20/02/2026
NKHANI YA CHISONI 😠💔
Bambo wachikuda mukumuonayu dzina lake ndi Calvin M***a wazaka 33 ,mzunguyo dzina lake ndi Adriaan Van Tonder wazaka 71.
Calvin ndi Adrienne amapanga rent pa yard imodzi ku Eloff, Mpumalanga. Chifukwa cha vuto lamadzi lomwe lili ku Eloff ko, a landlord anawayikila Jojo tank kuti azithandizika madzi akasiya. Ndiye akuti Jojo tank inali ndi ma pipe awili ina yopita mu room ya Calvin ina yopita mu room ya Adriaan,koma tankyi inayikidwa ku side ya room ya Adriaan.
Ndiye akuti tsiku lina Adriaan anadula pipe yamadzi yopita mnyumba mwa Calvin, zomwe zinampangitsa Calvin kuwauza a landlord. A landlord analamura kuti Adriaan abwezeletse pipe ija. Ndiye akuti Calvin anadzapita ku shop kukagura zinthu, tsiku lake lomwelo koma pobwelera anapeza kuti Adriaan wachotsanso pipe ija, ndipo mnyumba mwake mulibe madzi.
Akuti apa mpamene Calvin ananyamuka ndi mwana, wake wa 9 years kukalumikiza pipe ija. Akuti ali mkati molumikiza pipe ija mpamenetu mkangano unabuka pakati pa azibambo awiliwa. Akuti Adriaan mpamene anatenga mfuti mkumuombela Calvin kambiri mbiri ndipo anamwalira pamaso pa mwana wake (mnyamata) wa 9 years. 😠😠😠Mwana uja anayamba kukuwa ndipo mayi ake anabwela kumupeza Calvin waombeledwa. Akuti Adriaan ataona mkazi wa Calvin akulira anayamba kumuopsyezanso kuti nayenso amupha. Koma mkaziyo anakwanitsa kuyimbila apolisi ndipo Adriaan anamangidwa. Ndipo anakaonekela ku court lachiwiwili lathali pa 17 February ku Mpumalanga .
Zomvetsa chisoni kuti mwana wa 9 years anaonelera kuphedwa kwa bambo ake, ndipo ndi zinthu zoti zimpanga traumatise moyo wake onse. 💔 😠Komanso mkazi wa Calvin ndi oyembekezela. Ku South Africa ka nkhani pang'ono amaona kuti solution ndikupha eeish. Dziko la usatana ili. Munthu wazaka 71,zachidziwikile akafela kundende komko.