Umoyo FM Community Radio Station

Umoyo FM Community Radio Station Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Umoyo FM Community Radio Station, Radio Station, Saiti kadzuwa, Mangochi.

 Kampani ya H.Adam Wholesalers yati ngakhale nyengo yazachuma sili bwino iwo ayetsetsabe kupitilidza kuthandidza masewer...
07/06/2026



Kampani ya H.Adam Wholesalers yati ngakhale nyengo yazachuma sili bwino iwo ayetsetsabe kupitilidza kuthandidza masewero a mpira wamiyendo ku chigawo chakummawa,Mkulu owona za Malonda ku kampani yi Oster Banda ndi amene wanena izi loweruka pa 6 June 2026 pa bwalo la Vision ku Ntaja m'boma la Machinga pa masewero otsekulira ligi ya Durata Batteries Eastern Region Football Association.

"Tikufuna kuti ikhale ligi yopambana ngati pangakhale kusamvetsetsana,mbali zonse zikhalirane pansi kuti mpira upindure" Anatero Banda.

Mawu ake wapampando wa Bungwe la Eastern Region Football Association Issah Brahim anati zotsamwitsa zonse zomwe anali nazo chaka chatha azikonza ndipo chaka chino ligiyi ikhale yapamwamba. Brahim anathokonzanso kampani ya H.Adam kamba kobweranso chaka chino kuzathandiza ligi yi zomwe zawapatsa chilimbikitso.

Daud ntanthiko yemwe anaimilira Bungwe la FAM anati,ngati bungwe iwo ndi othokoza Kampani ya H.Adam ndipo wapempha Kampaniyi kuti ithandizenso ligi yachiwiri ya mchigawochi.

Masewero omwe anali pa tsikuli anakomera anyamata a Ntaja Rangers omwe anagonjetsa Nselema United ndi zigoli zitatu kwa chimodzi.

Kampani ya H.Adam Wholesalers ikuthandiza ligi ya mchigawo chakumawa ndi ndalama zokwana 36 million kwacha .

Wolemba: Williams Chande (07/06/2026)

.8Mhz

TIMVE MAGANIZO ANU Pamene Unduna owona za ubale wa dziko lino ndi maiko ena wati boma liyamba posachedwapa ntchito yotha...
06/06/2026

TIMVE MAGANIZO ANU

Pamene Unduna owona za ubale wa dziko lino ndi maiko ena wati boma liyamba posachedwapa ntchito yothandiza Amalawi omwe akufuna kubwerera mdziko muno kuchoka mdziko la South Africa . inu maganizo anu ndi oti chani pankhaniyi ?

Bungwe lomwe ndi la  za umoyo la Non-Communicable Diseases Alliance Malawi (NCD Alliance Malawi) lapempha boma ndi adind...
31/05/2026

Bungwe lomwe ndi la za umoyo la Non-Communicable Diseases Alliance Malawi (NCD Alliance Malawi) lapempha boma ndi adindo kuti akhanzikitse komanso kulimbikitsa ndondomeko zothana ndi kusuta fodya mdziko muno.

Bungweli lati matenda ambili pano akudza chifukwa cha fodya chomcho pakuyenera kukhanzikitsa njila zabwino zowonetsetsa kuti miyoyo ya anthu ikutetezeka. NCA Alliance Malawi yanenetsa kuti matenda monga cancer, kuthamangitsa kwa magazi, kupweteka kwa mtima, kuwonongeka kwa mapapo, kufa ziwalo, komaso sugar amayamba kamba ka kusuta fodya.

Bungweli kudzela mwa wapampando wake Maud Mwakasungula lalankhula izi mu mkalata yomwe yatulutsidwa kutsatila pomwe dziko limakukumbukila tsiku lolimbikitsa kuthana ndi kugwiritsa ntchito fodya la "World No To***co Day" lomwe ndi pa 31 May chaka chilichose.

Kalatayi yati kafukufuku wa bungwe la zaumoyo lapadziko lonse la World Health Organization waonetsa kuti anthu pafupifupi 8 Million akumwalila chaka ndi chaka kamba ka matenda amene amayamba ndi kusuta fodya. Iwo atinso kuno ku Malawi ndalama zochuluka pafupifupi K55. 2 Billion kwacha zikuonongeka chifukwa cha matendawa.

Pa izi a Maud Mwakasungula ati ngati dziko silikuyenera kungokhala koma kuchitapo kanthu potsatila njila zothana ndi kusuta fodya. Zina Mwa njila zomwe zatchulidwa ndi monga kusalola kusuta mmalo osiyanasiyana, kuletsa kunenelela malonda a fodya, kupititsa patsogolo uthenga wa kuipa kosuta komanso kuteteza achichepele ku mchitidwe osuta fodya.

Kalatayi yati ma kampani ambili opanga fodya ayamba kuchita ndi kuika zinthu zambili zokometsa kuti kusuta kudzioneka ngati kwa bwino zomwe zikukopa achinyamata ambili. Chomcho a Maud Mwakasungula amema achinyamata kuti asakopeke ndi zimenezi pakuti kusuta kuli ndi zotsatila zoipa pamoyo wa munthu. Padakali pano NCD Alliance Malawi yati ili tchelu kuteteza miyoyo ya mibado yamtsogolo.

Mwambo wa chaka chino wa World No To***co Day ukukumbulilidwa pa mutu oti "Unmask The Appeal : Countering Ni****ne and To***co Addiction ".

.6MHFM

Mangochi Youth Football Committee  pa 29 May 2026 inali ndi  mwambo opereka mphoto ku ma timu komanso osewera omwe achit...
29/05/2026

Mangochi Youth Football Committee pa 29 May 2026 inali ndi mwambo opereka mphoto ku ma timu komanso osewera omwe achita bwino mu wa ana achitsozera osapyola dzaka 14 komanso 16 ochokera m'bomali.

Mwambowu udachitikira pa Mangochi Stadium ndipo Mtsogoleri wa Mangochi Youth Football Committee Alfred Kabichi anati ndi okondwa kuti matimu omwe adachita bwino mu chikho cha Under 14 komanso Under 16 alandira mphoto zawo.

Kabichi anatinso ali ndi chikhulupiriro kuti chaka cha mpira cha 2026 kufika 2027 chikhale chapamwamba komanso adathokoza Bungwe la Eastern Region Youth Football Committee pobweretsa mphotozi mu nthawi yake.

Ndipo Mtsogoleri wa Bungwe la ERYFA Charles Dougras adati ngati bungwe likuyembezera kuti matimu omwe akutumikire mu chikho cha ana achisodzera osapyola dzaka 14,16 komanso 19 alimbikira mu ma Ligi awo zomwe akukhulupilira kuti zithandizire kubweretsa luso la osewerawo pa mbalambanda.

Dougras adaulura kuti ngati bungwe likuchita zothekera kuti timu yomwe idzachite bwino mu Ligi ya Under14 ikubwerayi nawonso azalandire chikho.

Muhammad Jackson osewera wa timu Muft Abbas Under 16 yemwenso analandira photo ya ndalama yokwana K20,000 anati ndi osangalala kuti walandira photo yi zomwe zamulimbikitsa kuti azalimbikire mu League ikubwerayi.

Wolemba Iqra Adani - Mangochi

24/05/2026

Utumiki otchedwa Disciple The Nation pa project ya "True Love Waits" omwe umakhudza achinyamata wati vuto lolowa m'banja anthu adakali achichepele likusokoneza chitukuko cha dziko.

Mmodzi wa nthumwi za gululi a Kephasi Zimba Mfune wati achinyamata ambili akumayamba mchitidwe ogonana anakali achichepele zomwe zikukolezela mchitidwe olowa m'banja asadakhwime. Izi akuti zikumapangitsa kuti asatenge gao lalikulu pa chitukuko cha dziko pakuti ambili akumakanika kumaliza maphunzilo awo komanso akumatenga matenda opatsilana pogonana.

Mai busa Mfune omwe amalankhula izi ku Namwela m'boma la Mangochi pa mpingo wa Namwela Zambezi Evangelical Church pansi pa Mitsidi Synod ati mchifukwa chake gulu lao anayambitsa ndondomeko ya True Love Waits pofuna kuphunzitsa achinyamata moyo odzisunga. Iwo ati achinyamata akuyenera kukhanzikika pa chiphunzitso cha chikhristu chomwe chimalimbikitsa kudikila osagonana mpaka atalowa m'banja.

Utumikiwu unali ndi maphunzilo amasiku atatu kwa achinyamata pa mpingo wa Namwela Z. E. C . Maphunzilowa anayamba lachisanu pa 22 May ndipo atha la Mulungu pa 24 May 2026. Mayi busa Mfune anati ndi okhutila ndi mmene maphunzilo ayendela.

Mmodzi mwa achinyamata amene anatenga mbali pa zochitikazi Grace Sinos anayamika mpingo wa Zambezi Evangelical Church polola kuti alandire maphunzilowa. Grace Sinos anati moyo wake wasinthika kutsatila maphunzilowa amene akhudza moyo wa wachikhalidwe ndi uzimu.

Mmau awo abusa apampingowo Reverend Synoden Dillah anayamika utumiki wa Descipling The Nation pa project ya True Love Waits kamba kokumbukila mpingo wa Namwela ndi maphunzilowa.

Utumiki wa Descipling the Nation pa ndondomeko ya True love Waits unayambika mchaka cha 2015 ndipo padakali pano ukufikila mipingo yonse ya Zambezi Evangelical Church mmaiko a Malawi ndi Mozambique.

Wolemba : Alice Emack

.6MHFM

NCD ALLIANCE MALAWI COMMENDS GOVERNMENT FOR CONTINUED EFFORTS IN COMBATING NON-COMMUNICABLE DISEASES, CALLS FOR GREATER ...
17/05/2026

NCD ALLIANCE MALAWI COMMENDS GOVERNMENT FOR CONTINUED EFFORTS IN COMBATING NON-COMMUNICABLE DISEASES, CALLS FOR GREATER STAKEHOLDER SUPPORT

Reported by Alice Emack.

The Non-Communicable Diseases Alliance Malawi (NCD Alliance Malawi) has commended the government for continuing with the recruitment of Health Surveillance Assistants (HSAs), describing the move as critical in strengthening healthcare delivery at the community level.

In a statement released today, the organisation’s Chairperson, Maud Mwakasungula, said HSAs play a vital role in reaching people in remote areas who are affected by various diseases, while also supporting disease prevention efforts. Mwakasungula said the continued recruitment of HSAs will greatly benefit the country’s health sector by improving access to quality healthcare services.

The remarks come as Malawi joins the rest of the world in commemorating World Hypertension Day, observed annually on May 17 to raise awareness about the signs, prevention and management of high blood pressure.

According to the organisation, hypertension remains one of the leading causes of death, highlighting the need for urgent and collective action in addressing the disease. NCD Alliance Malawi noted that the deployment of HSAs is one of the most effective strategies in combating non-communicable diseases because they are able to reach many communities across the country.

However, NCD Alliance Malawi says government alone cannot effectively manage the fight against hypertension and other non-communicable diseases without support from various stakeholders. Mwakasungula said this is why members of NCD Alliance Malawi are actively involved in awareness campaigns and community-based blood pressure screening programmes in different parts of the country. She further urged leaders and stakeholders to take an active role in supporting efforts aimed at preventing and controlling hypertension.

“NCD Alliance Malawi is taking action through its members, namely Moyowathu Health Care Services, Kidney Foundation of Malawi and Stroke Foundation of Malawi, which are actively conducting targeted hypertension screening exercises in selected areas of the country. Together with other key stakeholders, we are working to roll out blood pressure checks to reach communities in need,” reads part of the statement.

NCD Alliance Malawi has since pledged to continue implementing its interventions, saying the programmes are already producing positive results.

The organisation has also encouraged Malawians to regularly monitor their blood pressure in order to detect and manage hypertension early.

This year, World Hypertension Day is being commemorated under the theme: “Controlling Hypertension Together.”

.8Mhz

 Bungwe loyendetsa masewero ampira wamiyendo mchigawo chakummawa la Eastern Region Football Association ERFA lalengedza ...
13/05/2026



Bungwe loyendetsa masewero ampira wamiyendo mchigawo chakummawa la Eastern Region Football Association ERFA lalengedza kuti Chaka Cha mpira cha 2026 mpaka 2027 mu Premier Ligi chikuyamba pa 31 May 2026.

Malinga ndi Mlembi wamkulu wa bungweli Elia Canton Nyirongo walengedza izi kudzera mu kalata imene yatulusidwa lero.

Ma Timu a Ntaja Rangers komanso Nselema United ndi omwe akuzatsekulira Chaka Cha mpirachi pomwe azakhale akukumana pa bwalo la zamasewero la Vision ku Ntaja m'boma la Machinga.

Kampani ya H Adam ndi imene imathandiza Ligi ya mchigawo chi.

Wolemba : Williams Chande -13/05/2026

.8Mhz

Undule Mwakasungula has opposed calls to revoke licences of business operators resisting the implementation of the Elect...
12/05/2026

Undule Mwakasungula has opposed calls to revoke licences of business operators resisting the implementation of the Electronic Invoicing System (EIS), describing dialogue as the best way to address the ongoing dispute.

Speaking on the matter, Mwakasungula who is one of the advocates for human rights and good governance in Malawi, said government and the Malawi Revenue Authority should engage traders in constructive discussions to build consensus over the use of the modern tax system. He emphasized the need for authorities to clearly communicate the benefits of the EIS to the business community.

He however appealed to traders to recognise the importance of paying taxes, saying revenue collected by government contributes to national development and also supports the growth of businesses and the wider economy.

According to Mwakasungula, tax compliance remains a shared responsibility for all citizens and business operators. At the same time, Mwakasungula criticized some civil society organisations advocating for the revocation of licences from traders refusing to adopt the system, arguing that such pressure is not peaceful.

Mwakasungula’s remarks come amid plans by certain groups to stage demonstrations aimed at forcing the government to take action against traders who continue to reject the Electronic Invoicing System, a digital tax platform introduced to improve revenue collection and compliance.

Reported by Alice Emack

.8Mhz

Bungwe la Malawi Revenue Authority  lachititsa maphunziro apadera kwa atolankhani omwe amalemba nkhani zokhudza malonda ...
12/05/2026

Bungwe la Malawi Revenue Authority lachititsa maphunziro apadera kwa atolankhani omwe amalemba nkhani zokhudza malonda mdziko muno omwe akuchitikira ku Nkopola Lodge m'boma la Mangochi.

Polankhula Lolemba pa 11 May 2026, mkulu wa bungweli, Felix Tambulasi, adati cholinga cha maphunzirowa ndi kupereka ukadaulo kwa atolankhani omwe amalemba nkhani za malonda m'dziko muno kuti athe kupereka malipoti moyenera komanso kulimbikitsa kutsata njira zotolera misonkho zomwe boma linakhazikitsa komanso kuti anthu adziwe kufunika kopereka misonkho pofuna kutukula dziko lino.

A Tambulasi adatsindika kuti ngakhale atolankhani safunikira kukhala akatswiri azamisonkho, koma ali ndi udindo waukulu powonetsetsa kuti akulemba molondola kuti asasocheretse anthu ochita malonda komanso ena omwe amapeleka misonkho. Iye adatsindika kuti ndiudindo waukulu wa atolankhani polimbikitsa chikhulupiriro komanso kuthandiza boma kuti likwanitse kupeza ndalama zokwana K6.2 trilioni pokutha kwa ndondomeko ya chaka ya boma.

Bungweli lidakhazikitsa njira ya tsopano yotolera misonkho yotchedwa Electronic Invoicing System (EIS) pa chingerezi pa 1 May, 2026 ngati njira ya imodzi ya makono pofuna kupititsa patsogolo ntchito yotolera misonkho m'dziko muno.

"Ndikukutsimikizirani kuti IES sikuti ndi msonkho wa tsopano koma ndi njira chabe ya tsopano yomwe yakhazikitsidwa kuti tizilondoloza bwinobwino za msonkho wa VAT omwe amalawi amapereka", adatero Tambulasi.

Mkulu woona ntchito ku bungwe la atolankhani omwe amalemba nkhani za malonda m'dziko muno, Arthur Chokhotho anayamikira maphunzirowo, ponena kuti awathandiza atolankhani kumvetsa bwino nkhani zokhudza misonkho monga njira yatsopanoyi ya EIS kuti apereke malipoti moyenera kwa anthu m'dziko muno.

Wolemba : Amos Burton.

BOMA LIKAMBILANE NDI A MALONDAMtsogoleli wa chipani cha Umodzi a Thomas Kaumba watsutsana ndi ganizo lolanda ziphaso za ...
09/05/2026

BOMA LIKAMBILANE NDI A MALONDA

Mtsogoleli wa chipani cha Umodzi a Thomas Kaumba watsutsana ndi ganizo lolanda ziphaso za anthu amalonda omwe akutseka ma shop awo sinjila yabwino yothana ndikunsamvana komwe kulipo pa nkhani ya EIS.

Polankhula a Kaumba aloza chala boma kuti linalakwitsa kungoyamba ndondomekoyi opanda kuwaphunzitsa a malonda mokwanira bwino. Iwo akuti kusanvanaku ndi chizindikilo chachikulu kuti boma silinaphunzitse anthuwa mokwanira.

Pa ichi iwo akuti sibwino kupupuluma kuwalanda ziphaso zao Koma kuwaitana ndikuwauza bwino za ndondomeko ya EIS.

Malingana ndi Chipani cha Umodzi, ndondomeko ya EIS ndi ya bwino chifukwa ithandiza kudziwa amene asakupeleka misonkho Koma anena kuti chomwe chavuta ndi kuphunzitsa anthu za ubwino wa ndondomekoyi.

Iwo alozanso chala boma poika misonkho ya mbili m'dziko muno zomwe akuti zikupangitsanso anthu kusasiyanitsa njilayi ndi misonkho.

Mau a Kathumba akudza pamene a mabungwe ena omwe si aboma apempha boma kuti lilande ziphaso kwa amalonda omwe akunyozela kugwiritsa ntchito makina amakonowa pa misonkho.

Wolemba :Alice Emack

.8Mhz

Address

Saiti Kadzuwa
Mangochi
P.OBOX363

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

+265882570759

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Umoyo FM Community Radio Station posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Umoyo FM Community Radio Station:

Share

Category