Malawi Live Today

Malawi Live Today Malawi Live Today is the platform that gives you a straightforward and entertaining look at what's happening in politics.

Please Like/Follow our Malawi Live Today page for daily updates on the top political stories and breaking news.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko Lino Dr Jane Ansah wati mdziko muno muli Anthu omwe anabadwa akafula Koma ali ndi nzer...
06/12/2026

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko Lino Dr Jane Ansah wati mdziko muno muli Anthu omwe anabadwa akafula Koma ali ndi nzeru kuposa Anthu omwe anabadwa atali.

Iwo ati kufupika ndi nzeru ndi zinthu ziwiri zosiyana pomwe akafura amachitanso Bwino pa maphunziro awo.

“Pakati pathu pano tili naye mzathu kafula anakhonza 14 points pa Mayeso ake a MSCE, pomwe inu ndi ine sitinayipate 14 points yo. Kapena alipo pakati pathu pano amene anabadwa wamtali anakhonza 14 points ayimilire??, anafunsa Dr Ansah.

Pa mwambowu Pali akafula kuchokera ku chigawo chaku mpoto, pakati ndi kumwera.




Sipikala wanyumba ya malamulo walengeza kuti aphungu anyumba ya malamulo achita zokambirana zawo kuyambira pa 7 July mpa...
06/12/2026

Sipikala wanyumba ya malamulo walengeza kuti aphungu anyumba ya malamulo achita zokambirana zawo kuyambira pa 7 July mpaka pa 31 July 2026.

Malingana ndi kalata yomwe sipikalayu Samir Suleman watulutsa, zokambiranazi zidzachitikira kunyumba ya malamulo munzinda wa Lilongwe.

Mneneri wa nyumbayi Ian Mwenye wati mkumanowu aphungu akuyembekezeka kukambirana za malipoti amakomiti anyumba ya malamulo, malipoti ammaunduna komanso ma bilu.

Koma Mwenye wati pakadali pano mndandanda wa zinthu zomwe zikambidwe sizinadziwike kaamba koti komiti yoyendetsera zokambirana zanyumbayi ikadakonza.

Zokambiranazi ndi zachitatu mumkumano wa chinamba 52 wa aphungu anyumba ya malamulo.




06/12/2026

A Moses Kumkuyu ati chisankho chomwe anthu anachita mdziko muno anachita atatsogoleredwa ndi bodza

Iwo ati mwachitsanzo litangolowa boma latsopano la DPP mafuta anakwera mtengo kwambiri .

Iwo atinso zikukaikitsa ngati alimi atalimenso Chaka chanawa kamba koti mitengo ya mbeu pa msika yatsika kwambiri.



Today

A Moses Kumkuyu akuti ndiodabwa kumva kuti ulendo wa professor Arthur Peter Mutharika wa ku South Africa  ndi wa private...
06/12/2026

A Moses Kumkuyu akuti ndiodabwa kumva kuti ulendo wa professor Arthur Peter Mutharika wa ku South Africa ndi wa private visit.

Iwo akuti pamene amaona kalata ya ulendo wa a Mutharika anali onyadila kuti mkutheka akukakonza vuto la Xenophobia ku South Africa. Koma Iwo akuti sanakhutile kuona kumapeto kwa kalatayi kunena kuti akuyendela Ulendo wao wa private.

Malingana ndi a Moses Kumkuyu, dziko la Malawi lidakatenga mwai wa ubale wa SADC kukambilana ndi dziko la South Africa kuti liganizile za nkhaza zomwe a Malawi akulandila mdzikolo.

Iwo akuti sakulilila kuti a Malawi adzikhala ku South Africa koma ufulu wao kukuyenera kulemekezedwanso.

Iwo alankhula izi pa tsamba lawo la m'chezo.


Mtsogoleli wa dziko lino professor Arthur Peter Mutharika akhala akupita mdziko la South Africa lelo masana.Malingana nd...
06/12/2026

Mtsogoleli wa dziko lino professor Arthur Peter Mutharika akhala akupita mdziko la South Africa lelo masana.

Malingana ndi kalata yomwe tsamba lino laona yosayinidwa ndi mlembi wamkulu wa boma Dr Justin saidi , ulendowu ndi wa private.

Mtsogoleri wa dzikolinoyu anyamuka nthawi ya 2 Koloko masana kudzela pa bwalo la ndege la Kamuzu.


Nkhani ya pempho la kafukufuku oti  achitike pa Director General wa ACB sikuoneka tsogolo pomwe  pomwe adindo ena akuti ...
06/12/2026

Nkhani ya pempho la kafukufuku oti achitike pa Director General wa ACB sikuoneka tsogolo pomwe pomwe adindo ena akuti sanalandile uthenga ulionse.

Nkhaniyi yasindikizidwa mu nyuzipepala ya Times.


Nyuzipepala ya Nation yakhazikika pa nkhani ya ntchito za migodi mdziko muno.
06/12/2026

Nyuzipepala ya Nation yakhazikika pa nkhani ya ntchito za migodi mdziko muno.


06/12/2026

Bon Kalindo lero pa 12 June kung'alula za imfa ya Saulos Chilima.

Mavuto akakamila chipani cha MCP chomwe mtsogoleli wake ndi Dr Lazarus Chakwera. Izi zaoneka pamene a Jones Chamangwana ...
06/11/2026

Mavuto akakamila chipani cha MCP chomwe mtsogoleli wake ndi Dr Lazarus Chakwera.

Izi zaoneka pamene a Jones Chamangwana atula pansi udindo wa wachiwiri wa gavanala m'chipanichi ku chigao cha ku mmawa komanso kutuluka chipani cha MCP.

Kuphatikiza apo iwo apangitsa chipani cha MCP kuwelenga madzi a mphutsi pamene anenanso kuti saimilanso pa chisankho chomwe chichitike mdela la Balaka Mulunguzi pa mpando wa phungu wa nyumba ya malamulo.

Padakali pano iwo sadanene chifukwa chomwe apangila izi.


 Gulu la mabungwe omwe siaboma likuti anthu sanaiwale za zoipa zomwe zinachitika mu ulamulilo wa MCP.Mabungwewa akuti sa...
06/11/2026



Gulu la mabungwe omwe siaboma likuti anthu sanaiwale za zoipa zomwe zinachitika mu ulamulilo wa MCP.

Mabungwewa akuti sakufuna dziko kumangobweleza mavuto ofanana. Anatchula nkhani yogula fertilizer ku kampani yopanga za butchale kuti zinali zoipa.

Koma iwo akuti mmene zachitikila ku ESCOM zaonetselatu kuti dziko likutsatilabe ndondomeko zoipa. Izi akuti zipangitsa kupeleka ntchito kwa ma kampani osayenela.

Pa ichi Iwo apempha mtsogoleli wadziko kuti asalole kunamizidwa ndi alangizi ena amene safunila dziko lino zabwino.

Iwo akuti alole bungwe la ESCOM kupanga ziganizo mwa ukadaulo lao.


Address

United State Of American
Indianapolis, IN

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Live Today posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share