22/06/2026
*MAI WAMWALIRA PA MKANGANO WAKU CHIGAYO*
Apolisi ku Chikwawa amanga a Nales Stephano adzaka 45, ochokera m'mudzi wa Chambuluka m'bomali kamba kowaganizira kuti apha a Patricia Yosefe kutsatira mkangano womwe unabuka pa mzera wa anthu omwe amadikira kugaya chimanga pa malo a malonda a Bereu.
Malinga ndi mneneri wa polisi ya Chikwawa a Dickson Matemba, mdzukulu wa malemuyo anakangana ndi mayiyu pa nkhani yokhudza amene anayenera kutsogola pa mzera wogayira chimanga.
Malemu Patricia Yosefe omwe anali a zaka 83, atalowererapo pofuna kuthetsa mkanganowo, akuti mayiyo anamukankha mwamphamvu ndipo anagwa pansi.
Kutsatira kugwaku a Patricia Yosefe anakomoka ndipo anthu amene anali pafupi anawatengera ku chipatala kuti akalandire chithandizo.
Koma atafika kuchipatala, madotolo anatsindika kuti amwalira kamba kovulala kwambiri m'mutu.
Pakadali pano, apolisi akupitiliza kufufuza nkhaniyi ndipo ati mayiyu adzaonekera ku khoti kafukufuku akadzatha.
Kuwonjezera apo Iwo alimbikitsanso anthu kuti azithetsa mikangano mwa mtendere komanso kukambirana, m'malo mochita ziwawa zomwe zingabweretse mavuto aakulu kuphatikizapo imfa.