Tate Online

Tate Online Tate Online, we are dedicated to informing, educating, and entertaining the general public.

A Timothy Mtambo omwe ndiwachiwiri kwa mtsogoleri wachipani Cha AFORD ati ndi okhumudwa ndi mgwilizano omwe chipani cha ...
25/07/2025

A Timothy Mtambo omwe ndiwachiwiri kwa mtsogoleri wachipani Cha AFORD ati ndi okhumudwa ndi mgwilizano omwe chipani cha AFORD ndi DPP apanga.

Amtambo ayankhula izi lero pamsonkhano wa atolankhani omwe akuchititsa ku Ufulu Gardens mumzinda wa Lilongwe.

Mwazina Iwo anati sangaikire kumbuyo ganizoli chifukwa cha zofooka za chipani cha DPP monga kulephera kuyendetsa bwino dziko, kukondera mitundu ndi zina.

(Blessings Khumzana Mwale, 25/07/25)
Tate online

25/07/2025
Mtsogoleri wadziko lino Lazarus Chakwera yemwenso ndi mtsogoleri wachipani cha MCP lero akuyembekezeka kukhazikitsa ntch...
25/07/2025

Mtsogoleri wadziko lino Lazarus Chakwera yemwenso ndi mtsogoleri wachipani cha MCP lero akuyembekezeka kukhazikitsa ntchito yokopa anthu mchigawo chakumwera kuti adzamuvotele pazisankho chomwe chikudza miyezi yochepa ikudzayi.

Mlembi wankulu wachipanichi A Richard Chimwendo Banda ndi yemwe wanena izi, a Chakwera masiku apitawa adakhazikitsa ntchitoyi mchigawo chapakati komanso chigawo chakumpoto.

Mwazina a Banda anati chilichonse chili mchimake kuti mtsogoleri-yu akhazikitse ntchito yokopa wanthu-yi mchigawo chakummwera.

(Blessings Khunzana Mwale ,25/07/25)
Tate online

FinallyAPM mtsogoleri wa chipani cha DPP watulutsa running mate wake.  Justice Dr Jane ansah ndiomwe asakhidwa kukhala r...
25/07/2025

Finally
APM mtsogoleri wa chipani cha DPP watulutsa running mate wake. Justice Dr Jane ansah ndiomwe asakhidwa kukhala running mate

25/07/2025

Live from BICC

Mmawa uno chidwi cha a Malawi ambiri chalunjika ku BICC mumzinda wa Lilongwe komwe mtsogoleri wakale wadziko lino yemwen...
25/07/2025

Mmawa uno chidwi cha a Malawi ambiri chalunjika ku BICC mumzinda wa Lilongwe komwe mtsogoleri wakale wadziko lino yemwenso ndi mtsogoleri wachipani cha DPP Peter Muthalika akhale akupeleka kalata yake yodzapikisana nawo pazisankho ku bungwe la MEC.

Malingana ndima report omwe tawona Amutharika akuyenera kukapeleka makalatawa nthawi ya 10:00am

Mwazima President wakaleyu akhale akuwonetsanso yemwe atakhale wachiwiri wake pachisankho chomwe chikubwerachi.

(Blessings Khunzana Mwale, 25/07/25)
Tate online

Katswiri pankhani zaulimi Daniel Phiri wapempha boma kuti liyike chidwi chake pa ulimi wamthilira.Aphiri ayankhula izi l...
25/07/2025

Katswiri pankhani zaulimi Daniel Phiri wapempha boma kuti liyike chidwi chake pa ulimi wamthilira.

Aphiri ayankhula izi lero pomwe amayankhulana ndi Tate online,Mwazina Iwo ati dziko lino litha kukhala lodzidalira pachuma pokhapokha adindo atayika chidwi chawo paulimi wamthilira.

Koma Nduna yazaulimi aSam Kawale anati unduna wawo wayika njira zokhazikika zomwe zipititse ulimi wamthilira patsogolo.

(Eluby Mapemba)
Tate online

Mtsogoleri wa chipani cha National Democratic Party (NDP)  a Frank Tumpela Mwenefumbo omwe amayenera kukapeleka  zikalat...
25/07/2025

Mtsogoleri wa chipani cha National Democratic Party (NDP) a Frank Tumpela Mwenefumbo omwe amayenera kukapeleka zikalata zotsimikiza kuti ayima nawo pa zisakho zikudzazi pa 16th September 2025 ati sakapelekaso makalatawo kutengera nd zokambilana zomwe anali nazo dzulo ndi chipani cha Democratic progressive party (DPP)

Malingana ndi Dr. Mpokosa omwe ali wachiwiri wamtsogoleri kuchipani ati iwo ali pambuyo pa chipani cha DPP zomwe zikutsimika kuti apanga mgwirizano ndipo iwo pamodzi ndi chipani cha DPP akuyembekezeka kukapeleka makalata awo lero m'mawa uno.

Mmawu Ake Katswiri pankhani za ndale Chikondi Kamanga wati zipani zotsutsa boma zimayenera kubwera pamodzi ndikuchita mgwirizano ngati zikufuna kudzapambana koma Iwo anati mgwirizanowu sukhala ndi phindu kwenikweni kamba kakuti NDP ndichipani chaching'ono.

(Patricia Ketembo)
Tate online

* *Chipani cha AFORD chalengeza kuti chapanga mgwirizano ndi chipani cha DPP. Mtsogoleri wa chipanichi Enock Chihana wan...
24/07/2025

* *
Chipani cha AFORD chalengeza kuti chapanga mgwirizano ndi chipani cha DPP.

Mtsogoleri wa chipanichi Enock Chihana wanena izi pa msonkhano wa atolankhani ku Lilongwe komwe akuluakulu ena a DPP ali nawo.

Pa msonkhanowu pali mlembi wamkulu wa chipani cha DPP Peter Mukhito komanso a Sammeer Suleman, Ben Phiri mwa ena.

(Blessings Khunzana Mwale)
Tate online

Katswiri pankhani za ndale Chikondi Kamanga  wapempha zipani zotsutsa mdziko muno kuti zichotse dyera ndikupanga mgwiriz...
22/07/2025

Katswiri pankhani za ndale Chikondi Kamanga wapempha zipani zotsutsa mdziko muno kuti zichotse dyera ndikupanga mgwirizano ngati zikufuna kutenga boma pa 16 September.

Akamanga ayankhula izi lero kudzera pa phone yawo yammanja ndi Tate online pomwe amayankhapo pa mphekesera zomwe zikuveka kuti chipani Cha DPP chikufuna kuchita mgwirizano ndizipani zakumpoto.

Mwazina iwo anati ngati zipanizi sizikhala pansi ndikuvana chimodzi, asayembekezere kutenga boma miyezi yochepa ikudzayi.

(Blessings Khunzana Mwale 22/07/25)

22/07/2025

Pamene tangotsala ndi miyezi yochepa kuti dziko lino lichititse chisankho chosankha aphungu ,makhansala komaso president,andale ayamba kubwera poyera kulonjeza fundo zosiyasiyana Kwa Malawi.

Koma ndi udindo wathu ife ngati nzika kuvetsera ndikupanga chisankho choyenera.Tiyeni tilimbikitse mtendere Malawi wathu ndiyemweyu bas.Ife ngati a Tate online tikulonjezeni kuti tidzachita chilichonse kuti tikusangalatseni kukupatsani Uthenga oyenera komanso kuwonetsetsa kuti pasakhale kukondera kulikonse

Address

Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Tate Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share