Moses Chikolosa

Moses Chikolosa Father, Husband, Gospel Music Minister, Evangelist, Counsellor and a brother in Christ.

Mupite Patsogolo Pang'ono Mateyu 26:39 Yesu anapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti...Mord...
09/06/2026

Mupite Patsogolo Pang'ono

Mateyu 26:39 Yesu anapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti...

Mordecai anaonetsa kukhudzika kwake ndi uthenga komanso chilamulo chimene chinakhazikitsidwa ndi Mfumu Ahaswel komanso Haman.

Haman anatenga chilolezo kuti Ayuda onse aphedwe chifukwa Mordecai sanamugwadire komanso kumupembedza Iye.

Haman anali mwana wa Agag- Agag anali mwana wa Amalek, amaleki anali Mdzukulu wake wa Esau.
Esau anali mwana wa Isaac amene anaberedwa M'dalitso ndi Yakobo (Israel) .

Mordecai sakanagwarira Haman popeza panali udani pakati pawo kuyambira kale. (Exodus 17, 1 Samuel 15).
Dziwani kuti zochitika lero zidzachitikanso mwina zikhoza kungosintha maina kapena maonekedwe koma zinthu zake zimakhala zomwezo:

Kale timkamva kuti 'Chidyamakanda', lero tikumati 'Blesser', chonsecho onse zochita zawo ndi zimodzi, mwachitsanso.

Mordecai anasankha kupita chitsogolo pang'ono kuti apulumutse moyo wake pamodzi ndi mtundu onse wachi Yuda kudzera mwa Esther.

Monga Esther ( Esther 4):
Pena timaona ngati tili safe chifukwa tili pantchito.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa Makolo tilinawo.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa timadziwana ndi anthu a Chipani Cholamula.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa tili ndi maphunziro abwino.

Ayi ndithu abale, ifeyo tili Safe chifukwa Mulungu akulamulira.

Moyo uno suyenda mwa automatic koma ngati manual.
Tikuyenera kupita chitsogolo pang'ono ndi pemphero.
Moyo suli monga unalili dzana.
Moyo sukuyenda monga M'mene umkayendera musanadziwe Yesu.
Chilimikanibe mu pemphero.
Limbikiranibe osagona tulo m'moyo wa pemphero.

Pitani Chitsogolo Pang'ono mu gawo lililonse, chisomo chake chokwani.

Happy birthday Sister Hawah Daudih !Chisomo cha Mulungu chiyende nanu masiku onse a moyo wanu!Ndinu m'dalitso.
08/06/2026

Happy birthday Sister Hawah Daudih !

Chisomo cha Mulungu chiyende nanu masiku onse a moyo wanu!
Ndinu m'dalitso.

08/06/2026

Mulungu anamulenga aliyense momukhala-

Wamtali mwa unique.
Wamfupi momukhala bwino.
Oderako bwino.
Oyererako!

Osadzisiyanitsa ndi ena, Mulungu anakulengani kuti mukhale inuyo popanda kufaniziridwa ndi ena.
Osakhala moyo ofunitsitsa kuti mukhale monga M'mene ena amafunira mutakhala. Khalani inuyo basi!

Mulungu Akumenyereni Nkhondo, Nokha Mulephera.Nthawi zina anthu amafalitsa uthenga wabodza okhudzana ndife.Anthu sadzaso...
07/06/2026

Mulungu Akumenyereni Nkhondo, Nokha Mulephera.

Nthawi zina anthu amafalitsa uthenga wabodza okhudzana ndife.

Anthu sadzasowa okamba zolakwika zaife-
Anthu sadzasowa okunamizirani m'moyo uno.
Anthu sadzasowa okufunirani zoipa m'moyo uno.
Anthu sadzasowa okulemeberani malire m'moyo uno.
Anthu sadzasowa okuchepetsani komanso kusakuoapatsani mwayi.

Paumunthu timafunitsitsa kuti tibwenzere anthu akatichita chipongwe nthawi zonse.
Timafunitsitsa kuti tidziyeretse tokha anthu akayankhula zoipa za ife.
Timafunitsitsa kuti tidzipange defend anthu akatinamizira koma sitikuyenera kutero:

Lolani kuti akuyankhulireni kapena kukumenyerani nkhondo.
Panokha mulephera, panokha mutopa, panokha simukwanitsa kudzimenyera nkhondo m'moyo uno.

Lolani Mulungu akumenyereni nkhondo inu mulichete.
Zokhumudwitsa m'moyo uno sizimasowa, koma chiyembekezo mwa Mulungu chiripo ndithu.

“Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;chiyembekezo changa chichokera mwa Iye” Masalimo 62:5

07/06/2026

Mulungu Amapereka Chisomo Kwa Odzichepetsa

Miyambo 16:5
Yense wonyada mtima anyansa Yehova;
zoonadi sadzapulumuka chilango.

Chinthu chimodzi chomwe mawu a Mulungu amatilimbikitsa ndiye kudzichepetsa. Pa Yakobo 4:10, mawu a Mulungu akuti "Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani."

Mulungu amadana ndi anthu odzikweza ndipo monga baibulo lanenera pa pa vesi yathu yalero mawu akuti Yense onyada mtima anyansa Yehova. Tonse tikudziwa kuti akati kunyansa ndikutani?
Chi nthu chonyansa abale sichabwino koma ndi mmene Yehova amaonera anthu amene ali onyada kapenso kuti odzikweza.

Munthu onyada amadziona opambana paliponse pamene ali. Anthu ena amaoneka opanda pake kapena opanda ntchito pamanso pawo.
Munthu onyada salankhula anthu ena mwaulemu komanso zochita zake zimakhala zopanda ulemu ndipo anthu amamudandaula munthu wachonchoyu.
Tsoka lake ndilakuti ngakhale kuti munthu otere amadziwa zakhalidweli komabe sakhala okhudzika kuti anthu akudandaula zaiye.

Mawu a Mulungu akutichenjeza zakhalidwe limeneli ponena kuti adzalandira chilango ndithu. Tiyeni tiunike moyo wathu ndipo ngati mwaife muli mkhalidwe umenewu tilape ndikusintha mtima wathu.

Tizilemekeza anthu ena angakhale amene akuoneka opanda ntchito poti padziko pano palibe amene ali opanda Pake ndipo mawa limasintha.
Tiyeni timvere mawu a Mulungu ndikupumuka ku chilango.

Ambuye akudalitseni

06/06/2026

Palibe munthu amene angachite kanthu kabwino padziko popanda kuthandizidwa ndi Mulungu.

Mulungu akhale thandizo komanso kumbali yanu m'moyo, mudzina la Yesu Khristu.

06/06/2026

Mulungu alinawo mayankho ochuluka ngakhale vuto silinakufikireni.
Sadandaula Mulungu za vuto losowa mayankho pa moyo wako.

Amaperekeratu mayankho iwe usanadziwe kuti uli ndi vuto.

Mulungu atsogole patsiku lako lero mu dzina la Yesu Khristu.

05/06/2026

Phunzirani Kudzilimbikitsa Nokha-

Miyambo 18:21 Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.
Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

Musanafike pozitaya-
Musanafike pozinyanyala
Musanafike podzidelera nokha.
Musanafike podzilembera malire.
Musanafike podziweluza nokha.
Musanafike podzisala nokha-
Musanafike popanga chiganizo chimene mudzachidandaula moyo wanu onse- ndi pemphero langa kuti Mulungu akuyendereni!

Lengezani M'dalitso pamoyo wanu.

Osamachepetsa ndi kunyozetsa chiyambi chako, khulupiliranibe Mulungu kuti wasungira zazikulu pa moyo wanu.

Mkutheka simunafike pamene mumafuna mutafikira, koma yamikani Mulungu ndikukhala nacho chikhulupiliro popeza, simuli pamene munali dzana/dzulo.

05/06/2026

Ukakhumudwitsidwa ndi Moyo

“[ *Ana*] kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera.”
Luke 2:37

Pali Mzimayi wina wa Mzeru mu Uthenga wabwino, amene dzina lake ndi Ana.
Potengera ndi nyengo zimene amkadutsamo, kunali kophweka komanso kumvetsetseka kuti achite kosiyana ndi m'mene amachita.
Iye anasankha kukhala ndi chindunji pa Mulungu ndi kuuza aliyense za Yesu.

Pa Luke 2 akunena kuti, Ana anakhala wamasiye Kwa Zaka zokwana 84.
Mamuna wake anamusiya iye akadali wachitsikanabe.
Zokhala Mkazi wamasiye ali wachichepere, sizimene Ana anaganizako kapena kukonzekera m'moyo.

Pamene Mwamuna wake anamwalira, kunali kotheka kuti nayenso moyo wachikondi ukanafana mkusiya kukonda ena koma Ana anasankha kuthandiza anthu mothandizidwa ndi Mzimu Woyera.

Ana anasankha kukhazikika pa kusangalatsa Mulungu usana komanso usiku.

Kutaya okondedwa ndi chimodzi mwa chinthu chimene chili pamwamba pa zopweteka m'moyo uno.
Koma pali chimwemwe ndi machiritso pakutumikira Mulungu wa anthu osati anthu a Mulungu.

Khazikikani pa chikondi komanso kusangalatsa Mulungu.

Atatumikira Mulungu kwanthawi yaitali Ana, inafika nthawi imene anakumana ndi Yesu maso ndi maso!

Mwatumikira nthawi yaitali inde.
Mwadikira nthawi yaitali zoona.
Mwapemphera kwa kwanthawi tsopano.
Mwapirira inde.
Mwavutika ndi masautso a moyo uno zoona koma nthawi ikubwera imene Yesu akumana nanu ndi kusungunula chisoni chanu.
Nthawi ikubwera imene Yesu asungunula kusweka Kwa mtima wanu mkukupatsani Umboni.

04/06/2026

Mulungu Odziwa Chiyankhulo Cha Misonzi Yathu Alipafupi Nafe-

Zimene wachitira ena, akhoza kuchitiranso inu!

Musamukaikire.

Address

Box 8
Mwanza
314100

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Moses Chikolosa posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Moses Chikolosa:

Share