Neno Community Radio

Neno Community Radio NENO FM 107.6

Kuphunzitsa, Kudziwitsa komanso Kusangalatsa a Malawi a m'boma la Neno ndi maboma ena ozungulira.

Yemwe amafuna kupikisana nawo pa mpando wa Sipikala wa nyumba ya malamulo lero Lachitatu a George Katunga Million ati sa...
29/10/2025

Yemwe amafuna kupikisana nawo pa mpando wa Sipikala wa nyumba ya malamulo lero Lachitatu a George Katunga Million ati sapikisana nawonso pa mpandowu.

Iwo ati apanga chiganizochi kaamba koti anthu ambiri omwe amafuna mpandowu ndiwochokera kuchigawo chakumwera zomwe zawapangitsa kuti asinthe ganizo lawo ndikukhala pambuyo pa a Sameer Suleman achipani cha DPP.

Iwo atinso anachita zokambirana ndi aphungu anzawo komanso ndipo atinso mfundo zawo ndizofanana ndi za chipani cha DPP chomwe pena amachitsatira.

Padakali pano ndiye kuti omwe apikisane nawo pa mpandowu kumasanaku ndi a Sameer Suleman achipani cha DPP komanso a Akondwani Nankhumwa a PDP ndi a Peter Dimba a MCP ndipo mwambowu ukuyembekezeleka kuchitika 2 koloko masana.

Wolemba- Chifundo Masauli 29/10/2025

A Mutani Tambala omwe adapambana pa chisankho cha Phungu watsopano wa dera lakumwera kwa boma la Neno a chipani cha DPP ...
28/10/2025

A Mutani Tambala omwe adapambana pa chisankho cha Phungu watsopano wa dera lakumwera kwa boma la Neno a chipani cha DPP awalumbiritsa lero ku nyumba ya malamulo ku Lilongwe.

Polankhula atalumbilitsidwa, amai Tambala ati ayika chidwi chachikulu pothana ndi vuto la njala yomwe yakhudza kwambiri dera lawo.

Iwo ati ali ndi chiyembekezo kuti dera lawo lomwe linakhudzidwa ndi ng'amba mu nyengo ya ulimi ipindula nawo ndi chimanga chomwe boma lagula kale ku dziko la Zambia chomwe chikuyembekezeka kugawidwa kwa anthu.

Pankhani ya chitukuko a Tambala ati mogwirizana ndi masomphenya a mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika awonenetsetsa kuti akuika zokhumba za anthu akudera lawo patsogolo ndi cholinga chosintha derali.

Iwo ati agwira ntchito ndi anthu onse posetengera kusiyana pa ndale ndi cholinga chofuna kutukula derali.

Dera lakumwera kwa boma la Neno liri pansi pa mafumu awiri omwe ndi mfumu yaikulu Mlauli komanso Chikalema.

Michael Mollen
Neno FM News 28/10/25

Mtsogoleri wa dziko lino a Professor Arthur Peter Mutharika lero Lachiwiri wati chimanga chomwe Boma lagula kuchoka m'dz...
28/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino a Professor Arthur Peter Mutharika lero Lachiwiri wati chimanga chomwe Boma lagula kuchoka m'dziko la Zambia chiyamba kufika m'dziko muno Lachisanu sabata ino.

Prezidenti Mutharika walankhula izi m'boma la Mangochi pomwe ali paulendo opita ku Lilongwe, komwenso akuyembekezereka kukatsegulira zokambirana za aphungu a nyumba yamalamulo Lachisanu sabata ino.

Iwo anabwereza kuwuza anthu kuti palibe yemwe afe ndi njala pansi pa ulamuliro wawo. Iwo atinso kupita kwawo ku Lilongwe ndi chitsimikizo chotenga Boma.

Mawa Lachitatu aphungu akunyumba yamalamulo asankha sipikala wanyumba yamalamulo wachiwiri kwa sipikala komanso wachiwiri wina pa nsonkhano wa aphunguwa wanambala 52, omwe ndi oyamba wa aphungu omwe asankhidwa pa chisankho chomwe changochitika mdziko muno.

Aphunguwa omaliza akuwalumbiritsa lero pa mwambo omwe udayambika dzuro.

Wolemba Chifundo Masauli 28/10/2025

Timu ya Ligowe Young Soccer yati zokonzekera zikuyenda bwino pamasewera omwe akumane ndi timu ya Bangwe All stars Lowelu...
28/10/2025

Timu ya Ligowe Young Soccer yati zokonzekera zikuyenda bwino pamasewera omwe akumane ndi timu ya Bangwe All stars Loweluka lino mu ndime yamatimu amchigawo chakummwera mu chikho cha Castel.

Mphunzitsi wa timuyi Vexer Chiona Wati timu yake sikungofuna kungokwaniritsa masewerowa koma ikufuna kupeza chipambano ndikupitilira mundime Ina ya mpikisanowu.

Mphunzitsiyu wapemphanso ochemerera masewerowa kuti abwere mwaunyinji kudzawonera pabwalo lazamasewero la Neno kamba koti akufuna kugwiritsa ntchito mwai wosewerera pakhomo ngati mbali imodzi yofuna kupeza chipambano.

Timu ya Bangwe All Stars m'buyomu inasewerapo mu ligi yaikulu mdziko muno ya TNM super League.

Wolemba Dave Laudon 28/10/2025.

Apolisi m'dziko muno  amanga anthu asanu ndi m'modzi (6) omwe akuwaganizira  kuti adamenya ndi kuchitira chipongwe nkulu...
28/10/2025

Apolisi m'dziko muno amanga anthu asanu ndi m'modzi (6) omwe akuwaganizira kuti adamenya ndi kuchitira chipongwe nkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa anthu la (CDEDI) m'dziko muno aSilvester Namiwa ndi anthu ena ogwira ntchito m'boma pa nthawi yomwe amafuna kuchita ziwonetsero.

Kalata ya mneneri ya wachiwiri kwa m'neneli wa apolisi m'dziko muno Suprintendent Alfred Chinthere, yati omwe akuwaganizilawa anakaonekera kale kubwalo lamilandu Lolemba sabata ino ndipo akuyembekezeleka kukaonekalanso kubwaloku posachedwapa.

Anthuwa ndi Alfred Kadula, wazaka 43, Lameck Mandowa wazaka 42, Mabvuto Njuchi wazaka 27, Lester Kanjunga 38, Haward Hamuza ndi Joseph Tilibe Gideon azaka 50.

Anthu ogwira ntchito m'boma anawamenya ndikuwavulaza kaamba kochita zionetsero zosonyeza kusakondwa ndi ~malipilo omwe Boma limawapasa.

ASylvsster Namiwa omwe ndi Mkulu wa bungwe la CDEDi adawamenya kaamba kotsogolera zionetsero zokakamiza wapampando wa bungwe loona zachisankho la MEC Justice Annabel Mtalimanja ndi mkulu Andrew Mpesi kutula pansi maudindo awo.

Wolemba : Chifundo Masauli :28/10/2025

Zinthuzi :Social Media

Alimi a nsomba m' boma la Neno ati akukumana ndi mavuto a kusowa kwa mbewu yamakono ndi zakudya za nsomba.Wapampando wa ...
27/10/2025

Alimi a nsomba m' boma la Neno ati akukumana ndi mavuto a kusowa kwa mbewu yamakono ndi zakudya za nsomba.

Wapampando wa gulu la alimi a nsomba ku Mangadzi mdera la mfumu yaiku Mlauli a Paul Katema wati chakudya cha nsombachi amachigula pamitengo yokwera komanso amaononga ndalama zochuluka zoyendera pokagula ku Blantyre.

Mkulu owona za ulimi wansomba ku khonsolo ya boma la Neno a Mcloud Chimbidzi wati, padakali pano akulimbikitsa alimi kukonza okha chakudya cha nsomba pogwilitsa ntchito zipangizo zopezeka kumudzi monga deya, manyowa ndi zina.

A Chimbidzi ati ngakhale izi zili chomwechi alimi ena akulandila thandizo kuchoka ku pulojekiti ya Sustainable Aquatic Food project (SAF) ndithandizo lochoka ku GIZ yomwe ikuthandizila ndi zipangizo komanso upangili opanga mbeu ya nsomba.

Iwo ati kuchoka mwezi wa October chaka chatha kufika pano boma la Neno lakwanitsa kukolola nsomba zokwana makilogalamu 1,400 zomwe zabweletsa ndalama pafupifupi 9 million kwacha.

Boma la Neno lili ndi alimi a nsomba okwana 230 komanso madamu 245.

Neno FM News 27/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wati padakali pano adzigwirira  ntchito ku nyumba yawo ya ku M...
27/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wati padakali pano adzigwirira ntchito ku nyumba yawo ya ku Mangochi ngati nyumba yachifumu yovomelezeka.

Pulezidenti Mutharika wati nyumba ya Kamuzu ya m'boma la Lilongwe kunachitika zinthu zina zomwe zapangitsa kuti asakaloweko msanga mpaka ataikonzanso ndipo izi zitenga kanthawi.

Mtsogoleriyu walankhula izi pa mwambo otsekulira sabata yokumbukira asilikali akale omwe anamenya nawo nkhondo ziwiri zikulu-zikulu zapadziko lonse lapansi (Poopy week).

Iwo apereka ndalama zokwana K5 million kwa asilikali achikulirewo pambali ponena kuti akhazikitsa dongosolo lofuna kukweza miyoyo ya asilikali onse m'dziko muno.

Wolemba :Chifundo Masauli 27/10/2025

Apolisi ku Mwanza agwira ndi kutsekera mchitokosi a Felix Phiri komanso a James Gama kamba kothyola ndi kuba katundu pam...
27/10/2025

Apolisi ku Mwanza agwira ndi kutsekera mchitokosi a Felix Phiri komanso a James Gama kamba kothyola ndi kuba katundu pamalo ena ogona alendo m'bomalo.

Mneneri wa polisi ku Mwanza Sub-Inspector Hope Kasakula ndiye watsimikiza za nkhaniyi poyankhula ndi wailesi ya Neno.

A Kasakula ati abambo awiriwa akhala akubera anthu pamalo ogona alendowa pogwiritsa ntchito makiyi okonza okha omwe amatha kutsegula chitseko chilichonse.

Malinga ndi mneneri wa polisiyu wati lolemba sabata ino abambo awiriwa anawapeza mchipinda china chomwe eni ake anali akugwira ntchito zina ndipo anthu awumbandawa anakwanitsa kulowa pogwiritsa ntchito makiyi awo ndi kuba makina akompyuta ndi zina.

Padakali pano awiriwa akuwasunga mchitokosi cha apolisi pomwe akuyembekeza kukaonekera kubwalo ndimkuyankha mulandu othyola nyumba ndi kuba.

A Felix Phiri ndi adzaka 57 ndipo amachokera mmudzi mwa Kazimuta kwa mfumu yaikulu Njolomole ku Ntcheu pomwe a James Gama adzaka 47 amachokera mmudzi mwa Mbaisa kwa mfumu yaikulu Mpama ku Chiradzulu

Catherine Maulidi yemwe ndi mtolankhani wodziwika bwino amusankha kukhala ofalitsa nkhani za kunyumba ya boma komanso mn...
27/10/2025

Catherine Maulidi yemwe ndi mtolankhani wodziwika bwino amusankha kukhala ofalitsa nkhani za kunyumba ya boma komanso mneneri wa Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika.

Mlembi wamkulu mu ofesi ya Prezidenti ndi nduna zake Dr. Justin Saidi ndiye walengeza izi.

Catherine Maulidi wayamba kale kugwira ntchito yake.

Catherine Maulidi amagwira ntchito ku nyumba yosindikiza nyuzi ndi kuwulutsa mau ya Times.

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika akuyembekezeka kutsegulira zokambirana za aphungu anyumba ya m...
27/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika akuyembekezeka kutsegulira zokambirana za aphungu anyumba ya malamulo lachisanu sabata ino.

Kalaliki wa nyumba ya malamulo a Fiona Kalemba ndi omwe atsimikiza izi kudzera mu kalata yomwe atulutsa lolemba sabata ino.

Padakali pano aphungu omwe anapambana pa chisankho chapa 16 September chaka chino akuchita malumbiro awo mnyumbayi asadayambe kugwira ntchito yawo.

Mwambo olumbiritsa aphunguwa omwe ukutsogoleredwa ndi wachiwiri kwa mkulu wa mabwalo amilandu Justice Lovemore Chikopa uchitika masiku awiri, lolemba komanso lachiwiri sabata ino.

Mwambo olumbiritsa aphungu akunyumba yamalamulo wayamba lero Lolemba kunyumba ya malamulo munzinda wa Lilongwe ndipo uth...
27/10/2025

Mwambo olumbiritsa aphungu akunyumba yamalamulo wayamba lero Lolemba kunyumba ya malamulo munzinda wa Lilongwe ndipo utha mawa Lachiwiri.

aphungu 111 ndiomwe alumbire lero ndipo aphungu 55 alumbira kale kumawaku, aphungu ena 56 alumbira masanawa. Mawa alumbilitsa ena 113.

Akutsogolera mwambowu ndi wachiwiri kwa nkulu oweruza milandu m'dziko muno a Justice Lovemore Chikopa.

Lachitatu pa 29 October mwezi uno, aphunguwa akuyembekezeleka kusankha sipikala wanyumba yamalamulo, wachiwiri kwa sipikala komanso wachitatu wake.

Wolemba- Chifundo Masauli 27/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino a Arthur Peter Mutharika walamula kuti maboma khumi ndi limodzi (11) azindikilidwe  kuti kwagwa...
27/10/2025

Mtsogoleri wa dziko lino a Arthur Peter Mutharika walamula kuti maboma khumi ndi limodzi (11) azindikilidwe kuti kwagwa njala yoopsa.

Mlembi wankulu mu ofesi ya president ndi nduna zake a Dr. Justin Saidi, mkalata yomwe walengeza izi wati, mabomawa ndi Neno, Blantyre, Chikwawa, Phalombe, Mwanza, Mulanje, Nsanje, Salima, Lilongwe, Thyolo ndi Nkhotakota.

Iwo ati boma lili pa dongosolo lokonzekera kuyamba kupereka chakudya kwa mawanja a anthu 4 million omwe ali pachiwophyezo cha njala malinga ndi kafukufuku wa Boma.

Padakali pano Boma lapempha thandizo kwa omwe angathandize m'dziko momwe muno komanso mayiko akunja.

Wolemba- Chifundo Masauli :27/10/2025

Address

Neno

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Neno Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share