29/10/2025
Yemwe amafuna kupikisana nawo pa mpando wa Sipikala wa nyumba ya malamulo lero Lachitatu a George Katunga Million ati sapikisana nawonso pa mpandowu.
Iwo ati apanga chiganizochi kaamba koti anthu ambiri omwe amafuna mpandowu ndiwochokera kuchigawo chakumwera zomwe zawapangitsa kuti asinthe ganizo lawo ndikukhala pambuyo pa a Sameer Suleman achipani cha DPP.
Iwo atinso anachita zokambirana ndi aphungu anzawo komanso ndipo atinso mfundo zawo ndizofanana ndi za chipani cha DPP chomwe pena amachitsatira.
Padakali pano ndiye kuti omwe apikisane nawo pa mpandowu kumasanaku ndi a Sameer Suleman achipani cha DPP komanso a Akondwani Nankhumwa a PDP ndi a Peter Dimba a MCP ndipo mwambowu ukuyembekezeleka kuchitika 2 koloko masana.
Wolemba- Chifundo Masauli 29/10/2025