Moses Chikolosa

Moses Chikolosa Father, Husband, Gospel Music Minister, Evangelist, Counsellor and a brother in Christ.

11/08/2026

Mulungu akudalitseni ndi kukusungano.

Yehova awalitse nkhope yake pa inu,
nakuchitirani chisomo;

Yehova akweze nkhope yake pa inu,
nakupatsani mtendere.

10/08/2026

Ukatha Moyo Uno, Tidzaima Pamanso Pa Ambuye-

Aliyense adzaweruzidwa molingana ndi ntchito zake.
Nthawi yosankha kokafikira ndi Pano.

Kulibe kulapa moyo ukatha.

Kulibe mphamvu ya pemphero yopangitsa kusintha kofikira ukamwalira kale.

Ukamwalira, sumausa mwamtendere (rest in peace) chifukwa anthu akulembera pa manda ako kapena akupemphelera utamwalira kale.

Lero ndi tsiku labwino limene moyo wanu mukhoza kuupereka Kwa Yesu Khristu kuti aulamulire.

Masalimo 51:17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni. Inu Mulungu simudzawunyoza.

09/08/2026

Kupemphera kwenikweni Mkusiya zako, Mkupanga za ena!

Yesu anasiya Zake mmwamba kudzapanga

Kupemphera kwenikweni kwagona potumikira Mulungu mugawo lotumikira anthu ena.

Yesu samalola kusiya anthu alimmavuto mkupita kopemphera koma amayamba wathandiza anthu asanakapemphere.

Mateyu 26

09/08/2026

anautengera uthenga wabwino (Gospel) Ku China pamodzi ndi Catherine Mzumara mu 2021.

Limodzi anaimba nyimbo ya Kodi Ndalembedwa?

Funso lamphamvu kwaife otsala!

M'mawa uno mulembe zinthu zonse zimene mumakaikira kuti Mulungu sangakwanitse pamoyo wanu.Chinthu chimodzi chimene ndich...
09/08/2026

M'mawa uno mulembe zinthu zonse zimene mumakaikira kuti Mulungu sangakwanitse pamoyo wanu.

Chinthu chimodzi chimene ndichodziwikiratu mchakuti:
Mulungu ndiwamphamvu zonse.

Mulungu sanganame kapena kusiya kukukondani.

Mulungu sangalephere lonjezo lake pa inu.

08/08/2026

Malo amene mphamvu komanso mzeru zanu sizingakwanitse, Chifundo cha Mulungu chikuyankhulireni.

Mulungu Amasamala Zaine!Amakumbukira oiwalika onse!
07/08/2026

Mulungu Amasamala Zaine!

Amakumbukira oiwalika onse!

07/08/2026

Yesu ndi Thanthwe la Moyo wako mu dziko lotopetsa!

Musayende nokha mutsikuli- simungalimbe panokha.

06/08/2026

New Song Alert 🎶🎵

Nyimbo yatsopano



Moses Chikolosa
Moses Chifundo Chikolosa

Zinthu zina zimatheka ndi anthu Koma ZINTHU ZONSE zimatheka ndi Mulungu!
06/08/2026

Zinthu zina zimatheka ndi anthu Koma ZINTHU ZONSE zimatheka ndi Mulungu!

Address

Box 8
Mwanza
314100

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Moses Chikolosa posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Moses Chikolosa:

Shortcuts

Share