Patricia 2 Frakeza

Patricia 2  Frakeza Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Patricia 2 Frakeza, Digital creator, 5 buzzard Road Pelican park, Pelican Park.
(8)

Story teller
Entertainer
Comedian

Pano pamakhala nkhani zophunzitsa, zolangiza komanso zodziwitsa, kalikonse mukamva pano😋😋😋

I can do all things through christ who strengthens me🙏🙏🙏🙏

Mimba ya Mapasa -Episode 4Usiku utayamba kuda kwambiri, Lindah naganiza mwachangu kuti sikunali koyenera  kugona panja. ...
14/06/2026

Mimba ya Mapasa -Episode 4

Usiku utayamba kuda kwambiri, Lindah naganiza mwachangu kuti sikunali koyenera kugona panja. Sanafune kusowa malo ogona chifukwa anali ndi ndalama mu akaunti yake ya ku banki. Zinali ngati kuti ankadziwa kuti tsikuli lidzafika, choncho anali atakonzekera kale. Pamene anatsegula akaunti ya ku banki zaka zapitazo, anatenganso khadi la ATM limene analibisa mu chikwama chake cha ku sukulu.

"Nthawi yafika yoti ndigwiritse ntchito khadi ili. Ndakhala ndikupulumutsa ndalama kwa nthawi yayitali. Tsopano tsiku lovuta lafika ndipo ndalama zanga zindithandiza," adatero Lindah pamene amatulutsa khadi la ATM m'chikwama chake.

Anapita pa shop ndikuchotsa K50,000. Atachotsa ndalamazo, adagwiritsa ntchito K15,000 kugula foni ku shopu ya mafoni yomwe inali yotsegula, Ankafuna kukhala ndi foni kuti azitha kulankhulana ndi anthu.

"Tsopano ndipeze hotelo yogonamo usiku uno," adatero Lindah atatuluka m'sitolo ya mafoni.

Chifukwa anali ndi katundu wambiri, zinali zovuta kuyenda. Choncho anayimitsa taxi.

"Chonde nditengeni ku hotelo yapafupi," adauza driver wa taxi.

Driver anatsegula boot ya galimoto ndikumuthandiza Lindah kuyika katundu wake. Kenako analowa m'galimotomo ndipo anakhala pampando wakutsogolo. Pasanapite nthawi anafika ku hotelo yokongola.

"Ndikukhulupirira kuti si yokwera mtengo. Ndilibe ndalama zambiri. Ndikungofuna malo ogonamo usiku uno," adaganiza Lindah pamene amalowa m'hotelomo.

Anapita ku reception kukafunsa mtengo wa chipinda.

"K5,000 pa usiku umodzi," adatero receptionist.

Lindah analipira nthawi yomweyo. Ankadziwa kuti adzangogona usiku umodzi wokha chifukwa cholinga chake chinali kupeza nyumba yake mwamsanga m’mawa.

Atasonyezedwa chipinda chake, Lindah analowa mosangalala. Anakonza katundu wake kenako anapita kukasamba. Anaganiza zoyiwala mavuto onse kwa kanthawi. Atakhazikika bwino, anayitanitsa rice ndi nkhuku kuchokera ku canteen ya pa hoteloyo. Chakudyacho chinabwera ndipo anadya mosangalala kwambiri.

Kunyumba kwa azakhali ake sankadya bwino, ndipo sanazolowere kugwiritsa ntchito ndalama zake mopambanitsa pa chakudya. Koma usiku umenewu anaona kuti akuyenera kudya bwino.

"Sindingalole njala kundivutitsa. Ndiyenera kudya kuti mwana amene ali m'mimba mwanga nayenso apeze chakudya," adatero Lindah pomwe ankadya nkhuku yonse mpaka kuphwanya mafupa.

Atamaliza kudya, anagona pabedi ndikuyatsa foni yake yatsopano. Anatulutsa kabuku komwe analembamo nambala ya mayi ake ndipo anaimba.

"Moni amayi, madzulo abwino. Ndine Lindah . Iyi ndi nambala yanga . Ndagula foni, muisunge nambalayi" adatero.

Mayi ake anadabwa kumva kuti mwana wawo tsopano ali ndi foni.

"Ndani wakugulira foni? Kodi ndi azakhali ako?" anafunsa.

"Ndadzigulira ndekha amayi. Sindinabe foni kapena ndalama. Ndinagwira ntchito ndipo ndinasunga ndalama. Komanso sindilinso kwa azakhali anga. Andithamangitsa. Pakadali pano ndili mu hotelo," adatero Lindah .

Mayi ake anachita mantha.

"Eeh! Chachitika ndi chani? Wapalamula chani? Koma uli bwinobwno?" anafunsa mwachidwi.

"Ndili bwino amayi. Ndinapalamula chachikulu ndipo azakhali anaganiza zondithamangitsa. Sindikuwablema chifukwa mwina inenso ndikadachita chimodzimodzi,ndikadakhala mu nsapato yao"

"Cholakwacho ndi chani? Unaba ndalama zawo?" anafunsa mayi ake.

"Ayi amayi. Sindinabe chilichonse. Koma ndatenga pakati. Chomvetsa chisoni kwambiri n’chakuti mwamuna amene anandipatsa mimbayi anaikana ndipo anandisiya. Komanso wathawa. Azakhali sanathe kupirira zimenezi ndipo andithamangitsa."

Mayi ake anadabwa kwambiri.

"Watenga pakati? Lindah, ndikukhulupirira kuti ukunena nthabwala. Sunamalize ngakhale sekondale ndipo watenga kale pakati? Ukufuna kundichititsa manyazi?"

"Mimba si manyazi amayi. Ndanyamula mwana m'mimba mwanga osati nyama. Ndipo ndaganiza zosunga mwanayu. Ndikudziwa kuti kukhala mayi si kophweka, koma zimene zachitikazi sizingasinthidwenso. Ndikulakwa kutenga pakati ndisanakwatire, koma cholakwacho chachitika kale ndipo ndadzikhululukira. Tsopano ndikupempha kuti nanunso mundikhululukire.

Ndikudziwa mwakhumudwa ndipo mumafuna kuti ndidzakwatiwe kaye. Koma moyo si umayenda mofanana kwa aliyense. Sindikunyadira zolakwa zanga, koma sindidzasautsidwa nazo kwambiri chifukwa kudandaula sikuthetsa mavuto. Musadandaule amayi, ngakhale ndili ndi pakati, ndidzakupangitsanibe kundinyadira."

Mawu ake anakhudza mtima wa mayi ake ndipo analonjeza kuti adzamuthandiza.

"Koma ukutani kumeneko? Wagona masiku angati mu hotelo? Bwanji osabwerera kuno kumudzi? Ndiwe wamng'ono kwambiri. Kodi udzakwanitsa kulipira chilichonse ku Blantyre-ko?"

"Ndikhala bwino amayi. Ndinasunga ndalama kuchokera ku bizinesi yanga. Ndidzagwiritsa ntchito mwanzeru ndikuyamba moyo wanga."

Atanena zimenezo, Lindah anamaliza kuyankhula ndi mayi ake ndipo anagona tulo tamtendere ngati mwana.

Ikupitrira......

Like share andcomment Osaiwala kupanga follow Patricia 2 Frakeza

Lindah courageous girl..a girl with highself esteem🥳🥳🥳🥳🥳

14/06/2026

Agulu langa nonse amene kuli kunja kuno ambuye akutetezereni ...Mulungu aalipo ndipo atisamala 🙏🙏🙏🙏🙏

14/06/2026

Wynberg ccap and Joeslove ccap youth at ..Wynberg 💃💃💃💃💃

Tabwerako kumpingoo

Tyeni ku mphemphero koma zoti Dawood wathawa mwaona ??? Part 3 yafikatu  ya mimba ya mapasa       ゚
14/06/2026

Tyeni ku mphemphero koma zoti Dawood wathawa mwaona ???

Part 3 yafikatu ya mimba ya mapasa

Mimba ya Mapasa-Episode 3Lindah  anali wokonzeka kunena oona zokha zokha  ngakhale Dawood anamuchenjeza kuti asatchule d...
14/06/2026

Mimba ya Mapasa-Episode 3

Lindah anali wokonzeka kunena oona zokha zokha ngakhale Dawood anamuchenjeza kuti asatchule dzina lake ndipo kuti asawulule zomwe zinachitika. Ankadziwa kuti chimenecho chinali chiwopsezo chopanda mphamvu chifukwa Dawood sakanatha kumuchitira chilichonse. Choncho pamene azakhali ake anamukokera kupita ku chipinda chochezera ndikumufunsa amene anamupatsa mimbayo, sanachedwe koma kuyankha.

“Mtsikana iwe, pamapeto pa zonse wabweretsa manyazi m’nyumba mwanga. Wandiwonongera dzina. Kodi azimayi anzanga adzati chani? Ndi ndani wakupatsa mimba?” adafunsa mokwiya kwambiri.

“Dzina lake ndi Dawood . Ndi mmodzi mwa a IPTE 11 amene akugwira ntchito kusukulu kwathu,” anayankha Lindah. Sanali kulira koma mawu ake anali odzaza ndi chisoni.

“Taona iwe! Ndinakutumiza kusukulu kuti ukapeze maphunziro, koma m'malo mobwera ndi satifiketi wabwera ndi mimba. Anzako akukonzekera mayeso omaliza pamene iwe ukukonzekera kubereka. N’chifukwa chiyani wasankha kundichititsa manyazi?” adafunsa azakhali ake mokweza mawu.

“Azakhali, pepani. Ndalakwa, koma si mapeto a moyo. Ndidzapambana vutoli ndipo ndidzabwereranso kusukulu. Ndikudziwa kuti ndakukhumudwitsani, koma ndikulonjeza kuti ndikonza zonse,” adatero Lindah molimba mtima. Ngakhale azakhali ake anadabwa kuti sanali kulira.

“Ukonza bwanji? Kodi ukuganiza kuti kukhala mayi ndi masewera? Ndi udindo waukulu kwambiri ndipo munthu ayenera kukhala wokonzeka asanalowe mmenemo. Ndiwe wamng’ono kwambiri koma ukufuna kuwononga tsogolo lako ndi kubereka msanga? Ulibe manyazi!” adatero mokwiya kwambiri.

“Tsogolo langa silinawonongeke, azakhali. Musadandaule, ndidzabwereranso kusukulu,” adatero Lindah koma azakhali ake sanamvere.

“Khala chete! UKuyankhula kwambiri Nyamuka pamenepo unditengere kwa mwamuna amene wakupatsa mimba. Ayenera kukukwatira chifukwa sindikufuna kukhala ndi mayi wapakati m’nyumba mwanga,” adatero uku akumukokera kunja.

Nyumba ya Dawood sinali kutali ndi kumene Lindah ndi azakhali ake ankakhala. Pasanapite nthawi anafika ndipo anayima pakhomo la Dawood. Azakhali ake ndi amene anagogoda pakhomo koma palibe amene anayankha. Anatenganso mwala n’kumagogoda mwamphamvu, koma Dawood sanali m’nyumbamo.

Pamene ankangogogoda mosalekeza, mayi ena omwe ankakhala mumpanda omweo anamva phokoso ndipo anatuluka.

“Madam, vuto ndi chani? Kodi nkwabwino uko mwachoka ? Kodi pali amene wamwalira? Zikuoneka kuti Dawood palibepo pano. Akanakhalapo akanatsegula kale kale . Chavuta n’chani?” adafunsa akukwinya nkhope.

“Wamupatsa mtsikanayu mimba ndipo ndabwera kudzamupatsa mkazi wake,” anayankha azakhali ake mwaukali.

“Dawood kulibe. Ndipo sakhalanso kuno. Wasamutsidwa ndi IPTE 11 kupita ku Lilongwe , kwawo. Wachoka lero lomwe , mphindi zochepa musanafike. Ngati mukufuna kuonana nae , pitani ku Lilongwe,” adatero mayiyo.

Nthawi yomweyo zinadziwika kuti Dawood anathawa. Anakonza zonse bwino lomwe ndipo anakwanitsa kuwapusitsa. Azakhali ake anakwiya kwambiri atamva kuti Dawood wachoka m’taunimo. Anamukoka Lindah nkubwerera nae kunyumba.

“Sukhala m’nyumba mwanga ndi mimba imeneyi. Sindingakulole kukhala pano ndi kulera mwana. Pita ukatenge katundu wako ndipo uchoke. Bwerera kwa makolo ako ndikawauza kuti watenga mimba ya mwamuna amene sangakusamalire,” adatero.

“Chonde azakhali, sindingathe kupita kwa makolo anga ndekha ndili ndi mimba. Adzandikwiyira kwambiri. Ndiloleni ndikhale pano mpaka ndibereke. Ndilibe kwina koti ndipite,” anapempha Lindah, koma pempho lake silinamveke.

Ataona kuti Lindah akuchedwa, azakhali ake analowa m’chipinda chake, kutulutsa katundu wake ndi kumuponyera kunja. Kenako anamuuza kuti achoke nthawi yomweyo.

Unali madzulo pamene Lindah anapezeka m’munsewu osadziwa koti apite. Mwamwayi anali ndi ndalama zomwe anasunga kwa zaka zoposa zisanu. Kupatula kugulitsa mtedza kwa azakhali ake, Lindah anali ndi bizinesi yake yobisika kusukulu. Tsiku lililonse ankagula mtedza wokazinga, ma popcorn ndi machipsi ,nthochi kuti azikagulitsa kwa ophunzira anzake pa nthawi ya break. Pang’onopang’ono ankasunga phindu lake lonse.

Patatha zaka zisanu, ndalama zake zinali zitafika K200,000. Ankatumiza ndalama zonse ku akaunti ya banki yomwe anatsegula mwachinsinsi osadziwitsa azakhali ake.

Tsopano ali m’mphepete mwa msewu usikuwu,anayamba kuganiza mozama.

“Kodi ndigone mumsewu? Kodi ndibwerere kumudzi kwa makolo anga? Kapena ndipite ku Lilongwe kukamufunafuna Dawood?” adadzifunsa.

Maganizo ake anali balala,koma ankadziwa kuti ayenera kupanga chisankho mwachangu chifukwa usiku wu mumsewu simulator motetezeka.

Ikupitrira....

Like share and comment osaiwala kupanga follow Patricia 2 Frakeza

Apange bwanji Lindah???🙄🙄🙄🙄

Usiku wabwno anthu inu....Tonse tilote  mapasa a  Maria  🤣🤣🤣🤣🤣🤣
13/06/2026

Usiku wabwno anthu inu....

Tonse tilote mapasa a Maria 🤣🤣🤣🤣🤣🤣

Mimba ya Mapasa-  Episode 2Lindah  sanalinso  chimodzi modzi  kuyambira pamene  anazindikira  kuti ali ndi pakati. Ankag...
13/06/2026

Mimba ya Mapasa- Episode 2

Lindah sanalinso chimodzi modzi kuyambira pamene anazindikira kuti ali ndi pakati. Ankagona m’kalasi mosavuta nthawi iliyonse aphunzitsi akamaphunzitsa ndipo thupi lake linali lofooka kwambiri. Lindah ankadziwa kuti anthu ena anayamba kale kumunena chifukwa cha kusintha kwa khalidwe lake kusukulu. Koma anali atatsimikiza mu mtima mwake kuti ngakhale azavale manyazi otani , adzanyamula udindo wa zimene anachita.

“Ndikusunga mwana uyu ngakhale anthu atanena zotani. Ndibereka mwanayu ndipo ndidzamusamalira ndekha ngakhale Dawood atakana kundithandiza. Ndinalakwitsa kutenga pakati ndisanakwatiwe, koma moyo udakalipo. Ndikhala wamphamvu chifukwa cha ine komanso mwana amene ndili naye m’mimba mwanga ,” Lindah anadzilankhula yekha masana ena ali paulendo wobwerera kunyumba kuchokera kusukulu.

Atafika kunyumba, azakhali ake, Madam Patricia, anamupatsa mtedza wowiritsa kuti akagulitse monga mwa chizolowezi. Tsiku lililonse Lindah ankagulitsa zinthu m'misewu akachoka kusukulu. Pa limodzi mwa masiku amenewo ndi limene anapita kunyumba kwa Dawood ndipo zinachitika kumeneko ndi zomwe zinamupangitsa kukhala ndi pakati.

Lindah anali watopa kwambiri ndipo ankadziwa kuti akanagwa panjira ngati atapitiriza kugulitsa.

“Kodi ndingauze chani azakhali anga? Sindingangonena kuti sindikufuna kupita kukagulitsa malonda opanda chifukwa adzafunsa chifukwa chake. Kodi ndibisa bwanji mimbayi? Mimba siingabisike kwamuyaya. Posachedwapa idzaonekera ndipo aliyense, kuphatikizapo azakhali anga, adzadziwa kuti ndili ndi pakati,” Lindah anaganiza.

Thireyi ya mtedza inali patsogolo pake ndipo azakhali ake anamuuza kuti ayenera kugulitsa malomda onse asanabwerere kunyumba.

“Onetsetsa kuti wagulitsa zonse. Mtedzawu si wochuluka. Ungoyenda m’derali ndipo ugulitsa zonse mwachangu,” anatero azakhali ake osadziwa nkhawa yomwe inali mumtima mwa Lindah .

“Ukabwerako udzadya. Tsopano nyamuka uzipita chifukwa nthawi ikutha.”

“Inde azakhali,” anayankha Lindah.

Ananyamula thireyi ya mtedza pamutu pake n’kuyamba kuyenda. Ankayenda msewu ndi msewu akugulitsa, koma patatha ola limodzi pansi pa dzuwa lotentha, anatopa kwambiri moti sanathenso kuyenda. Anapeza mthunzi n’kukhala pansi kuti apume.

“Izi ndi zoopsa kwa thanzi langa komanso la mwana wanga. Sindingapitirize kugulitsa ndili ndi pakati. Ndiyenera kuchitapo kanthu mwamsanga,” anaganiza.

Atadzilimbitsa mtima, ananyamukanso ndi kupita molunjika kunyumba kwa Dawood.

“Sindikumva bwino. Ndikufuna ndalama kuti ndiyambe kupita kuchipatala kusikelo ya mimba. Sindikufuna kuti chilichonse chindichitikire ine kapena mwana. Komanso ndabwera kudzakudziwitsa kuti ndauza azakhali anga za mimba imeneyi. Ndikufuna kuwauza kuti ndili ndi pakati,” anatero Lindah atalowa m’chipinda cha Dawood.

“Usachite zimenezo. Ukufuna kuwononga moyo wanga? Kodi ukudziwa zimene sukulu ingandichite ikadziwa kuti ndapatsa pakati mwana wa sukulu? Ndakuuza kale kuti uchotse mimbayo. Tsopano ukunena kuti ukauza azakhali ako? Ndipo ndalama zake ziti zomwe ndikupatse? Ine sindinadye kuyambira m'mama wa chifukwa ndilibe ndalama. Kodi ndingapeze kuti ndalama zokupatsa?” Dawood anayankha mwakachetechete kuti anthu akunja asamve.

“Nanga ndipange chani? Sindingapitirize kugulitsa m'misewu ndili chonchi. Kodi mukuyembekezera chani? Kodi ndinadzitengera ndekha pakati? Pamene munkachita zimenezija simunaganizire zotsatira zake? Ndipo ndakuuzani kale kuti sindichotsa mimbayi. Ndikusunga mwana uyu zivute zitani,” anatero Lindah mokwiya.

“Ngati ukusunga mwana ameneyo, usatchule dzina langa kwa aliyense. Ndikana kulikonse komanso nthawi iliyonse. Chonde usawononge moyo wanga,” anatero Dawood.

“Kodi ukuganiza kuti chingakuchitikire ndi chani anthu akadziwa kuti ndiwe wandipatsa pakati? Sangakuphe. Anthu angolankhula basi. Malinga ndi ine, ndi bwino kunena zoona kusiyana ndi kubisa. Ndipo madzulo ano ndidzauza azakhali anga. Sindifa chifukwa cha zimenezi,” anayankha Lindah.

Ananyamula thireyi yake ndi kubwerera kunyumba ngakhale kuti anali asanamalize kugulitsa mtedzawo.

Atafika kunyumba, azakhali ake anali kukhitchini akuphika. Lindah anapita kumene iwo anali.

“Azakhali, pali china chake chomwe ndikufuna ndikuuzeni,” anatero Lindah .

“Chani? Ndikukhulupirira kuti wagulitsa mtedza wonse? Wabwera msanga kwambiri. Wamaliza kugulitsa?” anafunsa azakhali ake.

“Sindinakwanitse kugulitsa onse,” anayankha Lindah mofooka.

“Chifukwa chani? Ngati sunamalize kugulitsa, wabwereranji kunyumba kuno?”

“Ndili ndi pakati,” anayankha Lindah molimba mtima.

“Ukuti chani?” azakhali ake anafunsa modabwa kwambiri.

“Ndati ndili ndi pakati. Ndikudziwa kuti izi zikukudabwitsani koma ndi zoona. Chonde ndikhululukireni. Ndikupepesa kwambiri. Ndikutenga udindo pa zimene ndachita,” anatero Lindah.

Azakhali ake anasiya zimene ankachita n’kutembenukira kwa Lindah. Kenako anamugwira dzanja n’kupita naye kuchipinda chochezera kuti amufunse mafunso.

Ikupitrira...

Like share and comment komanso osaiwala kupanga follow .... Patricia 2 Frakeza
..

13/06/2026

Mkazi amene anataya nyumba yake

Part 22

Recho zasolobana,kusambera kuja eti ...kumabala mavuto zofunatu zonsezi🙄🙄🙄🙄🙄🙄

Like share and comment

Part 23 on the way🥳🥳🥳🥳🥳🥳🥳

Guys palibe munthu emwe samalakwa  chondee tigwrane manja timpempherere Racheal  kuchira kukuvuta uku🙄🙄🙄🙄🙄Part 22....20%...
13/06/2026

Guys palibe munthu emwe samalakwa chondee tigwrane manja timpempherere Racheal kuchira kukuvuta uku🙄🙄🙄🙄🙄

Part 22....20%loading ...is almost here osasunthaa

This life no balance  wina akuvutika kuchira wina wangopita kuti akaone kuti kamimba kakukula  bwanji 🙄🙄🙄🙄Part 22 ....80...
13/06/2026

This life no balance wina akuvutika kuchira wina wangopita kuti akaone kuti kamimba kakukula bwanji 🙄🙄🙄🙄

Part 22 ....80%loading 😋😋😋🫱

Osasuntha kuli kanthuuu.....

Address

5 Buzzard Road Pelican Park
Pelican Park

Telephone

+27725816358

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Patricia 2 Frakeza posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share