatane wa mpikisano wa chikho cha Airtel Top 8.

Umu ndimomwe matimu athambisirane kuyambira pa 13 Juni, 2026.


MANERELA+ urges Malawians to embrace HPV Vaccine The Malawi Network of Religious Leaders Living with or Personally Affec...
25/05/2026

MANERELA+ urges Malawians to embrace HPV Vaccine

The Malawi Network of Religious Leaders Living with or Personally Affected by HIV and AIDS (MANERELA+) has expressed concern over the low uptake of the Human Papillomavirus (HPV) vaccine among adolescent girls in Malawi.

In a statement released today and signed by acting executive director Canon Allie Mwachande, the organization has said myths and misinformation are discouraging parents and guardians from allowing their children to get vaccinated.

MANERELA+ described the HPV vaccine as a critical tool in the fight against cervical cancer, which remains one of the leading causes of death among women in Malawi.

The organization has therefore urged religious leaders, parents, government and civil society groups to work together in promoting awareness and encouraging communities to embrace the vaccine, especially in rural areas.

By Tony Kaziya Chikapa
media

In the picture is Mwachande

Alimbikitsa anthu kutsatira ndondomeko zopewera matenda a EbolaKutsatira kupezeka kwa matenda a Ebola m’dziko la Democra...
22/05/2026

Alimbikitsa anthu kutsatira ndondomeko zopewera matenda a Ebola

Kutsatira kupezeka kwa matenda a Ebola m’dziko la Democratic Republic of Congo (DRC) komanso Uganda, unduna wa zaumoyo ndi ukhondo m’dziko muno mogwirizana ndi mabungwe komanso ena wati wakhazikitsa ndondomeko zokonzekera ndi kupewera matendawa.

Ndondomekozi zakhazikitsidwa kutsatira kulengezedwa kwa matendawa ndi bungwe la zaumoyo pa dziko lonse la pansi (WHO), lomwe lati kubuka kwa matendawa m'maiko awiriwa ndi chinthu chodetsa nkhawa kwambiri pa umoyo wa anthu mu maiko osiyanasiyana.

Malingana ndi chikalata chomwe undunawu watulutsa ndipo chasayinidwa ndi mlembi ku unduna wa zaumoyo ndi ukhondo a Dr. Dan Namarika, matenda a Ebola ndi oopsa ndipo nthawi zambiri amapha. Undunawu wati matendawa amafalikira kudzera mu kukhudzana ndi magazi, madzi a m’thupi komanso zinthu zomwe zayipitsidwa ndi munthu kapena nyama yomwe ili ndi matendawa.

“Zizindikiro zodziwika bwino za matendawa ndi monga kutentha thupi mwadzidzidzi, kupweteka mutu ndi minofu, kufooka, kutopa, kusanza, kutsegula m’mimba komanso kutuluka magazi m’thupi popanda chifukwa chowoneka bwino," chatero chikalatacho.

Zina mwa ndondomeko zomwe undunawu waika pofuna kupewa matendawa ndi monga kuunika anthu (screening) malo okwerera ndenge komanso mu zipata zonse zolowera ndikutulukira m’dziko muno, kukhazikitsa malo osamalira odwala ozipatula ndikulandilira thandizo (isolation center).

Undunawu watinso kulimbikitsa ndondomeko zopewera komanso kuthana ndi matenda (infection and control center), komanso kukhala ndi mankhwala ofunikira, zida zodzitetezera (PPEs), zida zoyezera anthu komanso zida zoyezera matenda m’ma laboratory.

Choncho undunawu ukulimbikitsa anthu kuti akhale odekha, a tcheru komanso kupitiriza kutsatira njira zopewera matendawa monga kusamba m’manja pafupipafupi ndi sopo kapena kugwiritsa ntchito hand sanitizer, kupewa kukhudzana ndi anthu odwala ndinso za madzimadzi za m’thupi mwawo.

Undunawu wapempha anthu kumapereka lipoti ku chipatala mwachangu ngati awona munthu aliyense yemwe ali ndi zizindikiro zofanana ndi za Ebola komanso kugwirizana ndi akuluakulu a zaumoyo komanso kutsatira ndondomeko zowunika muzipata zolowera m’dziko muno (Points of Entry).

Kuonjezera apo undunawu watsimikizira anthu kuti pakadali pano palibe munthu aliyense yemwe wapezeka ndi matenda a Ebola m'dziko muno.

Wolemba: Faith kaisi MATHOTHO



Chithunzi ndi a Dr. Namarika

Address

Andiamo Loop Road
Lilongwe
NONE

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Montfort Media posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Montfort Media:

Share