02/06/2026
Ofesi yazaumoyo m'boma la Neno yati ngakhale kutenga pakati mosakonzekera kwatsika pakati paachinyamata osakwana zaka 18 m'bomali ofesiyi ikuvutikabe kuti chiwerengerochi chitsikiretu kwambiri.
Wachiwiri Kwa Mlangizi wa aChinyamata pankhani yakulera a Dalitso Samera wati nthawi ngati yomweyi muchaka cha 2025 atsikana omwe anatenga pakati osakozekera anali oposa 1900 pomwe chaka Chino chiwerengerochi chatsika kufika pafupifupi 1000 .
A Samera ati ngakhale chiwerengerochi chikutsika komabe zikhulupiliro zikulepheletsa kuti chiwerengerochi chitsikiletu kaamba koti makolo amaletsa achitsikana kutsata njira zakulera kaamba kazikhulupiliro zawo. Iwo anati achinyamata omwe ali ndi chidwi ndi njira za kulera amayenda mitunda yayitali kuti akapeze njirazi.
A Samera athokoza mabungwe osiyanasiyana kuphatikizapo bungwe la atsikana la Young women Rise (YOWORI) kaamba kothandizira kuti chiwerengerochi chitsike.
Mkulu wa ofesi ya YOWORI m'bomali a Promise Jalasi wati kudzera Ku thandizo la ndalama lochoka Ku bungwe la Amplify Change zathandizila kutsika kwachiwerengelochi.
A Jalasi alimbikitsa ntchito yopereka njira zakulera Kwa achinyamata kaamba koti iyi ndinjira yokhayo yomwe achinyamatawa angakwanilitse zofuna zawo pamoyo wawo.
Wolemba : Chifundo Masauli :02 /06/2026