Ntchewu Community Radio

Ntchewu Community Radio Your community voice and beyond

15/07/2026

|Dedza - Malawi


Anthu asanu ndi atatu afa ndipo ena asanu ndi mmodzi avulala pa ngozi ya galimoto yomwe yachitika mmawa wa lero pa msika wa Bembeke mu msewu wa Dedza - Ntcheu.

Malipoti akuti galimoto lonyamula katundu la mtundu wa Howo, imachokera ku Dedza Roadblock ndipo imafuna kupitilira galimoto ina kutsogolo kwake (overtake) mwatsoka inaombana ndi minbus yomwe imachokera mbali ya Ntcheu.

Olankhulira polisi ya Dedza a Beatrice Jefita atsimikiza za izi ndipo ati anthu asana ndi atatu wa nkuphatikizapo driver wa minibus yo anavulala modetsa nkhawa ndipo pomwe amafika nawo ku chipatala anali atafa kale.

Pomwe anthu ena asanu ndi mmodzi akadali mchipatala pomwe akulandira thandizo.

A Jefita ati polisi sinakwanitse kuzindikira anthu omwe afawa ndipo akawazindikira akhale akuwaziwitsa achibale awo a anthuwa komanso mtundu wa a Malawi.

Precious Wilson Charliey |Ntcheu


  MIGHTY WANDERERS YALANDIRA CHIPHATSO CHOWALOLA KUTENGA MBALI MU MPIKITSANO WA CAF Bungwe la  Football Association of M...
15/07/2026




MIGHTY WANDERERS YALANDIRA CHIPHATSO CHOWALOLA KUTENGA MBALI MU MPIKITSANO WA CAF

Bungwe la Football Association of Malawi - (FAM) lapereka chiphaso cha chilolezo, (Club Licence) ku Mighty Wanderers FC chowalola kutenga nawo mbali mu mpikisano wa CAF Champions wa 2026/27.

Malingana ndi FAM, Mighty Wanderers yakwaniritsa zofunikira zonse za Club Licensing, zomwe zimafunika kuti kalabu iloledwe kuyimira dziko pa mpikisano wa makalabu a Confederation of African Football (CAF).

Wanderers idazigulila malo mu mpikisanowu chifukwa idatenga ukaswiri wa TNM Super League mchaka cha 2025.

Wolemba: Yamikani Adam_Phalombe

  |Kasungu - Malawi  A Precious Jimy a zaka 25 komanso a Keliyati Kingsley a zaka 23, agamulidwa ndi bwalo la milandu la...
15/07/2026

|Kasungu - Malawi


A Precious Jimy a zaka 25 komanso a Keliyati Kingsley a zaka 23, agamulidwa ndi bwalo la milandu la Chief Resident Magistrate m'boma la Kasungu kukakhala ku ndende kwa chaka ndi miyezi 6 aliyense kaamba kodula mitengo ya kampani ya Press Agriculture m'bomali.

Malinga ndi a Bonex Banda, omwe ndi oimira boma pa milandu ati pa 1 mwezi uno anyamata awiriwa anadula mitengo 800 ya kampaniyi yomwe ndi ya ndalama zokwana K400,000.

Anyamatawa onsewa amachokera m'mudzi wa Lipalazo, mfumu yaikulu Chilowamatambe m'bomali.

Precious Wilson Charliey |Ntcheu


 Nduna ya za Ntchito, Joel Chigona, lero yayendera kampani ya Nutricom, yomwe imapanga chakumwa cha Kombucha ku Njewa mu...
15/07/2026



Nduna ya za Ntchito, Joel Chigona, lero yayendera kampani ya Nutricom, yomwe imapanga chakumwa cha Kombucha ku Njewa mu mzinda wa Lilongwe, kutsatira ngozi yomwe inaphetsa antchito awiri pa 13 July 2026 pamene ankayesetsa kukonza septic tank.

A Chigona ati cholinga cha ulendowu ndi kufufuza mwatsatanetsatane zomwe zinayambitsa ngoziyi komanso kuonetsetsa ngati kampaniyo inatsatira malamulo ndi njira zonse zotetezera antchito pa ntchito zoopsa.

Iwo ati zotsatira za kafukufukuyu zithandiza kudziwa chomwe chinachititsa kuti anthuwa agwere mu septic tank ndiponso ngati panali kusowa kwa njira zoyenera zachitetezo kuntchito.

Wolemba, Justice Mkalimwana Junior -Kasungu

  |South Africa  Mtsogoleri wa dziko la South Africa Cyril Ramaphosa wakana ntchito yolimbana ndi kusamutsa mzika za mai...
15/07/2026

|South Africa


Mtsogoleri wa dziko la South Africa Cyril Ramaphosa wakana ntchito yolimbana ndi kusamutsa mzika za maiko ena mosavomerezeka.

Mneneri wa mtsogoleri yu a Vincent Magwenya ati ali ndi nkhawa ndi ntchito yolimbana ndi kusamutsa kosaloledwaku, ndipo ati South Africa si dziko lokha lomwe kuli anthu olowa popanda zikalata zowavomereza kutero choncho ngati dziko ali ndi njira zoyenerera kutsatira pofuna kuthana ndi vutoli osati kupilikitsa mwa nkhaza ngati mmene zilili pakali pano.

Magwenya ati boma likukana kwamtu wa garu kampeniyi, ndipo adawonjezera kuti kabineti yao ikunyozeka kwambiri kaamba ka mchitidwewu.

Mawu a Magwenya akubwera pamene zionetsero zotsutsana ndi kusamutsa mzika za maiko ena zikupitilizabe m'madera angapo a dziko lo.

Precious Wilson Charliey |Ntcheu


  |Lilongwe - Malawi Mai Precious Billiat alamulidwa ndi bwalo lalikulu ku Lilongwe amangidwenso. Mai Billiat ndi mmodzi...
15/07/2026

|Lilongwe - Malawi

Mai Precious Billiat alamulidwa ndi bwalo lalikulu ku Lilongwe amangidwenso. Mai Billiat ndi mmodzi mwa omwe akuganiziridwa kuti adapha mzika ziwiri za mdziko la China mchaka cha 2023 ndipo adakhululukidwa ndi mtsogoleri wa dziko lino posachedwapa.

Oweruza mlanduwu a Eddah Ngwira-Mwakibinga ati anali odabwa kuti woganiziridwayu palibepo pa mndandanda wa anthu oganiziridwawa zomwe zinapangitsa kuti afunse ambali yaboma kuti afotokoze.

A Mwakibinga ati mtsogoleri wa dziko lino ali ndi mphavu yokhululukira munthu yekhayo yemwe wapezeka wolakwa osati yemwe mlandu wake sunathe.

Woyimira boma a Dzikondianthu Malunda ati iwo anapempha bwalo kuti lichotse pa mlanduwu woganiziridwayu yemwe ndi wa nambala 8 ponena kuti bwalo lipitilire ndi mlanduwu kwa anthu enawo zomwe bwalo lakana.

Mlanduwu ukuyembekezeka kupitilira pa 4 August.

Precious Wilson Charliey |Ntcheu


Big shout out to my newest top fans! 💎 Eph Wizy, Roseline Gwande, James Khembo, Bravo Wellington Thengo, Emmie Steven, J...
15/07/2026

Big shout out to my newest top fans! 💎 Eph Wizy, Roseline Gwande, James Khembo, Bravo Wellington Thengo, Emmie Steven, Joseph Chriford, Lydia Khalaveya, Mcolisisi Mshiga, Thokozani Gunde

Drop a comment to welcome them to our community,

  |MalawiSikuyamba kufinyidwatu ine..A Dzombe ati zaka zisanu ndi ziwiri, 7, zapitazo adayamba ntchito yofuna kumanga ma...
15/07/2026

|Malawi
Sikuyamba kufinyidwatu ine..

A Dzombe ati zaka zisanu ndi ziwiri, 7, zapitazo adayamba ntchito yofuna kumanga malo okwelera bus amakono amene akuti adaononga ndalama zoposera K500 million. Iwo ati sikoyamba kukumana ndi mavuto ofuna kubweletsa zitukuko mdziko muno.

Iwo ati pofuna kumanga zamakono, adakalembetsa pulani ya malo okwelera bus mdziko la China kumene anapeleka 50,000 USD plan imene anayikana koma atapeleka K13 million kenako adapeza kampani ina mdziko muno imene idawalembera plan ina imene anayilipira K100 million.

Koma akuti atayamba kulambura malowa, kudabwera munthu panjinga amene akuti ananena kuti akuchokera ku ofesi ya city ndipo adawauza kuti ameyenera kuonjezera ndalama ina.

Apa ndi pamene loto la a Dzombe lofuna kumanga malo okwelera bus amakono linathera.

A Dzombe afotokoza izi pamene amaonekera ku komiti ya nyumba ya malamulo.

Precious Wilson Charliey |Ntcheu


   Boma la China lapereka thandizo ladzidzidzi la chakudya ku Malawi la mtengo wa pafupifupi madola aku America okwana U...
15/07/2026




Boma la China lapereka thandizo ladzidzidzi la chakudya ku Malawi la mtengo wa pafupifupi madola aku America okwana US$3 miliyoni, zomwe zikufanana ndi K5.18 biliyoni.

Thandizoli likuwonjezera pa lina lomwe China inapereka koyambirira kwa chaka chino la mtengo wopitirira US$4 miliyoni.

Malingana ndi M'chikalata chake, Boma la China lati thandizo laposachedwali likusonyeza kudzipereka kwake kopitiriza kuyima limodzi ndi anthu a ku Malawi pa nthawi ya mavuto.

Wolemba:Kondwani Daniel(Machinga)

15/07/2026




Boma lati likufunika ndalama zokwana K24.7 biliyoni kuti libwezere kwawo a Malawi pafupifupi 15,000 omwe akadali ku South Africa, komwe akukumana ndi ziwawa za tsankho kwa alendo (xenophobia).

Mtsogoleri wa Department of Disaster Management Affairs (DoDMA), a Wilson Moleni, ati kuyambira pa 7 June mpaka 12 July 2026, boma lagwiritsa kale ntchito K7 biliyoni pobweza kwawo aMalawi okwana 41,976.

Koma Mtsogoleri wa bungwe la Centre for Social Accountability and Transparency (CSAT), a W***y Kambwandira, ati DoDMA iyenera kufotokoza mwatsatanetsatane momwe ndalama zokwana K7 biliyonizo zagwiritsidwira ntchito.

Pa anthu 41,976 omwe abwezedwa kuchokera ku South Africa pogwiritsa ntchito mabasi 628, 12,975, ndipo amayi, 459 oyembekezera, 29,025 ndi amuna, pomwe 2,497 ndi ana.

Wolemba:Kondwani Daniel(Machinga)

Address

Ntcheu, Tsangano
Ntcheu
0027754516860 /0027718212050/0027788637374

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ntchewu Community Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category