Neno Community Radio

Neno Community Radio NENO FM 107.6

Kuphunzitsa, Kudziwitsa komanso Kusangalatsa a Malawi a m'boma la Neno ndi maboma ena ozungulira.

01/09/2026



Bwalo la First Grade Magistrate ku Neno lalamula kuti mayi wina wazaka 24, Teleza Steven, akhale m’ndende kwa zaka 11 ndikukagwira ntchito yakalavulagaga chifukwa chopezeka olakwa pochita zogonana ndi mwana wamwamuna wazaka 17.

Izi zatsimikizidwa ndi mneneri wa polisi m'bomali Sergeant Rebecca Msoliza

Bwaloli linamva kuchokera kwa woimira boma pamlandu, Inspector Levison Musote, kuti pa 25 August 2026, Steven anagonana ndi mnyamatayo, yemwe iye ankati anali pachibwenzi naye.

Malinga ndi Musote, Steven anatenga foni ya mnyamatayo popanda chilolezo chake. Mnyamatayo anamutsatira mpaka kunyumba kwake pofuna kutenga foni yakeyo, ndipo atafika kumeneko, Steven anakakamiza mnyamatayo kuti agone naye.

Musote anapitiriza kufotokoza kuti m'mawa mwake, mnyamatayo anayamba kumva kupweteka m’ziwalo zake zoberekera. Iye anauza amayi ake za zomwe zinachitika, ndipo amayiwo anapita naye kupolisi. Kenako mnyamatayo anatumizidwa ku Chipatala cha Neno komwe atamuyeza zinasonyeza kuti anali ndi matenda opatsirana pogonana (STIs).

Pamene Steven anakaonekera kubwalo lamilandu anavomera mlanduwo.

Pofuna kupempha chifundo, Steven anauza khotilo kuti amupatse chilango chochepa chifukwa ali ndi ana awiri omwe amadalira iye.

Komabe, woimira boma Musote anapempha khotilo kuti lipereke chilango chokhwima, ponena kuti chikhale chenjezo kwa anthu ena omwe angafune kuchita zinthu ngati zimenezi.

Popereka chigamulo, First Grade Magistrate Margaret Khobidi adagwirizana ndi zomwe boma linanena ndipo anagamula kuti Steven akhale m’ndende kwa zaka 11 ndikukagwira ntchito yakalavulagaga.

Teleza Steven amachokera ku mudzi wa Mbilizi, mfumu yaikulu Mlauli m’boma la Neno.

Wolemba : Davie Laudon 01/09/2026

 Yemwe anali mkulu wa polisi m'boma la Neno Assistant Commissioner of Police Edwin Magalasi wamwalira. Mwana wawo omaliz...
01/09/2026



Yemwe anali mkulu wa polisi m'boma la Neno Assistant Commissioner of Police Edwin Magalasi wamwalira.

Mwana wawo omaliza Issac Magalasi watsimikizira Neno FM lero ponena kuti bambo ake amwalira dzuro pa chipatala cha Balaka atadwala nthenda ya Shuga komanso kuthamanga kwa magazi.

Iye wati bambowa akhala akudwala kwa kanthawi zomwe zinakakamiza kupuma pa ntchito ali pa polisi ya Lingadzi mu nzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi mwanayu, maliro aika mawa ku mudzi kwao m'boma la Zomba.

Mkulu wa mabungwe omwe siaboma m'boma la Neno a Russel Msiska wati imfayi ndiyophweteka kaamba koti aMagalasi anali patsogolo pa ntchito zokonzanso ntchito za chitetezo m'boma la Neno pa nthawi yawo.

 Boma la Malawi lati likuyembekezera kumaliza posachedwapa mgwirizano wolola dziko lino kulandira mphamvu ya magetsi yok...
01/09/2026



Boma la Malawi lati likuyembekezera kumaliza posachedwapa mgwirizano wolola dziko lino kulandira mphamvu ya magetsi yokwana 400Kv kuchokera ku Mozambique.

Izi zikubwera pomwe ntchitoyi yachedwa chifukwa cha ngozi yomwe inachitika pamalo ogwirira ntchito ku Mozambique, mu mtsinje wa Zambezi.

Malinga ndi kalata yosainidwa ndi mlembi wa Unduna wa Mphamvu, Elvis Thodi, ati ntchitoyi idayimitsidwa kwakanthawi pofuna kuonetsetsa kuti chitetezo cha ogwira ntchito chikutsatidwa.

Undunawu wati pa 8 August chaka chino akuluakulu adayendera malowa ndipo mphamvu za magetsi zidayamba kuperekedwa mongoyesera.

Boma lati likupitiriza njira zokwaniritsira mgwirizanowu kuti Malawi athe kuyamba kulandira mphamvu zonse zomwe zikuyembekezeredwa kuchokera ku Mozambique.

Wolemba: Philadelphia Samera
1/09/2026

 Mkulu waofesi yazaulimi m'boma la Neno aChimwemwe Bomba wayamikira ntchito  yomwe  oyendetsa galimoto zamtundu wa LandR...
31/08/2026



Mkulu waofesi yazaulimi m'boma la Neno aChimwemwe Bomba wayamikira ntchito yomwe oyendetsa galimoto zamtundu wa LandRover komanso njinga zamoto akugwira ponyamula katundu waulimi ochoka komanso kubwela m'boma la Neno.

A Bomba alakhula izi pa mpikisano omwe gulu la Ticheze Homestead linakonza wamalonda pakati pa alimi m'boma la Neno. Mpikisanowu unali wa magulu osiyanasiyana omwe amapikisana poonetsa mbewu, ziweto komanso katundu wina wazaulimi.

ABomba ati boma la Nenoli limatengedwa ngati Boma lovuta pa mayendedwe. Koma ma LandRover komanso njingazi zimachititsa kuti anthu aziyenda mosavuta pambali popempha anthu m'dziko muno kuti azipita m'bomali kukachita malonda awo.

M'modzi wa akuluakulu agulu la Homestead Titani Ticheze wati ali ndimalingaliro ochititsa mpikisanowu chaka chilichonse ndicholinga choti Boma ndi anthu am'maiko ena azidziwa zomwe alimiwa akuchita pa nkhani yazaulimi komanso kutukula Bomali.

Iwo ati kwa nthawi yayitali anthu akhala akutenga Boma la Neno ngati malo ovuta mayendedwe ndipo kuti pa chifukwa cha ichi malonda sangatheke. Koma izi nzoona mu nyengo ya mvula yokha. A Bomba alimbikitsa anthu kuti apite m'bomali kukagula Komanso kukagulitsa katundu wawo wa zaulimi.

 Mfumu Chekucheku ya m'boma la Neno yati siisekelera m'dindo aliyense yemwe angapezeke akuphwanya ufulu wamaphunziro wa ...
28/08/2026



Mfumu Chekucheku ya m'boma la Neno yati siisekelera m'dindo aliyense yemwe angapezeke akuphwanya ufulu wamaphunziro wa ana m'dera lake.Mfumuyi yanena izi pofuna kuti maphunziro apite patsogolo m'delari.

Polakhula ndi wayilesi ya Neno Mfumu Chekucheku yati yachita kafukufuku wake yemwe yapeza kuti adindo ena akumaphwanya dala malamuro zomwe ndi zodandaulitsa.

Iwo atinso aphunzitsi ena ndi aulesi kuphunzitsa zomwe zikumabwezeretsanso mbuyo maphunziro. Mfumimuyi yati palinso myambo ndi zikhalidwe zina zamakolo zomwenso zikulowetsa maphunziro pansi m'derali. Mfumu Chekucheku yati ionetsesa kuti zikhalidwe zoipazi sizikuchitika mdera lake.

A Chekucheku ati pofuna kuti pasapezeke mwana yemwe akungokhala, akhazikitsa makomiti apadera omwe aziyenda khomo ndikhomo kuonetsetsa kuti palibe mwana yemwe akungokhala pakhomo osapita kusukulu. Mwana yemwe angamupeze azifunsa zifukwa zomwe mwanayo sakupitira kusukulu. Iwo ati akapeza kuti palibe zifukwa zokwanira zomwe mwana sakupitira kusukulu azipereka zilango kwa makolo kaamba Koti pakadali Pano sukulu ndi zaulere .

Boma la Neno lakhala lisakuchita bwino pankhani yamaphunziro kwazaka zingapo .

 Akuluakulu awiri a  kampani ya boma yoyendetsa ntchito za mafuta  ya National Oil Company of Malawi (NOCMA) ali m’manja...
27/08/2026



Akuluakulu awiri a kampani ya boma yoyendetsa ntchito za mafuta ya National Oil Company of Malawi (NOCMA) ali m’manja mwa apolisi kaamba koti akukhudzidwa ndi nkhani ya ndalama zokwana K700 miliyoni zomwe akuti zinabedwa ku kampaniyi.

Oganiziridwawa ndi Wachiwiri kwa Mkulu wa NOCMA, Miklas Reuben, wazaka 54, komanso Mkulu Woona za Ntchito, Jacob Sesani, wazaka 49.

Malinga ndi Wachiwiri kwa Mneneri wa Apolisi, Alfred Chimthere, awiriwa akukayikiridwa kuti analephera kusamalira ndi kuteteza ndalama za kampaniyi komanso kuti adagwiritsa ntchito molakwika maudindo awo.

Apolisi ati anthuwa akuyembekezeka kukaonekera ku bwalo la milandu ndipo kafukufuku wa nkhaniyi akupitilirabe.

Wolemba: Philadelphia Samera
27/08/2026

 Kampani yopanga magetsi  ya Electricity Generation Company (ENGECO) yalengeza kuti makina ake sakwanitsa kupanga mphamv...
26/08/2026



Kampani yopanga magetsi ya Electricity Generation Company (ENGECO) yalengeza kuti makina ake sakwanitsa kupanga mphamvu ya magetsi okwanira omwe amafunikira mdziko muno mpaka chaka cha mawa cha 2027.

Malingana ndi kalata yomwe kampaniyi yatulutsa , makina ake a Nkula A omwe amapanga mphamvu ya magetsi okwana 35.1 Megawatts tsopano akungopanga 24 megawatts okha chifukwa cha kuonongeka kwa makina ake.

Kampani ya EGENCO yati vutoli silikonzeka msanga kufikila chaka cha mawa.

Posachedwapa bungwe logulitsa magetsi la ESCOM lidati likulandira mphamvu ya magetsi operewera muyeso omwe limafunikira. Ilo lidati pakadali pano likulandira mphamvu ya magetsi yokwana 347 megawatts okha mmalo mwa 430 megawatts yomwe imafunikila ndipo ikupelewela ndi 83 megawatts.

Wolemba: Innocent Saenda, 26/08/2026.

 Chionetsero cha za ulimi chichitika kuyambira mkuja pa 27 mpaka pa 29 mwezi uno.  Chionetserochi chichtikira ku Chichir...
25/08/2026



Chionetsero cha za ulimi chichitika kuyambira mkuja pa 27 mpaka pa 29 mwezi uno. Chionetserochi chichtikira ku Chichiri Trade Fair Grounds mu mzinda wa Blantyre. Pali chiyembekezo choti Alimi ndi anthu ena ogwira nawo ntchito pa zaulimi afika ku chionetserochii. Cholinga cha chionetserochi ndi kulimbikitsa ulimi wamakono komanso kulumikiza alimi ndi misika.

Chionetserochi chakonzedwa ndi Unduna wa Zaulimi mogwirizana ndi bungwe la makampani a za malonda mdziko muno la Malawi Confederation of Chambers of Commerce and Industry (MCCCI).
Malinga ndi Unduna wa Zaulimi, chionetserochi chichitika pa mutu wakuti “Kusintha Ulimi Kudzera mu Zamakono, Kuwonjezera Phindu pa Zokolola ndi Kulumikiza Alimi ku Misika.”

Undunawu wati wasankha mutuwu pofuna kulimbikitsa alimi kugwiritsa ntchito njira zamakono pa ulimi, komanso kuwathandiza kupeza misika yabwino yomwe ingawathandize kuwonjezera phindu pa zokolola zawo.

Wolemba :Philadelphia Samera
25/08/2026

Nenofmnews Kampani yothandiza alimi pa ntchito zawo ya Farmers Organisation Limited yalimbikitsa alimi ang’onoang’ono ku...
21/08/2026

Nenofmnews

Kampani yothandiza alimi pa ntchito zawo ya Farmers Organisation Limited yalimbikitsa alimi ang’onoang’ono kuti azithira makhwala ovomerezeka komanso oyenerera ku mbewu zawo pofuna kupewa kuwononga mbewu komanso kuika miyoyo ya ogula mbeuzo pa chiopsyezo.

Kampaniyi yapereka upangiriwu lero pamaphunziro omwe inakonza kwa alimi ang’onoang’ono a m’dera la Mfumu Yaikulu Govati m’boma la Mwanza.

Mkulu woyang’anira za malonda a anthu a sitolo zogulitsa zipangizo pa zaulimi ma agro-dealers, ndi alimi ang’onoang’ono ku kampaniyi, a Newman Kaphera, wati kampaniyi yawona kuti nkofunika kuphunzitsa alimi za mankhwala a mbewu ndi kagwiritsidwe ntchito kake koyenera chifukwa mankhwalawa akhoza kukhala poizoni ngati sagwiritsidwa ntchito moyenera.

A Kaphera achenjezanso alimi omwe amathamangira kugulitsa mbewu za m’minda, makamaka masamba, atangopopera mankhwala, kuti mchitidwewu ungaike miyoyo ya ogula pa chiopsyezo.

Iwo ati alimi ena amataya makasitomala chifukwa cha mchitidwewu, ngakhale kuti ena sangazindikire kuti kugulitsa mbewu asanatsatire nthawi yoyenera pambuyo popopera mankhwala kungawononge chitetezo cha ogula.

A Kaphera alimbikitsanso alimi kuti azipanga magulu kuti azipeza zipangizo zaulimi ndi mbewu zomwe zimapezeka ku Farmers Organisation Limited mosavuta.

Mmodzi mwa alimi omwe apindula ndi maphunzirowa, a George Mulelemba a m’mudzi wa Msembedzera, wati maphunzirowa awathandiza kwambiri kumvetsa njira zatsopano za ulimi komanso mankhwala oyenerera mu mbewu.

A Mulelemba ati akagwiritsa ntchito zomwe aphunzira pothandiza alimi ena a m’dera lawo kuti azithana ndi mavuto omwe amakumana nawo pa ulimi.

Iwo ati maphunzirowa apereka chidziwitso chomwe chingathandize alimi kusintha njira zawo zaulimi, kuonjezera zokolola ndi kuonetsetsa kuti zokolola zomwe amapereka kwa ogula ndi zotetezeka.

Wolemba: Jolam Chigonja
21/08/2026

 Bwalo lamilandu lalikulu munzinda wa Lilongwe lapereka belo Kwa omenyera ufulu wa anthu aSylvester Namiwa .Oweluza mila...
21/08/2026



Bwalo lamilandu lalikulu munzinda wa Lilongwe lapereka belo Kwa omenyera ufulu wa anthu aSylvester Namiwa .

Oweluza milandu kubwaloli a Mzondi Mvula ndiwo apereka belo.Popereka belo,aMvula anati aNamiwa apereke k5million ndimboni ziwiri zomwe chikole chake ndi 10 million kwacha.

Mwazina , aNamiwa awauzanso kuti asachitise misonkhano yatolankhani mpaka mlandu wawo uzathe,azikaonekera kubwalo lamilandu Lolemba lililonse Komanso apereke zitupa zawo zoyendera kubwaloli...

ANamiwa anawamanga pomulandu owaganizira kuti amafalitsa nkhani zabodza Komanso kufuna kuukira Boma.

Mlanduwu ukuyembekezereka kuzapitilira pa8 September chaka Chino .

Address

Neno

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Neno Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share