FUKIZ MW

FUKIZ MW Home of good stories

Laika wayamba kundimvetsa chisoni😪😪😪.----Chetee kuona ma photos ake akale
19/08/2026

Laika wayamba kundimvetsa chisoni😪😪😪.
----
Chetee kuona ma photos ake akale

"MUNDISAMALIRE PICTURE-YO" 💔___________________________________PART 9Written by Fukiz mw _____________________Izi zinaya...
18/08/2026

"MUNDISAMALIRE PICTURE-YO" 💔
___________________________________


PART 9


Written by Fukiz mw
_____________________

Izi zinayamba kundipatsa mantha kufikila tsiku la 5 lomwe ndimamva kupweteka ndikamakodza. Mikodzo ikandipola ndimachita kudela nkhawa kuti ndikakodzenso. Maganizo amandipeza kuti ndiwauze Agogo anga koma pena ndimazibweza . Izi zinandipangitsa kucheza masiku ochepa kenako ndinaganiza zobwerera ku Blantyre .

Ndinauyamba ulendo obwera kunyumba . Ndili bus ndinayamba kulingalira . " Ndakhala ndilipachibwazi ndi Sosten kwadzaka 8 . Kuchoka form 1 mpaka kukafika ku university koma sanandipatse matenda aliwonse . Uyu ndadziwananaye kumene miyezi itatu sinathe koma wandipatsakale matenda , tidziti palitsogolo apa?" Ndinapumila m'mwamba uku ndikuomba m'manja modzidandaulira . Kenako ndinayamba kudzifusa ndekhandekha .

"Laika ndye utanino pamenepa?"

Ndinatero ndikungolumaluma chalachanga . Kenako ndinati .

"Laika ukuyenera kuzemba ukwati umenewu."

Bus inayenda kufikila ndinakafika ku Blantyre chama 3 koloko masana . Nditafika pa gate yakwathu , ndinagogoda ndipo Achisale ananditsekulira . Atatsekula gate ndinaona Mamie ndi dad akuvina kusonyeza kuti alimchisangalalaro. Atandiona anandithanangira ndikuzandikumbatira. Kenako anandigwira mkono uku akuvinabe . Titalowa mnyumba anandionetsa malowolo omwe Uncle a Fukiz anabwera kuzasiya. Atatha kundionetsa amayi anayankhula alindichimwemwe ndipo anati:

"Sizokhazitu ayi, galimoto ya Ng'ombe 6 yanyamukakale kukasiya Ng'ombe-zo kwawo kwa Bambo ako."

Ndinazikakamiza kumwetulira, kenako ndinawatsamzika kuti ndikupita ku chipinda changa ndikapume . Ndinatenga handbag yanga ndikupita kuchipinda kukakhala pa bed langa chete uku ndikulingalira zothana ndi nthenda ija, chifukwa imandichititsa mantha. Ndilimkati molingalira ndinaona chitseko cha chipinda changa chikutsekuka uku mkulu wanga akuyankhula .

"Lai, osandiyimbila phone kuti......."

Anadukiza mau atandiona kuti ndikupukuta misozi kuti asayione. Nthawi yomweyo anabwera pa bed langa paja ndikuzakhala pambali uku akundifusa .

"Chavuta ndichani Laika?"

Ndinangokhala chete sindinamuyankhe koma misozi imatuluka. Kenako anandifusanso.

"Mphwanga tatena , kapena misoziyi ndiyachisangalaro kuti Fukiz ali serious zokukwatira eti?"

Ndinagwedeza mutu kusonyeza kukana . Nthawi yomweyo anandifusanso .

"Nanga ndichani tanenatu."

Anatero akutenga mutuwanga kugoneka pantima pake. Kenako ndinati.

"Flora,(Ma Peace) ndavulala."

"Wavulala pati? Bus yomwe munakwera munachita ngozi?😳"

Anandifusa mafuso awiri uku akundiyang'ana modabwa. Ndye pokuti kubisa matenda kuja ndi mtendere , ndinayimilira ndikuvula zovala zanga ndikumuonetsa. Atandiona zinamuopsa of course koma anapanga ngati munthu wamkulu kuti asandiopseze . Kenako anati:

"Siiwe oyamba dear , koma unamufotokozera doctor wa adad uja?"

"Ayi sindinamuyimbire chifukwa sindikufuna adad ndi Mamie adziwe."

"Usandiuze kuti ndi fukiz-tu"

"Ndyemweyo"

Anapumilamwamba kenako anati :

"Basi siyani kulirako, pukutani misoziyi tidzipita kuchipatala."

Tonse tinayimilira ndikuzikomzabwinobwino ndikutuluka kukatenga galimoto wakuchipatala. Titafika ndikumufotokozera Namwino , anandipatsa mankhwala okumwa komanso anasakaniza mankhwala ake muchijekison chachikulu chomwe anandibaya (Jenta). Ndinayamba ndakhalakaye pansi kufikila ululu utachepa. Kenako tinakwera galimoto kumabwerera kunyumba uku ndikumuuza Flora kuti :

"Ukwati uwu ndiuzemba"

Ngakhale ndinayankhula izi Flora sanandiyankhe amangoyendetsa galimoto. Sindikudziwa kuti m'mutu mwake mumkayenda chani panthawi imeneyi.

---

Masiku anapanga sabata ndipo masabata anapanga miyezi itatu. Pa miyezi itatu imeneyi, ubwezi wa ine ndi Fukiz unalibwinobe chifukwa ine ndimafuna nditathetsa ubweziwu kamba kokuti amandikana kuti sanandipatsire chizonono koma makolo anga amamuyikila kumbuyo Fukiz ngati ndimwana wawo weniweni kusiya ine . Zokamba zaine samamva koma amakhulupulira za Fukiz basi . Pa miyezi itatu yomweyo ndinali nditamisa period yanga zomwe zimatanthauza kuti ndiine oyembekezera. Thupi langa linayamba kufooka chifukwa chakudwaladwala. Week ino ndinatsekula m'mimba , week yamawa chimakhala chifuwa. Ndikachoka pa chifukwa ma rashes thupi langa lonse. Ngakhale izi zimandichitikila , makolo anga diso lawo amayang'ana zaukwati wanga basi omwe umafuna kuchitika mwezi otsatilawo. Ndye pokuti masiku anayandikila , analumikizana ndi designer waku South Africa kuti atipangire zovala ine ndi Fukiz zokuti tizavale pa ukwati . Kotero tsiku limenero tinanyamuka kuwapelekeza mamie ndi a Dad ku Bakili Muluzi international airport (Chileka) kuti azikapita kukakumana ndi Designer.

Titafika ku Airport tinatsika galimoto ndikuwapelekeza makolo athu mkati kuti akadinditse passport. Kumeneko tinapeza mzere ndithu wa Amwenye , amzungu ndi anthu okudafe. Titalowa mkati muja ndinaona Ma Peace akundikodola pa phewa.

"Lai, Laika wamuona Sosten?"

Anayankhula motsitsa mau. Ndinamwazamwaza maso koma sindimamuona. Kenako nanenso ndinamufusa motsitsa mau.

"Alikutiko?"

"Uyo mkatimo."

Nditaponya maso ndinamuona Sosten alibusy kudinda ma passport uku atavala Uniform ya immigration . Ntima wanga unagunda mwakamodzi ndikamodzi uku ndikudzifusa. "Zakhala bwanji Sosten kuyamba ntchito kuno? Ma connection amenewo wamupatsa ndani popeza kwawo ngati kuli ophunzira ndiyeyo?" Ndye pokuti Flora anabadwa mojijilikilako pang'ono kusiyana ndiine , ananyamuka kukakhala pamzeke ngati akukadinditsa passport uku atamutenga mwana wanga. Atafika iye anati:

"Mlamu, Clara akufuna Ice cream 🍦 "

Sosten anawayangana akumwetulira kenako anati:

"Ice cream apezeka koma andidikile pang'ono panjapo pokuti lunch time yafikakale."

Pomwe Sosten anayankha izi , Mamie anamuyitana Flora. Flora atapita , Mamie anati:

"Ma Peace, muzizipatsa ulemu , mlamu wanu monga simukumudziwa?"

"Ine ndi Sosten chilamu sichidzatha chifukwa tilindimagazi ake awa."

Anatero akumuloza Clara. Kenako amayi anayankhula mokwiya .

"Basi mwatipelekeza dzipitani kunyumba pompano."

Anatero akupita kukakwera Ndege. Ifenso tinanyamuka kupita pomwe tinayimitsa galimoto . Titafika ine ndinakwera galimoto koma Flora sanakwere analipanja ndi mwana wanga. Mosataya nthawi ndinaliza galimoto kuti mwina akamva kuti yalira abwera akwera , koma ndinadabwa akubwera pawindo ndikundifusa modabwa.

"Ukuliza galimoto ukupita kuti?"

"Kunyumba , bwanji?"

"Ayi dikilani mwana awonane ndi bambo ake."

Kenako ndinazimitsa galimoto ija ndikugejemula mpando ndikugona kumaseweretsa phone yanga. Lunch time itakwana ndinamuona Sosten akutuluka ndikubwera komwe kunali ife kuja . Anamunyamula Clara ndikubwera komwe kunali ine kuja uku phone yake akulira nyimbo ya Quaso(mbali yakuno the grass is greener). Anayenda kufika pa window kuzandipatsa moni wapamanja . Mwamanyazi ndinalandira chifukwa iye sanasunge mangawa kuti ndinamuthamangitsa kunyumba kwathu. Nditalandira moni wapadzanja uja, anabwerera kumakacheza ndi Flora uku akumulumphitsa mwana wake m'mwamba komanso kutoletsa ma photo. Mosatenga nthawi onse anayamba kudinadina pa phone kenako ndinamva akufusana ndi Flora.

"Yafika?"

"Eya yafika."

Pomwe amayankhula mau awa , ndinadziwa kuti akutumizilana ndalama. Zonse zitatheka , Flora ananyamuka kubwera komwe kunali galimoto kuja koma Clara akuwalilira bambo ake. Atakwera tinanyamuka kumabwerera kunyumba . Kenako anati:

"Mlamu wanditumizira K100 thousand akuti ya Ice cream. "

Sindinamuyankhe , ndimangoyendetsa galimoto zangaphe. Ndye chifukwa chokuti amangokamba nkhani ekhaekha koma ine sindimamuyankha , anadabwanazo ndipo anandifusa.

"Laika , phee ameneyu ukuganiza zichani?

Ndinapumila m'mwamba Kenako ndinati:

"Ukwati wangawu, ndiuzemba."

"Laika , aka ndikachiwiri ukundiuza kuti ukwati umenewu uwuzemba. Ukutanthauza chani ndipo uwuzemba motani?"

"Inenso sindikudziwayi koma ndiuzemba."

"Ukufuna uthawire kunja ? Ndye uthawira dziko lake litiro?"

"Sindikudziwa Darling."

Kenako tinayenda mpaka kukafika kunyumba komwe ndinapeza Fukiz wafika. Ndinapita pampando omwe anakhalawo ndikumakacheza uku tikukambirana nkhani za mimba yomwe ndinalinayo . Kenako Ma Peace pomwe amadutsa anayima ndipo anati:

"Komatu muziuzananso tsiku linayamba scale osamangokhala. Amakukalipiratu ukayamba scale mochedwa wekha ukudziwanso Laika."

"Eya ndikudziwa ndikayamba scale week yamawa. "

Tinacheza ndi Fukiz kufikila anatsamzika kumapita.

----

Week imodzi inadutsa . Ndipo week imeneyo, kunsana kwanga kunatuluka matuza ang'ono ang'ono koma ootcha ndiopweteka kwambiri . Ndye pokuti linali tsiku lomwe ndimafuna kukayamba scale , ndinaganiza kuti komko ndikamuonetse Doctor . Nditafika kuchipatala , ndinamufotokozera Namwino ndipo iye anandiuza kuti zomwe zanditulukazo ndimashingozi. Kenako anandipatsa mankhwala opaka komanso okumwa.

Nditatuluka kumeneko ndinapita kukapanga za Scale , koma Namwino wakumeneko anati sindingayambe scale ndisanayezetse . Izi zinandikakamiza kupita room yomwe amayezera magazi, ndipo atandiyeza, anandipeza kuti ndili ndikachirombo kuyambitsa AIDS.............


Tikumanenso mu part 10.


Ma Truck driver omwe akukambidwa munkhaniyi , ndi akumayiko akunja osati kwathu kuno kumalawi . Izi zilichonchi chifukwa ma truck driver akwathu kuno ndiodziletsa kwambiri komanso sapanganawo kusaweluzikaku . Inu amene muli ma Truck driver komanso azikazi ama truck driver, nkhaniyi musayitengere ayi ndimacheza chabe komanso ndinkhani zongopeka chabe izi. 🤸🤸

Ikupitilira.........


FUKIZ MW

Subscribe to get exclusive benefits:
https://www.facebook.com/100087613834930/subscribenow

18/08/2026

20:00

18/08/2026

Tsiku langa likuyendabwino , kaya tsiku lanu likuyenda bwanji?

"MUNDISAMALIRE PICTURE-YO" 💔 ___________________________________PART 8________Written by Fukiz mw _____________________F...
17/08/2026

"MUNDISAMALIRE PICTURE-YO" 💔
___________________________________


PART 8
________


Written by Fukiz mw
_____________________

Fukiz sanayankhe anangondigwira mkono ndikulowa mkati mwa KFC ija. Kenako anandisiya pampando iye ndikupita kukapanga order . Ndinakhala pampando ndisakusangalala kufikila anandipeza ndiliokhumudwa. Anayima kundiyang'ana kenako anandifusa .

"Are you ok?"

Ndinagwedeza mutu kusonyeza kuvomera kuti ndilibwinobwino. Sindimafuna kuonetsara kuti ndakwiya chifukwa ubwezi wathu unali ukuyamba kumene. Kenako ananjuta ndikuzagwira mkono wanga ndikuzati:

"Osazitengera zomwe amanena mzanga uja , chifukwa amacheza mopusa. "

"Inetu sindinakwiyeyi"

Ndinayankha motsitsa mau uku nditazolika pansi.

"Koma nkhope yako ikundiuza zambiri zomwe zilimkati mwantima wako ."

Kenako anayamba kumandinyengerera kufikila ndinabwerera mu mood mpaka anakatenga chakudya tinayamba kudya. Tilimkati mocheza anandifusa .

"Kodi dear , mawa iyenda bwanji?"

"Mawa ndikufuna ndipite kwa Jenda ndikawaone Agogo anga. Nanga iwe iyenda bwanji?"

Asanandiyankhe phone yake inayitana . Atapanga check anaona kuti ndi bambo ake . Nthawi yomweyo anayankha .

"Yes dad"

Bambo ake aja anamufotokozera kuti truck amaliza kuloda ndye mawa mam'mawa akuyenera anyamuke azipita ku Tanzania. Atadula phone ija anandiyang'ana kenako anati:

"Dear , mawa ndikuuyamba ulendo wanga waku Tanzania kukatula katundu wa company inayake . "

"Ubwerako litiro?"

"I don't know."

"Ok fine ndikufunila kuyenda ndambuye."

"Zokhazo basi?"

Anandifusa akundiyang'anitsitsa. Nthawi yomweyo ndinamufusa

"Umayembekezera chani?"

Anandiyang'ana m'maso kwambiri zomwe zinachititsa ine kuzolika pansi chifukwa ndinadziwa zomwe amafuna . Kenako anati:

"Lero ndikagone kwanu kapena ukagona kwathu?"

Ndinayang'ana kumbali uku ndikuseweretsa ma nails 💅 anga chifukwa yankho limandivuta kenako ndinati:

"Wina aliyense akagone kwawo."

"Why? Ndimaona ngati titsamzikanetu pa ulendo wangawu."

"Kutsamzikana kwake kotani koposera komwe tikutsanzikilana panomu? "

"Lai , ukudziwa chomwe ndikutanthauza , usamakhalengati mwanayi. Kapena sunandilandire ndi manja awiri muntima mwako?"

"Ine ndatero?"

"Sinanga ndikudabwa."

"Ok basi titsanzikana mawa chifukwa tikhala limodzi paulendowu . Sinditenganso galimoto yanga ija ayi. Ndikweranawo truck yanuyo ukanditsitsa pa Kasungu iwe uzikapitiliza ulendo wako."

Nditakamba izi anayimilira ndikundipatsa kiss patsaya . Kenako tinatuluka ndikukakwera galimoto ndikupita kwawo kukamusiya . Mosataya nthawi ndinabwerera kupita kunyumba komwe ndinadya ndikugona .

---

M'mawa kutacha tinayimbilana mafoni mpaka tinakakumana ku company komwe kunali truck kuja. Mosataya nthawi tinanyamuka ulendo wathu . Titafika pa Zalewa ndimangomva mau azimayi panja akumuhaka Fiancé wanga.

"Umakwana Fuki!!"

Fukiz sanayankhe koma analiza horn 📯 po! po! uku akupitiliza ulendo wathu . Tinayenda mpaka kukafika pa Balaka market pa Chikondi stop over . Anatsika kukagula tizokumwa . Alikumenekuja ndipamene ndimawamva azimayi apamenepo akuyankhula ndi Fiancé wanga .

"Fuki, tandigulireni kuchekuche muwiri"

"Aaah sorry ndilibe ndlama."

"Munayamba kuumila masiku ano inu."

Anangoseka kenako anabwera kuzakwera truck ija ndikunyamuka . Ntima unandipweteka ndipo ndinamufusa .

"Azimayi aja amakupempha ngati ndaniwawo?"

"Aaah afisi aku Ntcheu ameneuja(mahule)"

Atayankha izi tinayamba kucheza nkhani zathu ndikumaseka mpaka tinafika mu Lilongwe pa 6 miles pomwe anayimika truck ndikupita pa filling station. Sindikudziwa kuti amakatani koma ine anandisiya mu truck momwemuja chifukwa anandiuza kuti sakachedwa. Kenako ndinachoka pampando kupita pa bed kukagona uku ndikuseweretsa phone yanga. Mosataya nthawi , ndinamva mau achikazi akuyankhulana panja uku akufusana.

"Truck iyi ya Fukiz eti?"

"Eya ndiyomweyi."

Mosataya nthawi ndinamumva akugwiragwira chitseko . Izi zinandipangitsa kuchoka pa bed ndikusuzumila . Nditasuzumila ndinaphana maso ndi mzimayi m'modzi onenepa ndithu . Atandiona anatsekula chitseko ndikulowa . M'malo mokuti ine ndimufuse anayamba kundifusa ndiyeyo mokwiya.

"Ukupanga chani muno?"

Ine podzimva u MG1 ndinamuyankhanso mokula ntima .

"Ineyo ndamene ndikuyenera kukufusani kuti mukufuna chani muno?"

"Ukubweza moto? Uhule wanuwo muzipangila komko malire pa Dedza , mukalowa Lilongwe uno , mumakhala kuti mwalowa Territory yanga."

"Ndinu amayi ochititsa manyazi , m'malo mopeza mamuna wanu mulibusy ndi amuna amzanu mahule inu."

Ndikanadziwa mau okuti mahule sindikanalankhula . Anandigwira ndikundisumba ndimutu pachipumi . Ndinachoka pampando kupita pa bed ananditsatila komko kundiponda pansana uku atagwira madredi omwe ndinamanga. Chifukwa chakumva kuwawa ndinaphuluphutha . Kenako anandisama pakhosi kwinaku akundifusa.

"Ndiwe ukumapangitsa kuti Fukiz asamayankhe ma call anga eti? "

"Siine Aunt!"

Ndinatero chifukwa anali m'mayi wamkulube kusiyana ndiine . Mosataya nthawi ndinaona Fukiz, atalowa mu truck muja , kenako anakanganula mkono wanayi uja pakhosi panga. Anamukoka mpaka panja pa truck .

Nthawi yomweyo ndinadzuka pa bed paja ndikusisima. Kenako ndinayamba kulongedza zinthu zanga kuti ndituluke ndikakwere minibus ndipitilize ulendo wanga. Ndilibusy kuyangna handbag yanga ndinamumva mzimayi uja akumufusa Fiance wanga uja.

"Fukiz , sumandiyankha ma calls anga chifukwa cha mbululu-yi? (tadpole) Ndye ukamandizemba ndye ukuganiza kuti mwana wako uja azidya chani? "

Mzimayi uja atakamba izi ndinazifusa muntima . "Kodi Fukiz alindimwana ?😳" Mosatenga nthawi ndinatenga handbag yanga ndikutsekula chitseko cholinga ndituluke . Fukiz atandiona anathamanga kumazandibweza kuti ndisatsike .

"Please Laika, usatsike tiyeni tidzipita basi zatha."

"Ayi basi, kwatsalaku ndiyenda pa minibus."

"Ayi tsalani ndi akazanuwo."

Ndinayankhula ndikusisima . Kenako anabwera kuzandigwira ndikundibwezeletsa mu truck kenako ndipo anati:

"Ameneuja simkazi wanga , koma chinali chibwezi changa mpaka ndinachibelekela mwana . Please Laika , tisakhale busy ndinkhani zomwe zinachitika iwe ndi ine tisanakumane , chifukwa komwe iwe ukuchokera ulindimbiri yako, inenso komwe ndikuchokera ndili ndimbiri yanga . Ndye ndimaganiza kuti mbiri zonsezi tizifufute tiyambe moyo watsopano ndi banja latsopano. Ine ndikukonda posatengera zambuyo mwako kuti umayenda ndindani . Ndye nawenso ukonde Fukiz walero. "

"Koma ngati wafika pondimenya kusonyeza kuti simunathane kaya."

Ndinatero uku nditagwira chipumi changa pomwe anandisumba paja. Nthawi yomweyo Fukiz anayamba kuyendetsa truck kuchoka pamalo paja . Pomwe timachoka mkuti mzimayi uja atachokansonaye koma anauzidwa kuti ndiine mkazi wa Fukiz. Tinayenda mpaka tinakagona mu Dowa momwe ndinamupatsa ma key 🗝️ athupi langa kuti aliseweretse momwe angafunire .

M'mawa kutacha tinapitiliza ulendo wathu omwe ananditsitsila pa Kasungu iye kutenga nsewu opita ku Ntchisi pamene ine ndinakwera zopita kwa Jenda Mzimba .

-----

Masiku atatu anadutsa ndili mkumzimba kuja . Panthawi imeneyi mkuti Fukiz atachoka pa Songwe border kulowerera mu Tanzania . Pamasiku amenewo ndinayamba kumva kunyerenyetsa private part yanga . Izi ndimangozisiya chifukwa sindimamva kupweteka . Litadutsa tsiku limodzi, ndinaona kuti ndikupanga discharge mafinya from my private part. Izi zinayamba kundipatsa mantha kufikila tsiku la 5 lomwe ndinamva kupweteka ndikamakodza. Mikodzo ikandipola ndimachita kudela nkhawa kuti ndikakodzenso.................


Tikumanenso mu part 9


Wakumananazo ,  amayenda m'mbali Laika  . Amupeza mu truck momwemo 🙈🙈
17/08/2026

Wakumananazo , amayenda m'mbali Laika . Amupeza mu truck momwemo 🙈🙈

Akuti "mukutibweretsera zimwemwe zachilendo  m'manyumbamu" 🤣🤣🤣🤣🤣🤣🤣🤣-----Mwachidule ndingoti zikomo kwambiri kwanonse omw...
17/08/2026

Akuti "mukutibweretsera zimwemwe zachilendo m'manyumbamu" 🤣🤣🤣🤣🤣🤣🤣🤣

-----

Mwachidule ndingoti zikomo kwambiri kwanonse omwe mumakonda nkhani zanga , ndimakunyadiranso heavy 🤸🤸🤸🤸


Tsikulanu mwaliyamba bwaa?

MUNDISAMALIRE PICTURE-YO 💔 _____________________________________PART 7________Written by Fukiz _________________"Osadzab...
16/08/2026

MUNDISAMALIRE PICTURE-YO 💔
_____________________________________


PART 7
________


Written by Fukiz
_________________

"Osadzabweranso kuno ndipo usadzayelekeze kubwera kuzati ukudzaona mwana chifukwa mwana ndilera ndekha, lucky enough sunapeleke malowolo kapolo wachabechabe maso akuluakulu wamva?"

Atatero anatseka gate ija moyimenyetsa kuti phaaaa. Nthawi yomweyo ndinasasa fumbi Nsapato zanga ngati njira imodzi yokuti sundidzapondanso kukhomo limeneli . Mosataya nthawi ndinayamba kuyenda kumapita kwathu. Ndilimkati moyenda ndinalandira call . Nditapanga check ndinaona kuti ndi number ya Uncle (munthu yemwe amandilipilira school uja ndye ndinatchula kuti Uncle) . Apa sindinachedwe ndinayiyankha .

"Hello"

"Hello Sosten, ulikuti pakadali pano?"

"Ndili town ndikupanga zinazake Uncle ."

"Ok uli town momwemuno , ndye ukamaliza zomwe ukuchitazo undipeze ku office yanga room number 4 ."

"OK ndikubwera chifukwa zomwe ndinabwererazo ndamalizanso."

"Alright alright."

Kenako phone inaduka . Ndinayenda kupita ku immigration komwe amagwira ntchito . Nditafika kuntchitoko , ndinayenda straight ku room number 4 ndipo nditagogoda ndinawamva akuyankha .

"Yes come in."

Ndinatsekula ndikulowa ndikukakhala pampando . Titapatsana moni kenako anati:

"Pano ukupanga chanino mphwanga?"

Anatero akundiyang'ana uku akulumaluma cholembera chawo chomwe chinali m'manja. Kenako ndinayankha .

"Palibe ndikungokhala , koma ndalembera ma company angapo ndye akungoti anditengebe. "

"Umakumbukira mgwirizano omwe ndinapangana ndi sister ako panthawi yomwe anakusankhila ku BSS (Blantyre secondary school) kapena sanakuuze?"

"Anandiuza."

Ndinayankha nditagwetsa nkhope chifukwa ndimkaona ngati akufuna 10% yawo. Kenako anandifusa.

"Anamuuza kuti chani?"

"Anati mundilipira school kuchoka form 1 mpaka 4 . Ndikazachitanso bwino , muzandilipira ku University. Ndikazathana ndi University, muzandipezera ntchito kenako muzizandidula 10% pamalipiro anga akuntchito."

"Yeah za 10% ndinanenadi chifukwa nthawi imeneyija, ndinali ndili junior pamene pano ndine senior uzingoona ndilindi office yanga anandikweza udindo."

Atakamba mau awa , anayimilira pampando paja ndikundiuza kuti ndiwatsatile . Tinatuluka ndikuyenda mu corridor mpaka tinakafika mu office ina. Titafika kumeneko , zimaonetsa kuti taliwa mu office ya bwana wamkulu ndithu malingana ndiulemu omwe Uncle amapeleka . Kenako anati:

"Bwana , mwana wa sister wanga ndimanena uja ndameneyu."

Bwanayo anapumila m'mwamba uku akundiyang'ana. Kenako anati:

"Sitikutengera zibale, koma ma qualifications amunthu."

"Eya Bwana uyunso anakhoza bwino ngati ana anga aja. Mapepala ndikubweretserani mawa."

Anakamba izi chifukwa ana awo onse awiri amagwira ntchito ku immigration koma anawaponya kosiyana. Wina amagwira ku Bakili Muluzi Airport (Chileka) pamene wina anali ku Mzuzu immigration. Kenako anandiuza kuti ndiwapatse dzina langa . Sindinachedwe ndinalitchula . Mosataya nthawi anati:

"Ok dzina ndalitenga koma zingotengera ma process aboma kuti ayenda bwanji."

Kenako tinatsanzika ndikutuluka mu office muja . Ndye pokuti ndinatsogola ndiine Potuluka mu office muja , Uncle anandifusa za mayala anga omwe anali ong'ambika chifukwa chondikwenya ndikukankhidwa kuja.

"Tsono mayalawo bwanji, mumapanga ndewu?"

"Ayinso mtengo unandikola."

Nditayankha izi, tinayenda kukafika ku office kwawo . Kenako anati:

"Pano utha kumapita kunyumba koma madzulo ano undipatse mapepala ako chifukwa tsikulililonse ndidzakuyitana . Koma please ukazalembedwa ntchito , uzizaonetsa khalidwe labwino chifukwa ndayikila umboni kuti ndiiwe mwana wa sister wanga."

" Ndizayesetsa kutero Uncle."

Kenako ndinatuluka mu office ija kumapita kunyumba ndikungomwetulira ndekhandekha ndipo zokuti ndathamangitsidwa kubanja sizimadzwikanso.

LAIKA'S POV

Ntima wanga unali odzadza ndiukali chifukwa ndinakangana ndi Sosten . Nkwiyo onse unatha pomwe ndinaona galimoto yamakolo a Fukiz ikulowa kumpanda kwathu . Ndinangoyima pa window kumuyang'ana kunja kuja. Mosataya nthawi ndinaona Fukiz akutsika mgalimoto pamodzi ndi makolo ake. Fukiz anali mwana wa amzawo adad omwe amapanganawo business. Ndye amandikakamiza kuti ndimusiye Sosten nditengani ndimwana wamzawoyu kuti chuma chambali zonse ziwiri chikhale stable. Poyamba ndimakana malingana ndim'mene ndimamukondera Sosten . Koma pressure yomwe ndimalandira kuchokera kwa makolo anga inayamba kundisinthitsa maganizo pang'ono pang'ono kufikila tsiku ili ndinamuthamangitsa Sosten . Pomwe ndimadzayenga torch kuti ndikamuunikire njira yakwawo Sosten . Makolo anga ndiomwe anachita kundiuza kuti

"Tenga torch yayikuluyo. "

----

Ndilipawindo paja ndinawamva amayi akuzandiyitana .

"Lai , Apongozi ndi Fiancé wako abwera."

"Ok ndikubwera."

"Ubwere ukusangalala osati ubwe utakwiya ayi ukundimva?."

Amayi anatero akumwetulira chifukwa ndiomwe amayipatsa moto nkhaniyi kuti ndimusiye Sosten . Ndipo anawakakamiza bambo a Fukiz kuti andigulira galimoto cholinga ndisinthe maganizo anga . Adad ataona kuti ndavomera zokwatilana ndi Fukiz mwana wamzawo pa business , anandipatsa ulamuliro oyendetsa ma business awo ena ndi ena koma panthawi yomwe ndinali ndi Sosten, amandisala ma business amayendetsa okha ndi azibale anga.

Popeza kunabwera Apongozi anga , ndinayenda straight kupita kubafa . Nditamaliza kusamba , ndinapita kukawapatsa moni Apongozi anga komanso Fiance wanga. Tilipa sitting room paja makolo anga ndi makolo a Fukiz anali kukambirana .

"Ndye mukuona kuti tiyike ma million angati kuti ukwati wa anawa uzakhale wapamwamba?"

Mosataya nthawi ndinawamva amayi akutichitsa pazokambirana zawozo.

"Lai, tayambani mwasunthakaye ndi apongoziwa."

Izi zinatipangitsa kuchoka pa sitting room paja kupita mu quarters yomwe ndimakhala ndi Sosten ija kumakacheza ndi Fiancé wanga. Kenako tinagwirizana zokuti tipite town tikagike KFC . Mosataya nthawi ndinatenga ma key agalimoto yanga ndipo tonse tinakwera ulendo wa town .
Tilinjira ndipamene anayamba kukamba nkhani .

"Unali kuti nthawi yonseyi Laika?Ndikanakonda ndikanakudziwa usanakumane ndi atidyenawo aja. Chimakusangalatsa mwa ameneuja ndichani babe?."

Anatero akuseweretsa tsitsi langa uku akundiyanga. Ndinamwetulira kenako ndinati:

"Basi ndimaopa kuti ndikamusiya iyeuja , amuna ena azandiswera ntima."

"Yeah amuna nditonse koma quality ndiosiyana . Pomwe wabwera muntima wanga chonchimu, udziwe kuti wasiya ntima wako in safe hands and Kwa munthu oyenerera."

Ndinamwetulira kenako ndinati:

"Bola osadzandiliza"

"Mayazi , ukudziwa chani . M'dziko langa lachikondi , mulibemo njuchi koma muli uchi okha. Ndipo m'dziko langa munali mdima wandiweyani chifukwa munalibe kuwala, koma apa ndapeza dzuwa lomwe liziwalitsa dziko langa. "

Ndinamwetulira uku ndilibusy kuyendetsa galimoto kufikila tinafika pa KFC ya town . Titafika town tinapanga park ndikutsika . Tisanalowe mu KFC muja tinamva horn ya truck po po . Fukiz anatembenuka ndikumukuwira mzake wa truck uja .

"Ndakuona!! ndakuona!! ."

Ndipo mzakeyo anayankha uku alipachiongilero.

"Ndakuonanso iweyo. Kodi ulinawowo ndi madam akunyumba kapena zomwezi zatidyenawo timazitenga pa border-zi?

Fukiz sanayankhe anangondigwira mkono ndikulowa mkati mwa KFC ija.......


Tikumanenso mu part 8


15/08/2026

Pepatu pepa
🙈🙈

Laika ali mweeee kumwetulira hhhmmm 🙌🙌🙌🤸🤸🤸🤸
15/08/2026

Laika ali mweeee kumwetulira hhhmmm 🙌🙌🙌🤸🤸🤸🤸

Address

Blantyre
2022

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when FUKIZ MW posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share