Umoyo FM Community Radio Station

Umoyo FM Community Radio Station Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Umoyo FM Community Radio Station, Radio Station, Saiti kadzuwa, Mangochi.

09/10/2025

Pofuna kuthana ndikufala kwa matenda a khasa ya khomo la chibelekelo Unduna wa zaumoyo wati uyamba ntchito yopeleka katemera wa HVP kwa atsikana amene ali ndi zaka 9 mpaka 18 kuti you atetezeke ku matenda.

Polankhula ndi wailesi ya Umoyo FM lachitatu , mmodzi mwa akuluakulu ochekera ku unduna wa zaumoyo Daniel Njoka Mwaza anat matendawa akakhazika thupi la mayi pamakhala povuta kuti achile choncho anapempha atsikana omwe Ali ndi zaka 9 mpaka 18 kuti azabaise katemerayu kuti apewe matendawa mpaka tsogolo.

Iye analimbikitsa amayi kuti azipita kuchipatala kukayezetsa khasa ya khomo la chibelekelo.

Malinga ndi unduna wa zaumoyo katemela wa HPV ayamba kupelekedwa kuyambila pa 27 mpaka pa 31 October 2025.

Wolemba _Brian Mkonde .

President Professor Arthur Peter Mutharika has asked the new cabinet ministers and government officials to work with com...
08/10/2025

President Professor Arthur Peter Mutharika has asked the new cabinet ministers and government officials to work with competence and integrity.

Mutharika said this on Thursday at the swearing-in ceremony at Sanjika Palace.

Minister of Foreign Affairs George Chaponda, Minister of State Alfred Gangata, Minister of Finance Joseph Mwanamveka, Chief Secretary Justin Saidi, and Deputy Chief Secretary Stuart Ligomeka took the oath of office.

Regarding the appointment of Gangata as Minister of State, Mutharika said the decision was made to empower young people to take a leading role in economic development.

Reported by Madalitso Chitseko.

.8Mhz

Tnm Super League5 October 2025 Week 19Full-time Mzuzu City Hammers 1 - Civil Service United  2 Blue Eagles  1 - Karonga ...
05/10/2025

Tnm Super League

5 October 2025

Week 19

Full-time

Mzuzu City Hammers 1 - Civil Service United 2

Blue Eagles 1 - Karonga United 0

Dedza Dyanamos 0 - Mighty Wanderers 1

FCB Nyasa Big Bullets 2 - Silver Strikers 1

Creck Sporting Club 0 - Chitipa United 0

Wolemba Iqra Adani

Mtsogoleri wadziko lino Pro Arthur Peter Munthalika watsimikizira a Malawi kuti zinthu zisintha. Malingana ndi Munthalik...
04/10/2025

Mtsogoleri wadziko lino Pro Arthur Peter Munthalika watsimikizira a Malawi kuti zinthu zisintha.

Malingana ndi Munthalika anthu adavotela kusintha chomcho aonetsetsa kuti zokhumba za a Malawi zikukwaniritsidwa.

Munthalika alankhula izi pa mau ake kutsatila kulumbilitsidwidwa pa mpando wa mtsogoleli wadziko.

Malingana ndi a Munthalika, DDP yabwerelanso m'boma ndi masomphenya atsopano otukula dziko la Malawi.

Iwo anati dziko linaonongeka ndi njala, kusowa kwa ndalama Zakunja ndi ntchito zomwe anati ndimavuto ochita kuwakonza.

Koma iwo ati chipani cha DPP ndichokonzeka kuthana ndi mavutowo.

Iwo alimbikitsa anthu kukhala olimbikira, ololelana komanso osasankhana ndipo anatsindika kutumikira a Malawi mosatengera mbali.

Mtsogoleli wa dzikoyu wachenjeza ena adyera amene amakhala ndi mtima odzikundikira kuononga chuma cha boma kuti alibe gao mu ulamulilo wao ponena kuti zimaononga dziko.

"Kukhala m'boma sizikutanthauza kudzilemeretsa koma kutumikira anthu, aliyense amene awononge chuma cha boma ndithana naye". Anatelo a Munthalika.

Munthalika anapempha anso a malonda ochoka maiko ena kuti abwere ndi kuchita ma business awo pakuti mtendere wabwerela.

Wolemba :Alice Emack.

.8Mhz

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino Dr Jane Ansah ati dziko la Malawi likukula mu democracy. Dr Ansa ati izi zikuteng...
04/10/2025

Wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko lino Dr Jane Ansah ati dziko la Malawi likukula mu democracy.

Dr Ansa ati izi zikutengera ndimomwe ulamulilo wasinthila molemekeza malamulo.

Iwo ati a Malawi aike chikhulupiliro pa Munthalika pamene akhale akulamulila ponena kuti ndi munthu amene amadziwa za mavuto a wanthu komanso ma ufulu a wanthu ndipo ndiodzipereka pochita zinthu.

Iye walankhula izi pamau ake atalumbilitsidwa kukhala Wachiwiri wa mtsogoleli wadziko lino.

Wolemba: Madalitso Chitseko.

.8Mhz

Umoyo FM ingathe kutsimikiza kuti dziko la Malawi lili ndi mtsogoleli wadziko watsopano.Izi ndi kutsatila kulumbira kwa ...
04/10/2025

Umoyo FM ingathe kutsimikiza kuti dziko la Malawi lili ndi mtsogoleli wadziko watsopano.

Izi ndi kutsatila kulumbira kwa prof Arthur Peter Mutharika pa mpandowu.

A Munthalika amene anaima limodzi ndi Dr Jane Ansah kudzera chipani cha DPP anapambana pa zisankho za pa 16 September 2025.

Dr Jane Ansah alumbilitsidwa ngati wachiwiri kwa Mtsogoleri wa dziko.

Wolemba: Alice Emack.

.8Mhz

04/10/2025

Mmodzi mwa akatswiri owona za mavuto a matenda a mu ubongo Aphias Njewa wapempha Makolo amene ali ndi ana omwe ali ndi vuto la mu ubongo kuti adzipita nawo kuchipatala kuti akalandile thandizo loyenela.

Njewa walankhula izi pambuyo pa tsiku lokumbukila ana omwe ali ndi vuto la mu ubongo limene limakumbukilidwa pa 6 October chaka chilichose padziko lonse lapansi.

Polankhula ndi wailesi ya Umoyo Fm lachisanu, Njewa anati ana omwe ali ndi vuto la mu ubongo ali ndi Ufulu wachibadwe monga munthu aliyense potsindika kunena kuti anawa akuyenera kumasamalidwa monga mwana amene alibe ulumali wa mu ubongo.

Iye anapempha anthu kuti azitengapo gawo akaona mwana amene ali ndi vuto la mu ubongo powalimbikitsa omusamalira kuti apite naye kuchipatala.

Njewa anapitilira ndikupempha Makolo omwe amasamalira ana amene ali ndi matendawa kuti asamawasale anawa ponena kuti kutero ndikuwaphera ufulu wawo wachibadwidwe

Chaka Chino mwambo okumbukila tsiku la ana omwe ali ndi vuto mu ubongo ukachitikira pa bwalo la Masewero la Mangochi Stadium.

Wolemba _ Madalitso Chitseko

.8Mhz

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) amene anasankhidwa kukhala mtsogoleli wa dziko pa zisankho ...
04/10/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party (DPP) amene anasankhidwa kukhala mtsogoleli wa dziko pa zisankho za pa 16 September 2025 afika pa mwambo wolumbira pa Kamuzu stadium mu mzinda wa Blantyre.

Prof Munthalika akhale akulumbilitsidwa pa mpando wa mtsogoleli wadziko ndipo Dr Jane Ansah ngati wachiwiri wa dziko.

Wolemba: Madalitso Chitseko.

.8Mhz

04/10/2025

Amene akuyembekezeka kukhala Wachiwiri wa mtsogoleli wadziko lino Dr Jane Ansah afika pa Kamuzu stadium.

Atangofika pamalopa panamveka mphokonso la lachimwemwe.

Wolemba: Madalitso Chitseko.

.8Mhz

04/10/2025

Mwambo wolumbiritsa mtsogoleli wadziko komanso wachiwiri wake uchitika lelo mu mzinda wa Blantyre.

Prof Arthur Peter Mutharika ndi Dr Jane Ansah amene anapambana pa zisankho za pa 16 September 2025 akhale akulumbila pa udindo wa mtsogoleli wadziko ndi wachiwiri.

Padakali pano ena mwa adindo amdziko muno monga mtsogoleli wakale wadziko Dr Joice Banda afika kale pamalopa.

Mwambowu Ukuchitika pa mutu woti "The Return of Great Proven Leadership".

Wolemba:Madalitso Chitseko.

.8Mhz

MANGOCHI DISTRICT FOOTBALL ASSOCIATIONBungwe loyang'anira za masewero a mpira  mchigawo cha ku M'mawa la Eastern Region ...
28/09/2025

MANGOCHI DISTRICT FOOTBALL ASSOCIATION

Bungwe loyang'anira za masewero a mpira mchigawo cha ku M'mawa la Eastern Region Football lachititsa chisankho m'boma la Mangochi lomwe asakha atsogoleri tsopano bomali.

A Muhammed Beyard Makiyi asakhidwanso ku kukhala mtsogoleri wa Mangochi District Football Association.

Mwambowu udachitikira pa bwalo la masewero la Mangochi stadium.

A Muhammed anathokoza anthu ochokera ma zone omwe adatenga nawo gawo pa chisankhochi komanso ndi kukhala ndi chikuhulupiliro mwa iwo, ndipo awonetsetsa kuti maso mphenya awo otukura mpira ku midzi akwaniritsidwe.

M'mawu Joyce Mkupa anati ndi okondwa kwambiri kuti asakhidwa ngati Executive yemwenso ndi Munthu wa nkazi yekhayo mu komitiyi ndipo wati awonetsetsa akugwira ntchito modzipeleka.

Ndipo ma udindiwa asakhidwa motere

1. Chairperson :
-Muhammad Beyard, palibe opikisana nawo

2 Vice Chairperson

- Maxwell Yasin, palibe opikisana nawo
-
3. General Secretary :
-Islam Rajabu, palibe opikisana nawo

4. Vice Secretary :
-Daudi chitsa, palibe opikisana nawo

5. Treasure:
Richard Cha Limbani, palibe opikisana

Vice Treasure :Billy Shaibu, palibe opikisana

6. Vice Treasure and 6 Executive members

Jack Diness 5 votes

Osman maulidi 3 Votes

Alexnder chikolowa 3 votes

Joyce Nkupa 5 votes

Ayatu Shukran 7 votes

Yusuf Bindura 6 votes

Wolemba Iqra Adani

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party DPP Prof Arthor Peter Munthalika ndiye wapambana pa zisankho za m...
25/09/2025

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive Party DPP Prof Arthor Peter Munthalika ndiye wapambana pa zisankho za mtsogoleli wadziko.

Olembetsa analipo 7,203,390 ndipo amene anaponya voti ndi okwana 5,502,982 kuimira 76.4 percent. Mavoti owonongeka analipo 155,225 ndipo abwino analipo 5,347,757.

1. Dr. Joyce Hilda BANDA of the People's Party (PP), 86,106 votes.

2. Thokozani Manyika BANDA, INDEPENDENT; 22,614 votes.

3. Akwame BANDAWE of Anyamata, Atsikana, Azimayi (AAA), 40,052 votes.

4. Dr. Lazarus McCarthy CHAKWERA of Malawi Congress Party (MCP), 1,765,170 votes.

5. Kamuzu CHIBAMBO of People's Transformation Party (PETRA) 17,274 votes.

6. Adil James CHILUNGO, INDEPENDENT, 8,462 votes.

7. Cosmas Felix CHIPOJOLA, INDEPENDENT, 8,638 votes.

8. Dr. Dalitso KABAMBE of UTM Party (UTM), 211,413 votes.

9. Atupele Austin MULUZI of the United Democratic Front (UDF), 102,744 votes.

10. Prof. Arthur Peter MUTHARIKA of the Democratic Progressive (DPP), 3,035,249 votes kuimira 56.8.

11. Phunziro MVULA, INDEPENDENT, 9,378 votes.

12. Frank Tumpale MWENIFUMBO, of the National Development Party (NDP), 5,354 votes.

13. Dr. Kondwani NANKHUMWA of the People's Development Party (PDP), 12,251 votes.

14. Jordan SAUTI of the Patriotic Citizens Party (P*P) 2,196 votes.

15. Smart Mulumbe Swira, Indipendent, 1,848 votes

16. Milward TOBIAS, INDEPENDENT, 2,086 votes

17. Dr. Michael Bizwick USI of the Odya Zake Alibe Mlandu (Odya Zake), 16,922 votes

Wolemba: Iqra Adani.

.8Mhz.

Address

Saiti Kadzuwa
Mangochi
P.OBOX363

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

+265882570759

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Umoyo FM Community Radio Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Umoyo FM Community Radio Station:

Share

Category