Mabungwe Akuchitanji News Online

  • Home
  • Mabungwe Akuchitanji News Online

Mabungwe Akuchitanji News Online MA NewsOnline//The Real Voice of Organizations, Companies and Individuals
(1)

NYENGO YA USIKU UNO NDI MAWA PA 10 SEPT 2025Tiyembekezere nyengo ya fumbi mwapatalipatali komaso yozizira pang’ono m’mad...
09/09/2025

NYENGO YA USIKU UNO NDI MAWA PA 10 SEPT 2025

Tiyembekezere nyengo ya fumbi mwapatalipatali komaso yozizira pang’ono m’madera ambiri usiku uno ndi mawa m’mawa.

Mawa masana, tiyembekezere nyengo ya mitambo yapatalipatali ndi yotentha komanso ya mvula yowaza m’madera ochepa okwera amchigawo cha kum’mwera koma nyengo ya dzuwa ndi yotentha idzapitilira m’madera amzigawo zina.

LANGIZO: Tikumbukire kumwa madzi pafupipafupi.

MPHEPO: Iziomba kuchokera kumvuma...

LACHINAYI: nyengo ya dzuwa ndi yotentha idzapitirira...

 "TAMIA JA UJA AKUTI AMANGIDWE"Bwalo lamilandu lina  ku Lilongwe lagamula kuti apolisi amange Hannah Jabesi yemwe amadzi...
09/09/2025


"TAMIA JA UJA AKUTI AMANGIDWE"

Bwalo lamilandu lina ku Lilongwe lagamula kuti apolisi amange Hannah Jabesi yemwe amadziwika bwino m'masamba amchenzo ndi dzina loti (Tamia Ja) kaamba kolephera kutsatira ndondomeko za bwaloli.

Malipoti akuwonetsa kuti bwaloli lachita izi lero pomwe zadziwika kuti Jabesi wakhala akulephera kumakawonekera ku bwaloli kawiri konse kutsatira pomwe anapatsidwa belo pa mlandu womwe amayankha.

A Jabesi amayankha mlandu wofalitsa uthenga woti munthu wina ali ndi matenda a HIV/AIDS.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Bungwe lowona zamphamvu la Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) latsutsa malipoti oti lakhazikitsa ndondomeko yoti...
09/09/2025


Bungwe lowona zamphamvu la Malawi Energy Regulatory Authority (MERA) latsutsa malipoti oti lakhazikitsa ndondomeko yoti anthu m'dziko muno adzigula mafuta a galimoto m'malo omwetsera mafutawa kuyambira nthawi ya 6 m'mawa kulekera nthawi ya 6 koloko madzulo.

Izi zikudza kutsatira kalata ina yomwe ikuyenda m'masamba amchenzo osiyanasiyana yokhudza izi.

Koma malingana ndi uthenga womwe bungweli lalemba pa tsamba lake la mchenzo la Facebook malipotiwa ndi abodza ponena kuti sinatulutse kalatayi.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Chipani cha UTM lero chichititsa msonkhano wa atolankhani ku Blantyre.Malingana ndi uthenga wake msonkhanowu uchitikira...
09/09/2025


Chipani cha UTM lero chichititsa msonkhano wa atolankhani ku Blantyre.

Malingana ndi uthenga wake msonkhanowu uchitikira ku Mount Soche Hotel mu m'zindawu.

Msonkhanowu uyamba nthawi ya 2 koloko madzulo anu.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/Ndi ena.

 "SITIKUTENGA NAWO MBALI PA MTSUTSOWU IFE"-DPPChipani cha DPP chati mtsogoleri wake Peter Mutharika satenga nawo mbali p...
09/09/2025


"SITIKUTENGA NAWO MBALI PA MTSUTSOWU IFE"-DPP
Chipani cha DPP chati mtsogoleri wake Peter Mutharika satenga nawo mbali pa gawo lachiwiri la mtsutso wa anthu omwe akufuna kudzapikisana nawo pa mpando wa mtsogoleri wa dziko.

Chipanichi chanena izi pomwe komiti yomwe ikuyendetsa mwambowu yati pakadali pano zonse zokhudza mwambowu zili m'chimake.

Poyankhulapo pa nkhaniyi mneneli wa chipani cha DPP Shadreck Namalomba wati chipanichi sichikugwilizana kwa mnanu ndi ndondomeko zoyendetsera mtsutsowu.

A Namalomba ati chipanichi chimatsatira mfundo zake ndipo mtsutsowu sukulingana ndi izi.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Lero ndipa 09 September  chaka cha 2025.Apatu kwatsala masiku 7 kuti dziko lino lichititse zisankho za mtsogoleri wa dz...
09/09/2025


Lero ndipa 09 September chaka cha 2025.

Apatu kwatsala masiku 7 kuti dziko lino lichititse zisankho za mtsogoleri wa dziko, aphungu akunyumba yamalamulo ndi makhansala pa 16 September pano.

Kwa aMalawi omwe munalembetsa mkaundula wa voti tikukulimbikitsani kuti mukavote mwaunyinji ndi kusankha atsogoleri aku mtima kwanu.

Kumbukirani kuti voti yanu ndi ufulu wanu!!

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 "KOMATU INU OTSUTSA BOMA NDIYE MWAWUPONDA"- ChakweraMtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera wati akuluakulu a chip...
08/09/2025


"KOMATU INU OTSUTSA BOMA NDIYE MWAWUPONDA"- Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera wati akuluakulu a chipani china chotsutsa boma ndiomwe akhala akuchititsa kuti katundu adzikwera mitengo mdziko muno.

Iwo ati akukhulupilira kuti akuluakuluwa akhala akugwilizana ndi eni kampani komanso anthu ena kuti adzikweza mitengo ya katundu wawo pofuna kuwonetsa kuti boma lawo lalephera.

A Chakwera atinso akudziwa bwino lomwe za m'chitidwe wa anthuwa ponena kuti anthuwa atamva kuti iwo lero ayankhula ku mtundu wa aMalawi anachititsa msonkhano wa atolankhani pomwe anakutsutsa za zomwe iwo anakonza kuti afotokozere.

Komabe iwo ati ngakhale kuti anthuwa akhala akuchita izi boma lawo layesetsa kukonza ndondomeko zothanirana ndi mavuto ena a mtunduwu.

# MA NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/Ndi Anthu ena

 Mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera walengeza kuti anthu ayamba kugura feteleza wamu  ndondomeko ya Affordable...
08/09/2025


Mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera walengeza kuti anthu ayamba kugura feteleza wamu ndondomeko ya Affordable Input Program (AIP) kuyambira pa 1 October chaka chino.

A Chakwera anenena izi madzulo ano pomwe amayankhula ku mtundu wa aMalawi ku kunyumba ya chifumu ya Sanjika ku Blantyre.

Malingana ndi a Chakwera anthu adzigura fetelezayu pa mtengo wa 15,000 kwacha pa thumba limodzi lolemera makilogalamu 50.

Iwo ati pakadali pano feteleza wina wa ndondomeko ya alimi omwe ali ndi minda ikuluikulu wafika kale m'malo onse ogulitsira fetelezayu ndipo alimi ayamba kugura mawa pa mtengo wa 90,000 Kwacha pa thumba limodzi lolemera makilogalamu 50.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Kwangotsala mphindi 12 zokha kuti mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera ayankhule ku mtundu wa aMalawi.Iwo akhal...
08/09/2025


Kwangotsala mphindi 12 zokha kuti mtsogoleri wa dziko lino Dr.Lazarus Chakwera ayankhule ku mtundu wa aMalawi.

Iwo akhala akuyankhula kuyambira 7 koloko madzulo ano ku nyumba ya chifumu ya Sanjika.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/Ndi Anthu ena

 Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la MEC lati lamaliza kulandira mabaloti pepa omwe anthu agwiritse ntchito popony...
08/09/2025


Bungwe loyendetsa zisankho mdziko muno la MEC lati lamaliza kulandira mabaloti pepa omwe anthu agwiritse ntchito poponya voti pa zisankho zapa 16 September pano.

Wapampando wa bungweli Justice Annabel Mtalimanja wanena izi lamulungu lapitali pa msonkhano wa atolankhani mu m'zinda wa Lilongwe.

Poyankhula pa msonkhanowu a Mtalimanja ati pakadali pano mabalotiwa akuwasunga ku bwalo la ndege la Kamuzu mu m'zinda wa Lilongwe.

Iwo atinso mabalotiwa ndiotetezeka ponena kuti akuluakulu a nthambi zachitetezo monga apolisi ndi asilikali akupereka chitetezo ku mabalotiwa.

Malingana ndi a Mtalimanja bungweli mawa liyamba kutumiza mabalotiwa m'madera aphungu kuyambira mawa pa 9 September.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Akuluakulu ena a chipani cha DPP akuchititsa msonkhano wa atolankhani mu m'zinda wa Blantyre.Akuluakuluwa ndi a Ben Phi...
08/09/2025


Akuluakulu ena a chipani cha DPP akuchititsa msonkhano wa atolankhani mu m'zinda wa Blantyre.

Akuluakuluwa ndi a Ben Phiri,Sameer Suleman, Shadreck Namalomba komanso Mary Navicha.

Pa msonkhanowu akuluakuluwa akufotokozera zokhudza kukwera kwa mitengo ya katundu mdziko muno komanso zisankho za chaka chino.

Anthuwa akuti boma lalephera kupititsa patsogolo moyo wa aMalawi ndipo nkofunika kuti apereke mpata ku boma la chipanichi ndi mtsogoleri wake Peter Mutharika kuti moyo wawo upite patsogolo.

Anthuwa atinso nkofunika kuti anthu akavote mwaunyinji ndi kusankha utsogoleri wa chipanichi pa zisankho zomwe zichitike pa 16 September pano.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

 Unduna wowona za maboma ang'ono, umodzi ndi chikhalidwe walengeza  kuti pa 16 September chaka chino lomwe ndi tsiku lop...
08/09/2025



Unduna wowona za maboma ang'ono, umodzi ndi chikhalidwe walengeza kuti pa 16 September chaka chino lomwe ndi tsiku loponya voti kukhala tchuti mdziko muno.

Kalata yomwe wasainira ndi mlembi mu undunawu Richard Hara yati izi zili mgawo lachiwiri la ndime 77 ya malamulo oyendetsera zisankho za mtsogoleri wa dziko, aphungu akunyumba yamalamulo ndi makhansala.

Kalata yomwe wasainira ndi mlembi mu undunawu Richard Hara yati izi zilichomwechi pofuna kupereka mpata wokwanira kwa aMalawi kuti adzawonetse ufulu wawo woponya voti.

Undunawu wafunira mafuno abwino anthu patsikuli.

NewsOnline Kukupatsirani Nkhani Zamabungwe/Kampani/ Ndi Anthu ena

Address


Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mabungwe Akuchitanji News Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share