30/05/2026
Anthu ochuluka okonda timu ya Arsenal yaku Mangalande ali pa m'dipiti kuzungulira mzinda wa Mzuzu ngati chikondwelero choti timuyi inakhala akatswiri a mpikisano wa English Premier League wa m'kacha chino patadutsa zaka pafupifupi 22.
M'dipitiwu omwe wayambila pa bwalo la zamasewero la Katoto uli ndi anthu omwe avala makaka a timuyi ndipo patsogolo pawo pali munthu amene wanyamula chikho chonga cha UEFA Champions League.
Ulendo wawo ukathera ku Chris Garden komwe kukakhale kuonera masewera amundime yotsiliza ya mpikisano wa UEFA Champions League pamene ikhale ikumenya ndi timu ya Paris St. German (PSG).
Arsenal ikapambana kakhala koyamba kutenga chikhochi.
Olemba Frank Mkanalumo