04/09/2026
KUKWATIRA NDI WAKUBA â EPISODE 1
Aggie anali mkazi wokongola kwambiri moti anthu ena ankati amaoneka ngati tomato wa fresh. Khungu lake linali losalala ngati mkaka, ndipo nkhope yake inkawoneka ngati ya ka mulungu kakumadzi.. Anakwatirana ndi billionaire wina dzina lake Cosmas, yemwe anali wamalonda komanso wogulitsa zinthu zosiyanasiyana ku Blantyre. Aggie anali ndi zaka 25 zokha, pomwe mwamuna wakeyu anali ndi zaka 35.
Iwo ankakhala mânyumba yayikulu komanso yapamwamba kwambiri ku Namiwawa, komwe ndi limodzi mwa madera olemera kwambiri ku Blantyre ko. Aggie anali ndi chilichonse chimene ankafuna. Zovala zamtengo wapatali, nsapato za ma designer, magalimoto, ma perfume komanso zodzikongoletsera zamtengo wapatali.
Mwamuna wake anamuuza kuti asamagwire ntchito. Choncho ankangokhala kunyumba ngati mkazi wapakhomo, kudya, kupuma komanso kusangalala ndi ndalama za mwamuna wake.
Koma panali vuto limodzi limene Aggie sankatha kulithetsa.
Vutolo linali chizolowezi chakuba.
Aggie anali wakuba. Ankakonda kuba zinthu kulikonse kumene wapita. Ichi chinali chinthu chimene ankadana nacho mwa iyemwini, koma zinkawoneka ngati mzimu winawake wachikunja ndi umene unkamuletsa. Nthawi iliyonse mzimuwo ukamugwira, ankayenera kuba chinachake kuti thupi lake likhale bata.
Ngakhale atakhala kunyumba yake yayikuluyi, chilakolako chotuluka kupita kukaba chimkamugwira. Sankatha kulimbana nacho. Zinali ngati matenda. Mumtima mwake munali wakuba.
Nthawi zonse Aggie akapita kumsika, ankabwerera ndi chinthu chimene wabako. Nthawi zina ankaba zodzikongoletsera. Nthawi zina ankaba botolo la perfume. Nthawi zina ankaba zinthu wamba monga thumba la mpunga, mapaketi a ma spaghetti kapena makatoni a mkaka.
Cosmas sankakayikira chilichonse. Ankaganiza kuti mkazi wake ankangogula zinthu zambiri chifukwa cha kukongola kwake komanso kukonda zinthu zapamwamba. Sankadziwa kuti ankaba zina mwa zinthuzo.
Ngakhale Aggie mwiniwake sankamvetsa zimene zinkamuchitikira. Akaba, ankakhala mâchipinda chake ndi kulira kwambiri.
âMulungu wanga, chifukwa chani ineyo?â Aggie ankatero. âNdili ndi chilichonse chimene mkazi angafune. Ndili ndi ndalama, ndili ndi mwamuna wachikondi, ndili ndi zovala ndi golide, ndili ndi nyumba yayikulu kuno. Koma chifukwa chani ndikubabe? Chifukwa chani ndimatenga zinthu za anthu nâkubisa ngati kuti ndilibe chilichonse?â
Ankaliira nthawi zonse msungwanayu. Koma sakanatha kusiya.
Ngakhale atayesetsa bwanji, nthawi iliyonse mzimuwo ukamugwira, ankayenera kuumvera. Ankafunika kuba chinachake kuti thupi lake likhazikike. Inali nkhondo yaikulu yomwe inali kuchitika mumtima mwake.
Mâmawa wina, Aggie anavala zovala zokongola kwambiri ndipo anamuuza dalaivala wake kuti amutengere ku supermarket.
Kunyumba kwawo kunalibe chimene chimasowa, koma chilakolako chotuluka kumpandaku chinali champhamvu kwambiri. Anavala gown yofiira, nsapato zakuda za design ndipo ananyamula handbag yagolide.
Atangofika ku supermarket, anthu anayamba kumuyangâana ndi kusirira kukongola kwake komanso mmene anavalira. Anatenga basket nâkuyamba kuyenda mâmashelefu.
Anasankha zakudya zina komanso mabotolo angapo a w**e.
Koma pamene ankayenda, mzimuwo unabweranso.
Mwadzidzidzi anayamba kusakhazikika. Manja ake anayamba kunjenjemera. Anadziwa kuti ankafunikira kuba basi.
âNthawi yakuba yafika.â Anadziuza ekha mumtima.
Aggie anatenga botolo limodzi la w**e la mtengo wapatali kwambiri nâkulilowetsa mwachangu mu handbag yake. Ankaganiza kuti palibe amene wamuwona.
Koma kamera ya chitetezo yomwe inali pakona ya supermarket inajambula zonse.
Atangosiya basket nâkuyesa kutuluka, alarm yomwe inali pakhomo inalira.
Security guard anamuyimitsa nthawi yomweyo.
âMadam, chonde dikirani. Pali vuto pano,â anatero mwamunayo mokweza.
Aggie anayamba kunjenjemera. Mtima wake unayamba kugunda kwambiri. Anayesetsa kumwetulira nâkuchita ngati kuti zonse zili bwino, koma ankadziwa kuti wagwidwa.
âMadam, chonde tsegulani chikwama chanu,â anatero security guard.
âMuli chani nchikwama changa?â Aggie anafunsa akuyesera kuseka.
âMulibe chilichonse mâchikwama changa. Ndi zinthu zanga zokha,â anatero ndi mawu ofatsa.
âIne sindine wakuba. Mungandichititse bwanji manyazi pamaso pa anthu onse chonchi?â anatero.
Koma security guard sanamumvere. Anamâlanda handbagyo mâmanja nâkutsegula pamaso pa anthu onse.
Atatsegula chikwamacho, anatulutsa botolo la w**e limene Aggie anali ataba.
Anthu onse mu supermarket anayamba kufuula modabwa. Sanakhulupirire kuti mkazi wokongola komanso wolemera chonchi anali wakuba.
Aggie nthawi yomweyo anagwada pansi chifukwa cha manyazi.
âChonde, ndikhululukireni. Zinali zolakwika. Sindikudziwa chimene chinandipangitsa kuchita zimenezi. Ndili ndi ndalama. Mwamuna wanga ndi wolemera. Chonde musandichititse manyazi. Ndikupemphani mâdzina la Mulungu,â anatero.
Anthu mu supermarket anayamba kunongâonezana komanso kumunena.
Ena anayamba kunena kuti mwina wakhala akuba kwa nthawi yayitali.
âChoncho mkazi wokongola uyu ndi wakuba? Ndi manyazi otani amenewa? Kodi mkazi wa billionaire angabe w**e wamba?â anatero munthu wina yemwe ankammudziwa bwino, ali pakati pa anthu ogula.
Manager wa supermarket anatuluka nâkumukalipira.
âMadam, mukafotokoza zonsezi ku polisi.â
Security guard anamugwira Aggie padzanja. Sanamvere kulira kwake.
Anayesetsa kufotokoza, koma palibe amene ankafuna kumumvera.
âNdati ndikhululukireni chonde. Ndidzalipira w**eyo. Nditha kulipira ngakhale zinthu zonse zomwe zili mu supermarket muno. Chonde musandichititse manyazi. Mwamuna wanga sakuyenera kudziwa zimenezi,â Aggie analira ndi kupempha ngati mwana.
Koma manager anali atakwiya kwambiri.
Anauza security guard kuti:
âImbirani apolisi nthawi yomweyino. Mkazi uyu akuyenera kumangidwa. Akakumane ndi manyazi chifukwa cha zimene wachitazi.â
Thupi la Aggie linayamba kufooka. Anayamba kunjenjemera ndi kulira.
Nthawi yomweyo, apolisi awiri anafika ku supermarket ku . Anali atadziwitsidwa kale.
Analowa atavala yunifolomu ndipo atanyamula zida zawo. Anthu anasonkhana kuti aone zimene zichitike.
Apolisiwo anafunsa chomwe chachitika.
Manager wa supermarket anawafotokozera zonse ndipo anawaonetsa kanema wa CCTV womwe unasonyeza mmene Aggie anabera w**eyo.
Aggie anagwa pansi akulira komanso kupempha.
Anapepesa, koma apolisi sanamumvere.
âChonde, ndilipira. Ndilipira kawiri mtengo wa w**eyo. Chonde musayimbire mwamuna wanga,â Aggie anatero.
Koma palibe amene anamumvera.
Anamugwira padzanja, ndipo anamutulutsa kunja.
âMuli mâmanja mwa apolisi,â mmodzi mwa apolisiwo anatero.
Aggie analira kwambiri pamene amamutenga nâkukamuika mâgalimoto ya apolisi.
Dikirani Episode yotsatira.
Ichi ndee nchiwanda ndithu mmmm