Malawi Live Today

Malawi Live Today Malawi Live Today is the platform that gives you a straightforward and entertaining look at what's happening in politics.

Please Like/Follow our Malawi Live Today page for daily updates on the top political stories and breaking news.

Bungwe la Beauty Malawi pamodzi ndi mtsogoleli wa dziko Professor Arthur Peter Mutharika komanso mai wa fuko madame Getr...
07/13/2026

Bungwe la Beauty Malawi pamodzi ndi mtsogoleli wa dziko Professor Arthur Peter Mutharika komanso mai wa fuko madame Getrude Mutharika apeleka katundu osiyanasiyana kwa anthu amene afika kuchoka ku South Africa kuthawa Xenophobia.

Katunduyu wapelekedwa pa Joice Chitsulo stadium m'boma la Mwanza komwe anthuwa akumafikila.
Mmau ake mkhalapampando wa bungweli a Dingswayo Jele anati mtsogoleli wadziko lino komanso mayi wa fuko ndi okhudzika kwambiri ndi mavuto amene a Malawi akumana nao m'dziko la South Africa.

Katundu amene wapekedwa ndi wa ndalama pafupifupi 100 million kwacha. Mwa zina pali zofunda, ufa, soap ndi sugar.


07/13/2026



Nduna ya za masewero a Alfred Gangata anayankha ena mwa mafunso pa zomwe anapeleka za ku unduna wao.


07/13/2026

Mtsogoleri wa nyumba yamalamulo a Jappie Mhango apempha aphungu a nyumba yamalamulo kuti asamapite ku nyumbai ataledzela.

Mawuwa analankhulidwa pamene iwo amayankha zomwe phungu wa dela la Lilongwe Nyanja anafusa zokhudza kakhalidwe ka nyumbayi pamene aphungu ena ndi nduna anakhala mosiyana ndi m'mene amayenera kukhalila ku mbali yolamula.

Koma poyankhapo mtsogoleli wa nyumbayi anati sibwino kumapita kunyumbayi atachita ka cha kumwa. Iwo anati nyumbayi ikuyenera kumakhala ndi chidwi pa zinthu zopindulila dziko.

Izi sizinasangalatse Phunguyu amene anapempha sipikala kuti a Jappie Mhango abweze mau amene analankhulawa.


07/13/2026

Phungu wa dela la Dedza Kasina Joshua Malango wati ndikofunika kuti unduna woona za chitetezo fotokoze za mphekesela zomwe zikunveka zokhudza Sitima ya m'dziko la Tanzania yomwe inafika pa doko la Monkey Bay mosatsata ndondomeko.

Iwo ati izi ndi zofunika ku dziko pakuti ndi zokhudza chitetezo.

Koma poyankhapo sipikala wa nyumba yamalamulo a Sameer Sulemani anapempha Phunguyu kuti atsatile ndondomeko yabwino yobweletsela nkhaniyi ku nyumbayo.


Ena mwa ophunzira okhudzika a sukulu za ukachenjede akapeleka kalata ya madando ku nyumba ya malamulo.Ophunzilawa akuti ...
07/13/2026

Ena mwa ophunzira okhudzika a sukulu za ukachenjede akapeleka kalata ya madando ku nyumba ya malamulo.

Ophunzilawa akuti sakugwirizana ndi kukwela kwa mitengo ya ndalama zolipila fees. Pa ichi iwo kudzela mu kalata yomwe alemba apempha nyumba ya malamulo kuti ikambilane ndi adindo kuti abweze chiganizocho.

Polandila Kalatayi phungu wa dela la Lilongwe Nyanja aBaba Steven Malondera anati kalatayo ikafika koyenera.

Kalata ya ophunzilawa ya sainidwa ndi Shakira Rejoice Mbambha, Lovei Mirenda, Prince Mattaka ndi Shewana Kasumbwa.


Ofesi ya Malawi Lake Services yati anthu komanso nyumba zofalitsa nkhani asamakonde kufalitsa zabodza pa masamba a mchen...
07/13/2026

Ofesi ya Malawi Lake Services yati anthu komanso nyumba zofalitsa nkhani asamakonde kufalitsa zabodza pa masamba a mchenzo.

Muku wa nthambi yoona zapanyanjayi a Joseph Banda ati anthu ena akufalitsa zoipa zokhudza Sitima yomwe inayima pa doko la Monkey Bay.

Malingana ndi a Banda sitimayi yanyamula miyala ya Malasha ndipo ilibe chiopsezo chilichose ku dziko.

Kunali chipwirikiti ku Lilongwe mdela la Chinsapo pamene oitanika ma minibus akulimbilana mgodi.Magulu awiri amene ena n...
07/13/2026

Kunali chipwirikiti ku Lilongwe mdela la Chinsapo pamene oitanika ma minibus akulimbilana mgodi.

Magulu awiri amene ena ndi a kwa Nsanga ndipo ena ndi a kwa Nsiwa m'delali onse akufuna atatenga ulamulilo wa malo oitanila ma minibus. Chifukwa chonsanvana kumenyana kwa kukulu kunachitika ndipo ena avulazidwa pomwe atemedwa.

Zinatengera apolisi kuphulitsa utsi okhetsa msozi kuti anthu abalalike. Apolisi tsopano akhanzikitsa zokambilana pakati pa magulu awiriwa.


07/13/2026

Chipani cha UTM chili ndi nsonkhano wa adindo akuluakulu a chipanichi.

Mkumanowu ukuchitika ku likulu la chipanichi ku Area 10 mu nzindau wa Lilongwe. Dr Dalitso Kabambe amene ndi mtsogoleli wa chipanichi ali nao pa mkumanowu.

Mwazina chipanichi akuti chayamba Zokonzekera za chisankho cha 2030.


Mlandu wokhudza infa ya Dr Victoria Bobe ukupitilila lelo ku bwalo la milandu.Mboni ya boma amene ndi wapolisi wazofufuz...
07/13/2026

Mlandu wokhudza infa ya Dr Victoria Bobe ukupitilila lelo ku bwalo la milandu.

Mboni ya boma amene ndi wapolisi wazofufuza a Christopher Pangeti ndi amene a kupeleka umboni pamene akuwafunsa mafunso.

Pofotokoza iwo akuti analephela kukatenga nfuti yomwe inagwiritsidwa ntchito poombela Dr Bobe komwe anauzidwa kuti inakwililidwa pansi m'dziko la Mozambique. Iwo anati anachita izi pa zifukwa za chitetezo chao.

A Pangeti akananso zakuti apolisi anavulaza oganizilidwa. Iwo akuti oganizilidwawa amkaulula okha osati kuwakakamiza.

A Sylvester Ayuba James amene ndi phungu wa nyumba yamalamulo wa dela la Nkhotakota Central wati boma la DPP likuoneka  ...
07/13/2026

A Sylvester Ayuba James amene ndi phungu wa nyumba yamalamulo wa dela la Nkhotakota Central wati boma la DPP likuoneka kuti lilibe ndalama.

Iwo ati mpaka pano za CDF sizikulondeka pamene ma Khonsolo sanalandilebe 5 billion yomwe inalonjezedwa. Koma a James ati ndi zoseketsa kuti boma likungochulukitsa zokamba opanda chochitika.

Padakali pano iwo apeleka ganizo lakuti Mwina boma litsitse mlingo wa ndalamazo kuchoka pa 5 billion imene yakhala ikukambidwa.


Address

United State Of American
Indianapolis, IN

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Live Today posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Featured

Share