Neno Community Radio

Neno Community Radio NENO FM 107.6

Kuphunzitsa, Kudziwitsa komanso Kusangalatsa a Malawi a m'boma la Neno ndi maboma ena ozungulira.

MaKhonsolo  a  maboma  a Mwanza ndi Neno lachiinayi sabata ino  asainirana mapangano a m'gwilizano ndi wayilesi ya Neno ...
08/08/2025

MaKhonsolo a maboma a Mwanza ndi Neno lachiinayi sabata ino asainirana mapangano a m'gwilizano ndi wayilesi ya Neno kuti wayilesiyi iziulutsa mapulogalamu amaphunziro akupulayimale amumabomawa.

A Fredrick Kaphuka Malango omwe ndi m'modzi mwa akuluakulu oona zamaphunziro m'boma la Mwanza ati cholinga chawo ndikupititsa patsogolo maphunziro a mma'boma awiliwa kaamba koti zaka zingapo mabomawa samachita bwino kumbali ya chiwerengero cha ana okhoza mayeso a maphunziro awo.

A Malango ati ophunzirawa aziphunzila kudzera pawayilesi pogwilitsa ntchito mafoni akompyuta yammanja (tablet fon) omwe anawapeleka kale musukulu zamabomawa.

Iwo pempha makolo kuti atenge udindo ophunzitsa ana awo akakhala pakhomo ndicholinga choti mapulogalamuwa abale zipatso.

Mmau ake mkulu oyang'anira ntchito za wayilesi ya Neno a Jane Chinkwita ati mgwilizanowu ndiothandiza kwambiri kaamba koti makolo azitha kutsatira maphunzirowa kudzera pawayilesi ndi kupeza luntha la momwe angaphunzitsile ana awo akakhala pakhomo.

Iwo ati aonetsetsa kuti akugwira ntchitoyi modzipeleka komanso mwa ukadaulo ndicholinga choti mabomawa atukuke.

Wayilesi ya Neno imamveka mmaboma a Blantye, Mwanza, Ntcheu ndi maboma ena ozungulira.

Wolemba Chifundo Masauli 08/08/2025

08/08/2025

Apolisi ku Neno ati akufunafuna anthu omwe apha a Alex Michael omwe amayendetsa za kabaza.

M'neneli wa apolice m'bomali a Rebecca Msoliza wati malemuwa amanyamula anthu ku Neno turn off ndipo usiku wa lachinayi pa 7 August adanyamula anthu ena awiri omwe anawauza kuti akawasiye ku Chigona.

Iwo ati akudutsa pamalo ena omwe pali njanje oganizilidwawo anathila mmaso tsabola opela malemuyo, ndi kumumenya m'mutu mpaka kukomoka kenako ndikumubela njinga ya mtundu wa Lifan.

A Msoliza ati anthu ena omwe amadutsa pamalowa mmawa kutacha ndiwo anamupeza munthuyo ndikudziwitsa a mfumu a dera lo.

Pochita kafulufuku wawo apolisi ati apeza tsabola opela pamalowa.

A Msoliza ati zotsatila za pachipatala cha Ligowe zasonyeza kuti munthuyo wafa chifukwa chotaya magazi ochuluka.

Padakali pano kafukufuku wa apolisi alinkati kuti apeze anthu omwe achita za upanduzi.

Wolemba Chifundo Masauli 08/08/2025

08/08/2025

Matimu makumi atatu ndi imodzi(31) apikisana mu chikho cha Castel Challenge chaka chino m'boma la Neno.

Matimuwa apikisa m'ma zone mwawo ndipo matimu asanu ndi atatu (8) adzapikisana mu zone ya Chikonde, anayi mu zone ya Kambale, anayi mu zone ya Matope, asanu mu zone ya Lisungwi, awiri mu zone ya Chifunga, asanu mu zone ya Ligowe, ndiponso asanu mu zone ya Malimba.

Wapampando wa Neno District Football Association (NDFA) a Henry Mkandawire ndiwo anena izi powuza wailesi ino.

Iwo apempha otsatira matimu ndi osewera kupewa mchitidwe wa ziwawa mu nthawi yomwe masewerowa akuchitika.

Pali chiyembekezo chakuti timu yomwe ikhale katswiri m'boma la Neno chaka chino ilandila mphoto ya ndalama zokwana K1, million. Iwo ati timu yopambanayo idzapikisananso ndi matimu ena omwe adzapambane m'maboma ena kudzanso a mu ligi yaikulu ya mdziko muno ya TNM.

Chiyembekezo china ndichakuti matimu 16 omwe achite bwino mu mpikisanowu adzapikisana nawo mu ligi ya National Bank Division yomwe iyambike posachedwapa.

Wolemba: Innocent Saenda, 08/08/2025.

Mkulu wa nthambi ya alangizi azaulimi mchigawo cha zaulimi cha Blantyre ADD a Getrude Kumwenda alimbikitsa alimi kuti  a...
07/08/2025

Mkulu wa nthambi ya alangizi azaulimi mchigawo cha zaulimi cha Blantyre ADD a Getrude Kumwenda alimbikitsa alimi kuti azidalira ulimi wathilira kwambiri kuposa wa mvula kaamba koti ndi ulimi omwe ungathe kutukula miyoyo yawo.

A Kumwenda alakhula izi m'boma la Neno mdera la mfumu yayikuklu Symon pomwe amakhazikitsa ulimi wa nthilira pa ganizo loti
"Kusintha ulimi pogwilitsa ntchito ulimi wa nthilira, kusamala zachilengedwe kuti pakhale chakudya chokwanila komanso kutukuka pachuma. "

A Kumwenda ati nyengo inasintha ndipo pano ulimi odalira mvula siwodalilikanso.

Iwo ati anthu asamangodalira zolandira koma azilimbikila pawokha ndicholinga choti asinthe miyoyo yawo.

M'mawu ake Bwanankubwa wabomali Mayi Rosemary Nawasha wati Boma likudziwa kuti m'dziko muno muli njala chifukwa chake akupeleka ngongole kudzera ku bungwe la NEEF ndicholinga choti alimi apeze zipangizo zaulimi mosavuta ndi kutukula miyoyo yawo.

Komabe ngakhale panali kuyamikira khonsolo ya Boma la Neno pochilimika kukweza ntchito zaulimi, Agulupu a Mtengula anapempha khonsoloyi kuti imange changu mlatho wa Mtsimuke kaamba koti alimi amakanika kukagulitsa zinthu zawo kumadera ena kaamba kavuto lamayendedwe.

Wolemba Chifundo Masauli 07/08/2025

Apolisi ku Mwanza atsekera amai awiri mchitokosi kamba kopezeka ndi mafuta agalimoto olemera ma lita makumi atatu (30 li...
07/08/2025

Apolisi ku Mwanza atsekera amai awiri mchitokosi kamba kopezeka ndi mafuta agalimoto olemera ma lita makumi atatu (30 litres).

Mneneri wa apolisi ku Mwanza Sub-Inspector Hope Kasakula wauza wailesi ya Neno kuti amaiwa omwe ndi a Grace Martin komanso a Beauty Limbe awagwira lachinayi sabata ino.

A Kasakula ati agwira amaiwa pomwe apolisi ali mkati mwa ntchito yothana ndi mchitidwe osunga ndi kugulitsa mafuta agalimoto mbali mwa nseu ndi mnyumba za anthu yomwe ayamba m'bomali.

A Beauty Limbe ndi adzaka 47 pomwe a Grace Martin ndi adzaka 39 ndipo onse amachokera mmudzi mwa Liwonde, mfumu yaikulu Kanduku m'boma la Mwanza.

Neno FM News 07/08/2025.

Mwa anthu 20 omwe adalembetsa kuti adzapikisane pa chisankho pa mpando wa mtsogoleri wa dziko lino, Bungwe loyendetsa ch...
06/08/2025

Mwa anthu 20 omwe adalembetsa kuti adzapikisane pa chisankho pa mpando wa mtsogoleri wa dziko lino, Bungwe loyendetsa chisankho la MEC lavomereza anthu 17 okha.

Izi zili mu kalata yomwe wasainira ndi mneneri wa bungweri a Sangwani Mwafulirwa yomwe bungweli latulutsa lachitatu sabata ino.

Bungweri lati anthuwa awavomereza ataunika kalata zawo pomwe anthu atatu achotsedwa pa ndandandawu.

Maina omwe palibe ndi monga a David Mbewe achipani cha Liberation for Economic Freedom (LEF) a Daniel Dube achipani cha National Patriotic Party (NPP) komanso a Reverend Hardwick Kaliya omwe amaima paokha.

Ena mwa anthu omwe avomerezedwa pa chisankhochi ndi mai Joyce Banda (PP), Lazarus Chakwera (MCP), Dalitso Kabambe (UTM), Peter Muthalika (DPP), Atupele Muluzi (UDF) komanso a Michael Usi (Odya Zake Alibe Mlandu)

Neno FM News 06/08/2025

Khonsolo ya boma la Neno yalamula eni malo omwela mowa omwe ali nkati mwa depoti ya bomali kuti atseke malo omwela mowaw...
06/08/2025

Khonsolo ya boma la Neno yalamula eni malo omwela mowa omwe ali nkati mwa depoti ya bomali kuti atseke malo omwela mowawa kuyambila lero chifukwa cha uve.

Kalata yomwe wailesi ino yaona yomwe wasayinila ndi bwanankubwa wa bomali Mai Rosemary Nawasha yati malowa akusowa ukhondo kotelo akhale otseka kufikila vutoli atalikonza.

Iwo apempha ngwirizano pakati pa khonsoloyi ndi eni mabala omwe ali kumalowa poonetsetsa kuti vutoli latha.

Anthu omwe amachita malonda ogulitsa mowa mu depotiyi ati tiwapatse nthawi asanayankhulepo pankhaniyi.

Mwa zina malowa ati ali ndi zimbuzi zolipila zokha zomwenso ndi zosasamalika ndipo kawiri kawiri zimakhala zotseka zomwe zimachititsa anthu ambiri kutaya madzi paliponse.

Izi ati zikupeleka chiopsyezo cha kufala kwa matenda obwera chifukwa cha uve.

Wolemba: Jane Chinkwita 6/8/25

05/08/2025

Apolisi m'boma la Neno achenjeza anthu kuti asamaganize zodzipha akakumana ndi mavuto osiyana siyana.

Izi zikudza pomwe apolisi ku zalewa akusunga nchitokosi a Wisiki Kaliponda azaka 68 omwe akuwaganizira kuti amafuna kudzipha.

Nneneli wa apolisi a Rebecca Msoliza ati pa 3 August, apolisi analandila report kuti bamboyi wadziponya mu mtsinje wa Shire ndipo madzi atamukokolola anaphata pa malo ena ndipo anayamba kukuwa kuti anthu amuthandize.

Anthu atamva mfuwu anathamangila kumalowa komwe anapeza a Wisiki atayima pamwala uku akulira ndipo anawapulumutsa ndikupita nawo ku police komwe anawatsekela.

Atawafunsa iwo anati kwawo ndi ku Balaka ndipo amafuna kudzipha chifukwa chokusemphana maganizo pa nkhani za m'banja ndi akazi awo.

A Wikisi Kalaponda amachokela mmudzi ma Mpulula Kudera la mfumu yaikulu Nsamala m'boma la Balaka.

A Msoliza ati apolisi apezanso thupi la a Mark Shannon Munthali azaka 41 omwe anaziponya mumtsinje omwewu pa 29 July chaka chino pa zifukwa zodziwa okha.

A Munthali omwe anali manejala wa kampani ina ya insurance ku Lilongwe anafika pa malo ena omwela mowa ku zalewa pomwe anayimika galimoto yawo ndikuuza ogulitsa mowa pamalowo kuti munthu wina abwera adzayitenge.

A Msoliza ati a Munthali anayamba kuyenda molunjika ku mlatho kenako anaziponya muntsinjewu kufikila pa 4 August pomwe thupi lawo adalipeza likuyandama mu mtsinjewu ku dera la Chimwambiya.

Iwo ati zotsatila za pachipatala cha Zalewa zasonyeza kuti aMunthali anafa chifukwa chobanika.

Malemuwa amachokela mmudzi mwa Ngozi Kudera la mfumu yaikulu Kyungu ku Karonga.

Wolemba: Jane Chinkwita 5/7/25

Apolisi ku Mwanza agwira ndi kutsekera mchitokosi a Issah Hassan kamba kopezeka ndi mankhwala a chipatala popanda chilol...
03/08/2025

Apolisi ku Mwanza agwira ndi kutsekera mchitokosi a Issah Hassan kamba kopezeka ndi mankhwala a chipatala popanda chilolezo.

Ofalitsa nkhani za apolisi m'bomali Sub-Inspector Hope Kasakula wauza wailesi ya Neno kuti apolisi agwira mkuluyu pa chipata cha bomali pomwe anali paulendo opita mdziko la South Africa.

A Kasakula ati mwazina mkuluyu anamupeza ndi mabotolo amankhwala olera, ochepetsa ululu, otalikitsa moyo kwa anthu omwe ali ndi kachilombo ka HIV ndi ena ambiri.

Padakali pano mkuluyu akumusunga mchitokosi pomwe akuyembekezera kukonekera ku bwalo ndi kuyankha mulandu opezeka ndi mankhwala popanda chilolezo

A Hassan omwe ndi adzaka 42 amachokera mmudzi mwa Kanyangale, mdera la mfumu yaikulu Mwanzama m'boma la Nkhotakota.

Neno FM News, 03/08/2025.

Gulu la anthu achikulire ku Neno lamulungu sabata ino layenda ulendo wandawala  kuchoka pansika wa Ligowe kukafika pamwa...
03/08/2025

Gulu la anthu achikulire ku Neno lamulungu sabata ino layenda ulendo wandawala kuchoka pansika wa Ligowe kukafika pamwala oyera ndicholinga chofuna kupeza thandizo la ndalama zomangira ofesi yawo.

Mkulu wagululi lomwe akulitcha kuti Neno Elderly a Bridget Chipangula auza Neno FM kuti akufuna kukhala ndi malo okhazikika komwe anthu achikulire atha kumakatula nkhawa zawo.

Achipangula ati anthu achikulire akakakumana ndinkhanza akumasowa kokanena choncho akakhala ndi ofesi yawo akakumana ndinkhanza azitha kukanena mosavuta.

aChipangula atinso malo omangira ofesi alinawo kale pomwe mfumu yayikulu Mlauli ndiomwe anawapatsa malowa.

Gululi lapempha anthu akufuna kwabwino kuti alithandize ncholinga choti nkhumbo lawo likwanilitsidwe.

Wolemba Chifundo Masauli 03/08/2025

30/07/2025

Felix Njawala, UTM shadow MP (Mwanza Central Constituency) kuyankhula atapereka nomination papers pa Mphande TDC lachitatu masana.

30/07/2025

Moses Bingalasi Walota, indipendent shadow MP (Mwanza Central Constituency) kuyankhula ndi Neno FM atapereka nomination papers

Address

Neno

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Neno Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share