21/07/2025
*ZAUMOYO*π¨βπ»βοΈπ²πΌβοΈ
Akuluakulu pachipatala cha Mponela ku Dowa, ati odwala pachipatalachi akudya kamodzi patsiku, kaamba ka kuvuta kwa zinthu.
Namwino wa pachipatalachi, a Felix Mtuwana, wati anthu omwe ali ndi kuthekera awathandize ndi zofunikira kuti odwala adzikwanitsa kudya katatu ngati momwe zimayenera kukhalira nthawi zonse.
Iwo apereka pempholi pomwe nzika ya m'boma la Dowa, yomwe pano imakhala m'dziko la United States of America, a Phillipina Phiri Msiska, anapereka katundu osiyana siyana mzipinda zonse za odwala pachipatalachi, za ndalama zoposa K1 million.
A Susan Phiri Kondowe, womwe anakapereka katunduyo m'malo mwa nzikayi, anati thandizolo lomwe mkuphatikizapo shuga, sopo komanso m'chere, linadza pozindikira kuti odwala ena amasowekera zambiri pomwe ali m'chipatala, kaamba ka umphawi.
M'modzi mwa odwala pachipatalachi, a a Chrissy Chabwera, am'dera la mfumu yayikulu Dzoole m'bomali, wati akuvutika kuti apeze zofunika pa moyo wawo watsiku ndi tsiku, choncho lathindizolo lichepetsa ena mwa mavutowo.
*π« #(1) ZBS ZIKACHITIKA MUMVERA PANO [email protected]*
π¨βπ»βοΈπ²πΌβοΈπ‘π»ππ²πΌπ²πΌπ²πΌπ²πΌπ²πΌπ²πΌπ²πΌ