Malawi 1st Headlines

  • Home
  • Malawi 1st Headlines

Malawi 1st Headlines News and Entertainment

Nkhamu la undipondera mwana lasonkhana pa bwalo la za masewero la Dowa boma pomwe pakhale nsonkhano wa chipani cha Malaw...
25/05/2025

Nkhamu la undipondera mwana lasonkhana pa bwalo la za masewero la Dowa boma pomwe pakhale nsonkhano wa chipani cha Malawi Congress (MCP).

Alendo olemekezeka pa nsonkhanowu ndi mlembi wa mkulu wachipanichi yemwenso ndi nduna ya za maboma ang'ono ang'ono ndi chikhalidwe a Richard Chimwendo Banda komanso nduna ya za ulimi a Sam Dalitso Kawale.

Nsonkhanowu wabweletsanso pamodzi anthu odziwika ena monga nduna yoona zakusasiyana pakati pa amayi ndi abambo a Jean Sendeza ndi wachiwiri wake a Halima Daudi, nduna ya za malo a Deus Gumba, Mkulu wa achinyamata Steven Baba Malondera komanso a Patrick Zebron Chilondora yemwe ndi Region Chair wachipanichi.

14/12/2023

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipani cha DPP yemwenso ndi mtsogoleri wotsutsa boma nyumba yamalamulo a Kondwani Nankhumwa wati ndi wokonzeka kukapikisana ndi a Peter Mutharika ku msonkhano waukulu wosankha atsogoleri a chipanichi.

A Nankhumwa, mu chikalata chimene atulutsa, ati ndi okondwa kuti bata m'chipani cha DPP layamba kubwera tsopano.

Iwo ayamikira a Mutharika pozindikira kufunika kwa malamulo komanso kuonetsetsa kuti chisankho chosankha atsogolerichi chachitika pasanathe masiku 90, ngati mmene bwalo la milandu lidanenera.

Koma a Nankhumwa, m'chikalatachi, adabwa kuti n'chifukwa chani mbali ya a Mutharika sadakhazikitse komiti yoyendetsa chisankhochi ponena kuti kungokhazikitsa komiti yobweretsa bata kukubweretsa mafunso ambiri.

A Nankhumwa ati akufuna chisankhochi chidzayende bwino ndipo onse opikisana apatsidwe mpata.

14/12/2023

Kampani ya network za lamya za m'manja ya Telekom Networks Malawi (TNM) yalengeza kuti yakweza mitengo ya mabandulo ake.

Malingana ndi uthenga omwe kampaniyi yatulutsa yati kukwezaku kukuyamba mawa lino pa 15 December 2023.

Kampaniyi yakweza mitengoyi ndi pafupifupi 20 kwacha pa 100 kwacha iliyonse.

Iyo yati izi achita malinga ndi kugwa kwa mphamvu ya ndalama ya kwacha mwezi wapitawu.

45 students from Lunzu Secondary School are receiving treatment at Mlambe Hospital in Blantyre on suspected food poisoni...
25/09/2023

45 students from Lunzu Secondary School are receiving treatment at Mlambe Hospital in Blantyre on suspected food poisoning.

The three of them have been admitted for observation while the 42 have been sent back to the school campus, according to confirmed reports from the ministry of education.

Spokesperson for the ministry of education Mphatso Nkuonela says the ministry has temporarily suspended the use of all food items at the school.

Address


Opening Hours

Monday 06:00 - 18:00
Tuesday 06:00 - 18:00
Wednesday 06:00 - 18:00
Thursday 06:00 - 18:00
Friday 06:00 - 18:00
Saturday 06:00 - 18:00
Sunday 06:00 - 18:00

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi 1st Headlines posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

  • Address
  • Opening Hours
  • Alerts
  • Claim ownership or report listing
  • Want your business to be the top-listed Media Company?

Share