09/06/2026
Mupite Patsogolo Pang'ono
Mateyu 26:39 Yesu anapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti...
Mordecai anaonetsa kukhudzika kwake ndi uthenga komanso chilamulo chimene chinakhazikitsidwa ndi Mfumu Ahaswel komanso Haman.
Haman anatenga chilolezo kuti Ayuda onse aphedwe chifukwa Mordecai sanamugwadire komanso kumupembedza Iye.
Haman anali mwana wa Agag- Agag anali mwana wa Amalek, amaleki anali Mdzukulu wake wa Esau.
Esau anali mwana wa Isaac amene anaberedwa M'dalitso ndi Yakobo (Israel) .
Mordecai sakanagwarira Haman popeza panali udani pakati pawo kuyambira kale. (Exodus 17, 1 Samuel 15).
Dziwani kuti zochitika lero zidzachitikanso mwina zikhoza kungosintha maina kapena maonekedwe koma zinthu zake zimakhala zomwezo:
Kale timkamva kuti 'Chidyamakanda', lero tikumati 'Blesser', chonsecho onse zochita zawo ndi zimodzi, mwachitsanso.
Mordecai anasankha kupita chitsogolo pang'ono kuti apulumutse moyo wake pamodzi ndi mtundu onse wachi Yuda kudzera mwa Esther.
Monga Esther ( Esther 4):
Pena timaona ngati tili safe chifukwa tili pantchito.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa Makolo tilinawo.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa timadziwana ndi anthu a Chipani Cholamula.
Pena timaona ngati tili safe chifukwa tili ndi maphunziro abwino.
Ayi ndithu abale, ifeyo tili Safe chifukwa Mulungu akulamulira.
Moyo uno suyenda mwa automatic koma ngati manual.
Tikuyenera kupita chitsogolo pang'ono ndi pemphero.
Moyo suli monga unalili dzana.
Moyo sukuyenda monga M'mene umkayendera musanadziwe Yesu.
Chilimikanibe mu pemphero.
Limbikiranibe osagona tulo m'moyo wa pemphero.
Pitani Chitsogolo Pang'ono mu gawo lililonse, chisomo chake chokwani.