10/08/2026
Mlembi wamkulu wa Boma, Justin Saidi, wati malemu Brian Banda anali ndi masomphenya ofuna kusintha Malawi Broadcasting Corporation (MBC) kukhala bungwe lotumikira anthu onse m’dziko muno.
Saidi wati mtsogoleri wa dziko komanso anthu ena ambiri akumva chisoni ndi imfa ya Banda, yemwe anali ndi masomphenya okweza kayendetsedwe ka MBC.
Iye wapempha ogwira ntchito onse ku MBC kuti apitirize masomphenya omwe Banda anali nawo pa kayendetsedwe ka bungweli.
Saidi wati analankhula ndi Banda sabata yatha ndipo wati imfa yake yamukhudza kwambiri.
“Ine ndayankhula naye last week yomweyi. Pakumva kuti wamwalira ndi zachisoni. Ambuye amulandire. Atichitire chisoni. A President akulira nanu ndipo sakutayani,” atero Saidi.
Mwambo waMaliro a malemu Brian Banda ukuchitikira ku M’banda Village, Chileka, Blantyre.
Wolemba: Chrispin Tsitsamanja