Neno Community Radio

Neno Community Radio NENO FM 107.6

Kuphunzitsa, Kudziwitsa komanso Kusangalatsa a Malawi a m'boma la Neno ndi maboma ena ozungulira.

 Ofesi yazaumoyo m'boma la Neno yati  ngakhale kutenga pakati mosakonzekera   kwatsika pakati paachinyamata osakwana zak...
02/06/2026



Ofesi yazaumoyo m'boma la Neno yati ngakhale kutenga pakati mosakonzekera kwatsika pakati paachinyamata osakwana zaka 18 m'bomali ofesiyi ikuvutikabe kuti chiwerengerochi chitsikiretu kwambiri.

Wachiwiri Kwa Mlangizi wa aChinyamata pankhani yakulera a Dalitso Samera wati nthawi ngati yomweyi muchaka cha 2025 atsikana omwe anatenga pakati osakozekera anali oposa 1900 pomwe chaka Chino chiwerengerochi chatsika kufika pafupifupi 1000 .

A Samera ati ngakhale chiwerengerochi chikutsika komabe zikhulupiliro zikulepheletsa kuti chiwerengerochi chitsikiletu kaamba koti makolo amaletsa achitsikana kutsata njira zakulera kaamba kazikhulupiliro zawo. Iwo anati achinyamata omwe ali ndi chidwi ndi njira za kulera amayenda mitunda yayitali kuti akapeze njirazi.

A Samera athokoza mabungwe osiyanasiyana kuphatikizapo bungwe la atsikana la Young women Rise (YOWORI) kaamba kothandizira kuti chiwerengerochi chitsike.

Mkulu wa ofesi ya YOWORI m'bomali a Promise Jalasi wati kudzera Ku thandizo la ndalama lochoka Ku bungwe la Amplify Change zathandizila kutsika kwachiwerengelochi.

A Jalasi alimbikitsa ntchito yopereka njira zakulera Kwa achinyamata kaamba koti iyi ndinjira yokhayo yomwe achinyamatawa angakwanilitse zofuna zawo pamoyo wawo.

Wolemba : Chifundo Masauli :02 /06/2026

  Ofesi yoyang'anila ulimi wa nsomba m'boma la Neno yati ndikhumbo lake kuti  anthu ambiri m'bomali athe kupeza nsomba m...
01/06/2026



Ofesi yoyang'anila ulimi wa nsomba m'boma la Neno yati ndikhumbo lake kuti anthu ambiri m'bomali athe kupeza nsomba mosavuta zoweta okha pogwilitsa ntchito migolo.

Nkulu wa ofesiyi a Macloud Chimbidzi wati anthu ambiri amadalira kugula nsomba m'matauni kapena kwa alimi ena akulu akulu omwe ali ndi madamu akakolola.

Iwo ati ofesiyi ikunka niphunzitsa anthu za momwe angawetele nsomba pogwiritsa ntchito migolo kapena mathanki pakhomo zomwe akhonza kudya ndikupititsa patsogolo thanzi m'mabanja awo.

A Chimbidzi ati ulimi wu umangofunikila madzi opanda mankhwala, mbeu ya nsomba, thanki, mapayipi komanso kutsatila ulangizi omwe ofesiyi imapeleka.

Padakali pano ndi mlimi m'modzi yekha ochokera m'mudzi mwa Galeta kwa mfumu yaikulu Chekucheku m'boma la Neno amene akuchita ulimi oweta nsomba muma thanki.

 Mtsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika watsimikizira anthu m'dziko muno kuti ubale wake ndi wachiwiri...
01/06/2026



Mtsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika watsimikizira anthu m'dziko muno kuti ubale wake ndi wachiwiri wake Dr Jane Ansah ulibwinobwino ndipo palibe kugawanikana kulikonse.

Pulezidenti walakhula izi Lero ,kudzera mkalata yomwe wasaina ndi mlembi wamkulu mu ofesi ya Pulezidenti ndi nduna zake Dr.Justin Saidi.

Pulezidenti Mutharika wati chidwi chake chagona pokweza chuma cha dziko lino m'magawo achakudya, kupezera mwayi n'zika zonse pazosowa zawo mwazina choncho anthu asatekeseke ndi mphekesera zofuna kusocheletsa anthu.

Mtsogoleriyu watinso a Malawi asamvere zokamba anthu ena omwe akufalitsa nkhani zoti ubale wawo ndi achiwiri awo sulibwino, ponena kuti mtsogoleri wa dziko amatuma nthumwi zake malingana ndi kufunikira kwa mwambo ofunika kutuma okamuyimilirawo.

Izi zadza pomwe magulu ena amafalitsa nkhani yoti mtsogoleriyu analephera kukhala nawo pa nkumano wa nduna zake sabata yatha munzinda wa Lilongwe ndipo Malo mwake anatuma nduna yoona za maubale adziko lino ndi mayiko akunja a George Chaponda zomwe anthu ena amati ngati ubale ndiwachiwiri wawo ulibwinobwino akanatuma wachiwiri wawoyo.

Wolemba : Chifundo Masauli -01 /06/2026

 Apolisi m'boma la Neno amanga Mphunzitsi wa sukulu ya primary Yotam Vescan wadzaka 36 pomuganizira kuti amachita zogona...
31/05/2026



Apolisi m'boma la Neno amanga Mphunzitsi wa sukulu ya primary Yotam Vescan wadzaka 36 pomuganizira kuti amachita zogonana ndi mwana wa mkazi wa dzaka 14 .

Ofalitsa nkhani za apolisi mb'omali Rebecca Msoliza watsimikiza za kumangidwa Kwa Mphunzitsiyu.

A Msoliza ati izi zinachitika pa 25 April 2026.

A Msoliza ati kafukufuku wa polisi wapeza kuti mwanayu ndiwophunzira wa standard 8 pa sukulu ya Chikonde.

Patsikuli mwanayo amachokera ku sukulu kokawelenga chigawo chakumadzulo ndipo anakumana ndi Vescan yemwe anamutengera muchinyumba chosatha ndikuchita naye zogonana.

Mwanayu sanawuze munthu zankhanza zomwe anachitiliridwazi kufikira pa 29 April pomwe ati anayamba kumva kupweteka mmimba .

Makolo amwanayu anamutengera kuchipatala komwe achipatala atamuyeza zinadziwika kuti mwanayu anagwiriridwa.

Yotamu Vescan amachokera mmudzi mwa Maere mfumu yaikulu Dambe m'boma la Neno ndipo akawonekera kubwalo lamilandu posachedwapa kuti akayankhe Mlandu ogonana ndi mwana.

Wolemba: Davie Laudon 31/05/2026

Nzika zadziko lino zoposa 2,000 zapempha boma la Malawi kuti liwathandizire ndimayendedwe kuti abwerere kuno kumudzi kuc...
31/05/2026

Nzika zadziko lino zoposa 2,000 zapempha boma la Malawi kuti liwathandizire ndimayendedwe kuti abwerere kuno kumudzi kuchoka mdziko la South Africa komwe nzika zadzikolo zikuchitila nkhanza anthu obwera.

Mlembi wamkulu wa ofesi ya Mtsogoleri wadziko lino ndi nduna zake Dr Justin Saidi wati chiwerengero Cha anthu omwe ali mdziko la South Africa omwe akufuna kubwerera mdziko muno kaamba koopa zipolowe zomwe zikuchitika mdzikolo chakwera kuchoka pa anthu 300 kufika pa 2000..

A Saidi ati anthuwa akuyembekezera kufika mdziko muno kumapeto a sabata ino pa bus.

Nzika zadziko la South Africa zakhala zikuchita zipolowe pofuna kuthamangitsa anthu obwera ati kaamba koti akumawatengera malonda komanso ntchito zomwe nzika za mdzikolo zikuyenera kumagwira.

Wolemba: Davie Laudon 31/05/2026

 Akuluakulu amabodi aMBC komanso MACRA apezeka kuti sadaphwanye malamulo alionse pakalembedwe ntchito Ka akuluakulu  ake...
30/05/2026



Akuluakulu amabodi aMBC komanso MACRA apezeka kuti sadaphwanye malamulo alionse pakalembedwe ntchito Ka akuluakulu ake.

Komiti yanyumba yamalamulo yoona zolemba anthu ogwira ntchito za Boma ya Public Appointment Committee (PAC) kudzera kwa wachiwiri wapampando wa bungwe la PAC aJoshua Malango ndiwo atsimikiza za izi.

Bungwe la Pac lidayitanitsa akuluakuluwa kutsatira madandaulo amene adalandira okhudza kulembedwa kwa mkulu wa MBC a Brian Banda komanso wa Macra a Mayamiko Nkoloma Koma akuti atawafunsa akuluakulu amabodiwa apeza kuti sadalakwitse kalikonse.

Wolemba: Chifundo Masauli:30/05/2026

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wasankha a Thoko Tembo kukhala nduna ya zamigodi.Poyamba undun...
29/05/2026

Mtsogoleri wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wasankha a Thoko Tembo kukhala nduna ya zamigodi.

Poyamba undunawu unaphatikizana ndi unduna owona za mphamvu omwe umatsogozedwa ndi a Jean Mathanga.

Asanasankhidwe pa udindowu a Tembo anali wachiwiri kwa nduna ya zaulimi

Michael Mollen
Neno FM News 29/05/26

 Bungwe la Boma lomwe limagula ndi kugulitsa mbeu la ADMARC lati liyamba kugula chimanga Kwa alimi  mdziko muno kuyambir...
29/05/2026



Bungwe la Boma lomwe limagula ndi kugulitsa mbeu la ADMARC lati liyamba kugula chimanga Kwa alimi mdziko muno kuyambira mwezi wamawa pa1 June .

Kalata yomwe bungweri yatulutsa ndipo wasaina ndi mkulu kubungweli aBen Botolo yati bungweli lizigula chimangachi pamtengo ovomelezeka ndi Boma wa 900 kwacha pakilo.

Bungweli lapempha alimi kuti azigulitsa chimangachi Kwa misika yovomelezeka ya ADMARC mumadera mwawo.

Iwo atinso alimi azigulitsa chimanga chomwe chili chouma bwino komanso chabwino kuti azigulitsa pamtengo wabwino kubungweli.

Izi zikuthandauza kuti bungweli lizigula thumba lachimanga lolemera makilo 50 pamtengo wa 45,000 kwacha.

Wolemba Chifundo Masauli 29/05/2026

 Nduna yazachuma aJoseph Mwanavekha yatsimikizira anthu m'dziko muno kuti sakufuna kuzakambilana ndi  gulu la IMF zakuch...
27/05/2026



Nduna yazachuma aJoseph Mwanavekha yatsimikizira anthu m'dziko muno kuti sakufuna kuzakambilana ndi gulu la IMF zakuchepetsa mphamvu yandalama yakwacha.

Gulu la bungwe lalikulu la za chuma la International Monetary Fund (IMF) likubwera m'dziko muno mmasiku akudzawa, ndipo likuyembekezeka kudzakambirana ndi boma la Malawi kuyambira pa 9 mpaka pa 18 June mwezi wamawa.

Nthumwizi zikhala zikukambirana zatsogolo lopereka ngongole ku dziko lino yachiwongola dzanja chochepa (Extended Credit Facility) yomwe boma la MCP lidaithetsa kaamba ka mfundo zina zomwe silimagwirizana nazo.

AMwanamvekha atinso zokambiranazi zidzalunjika pamfundo zofuna kukonza chuma cha dziko lino basi.

M'zaka za 2020 komanso mu May 2025, ngongoleyi anaithesa kaamba kosakwaniritsa mfundo zina ndi Boma lomwe lapitali

Wolemba: Chifundo Masauli 27 /05/2026

 Bungwe loyendetsa chisankho m'dziko muno la Malawi Electrol Commission (MEC) lalengeza  kuti mkulu oyang'anira chisankh...
27/05/2026



Bungwe loyendetsa chisankho m'dziko muno la Malawi Electrol Commission (MEC) lalengeza kuti mkulu oyang'anira chisankho a Andrew Mpesi watula pansi udindo wake.

Mneneri wa bungweli a Sangwani Mwafulirwa watsimikizira wailesi ino zankhaniyi mukalata yomwe atulutsa lero. Koma iwo sananene zifukwa zomwe a Mpesi achitira izi.

Iwo ati a Mpesi apitilirabe kugwira ntchito yawo ku bungweli mpaka pa 21 August 2026 poti malamulo a MEC amapatsa mpata wa miyezi itatu kwa munthu otere kuti atsikizitse ntchito zake komanso kupereka zofunika kwa mlowa m'malo wake.

Bungwe la MEC layamikila aMpesi pantchito yotamandika yomwe ati akhala akugwira kubungweli monga kukonzanso madera a phungu akunyumba ya malamulo ndi kusintha malamulo ena oyendetsera chisankho.

Wolemba : Chifundo Masauli 26/05/2026

Address

Neno

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Neno Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share