Moses Chikolosa

Moses Chikolosa Father, Husband, Gospel Music Minister, Evangelist, Counsellor and a brother in Christ.

23/08/2025

Ena anapita kunyumba kwa Rahab koma sanapitireko ma service a prostitution (Uhule)!

Ndi nthawi yochuluka bwanji imene tasemphanitsa zimene Mulungu amafuna ndi anthu amene takumana nawo pokwaniritsa chokhumba chathu?

Joshua 2

23/08/2025

Ambuye, Muchite Ntchito Yanu Mwa Ine!

Osamachepetsa Chiyambi Chanu.Ndimachitenga kukhala chisomo kuti ndinapezeka nawo pa Nsonkhano waukulu wa Fountain of Vic...
22/08/2025

Osamachepetsa Chiyambi Chanu.

Ndimachitenga kukhala chisomo kuti ndinapezeka nawo pa Nsonkhano waukulu wa Fountain of Victory ku Balaka mu Chaka Cha 2016 pamene ndi mtima wanga onse ndimkamuthandizira Minister Stevie Wazisomo Muliya .

Anaitanidwa kukhala mlendo wamkulu wa maimbidwe ndipo ndinachitenga chamwayi kumuthandizira (Kumbuyoko muzovala za blue).

Mulungu nthawi zonse amapereka Masomphenya a moyo wako koma sapereka ndondomeko ya m'mene uyendere.

Yosefe anali ndi maloto odzakhala Mtsogoleli koma abale ake omwe sanakhulupilire za Masomphenya ake.
Abale ake omwe anamukana, kumugulitsa zimene mapeto ake, ananamiziridwa, kuponyedwa kundende osalakwa komanso kuchedwetsedwa ndi kusakumbukiridwa.
Yosefe anali ndi kuthekera kusiya mkuiwala maloto ake, koma anakhalabe Okhulupilika ndi chindunji pa loto lake.

Musafooke pa maloto anu.
Mulungu waikiratu anthu othandizira m'moyo wanu.
Phunzirani kuchokera kwa anthu achikulire komanso amzeru.
Musaoneke amzeru kwambiri mukakhala pamodzi ndi anthu ozindikira.
Dzilumikizeni ndi anthu aphindu m'moyo.
Musadzisiyanitse ndi kuchita bwino kwa ena.
Khalanibe pamalo panu.
Kankhanibe.
Pitanibe chitsogolo.
Pempheranibe.
Khulupiliranibe Mulungu popeza salephera.

22/08/2025

Malonjezo a Mulungu ali INDE komanso AMEN.

Zimene ananena, zikhulupilireni mzotheka.

Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.
Joshua 21: 45

Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna,
ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.”
Isaiah 55: 11

21/08/2025



Estere 4:14
Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”

Mulungu wathu ndiwamphamvu kuposa mmene ife timaganizira ndipo amachita kuposa kumvetsetsa kwathu.
Mulungu amaona zamtsogolo kutali ndipo sitingawerenge ngakhale zaka kuti amalekeza pati.

Tikawerenga nkhani ya Estere pali zambiri zomwe tingaphunzirepo ndipo china mwa zimenezi ndi mmene Mulungu anakonzeratu chipulumutso cha a Yuda ku Susa. Mulungu anadziwa kuti tsikulina wina wake apangira chiwembu a Yuda ndipo chifukwa cha chimenechi anaika Estere akhale mkazi wamfumu panyengo yomweyo. Ndipo kupezeka kwa Estere ku palisi kunapangitsa mtungu onse wa a Yuda apulumuke.

Mvetserani!
Pa zonse zomwe inu mukudutsa, nyengo zanu zooneka zolimbazo, zopanda chiyembekezo, zowawazo, dziwani kuti Mulungungu anakonzeratu chipulumutso ndi chigonjetso chanu. Inuyo chomwe mungapange ndikukhulupilira Mulungu ndikuitanira padzina lake ndi mtima wanu onse ndipo mupambana. Mulungu wathu amamva mapemphero ndipo pamene oyipayo waika chionongeko iyeyo amaikapo chipambano.

Ambuye akudalitseni.

21/08/2025

Mulungu akudalitseni kuti muike chimwemwe pankhope ya ena mu dzina la Yesu Khristu.

Inuyo mudalitsika ndithu chifukwa cha misonzi ndi kusowa mtendere Kwa anthu ena.

Mupitebe Chitsogolo Pa Matthew 8:25 Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”Cholinga ch...
20/08/2025

Mupitebe Chitsogolo

Pa Matthew 8:25 Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”

Cholinga chenicheni cha namondwe sikunali kumuzuza Yesu ndi Ophunzira ake ayi koma kunali kufuna kukanikitsa ntchito yaikulu imene inakachitika tsidya lina yopulumutsa munthu ogwidwa ndi Mzimu oipa.

Nkhondo zimene mukukumana nazozi, taonani patsogolo pang'ono ndipo muona kuti zalerozi zikufuna musafikire chenicheni cha moyo wanu.
Palasanibe.
Khulupiliranibe.
Pempheranibe.
Lambiranibe mpaka mufika tsidya lina.

20/08/2025

Mtendere wa Mulungu ukhale nanu.

Mukhale ndi mtendere ndi aliyense mutsikuli.

19/08/2025

Ikhani Chikhulupiliro Mwa Mulungu Ekha

Maliro 3:25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo.

Chinsinsi chokhala ndi mtendere mu dziko losautsali, dziko lokhumudwitsa komanso dziko lodzala ndi zofooketsa komanso uchimo ndi kukhala ndi Mulungu basi!

Osaika chikhulululo chanu mwa anthu chifukwa, akhoza kukukhumudwitsa.

Osaika chikhulululo chanu mwa ndalama/bank account yanu chifukwa, zikhoza kutaika.

Osaika chikhulululo chanu mwa nyengo chifukwa, zimatha kusintha.

Osaika chikhulululo chanu mu zinthu zadziko lapansi chifukwa, sizokhalitsa-

Kumbukirani malonjezo a Mulungu amene ndi Inde komanso Amen.
Mulungu amene anakhala Okhulupilika nthawi yambuyo, adzakhala wabwinonso lero mpaka kalekale.

Nthawi zina timakhumudwa pamene anthu ena alephera kupezeka m'moyo wathu zinthu zikathina ngakhale kuti ife timapezeka m...
19/08/2025

Nthawi zina timakhumudwa pamene anthu ena alephera kupezeka m'moyo wathu zinthu zikathina ngakhale kuti ife timapezeka m'moyo mwawo!

Abale musakhumudwe kapena Kusunga mangawa!
2 Timothy 4:16

19/08/2025

Lero pamene mukuliyamba tsikuli, muona komanso kukumana ndi ziphona zochuluka;
— Ziphona zotsamwitsa zachuma.
— Ziphona zodzetsa mantha.
— Ziphona zogwetsa mphwayi.
— Ziphona zochedwetsa.
— Ziphona za kusavomelezedwa.

• Chindunji chanu chilunjike pa Mulungu wamkulu amene wakuzungulirani ndi mphamvu yake.

Mulungu akufuna inu mukhazikike pa chilungamo chakuti, zinthu zonse ndi Mulungu mzotheka.

"Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”.'"
Numeri 13:30

19/08/2025

Ambuye mutikhululukire ife, zochimwa zathu.

Address

Box 8
Mwanza
314100

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Moses Chikolosa posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Moses Chikolosa:

Share