29/08/2026
Bungwe la Thembi Community Initiative lati ligawa chimanga chokwana matani 75 kwa anthu 2,000 m’boma la Chitipa.
Mkulu wa bungweli, Patrick Ziba, wati anthu omwe alandire thandizoli ndi omwe amasamalira ana komanso omwe ali ndi kachilombo ka HIV.
Iye anati thandizoli lipelekedwa kuyambira mwezi wa December chaka chino mpaka mwezi wa January chaka cha mawa, miyezi yomwe mawanja ambiri amkhudzidwa ndi njala.
Mkulu wa ofesi yoona chisamaliro cha anthu m'boma la Chitipa, Rosemary Mahata, wayamika bungweli kaamba ka ntchitoyi ponena kuti zithandiza kulimbikitsa thanzi labwino kwa anthu ovutikitsitsa.
Pakadali pano, bungweli likuthandizanso ana 400 m’boma la Chitipa pa nkhani ya maphunziro komanso zosowa zina zosiyanasiyana.
-Asimenye Sibale-