Malawi Live Today

Malawi Live Today Malawi Live Today is the platform that gives you a straightforward and entertaining look at what's happening in politics.

Please Like/Follow our Malawi Live Today page for daily updates on the top political stories and breaking news.

Mtsogoleri wa dziko la United States of America Donald Trump wati tsopano adziyendetsa dziko la Venezuela mpaka pomwe ku...
01/03/2026

Mtsogoleri wa dziko la United States of America Donald Trump wati tsopano adziyendetsa dziko la Venezuela mpaka pomwe kutachitike chisankho chosankha mtsogoleri wina.

Trump amayankhula pa Wailesi ya Kanema madzulo ano

Iye walanda dziko la Venezuela kumasanaku atadzidzula dzikolo kuti likusunga anthu amene akulowa mankhwala ozunga bongo ku America ko, zomwe mtsogoleri wa dziko la Venezuela Nocorus Maduro watsutsa ponena kuti izi ndi Mphanvu za America zofuna kulanda zitsime za mafuta mdziko la Venezuela

Padakali pano mtsogoleri wa dziko la Russia a Vladmir Putin wati akutsatira mwachidwi nkhaniyi ndipo ali mbali ya Venezuela




Nduna ya zachuma a Joseph Mwanamvekha yati ikukhulupirira kuti thumba la Chimanga lifika 20, 000 pofika August Chaka chi...
01/03/2026

Nduna ya zachuma a Joseph Mwanamvekha yati ikukhulupirira kuti thumba la Chimanga lifika 20, 000 pofika August Chaka chino.

Iwo amayankhula izi pa Msonkhano womwe anachititsa phungu wa dera la kumpoto kwa boma la Phalombe a Feston Chauma.

Iwo ati boma laika ndondomeko zothandiza kuti mdziko muno mukhale chakudya chokwanira zomwe zichititse kuti chimangachi chitsike kwambiri.

Mau a Mwanamvekha akudza pomwe Madera ena sanalandirebe zipangizo zotsika mtengo za (FISP) zomwe zikhoza kusemphanitsa loto la laboma kokhala ndi chakudya chokwanira.




Mkulu woona zokopa anthu ku chipani cha MCP a Moses Kunkuyu wati Amalawi tsopano akuyenera kusiyanitsa pa ulamuliro umen...
01/03/2026

Mkulu woona zokopa anthu ku chipani cha MCP a Moses Kunkuyu wati Amalawi tsopano akuyenera kusiyanitsa pa ulamuliro umene uli pano ndi ulamuliro wa mmbuyomu.

A Kumkuyu ati akadakhala kuti amalawi anasankha a Chakwera pano bwenzi a atayamba kale kugawa chakudya koma kuli zii, Pano bwenzi a Chakwera atapita kale kukayendera anthu amene akhudzidwa ndi madzi osefukira ku Nkhotakota koma anthu ali okha.

Iwo amayankhula izi pa mapemphero a padera amene amayi a chipanichi a m'chigawo cha kummwera akonza kupempherera chipanichi komanso utsogoleri wa dziko lino.

A Kunkuyu ati milandu imene atsogoleri a chipanichi akuwaimba ndi yotseketsa koma apempha mamembala a chipanichi kuti akhale odekha panthawiyi.




  Mtsogoleri wa dziko la United States of America Donald Trump wati asilikali ake amanga mtsogoleri wa dziko la Venezuel...
01/03/2026



Mtsogoleri wa dziko la United States of America Donald Trump wati asilikali ake amanga mtsogoleri wa dziko la Venezuela Nicholas Maduro komanso mkazi wake.

Malinga ndi kanema wa Donald Trump polemba pa tsamba lake la X, izi zikutsatira mobomba omwe asilikali a US aphulitsa munzinda wa Caracas.

Dziko la America likudzudzula a Maduro kuti amasunga anthu amene amabweretsa mankhwala ozunguza ubongo m’dziko la America.

Mtsogoleri wa dziko la Venezuela you koma wakhala akutsutsa nkhaniyi ponena kuti America ikungofuna kuba mafuta komanso miyala ina ya mtengo wapatali mdzikolo.

Dziko la America silinanene komwe a Maduro akuwasunga.




U.S. yaphulitsa mabomba mu Capital City ya Venezuela Kwachema!
01/03/2026

U.S. yaphulitsa mabomba mu Capital City ya Venezuela Kwachema!

Nyuzipepala ya Weekend Nation yatsimikiza kuti  bungwe la MRA laimitsa Kaye ntchito yopereka ntchito ya chitetezo ku kam...
01/03/2026

Nyuzipepala ya Weekend Nation yatsimikiza kuti bungwe la MRA laimitsa Kaye ntchito yopereka ntchito ya chitetezo ku kampani ya Masters Security , yomwe ayeni ake ndi a Alfred Gangata,.nduna ya zadziko, Iringa Security Services komanso Kamu Guard Services ya ndalama zokwana 5.4 billion kwacha.




Boma likupitirira kubwereka ngongole zochuluka, ngakhale ilo lomwe lakhala likunena kuti lifuna kusiya kuchita izi.Izi z...
01/03/2026

Boma likupitirira kubwereka ngongole zochuluka, ngakhale ilo lomwe lakhala likunena kuti lifuna kusiya kuchita izi.

Izi zachititsa kuti anthu ofuna ngongole ku ma bank akanike Kutenga ngongolezo kamba koti padakali pano boma lanyamula kale pafupipifupi 80% ya ndalama kumeneko, malingana ndi Malawi News

Izi zichititsanso kuti ngongole ya dziko lino ikwere kuchoka pa 21 trillion pofika ku December Chaka chatha, ndipo ngongole zonsezi ndizobwemzedwa ndi misonkho ya a Malawi.




Bungwe la Public Affairs Committe lati boma likuyenera kuonetsa chamuna pa ntchito yoteteza chuma cha dziko lino ponena ...
01/02/2026

Bungwe la Public Affairs Committe lati boma likuyenera kuonetsa chamuna pa ntchito yoteteza chuma cha dziko lino ponena kuti kutumiza anthu kukagwira ntchito malo ena pa grade imodzi ndikuononga chuma cha boma.

Mneneri wa bungweli a Gilfprd Matonga wati boma likulipira anthu awiri pa ntchito imodzi mu dzina lakutumiza munthu kukagwira ntchito kwina popanda kusintha malipiro awo.

Iwo ati izi sidzikugwirizana ndi kuteteza chuma cha boma ndipo m'modzi pa awiriwo amayenera kuchotsedwa ntchito

Mneneri wa boma a Shadreck Namalomba wati afufuze Kaye asanayankhe koma wagwirizana ndi PAC kuti ikunena zoona ndipo nkhaniyi ayiunikira bwino.




Bungwe la Malawi Revenue Authority lati siliperekanso ntchito yopereka chitetezo ku kampani zitatu zomwe zimagwira ntchi...
01/02/2026

Bungwe la Malawi Revenue Authority lati siliperekanso ntchito yopereka chitetezo ku kampani zitatu zomwe zimagwira ntchitozi mdziko muno.

Mu kalata yomwe tawona ,bungweli kudzera mu komiti yake ya Internal Procurement and Disposal of Assets sinanene zifukwa zomwe yasinthira ganizoli m'malo mwake yangoti ntchitoyi ayilengezetsanso.

Kampani zitatu, Masters Security, Iringa Security komanso Kamu Guard Services zikanalandira ntchitoyi pa mtengo wa 5.4 billion kwacha kwa miyezi 24 kuti zipereke chitetezo ku maofesi a bungweli mzigawo zonse zamdziko muno.

Mabungwe omwe si aboma koma monga la HRDC, National.Advocacy Plartform ksmso CSAT anatsutsana kwanthunthu ndi ganizoli ponena kuti siinalengezedwe bwino lomwe.

Mneneri wa bungwe MRA a Wilma Chalulu koma anati ntchitoyi inalengezedwa bwino lomwe pa 25 November Chaka chatha ndipo kampani zosiyanasiyana zinapereka mitengo ya momwe zingagwirire ntchitozi.




01/02/2026

Bungwe loona za Misewu mdziko muno la Roads Authority ladzudzula anthu amene akulima mphepete kwambiri mwa msewu ponena kuti akuthandizira pakuonongeka kwa Misewu mdziko muno.

M'modzi mwa akulu a bungweli a Joel Longwe anena izi pomwe bungweli lakonza msewu wonhoyembekezera pa Mpasadzi m'boma la Kasungu kutsatira kuduka kwa msewu lunayambira kwa sabata ino.

Iwo ati zoterezi zimalepheretsa bungweli kutakasakuka pogwira ntchito zake.

Padakali pano bungweli lakonza msewu wonhoyembekezera pamalopa ndipo galimoto zayamba kudutsa pang'ono pang'ono.




01/02/2026

Ken Msonda wachiwiri wa mneneri wa chipani Cha MCP wang'alula chipani Cha DPP akuti chikungofuna njira yobera ndalama zakafukufuku ya ngozi ya ndenge yomwe boma la DPP lalonjeza kuchita.

Nyuzipepala ya Nation yati Ofesi ya wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yazemba kuyankha ngati Wachiwiri kwa mtsogole...
01/02/2026

Nyuzipepala ya Nation yati Ofesi ya wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino yazemba kuyankha ngati Wachiwiri kwa mtsogoleriyu Mayi Jane Ansah amagwiritsa ntchito ndalama za boma paulendo wawo wa ku UK kapena ayi.

Izi zikuchitika pomwe lachiwiri mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika anati mayi Ansah anawatsimikizira kuti paulendowu agwiritsa ntchito ndalama zawo.

Mauwa awutsanso phokoso chifukwa akusiyana ndi zomwe nduna yazofalitsa nkhani a Shadrick Namalomba adanena kuti mayi Ansah agwiritsa ntchito 168 million kwacha pa ulendo onsewu.

A Joshua Chisambere akuti akugwirizana ndi zomwe a Mutharika ananena zokhuza ndalama za pa ulendowu ponena kuti Mayi Ansah ndi munthu womvetsetsa pomwe a Onjezani Kenani akuti mtsogoleri wa dziko lino ananamizidwa kuti mayi Ansah anagwiritsa ntchito ndalama zawo.

Mayi Ansah anachoka mdziko muno pa 26 December ndipo akuyembekezeka kubwerera mdziko muno pa 10 January.




Address

United State Of American
Indianapolis, IN

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Live Today posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share