08/06/2026
Pafupifupi a Malawi 150 Omwe Akuthawa Nkhanza Zosiyanasiyana ku South Africa,Omwe Amayembekezeka Kufika M'dziko Muno Usiku Uno,Alephera Kufika Ndipo Afika Mawa M'mawa!
__Mongokumbutsananso,mukafika dziwani kuti pano m’midzimu kokumba manda kuli ma committee; sizachinam'balala ngati zakale zija. Ngati muzichalilira nsima yakumeneko, muwuponda.
Kuli oyimba winawake waku Mbayani yemwe zochitika zake zikuwonetsa ngati mutu wake sukugwira bwino ntchito. Panopa watulutsa kale nyimbo 60 zomwe akuti ndi za "ma Slime."
Mahule anasintha dzina; pano tikuwatcha kuti ma "baddie," ndipo ambiri akupezeka m'ma university.
Ana aja munkapempha kuti muwone zithunzi zawo koma osawatumizira chithandizo,anakula ndipo zikuwayenderanso.
Mupeza Kuno kuli gulu linalake lotchedwa Madness, muli anyamata a nkhope, komanso miyendo yachilendo musadabwe ayaka moto pano ndi amenewo.
Chiphadzuwa cha Malawe momwe munachisiyira muja sichinapezebe banja ndimomuja ndithu.
Ma disco anatha; ngati mwabwera ndi ma sabufa amatabwa aja,muzimvera nokha.
Pano kuli ma translator; mukamatiyankhula Chizulu cha broken, muchita manyazi.
Kwa anzathu akumpoto, mwina mudabwa kuti pano soya pieces ndi K2,000 zinthu zinakwera ndithu.
Komanso Zomatchula K100 kuti ngati R100 kumasokoneza dala, anthu akutopelani nazo.
Zotukwana ma president ngati momwe munkachitira muli kumeneko, mukapitiliza kuno, Mkulukutamoyo ndiye akunjatani sakusekelera.
Ndege pano akukwera ngakhale anthu osasamba, bola ali ndi ndalama; mwina mudabwa.
Bullets yapano siyaachina Fodya ija zikuvutilako ndithu.
Misewu yathu inasinthanso pano ndi ndendende achina Belleville,Mokopane,Sosolburg,Vryburg Zakumeneko
Mukamadya tiwana simuchedwa kukaidziwa Maula ndi Mikuyu,oyimba mnzanu wakonko anachimina.
Kumapeto mwina mudabwa kuli madala enaake okhala ngati adzola ufa ku tiktokoku amakonda kunena kuti mkudzukudzu dziwani siwufa umenewo ndi dry skin chabe tikuuzilenitu musanawapute chifukwa nde amalalata nditimawu tawo.