02/01/2026
News
Purezidenti wa United States, a Donald Trump, achenjeza kuti dziko la US lingalowererepo ku Iran ngati boma la dzikolo lingaphe opanga demonstration. Izi zapangitsa akuluakulu a boma la Iran kunena kuti kulowererapo kulikonse kwa America kungadutse malire (crossing red line).
Muthenga womwe a Trump anayika pa malo ochezera pa intaneti Lachisanu, adanena kuti ngati akuluakulu a ku Iran angawombe ndi kupha ochita zioneselo, US ( idzabwera kudzawathandiza) Iye anawonjezera kuti, Takonzeka kwathunthu ndipo tili okonzeka kuchitapo kanthu, ngakhale sanalongosole bwinobwino tanthauzo lake.
Zionetsero ku Iran zalowa tsiku lachisanu ndi chimodzi, ndipo ndi zazikulu kwambiri kuyambira mu 2022, pamene imfa ya mtsikana wazaka 22, Mahsa Amini, yemwe anamwalira ali m’manja mwa apolisi, inayambitsa zionetsero m’dziko lonse. Zionetsero zapano zidayambitsidwa ndi kugwa koopsa kwa mtengo wa ndalama ya dzikolo. ( Kusika phamvu kwa ndalama ya Iran 🇮🇷)
Lamlungu, rial ya ku Iran inatsika kwambiri kufika pafupifupi 1.4 miliyoni motsutsana ndi dola ya ku US, zomwe zawonjezera mavuto azachuma omwe dzikolo linali kale nawo.
Nduna Yoona za Zakunja ya Iran, a Abbas Araghchi, adadzudzula mawu a Trump, kuwatcha osaganizira komanso owopsa, ndipo adanena kuti asilikali a dzikolo ali okonzeka. Iye adanenanso kuti zionetsero zambiri zakhala zachilungamo komanso zopanda chiwawa, koma adachenjeza kuti kuwononga katundu wa boma sikuloledwa.
Poganizira kuti Purezidenti Trump adagwiritsa ntchito National Guard mkati mwa malire a dziko la US, iye ayenera kumvetsa kuti kuwononga katundu wa boma ndi mlandu womwe sungalekereredwe, adatero Araghchi.
Malinga ndi malipoti, anthu osachepera asanu ndi awiri amwalira chifukwa cha zipolowezi. Makanema omwe akufalikira akuwonetsa asilikali achitetezo atanyamula mfuti za shotgun, ndipo kumamveka phokoso la mfuti kumbuyo.