Malawi Live Today

Malawi Live Today Malawi Live Today is the platform that gives you a straightforward and entertaining look at what's happening in politics.
(1)

Please Like/Follow our Malawi Live Today page for daily updates on the top political stories and breaking news.

10/31/2025

Matupi a anthu Asanu ndi atatu, omwe anamwalira pangozi ya bus mu Mzinda Limpopo mdziko la South Africa Alowa mdziko muno kudzera pa chipata cha Mwanza.

Boma lakonza mapemphero pofuna kupereka ulemu otsiliza komwe Mlangizi wa mtsogoleri wa dziko lino pa nkhani za Chipembezo Apostle Timothy Khoviwa akhala nawo pa mwambowu




10/31/2025

Powerful Speech yomwe wayankhula Pulezidenti Peter Mutharika ku Parliament lero.

Mtsogoleri wa dziko lino walengeza kuti boma libwereranso ku ndondomeko yakale yogulira mafuta a galimoto yomwe aliyense...
10/31/2025

Mtsogoleri wa dziko lino walengeza kuti boma libwereranso ku ndondomeko yakale yogulira mafuta a galimoto yomwe aliyense amene Ali ndi kuthekera, akhoza kupikisana nawo kuti agulitse mafuta.

Izi zikutanthauza Kuti ndondomeko yogula mafuta mu njira ya boma ndi boma limzake yatha

A Mutharika atinso mafuta akusowa mdziko muno kamba koti ndalama zakunja zikusowa mdziko muno, chinthu chomwe boma lawo likukonza




Mtsogoleri wa dziko linoyunso walongosola kuti sukulu iliyonse yaboma ya Primary kapena Secondary isaitanitse ndalama zi...
10/31/2025

Mtsogoleri wa dziko linoyunso walongosola kuti sukulu iliyonse yaboma ya Primary kapena Secondary isaitanitse ndalama zina zilizonse zaboma kupatula ndalama ya boarding , sukulu zikatsekulilidwa Chaka chamawa

A Mutharika alengezanso kuti Constituency Development Fund ikwera kuchoka pa 200 million kufika pa 5 Billion

Mu ndalamazi muli ndalama zokwana 100 million ya ngongole za achinyamata ndi amayi




Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika walengeza kuti mtengo wa fetereza wa makuponi tsopano uli pa K10 000 kuchoka ...
10/31/2025

Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika walengeza kuti mtengo wa fetereza wa makuponi tsopano uli pa K10 000 kuchoka pa K15, 000.

A Mutharika alengezanso kuti ndondomeko ya zipangizo zotsika mtengoyi idzitchedwa kuti Farm Input Subsidy Programme FISP kuchoka ku Affordable Inputs Programme




Aphungu a Nyumba ya Malamulo afika ochulukirapo ku Nyumba ya Malamulo komwe mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika a...
10/31/2025

Aphungu a Nyumba ya Malamulo afika ochulukirapo ku Nyumba ya Malamulo komwe mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika akukatsegulira mkumano wa aphungu mnyumbayi.

Uwu ndi mkumano wa nambala 52 wa aphungu a Nyumba ya Malamulo

Wachiwiri wina kwa mtsogoleri wa dziko lino a Enock Chihana komanso wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Mayi Jane Ansah afikanso kunyumbayi




10/31/2025

Mpungwe pungwe ku MCP anthu ena sakungwirizana ndikusankhidwa kwa Simplex Chithyola Banda ngati leader of opposition ku parliament.

Times Group inachita kukonzanso nyuzipepala yawo itatuluka kuti alembe nkhani yokhuza Cabinet yatsopano.Siyanitsani Mala...
10/31/2025

Times Group inachita kukonzanso nyuzipepala yawo itatuluka kuti alembe nkhani yokhuza Cabinet yatsopano.

Siyanitsani

Malawi Live Today

Kutsekulira mkumano wa aphungu a Nyumba ya Malamulo wa number 52 Zonsezi mudzimvera pompano pa Malawi Live Today
10/31/2025

Kutsekulira mkumano wa aphungu a Nyumba ya Malamulo wa number 52

Zonsezi mudzimvera pompano pa Malawi Live Today


Chipani cha UTM chati anthu ake oposa 2 million anavotera Proffessor Peter Mutharika ndi Chipani cha DPP mu masankho ang...
10/31/2025

Chipani cha UTM chati anthu ake oposa 2 million anavotera Proffessor Peter Mutharika ndi Chipani cha DPP mu masankho angothawa

Mneneri wa Chipanichi a Felix Njawala wati chachikulu chomwe masapota a Chipanichi ankafuna ndikuchotsa boma lachipani cha MCP

Iwo ati kusachita bwino kwake sikukutanthauza kuti Chipanichi chilibe mphanvu

Katswiri pa nkhani za ndale a George Chaima wati zomwe chikunena Chipanichi ndizosamveka potengera m'mene chinachitira

Iwo alangiza Chipanichi kuti chikhale pansi ndikukonza zinthu zawo msanga , mphanvu zonse zachipanichi zisanathe




Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika tsopano atulutsa ndandanda wonse wa nduna zawo
10/30/2025

Mtsogoleri wa dziko lino a Peter Mutharika tsopano atulutsa ndandanda wonse wa nduna zawo




Chithunzi chili m'musichi chautsa manong'onong'o mdziko muno pomwe ena akuti Chipani cha MCP chikudziwapo kanthu pa achi...
10/30/2025

Chithunzi chili m'musichi chautsa manong'onong'o mdziko muno pomwe ena akuti Chipani cha MCP chikudziwapo kanthu pa achinyamata a zikwanje omwe anamenya ndikuvulaza mkulu womenyera ufulu wa anthu a Silvester Namiwa.

Izi zinachitika mu June Chaka chino ndipo mtsogoleri wakale wa dziko lino a Lazarus Chakwera anati pakhale kafukufuku pa kunenyedwa kwa a Namiwa koma palibe chomwe chinachitika

Lero kumasanaku bwalo la Principal Resident Magistrate ku Lilongwe lati anthu asanu ndi anayi omwe lawavomereza belo akhalabe mchitokosi cha apolisi mpaka mawa kamba koti maofesi ena monga owerengetsera ndalama adali otseka

Wogamula milandu Benjamin Chulu wati ndondomeko zina zotsiliza za belo adzazimaliza lachisanu mmawa pomwe anthuwa adzatuluke.

Anthuwa akuyankha milandu isanu ndi umodzi imene ndi monga kuvulaza munthu, kuba katundu komanso kuotcha katundu.

Mchithunzichi akuluakulu a chipani cha MCP a Moses Kunkuyu komanso a Jessie Kabwila anafika ku bwaloli kudzamva nawo nkhaniyi ponena akuti anthu ena omwe akuzengedwa milanduyi akuwadziwa

Inu nkhaniyi mukuimvetsa bwanji?


Address

United State Of American
Indianapolis, IN

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Live Today posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share