06/12/2026
Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko Lino Dr Jane Ansah wati mdziko muno muli Anthu omwe anabadwa akafula Koma ali ndi nzeru kuposa Anthu omwe anabadwa atali.
Iwo ati kufupika ndi nzeru ndi zinthu ziwiri zosiyana pomwe akafura amachitanso Bwino pa maphunziro awo.
“Pakati pathu pano tili naye mzathu kafula anakhonza 14 points pa Mayeso ake a MSCE, pomwe inu ndi ine sitinayipate 14 points yo. Kapena alipo pakati pathu pano amene anabadwa wamtali anakhonza 14 points ayimilire??, anafunsa Dr Ansah.
Pa mwambowu Pali akafula kuchokera ku chigawo chaku mpoto, pakati ndi kumwera.