Litala fm

Litala fm Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Litala fm, Radio Station, Magalasi Road, Nyambadwe.

Empowering the powerless through building general life skills and transforming people into disples of Jesus Christ, So that they can make a meaningful contribution to the society in Malawi.

Bungwe lophunzitsa anthu zinthu zosiyanasiyana la National Initiative for Civic Education (NICE) lati ndi kofunika kuti ...
20/08/2025

Bungwe lophunzitsa anthu zinthu zosiyanasiyana la National Initiative for Civic Education (NICE) lati ndi kofunika kuti omwe akupikisana pa chisankho cha pa 16 September azigwiritsa ntchito mwayi wa mitsutso ngati potambasulira anthu mfundo za chitukuko zomwe azachite akazapambana pa chisankhochi.

Mkulu woyendetsa ntchito za bungweli m'boma la Blantyre a Glory Ngosi Maulidi ayankhula izi lero pa bwalo la sukulu ya pulaimale ya Makhetha mdera la Ndirande Makhetha pa mtsutso wa opikisana pa mipando ya khansala ndi phungu mderalo.

Iye wapemphanso mafumu kuti apereke mwayi wofana kwa omwe akupikisana akafuna kuchitisa misonkhano ku madera awo, zomwe zingathandizire kupewa ziwawa mu nthawi ino yokopa.

Poyankhulapo mlembi wamkulu wa chipani cha United Democratic Front (UDF) yemwenso akupikisana nawo pa mpando wa phungu m'derali, Genarino Lemani wapempha zipani komanso opikisana kuti asunge bata ndi mtendere mu nyengo ino yokopa anthu.

Omwe anatenga nawo mbali pa mtsutsowu ndi monga aphungu a zipani za UDF,DPP, AFORD, MCP ndi ena oyima pawokha komanso makhansala a zipani za UTM, Odya zake alibe Mlandu, ndi enanso oyima pawokha.

Bungwe la National Initiative for Civic Education - NICE Trust lapempha anthu omwe akupikisana nawo m'maudindo osiyanasi...
03/07/2025

Bungwe la National Initiative for Civic Education - NICE Trust lapempha anthu omwe akupikisana nawo m'maudindo osiyanasiyana pa chisankho cha pa 16 September chaka chino kuti asunge bata mu nthawi yomwe adzichita misonkhano yokopa anthu.

Mkulu woyendetsa ntchito za bungweli ku Blantyre, Glory Ngosi Maulidi, wanena izi lero pa bwalo la sukulu ya pulaimale ya South Lunzu ku Machinjiri mu mzinda wa Blantyre pa mtsutso omwe bungweli linakonzera anthu omwe akupikisana pa uphungu komanso ukhansala ku deralo.

Iye wati ndi kofunika kuti anthu akhale ndi chidwi pomva mfundo za adindo omwe akhale akuwafikira ku madera awo ndi kudzasakha moyenera.

Pothilirapo ndemanga, mkulu wa bungwe la Institute for Policy Interaction (IPI), Nandin Patel, wapempha aphungu omwe akuyimira pa chisankhochi kuti akadzasakhidwa adzawonetsetse kuti akumapezeka mu nyumba ya malamulo komanso ku dera komwe akuyimira, osati kutanganidwa ndi zinthu zawo monga zakhala zikuchitikira m'mbuyomu.

Omwe anatenga nawo mbali pa mtsutsowu ndi aphungu oyima pawokha komanso a chipani cha United Democratic Front (UDF) pamene makhansala anali ochokera m'zipani za UTM, Odya Zake Alibe Mlandu ndi ena oyima pawokha.
fm

21/02/2025

program yanu ya pamtondo 09:00am mpaka 10:00am Azimai tieni tikaipatse moto 🔥🔥🔥🔥 pelelekani maganizo anu ndikufunila zabwino anzanu poimba foni kapena uthenga wapamanja kapena Whatsapp.

0984757692

Nthambi ya achinyamata ku chipani chotsutsa boma cha DPP lotchedwa “Blue League” ladzuzula khalidwe losasonyeza ngodya z...
22/01/2025

Nthambi ya achinyamata ku chipani chotsutsa boma cha DPP lotchedwa “Blue League” ladzuzula khalidwe losasonyeza ngodya za demokalase lomwe mkulu wina wa chipani cha MCP, a Jessie Kabwira waonetsa, ponena kuti mtsogoleri wa chipani cha DPP, a Peter M***arika akuchita kukamizidwa ndi anthu ena kuti ayime ndi kupikitsana nawo pa zisankho za chaka chino kamba koti iwowa ndi achikulire.

Malingana ndi kalata lomwe latulutsidwa ndi gulu la achinyamatali, Mkulu ofalitsa ma uthenga, a Alex Business amema a Kabwira kuti abwere poyera ndikupepesa kwa chipanichi, ponena kuti izi zikoledzera ma udani komanso kuti zikusonyeza kuti iwowa sakulemekeza mtsogoleri wa chipani cha DPP, a M***arika.

Gululi latsindika kuti lipitiriza kupititsa pa tsogolo ntchito zosonyeza khalidwe lopatsana ulemu, zololerana komanso za umodzi pa ndale ndipo iwo amema a Malawi kuti agwire nawo ntchitoyi limodzi.

The Minister of Labour, Vitumbiko Mumba has applauded Mzuzu Technical College for their enhancement in innovations, espe...
22/01/2025

The Minister of Labour, Vitumbiko Mumba has applauded Mzuzu Technical College for their enhancement in innovations, especially in renewable energy and agriculture mechanization citing that such developments will help in boosting the country’s economy and development.

The Minister made the sentiments during a familiarization tour at Mzuzu Technical College, where various students showcased multiple pavilions concerning agricultural mechanization and renewable energy.

According to the Minister, these innovations will be an effective key factor in the implementation and realization of the Agriculture, Tourism, and Mining-ATM strategy.

12/12/2024

M***a kupereka mafuno abwino kwa abale ndi alongo mu program ya "Aswelele uli?" kuyambira nthawi ya 12 koloko mpaka 1 koloko masana ano.

Litala FM 105.0Mhz chigawo chaku m'mawa komanso 104.8Mhz chigawo chaku m'mwera.

Address

Magalasi Road
Nyambadwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Litala fm posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Litala fm:

Share

Category