Moses Chikolosa

Moses Chikolosa Father, Husband, Gospel Music Minister, Evangelist, Counsellor and a brother in Christ.

08/11/2025

Mulungu ndi Wakale-Kale ndipo sakusintha.
Zinthu zambiri padziko zasinthidwa chifukwa cha kusintha kwa nthawi koma Mulungu ali yemweyo.

08/11/2025

Personally ndatchulidwapo maina m'moyo:

1. Ndatchulidwapo kuti opemphapempha.

2. Ndatchulidwapo kuti opanda tsogolo.

3. Ndanenedwapo kuti opanda phindu-

4. Ndanenedwapo kuti Osaphunzira.

Mulungu ndiokhulupilika kuposa maganizo athu.
Lero ndine Mboni yaukulu wa Mulungu. Wasintha mbiri Yanga Mulungu.
Wandichotsa kosakumbukiridwa, ndipo wandisiya pena.

08/11/2025

Kangamirani kwa Yesu ekha, Munthu amalephera.

Munthu amasinthasintha ndipo amakhumudwitsa.

07/11/2025

Ezekiel 16:14Ndi mbiri yako inabuka mwa amitundu chifukwa cha kukongola kwako; pakuti ndiko kwangwiro, mwa ulemerero wanga ndinauika pa iwe, ati Ambuye Yehova.
15 Koma unatama kukongola kwako, ndi kuchita zachigololo potama mbiri yako, ndi kutsanulira zigololo zako pa munthu aliyense wopitapo; unali wake.

Mu chapter ichi Mulungu akupitiliza kudandaula ndi khalidwe lomwe Ayuda amachita. Ndipo akunena mmene Mulunguyo anawatolera kotaika ndikuwakongoletsa komanso kuwalemeretsa ndipo mbiri yawo inapita patali. Koma pakupita panthawi Ayuda anaiwala Mulungu amene adawakongoletsa ndikuwalemeletsa ndipo adayamba kugwilitsa ntchito mdalitso omwe adapatsidwa ndi Mulungu polambira mafano. Izi zidadzutsa mkwiyo wa Mulungu pa iwo.

Apatu tikuphunzirapo pofananitsa ndimomwe ifenso timachitira lero lino. Nthawi zambiri timamutaya Mulungu chifukwa cha mdalitso omwe Mulunguyo watipatsa. Tili mmavuto tinali kumukakamira, kukhala okhulupilika pamanso pake koma Mulungu anangotidalitsa basi tapeza milungu ina tayamba kuilambira. Kumaitumikira ndizomwe Mulungu watidalitsa nazo. Banja kusokonekera chifukwa chamdalitso, kusiya kupita ku church kapena kuutumiki chifukwa cha mdalitso, kusiya kulemekeza ena chifukwa Mulungu watikweza, kusiya kuyanjana ndi anthu ena chifukwa chamdalitso. Ayi abale, tiyeni titumikire Mulungu munyengo zonse.

Ambuye akudalitseni pamene mukulingalira zobweleranso kwa Mulungu kukamutumikira iye yekha ndi mdalitso womwe wakupatsani.

Amen!

Dzikumbutseni kuti Mulungu ndiwabwino.Dzikumbutseni kuti Mulungu alipafupi ndi moyo wanu.Dzikumbutseni kuti Mulungu amas...
07/11/2025

Dzikumbutseni kuti Mulungu ndiwabwino.

Dzikumbutseni kuti Mulungu alipafupi ndi moyo wanu.

Dzikumbutseni kuti Mulungu amasalama za inu.

Dzikumbutseni kuti Mulungu alinawo malingaliro abwino pa inu.

Dzikumbutseni kuti Mulungu akudziwa mawa lanu.

Dzikumbutseni kuti Mulungu amakukondani.

07/11/2025

Pazimene mukudziwa ngati anthu kuti mukudutsa muzotsamwitsa.

Pazonse zimene mukudziwa kuti ndi zosautsa.

Pazimene mukudziwa kuti ndi zosowetsa mtendere pamoyo wanu, dziwani kuti Mulungu akudziwa zochuluka kuposa zimene mukudziwa.

Nkhawa, mafunso, kaya kupanika konse, mutulireni Mulungu wamoyo amene amaona zonse.

06/11/2025

Mu nyengo zako zovutazo, Yesu amasendera chifupi nawe kuti usendere chifupi naye!

Yesu ndi bwenzi la Ofooka.
Bwenzi la Osowa.
Bwenzi la Othodwa.
Bwenzi la okhala kakasi.

Yesu yemweyo, tsiku lomwelo, maliro omwewo a Lazarus koma anapereka mayankho osiyana kwa Maria komanso Marita.

Chitani kena kake kuti mpaka Yesu Khristu avutidwe mumtima.
Yohane 11

06/11/2025

2 Mafumu 6 and Chapter 7

Imodzi mwa nkhani imene imandipatsa chidwi ndi imene imapezeka pa 2 Mafumu 6 mpaka Chapter 7. Nthawiyi anthu amasowa chakudya ndipo zinafika pakuti anthu amapha ana awo cholinga asafe ndi njala. Mfumu itaona zoterezi inalingalira zakupha munthu wa Mulungu Elisha.

Elisha atamva sanagwedezeke koma anapeleka uneneli kuti, mu tsiku lotsatira anthu adzadya ndipo vuto lonse lidzatha. Atayankhula izi, wamkulu wina wankhondo atamva anakaikira ndipo anankhula kuti nzosatheka kutero.

Elisha anamuuza munthu amene anakaikira uneneli wake kuti ndi maso ake adzaona koma ndi pakamwa pake sadzadya.

Mulungu anagwiritsa ntchito mapazi a anthu akhate anayi kumveka ngati mkokomo wa asilikali ankhondo ndipo zakudya zochuluka zinapezekadi monga mwa uneneli.

Ndimalimbikitsika kuti, Mulungu amene anayankhula mau ochuluka okhudzana ndi moyo wathu ndi okhulupilika kukwaniritsa mau ake.
Mulungu akhoza kugwiritsa ntchito chilichonse nthawi ina iliyonse.

Mulungu ali ndi njira zosazoloweleka. Miyoyo yathu ikuyenera imudalire Mulungu nthawi zonse.

God is able to do so much more than we could ever ask. He is able to do so very much more than we could even think. He does such great things because he works so powerfully in us.
Ephesians 3:20

05/11/2025

Uthenga Wachiponyeponye!

Ulaliki wa pamaliro ku Misewu 4 ku Phalombe.

05/11/2025

Ndipemphero langa kuti Mulungu akuimilireni.
Aimilire pamene dzina lanu litchulidwa (pabwalo la onyoza komanso pamene ena akhoza kudalitsa moyo wanu).

Mulungu aimilire ndipo choipa chisakugwereni.

Aimilire Mulungu pa moyo wanu ndipo malire anu akuzidwe.

04/11/2025

Pano pali Mnyamata!

Pano pali Mzimayi!

Pano pali M'bambo!

Muli opezeka kugwiritsidwa ntchito ndi Mulungu?

John 6

04/11/2025

Pena ukaona zimene zikuchitika pamoyo wako, umaona ngati Mulungu kulibe kapena watalikirana nawe koma ayi ndithu, God is in the neighborhood!

Mulungu alipafupi Nawe.

Muzonse zimene mudutsemo lero, limbikitsikani kuti Mulungu alinanu chifupi.

Address

Box 8
Mwanza
314100

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Moses Chikolosa posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Moses Chikolosa:

Share