Ndale zaku malawi

Ndale zaku malawi Our page promotes transparency, justice, & equality, fighting against, corruption nepotism, and tribalism.

As a true advocate 4 democracy & human rights, it opposes unlawful arrests, aiming to build a nation where integrity prevails & all voices matter

27/08/2025

Kodi zija achakwera ankati pakhale dongosolo loti ma driver azilipirilatu ndalama yopalamulila (azipalamuliratu) kuti akapalamula asamamangidwe, kaya wagunda munthu ndikupha azikhala kuti alibe mulandu, zili pati pano????

26/08/2025

Kunadzadza ku nkhotakota


26/08/2025

Mzimu waGadama..🎶

26/08/2025

Kodi cement uja akuti anatsitsa ntengo uja ukupezekela kuti chakwanuko?

 Mtsogoleri wa chipani cha DPP a Peter Mutharika wati misonkhano yoimaima yomwe akuchititsa kuyambira sabata yatha, yach...
26/08/2025


Mtsogoleri wa chipani cha DPP a Peter Mutharika wati misonkhano yoimaima yomwe akuchititsa kuyambira sabata yatha, yachititsa manyazi anthu omwe ati amawafunira zoyipa.

A Mutharika amalankhula izi pa Nkhotakota Boma pomwe ayima paulendo wawo wochoka ku Mzuzu komwe anakachititsa msonkhano.

Mwazina iwo ati chipani chawo chikalowa m'boma pa 16 September, adzalimbana ndi mavuto monga njala, kukonza misewu komanso nkhani za chuma zomwe ati zasokonekera mu ulamulito omwe ulipo pano.

A Mutharika akuyembekeza kuyimanso pa msika wa Kaphatenga m'boma la Salima.

(by Benson Kamonjola-Nkhotakota:08/26/2025)

 ZITUKUKOZI ZANGOYAMBA CHABE - MAI GRACE MUMBA.Mkazi wa Vimbuko Mumba, Grace Mumba, wati, a Mumba apanga zitukuko zochul...
26/08/2025


ZITUKUKOZI ZANGOYAMBA CHABE - MAI GRACE MUMBA.

Mkazi wa Vimbuko Mumba, Grace Mumba, wati, a Mumba apanga zitukuko zochuluka ku dera lapakati m’ boma la Mzimba. Iwo adalankhula izi pomwe amatsegulira ntchito yolambula misewu yomwe idaonongeka kuderali. Mwambo otsegulira ntchito yolambula misewuyi, udachitika pa sukulu yasekondale yoyendera ya Euthini, Lolemba pa 25 August 2015.

Mai Mumba ati, a Mumba chionetsereni chidwi chofuna kudzayimira ngati phungu kuderali, apanga zitukuko zambiri monga kugula galimoto zonyamula odwala, kupereka simenti okwana matumba 3000 ku sukulu zonse zomwe ziri m'derali, komanso kulambula misewu yonse yowonongeka m’derali. Iwo adapitiriza kunena kuti, patsikuli, adabwera ndi makontilakitala omwe agwire ntchito yokonza mijigo yomwe idaonongeka kuderali, yokwana 50, zomwe zitenge ndalama zokwana K296 million.

"Ine ngati mkazi wa Engineer Mumba ndikudziwa kuti zitukuko zomwe zayambikazi sizithera pomwepa, ndipo zangoyamba chabe" atero mai Grace Mumba. Iwo adapempha anthu a derali kuti azapange chisankho chanzeru pazisankho zikubwerazi.

Vitumbuko Mumba ndi nduna yoona za mafakitale ndi malonda, ndipo m’tsogoleri wa chipani cha MCP, Lazarus Chakwera adasankha a Mumba kukhala oyenda nawo (running mate) pa chisankho cha pa 16 September.

Pa nthawi yomwe mayi Mumba amalankhula idzi, amuna awo a Vitumbiko adali mu dziko la Mozambique komwe amagwira ntchito zina za boma.

Olemba: Lauryn Tembenu



 Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleri wa chipani cha Odya Zake Alibe Mlandu,  a Michael Usi wa...
24/08/2025


Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yemwenso ndi mtsogoleri wa chipani cha Odya Zake Alibe Mlandu, a Michael Usi wati a Malawi amayenera kupepesedwa ndi momwe atsogoleri ayendetsera dziko lino.

A Usi omwe amachititsa misonkhano yoimaima m'boma la Zomba alankhula izi madzulo ano kwa anthu okhala ku Chinamwali m'bomali.

Anthu ochuluka anakhamukira mmalo onse omwe a Usi anayima, monga Thondwe, Zaone, Mayaka komanso Jali.

(by Raphael Mlozoa-Zomba:08/24/2025)


24/08/2025

Uyu akudziwa chomwe akuchita

Akabambe alemba izi pa tsamba lawo la Facebook:Osalola kunamizidwa ndi anthu osachita nalo bodza manyanzi olo atakhala m...
23/08/2025

Akabambe alemba izi pa tsamba lawo la Facebook:

Osalola kunamizidwa ndi anthu osachita nalo bodza manyanzi olo atakhala m'busa, ngakhale malemba ananena momveka bwino kuti ambiri aneneri onyenga adzadzuka masiku otsiriza. MCP komanso Achakwera analonjeza amalawi 4 million jobs mu 2019. Ife tinalonjeza 1 million jobs, akanika kukwaniritsa 1 million jobs akuti manifesto yathu sinali realistic, nanga 4 million yawoyo apanga create how many jobs, koma pakati pa 4 million jobs and 1 million jobs who was not realistic?

Fertilizer anapanga promise K25,000.00 paliponse from Nsanje to Chitipa (universal subsidy program), kawerengeni manifesto yawo ya 2019 muzipeza. Actually, costing of universal subsidy from Nsanje to Chitipa was way expensive than making K4,495.00 to a few people. Lero, ngakhalenso anapanga adopt idea ya K4,495.00 which worked in the only first year Dr. Chilima was part of the cabinet analepheranso to sustain.

Nkhani iri apa ndi dyera. Anthuwa ankawona ngati Boma limangoziyendera ngati wamisala. Zoti someone has to control and work behind the scene sankadziwa, we trusted the economy on pastors, bambo m'busa, mwana m'busa, mpongozi naye m'busa, lero economy has been m'busalized, aliyense angolira mayo mayo, tonse ndife alazalo aumphawi amasikini, akafa nsiyanji.

Ndimanena mobwerezabwereza kuti ulendo uno osapereka Boma kwa anthu omwe alibe zoziyenereza kuyendetsa economy yathuyi. It's really sad that a pastor can stand and disown his own promises. Palibe anawakakamiza abusa to adopt UTM manifesto in 2020, anali ndi ufulu opitiliza ndi Hi 5. Zomwe akupanga apa zusonyeza kuti abusa aja ngosakhulupilika, don't trust him on anything, not even with a bottle of brandy.

Amalawi tiphunzire kumawona small things and taking lessons from there. Zimathandiza kupewa mavuto ambiri patsogolo. Kukakana akukana leroli, mukuona ngati 2030 sadzakananso? Ife tikuti let's vote for change, vote for Dr. Kabambe, the only leader who shall up and account for every promise he made. Mwanamizidwa nthawi yayitali palibe waona kusintha, Singapore sitinamuone, try us, change is here






23/08/2025

Koma bakili Muluzi tv idzapumako? Uthenga wa a Mumba uwu


23/08/2025

the DC Part 3

23/08/2025

Zomwe anayankhula a Bon Kalindo lelo ku m'mawaku (23/08/2025)


Address

Area 49 Lilongwe
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ndale zaku malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share