01/09/2026
Bwalo la First Grade Magistrate ku Neno lalamula kuti mayi wina wazaka 24, Teleza Steven, akhale m’ndende kwa zaka 11 ndikukagwira ntchito yakalavulagaga chifukwa chopezeka olakwa pochita zogonana ndi mwana wamwamuna wazaka 17.
Izi zatsimikizidwa ndi mneneri wa polisi m'bomali Sergeant Rebecca Msoliza
Bwaloli linamva kuchokera kwa woimira boma pamlandu, Inspector Levison Musote, kuti pa 25 August 2026, Steven anagonana ndi mnyamatayo, yemwe iye ankati anali pachibwenzi naye.
Malinga ndi Musote, Steven anatenga foni ya mnyamatayo popanda chilolezo chake. Mnyamatayo anamutsatira mpaka kunyumba kwake pofuna kutenga foni yakeyo, ndipo atafika kumeneko, Steven anakakamiza mnyamatayo kuti agone naye.
Musote anapitiriza kufotokoza kuti m'mawa mwake, mnyamatayo anayamba kumva kupweteka m’ziwalo zake zoberekera. Iye anauza amayi ake za zomwe zinachitika, ndipo amayiwo anapita naye kupolisi. Kenako mnyamatayo anatumizidwa ku Chipatala cha Neno komwe atamuyeza zinasonyeza kuti anali ndi matenda opatsirana pogonana (STIs).
Pamene Steven anakaonekera kubwalo lamilandu anavomera mlanduwo.
Pofuna kupempha chifundo, Steven anauza khotilo kuti amupatse chilango chochepa chifukwa ali ndi ana awiri omwe amadalira iye.
Komabe, woimira boma Musote anapempha khotilo kuti lipereke chilango chokhwima, ponena kuti chikhale chenjezo kwa anthu ena omwe angafune kuchita zinthu ngati zimenezi.
Popereka chigamulo, First Grade Magistrate Margaret Khobidi adagwirizana ndi zomwe boma linanena ndipo anagamula kuti Steven akhale m’ndende kwa zaka 11 ndikukagwira ntchito yakalavulagaga.
Teleza Steven amachokera ku mudzi wa Mbilizi, mfumu yaikulu Mlauli m’boma la Neno.
Wolemba : Davie Laudon 01/09/2026