14/06/2026
Mimba ya Mapasa -Episode 4
Usiku utayamba kuda kwambiri, Lindah naganiza mwachangu kuti sikunali koyenera kugona panja. Sanafune kusowa malo ogona chifukwa anali ndi ndalama mu akaunti yake ya ku banki. Zinali ngati kuti ankadziwa kuti tsikuli lidzafika, choncho anali atakonzekera kale. Pamene anatsegula akaunti ya ku banki zaka zapitazo, anatenganso khadi la ATM limene analibisa mu chikwama chake cha ku sukulu.
"Nthawi yafika yoti ndigwiritse ntchito khadi ili. Ndakhala ndikupulumutsa ndalama kwa nthawi yayitali. Tsopano tsiku lovuta lafika ndipo ndalama zanga zindithandiza," adatero Lindah pamene amatulutsa khadi la ATM m'chikwama chake.
Anapita pa shop ndikuchotsa K50,000. Atachotsa ndalamazo, adagwiritsa ntchito K15,000 kugula foni ku shopu ya mafoni yomwe inali yotsegula, Ankafuna kukhala ndi foni kuti azitha kulankhulana ndi anthu.
"Tsopano ndipeze hotelo yogonamo usiku uno," adatero Lindah atatuluka m'sitolo ya mafoni.
Chifukwa anali ndi katundu wambiri, zinali zovuta kuyenda. Choncho anayimitsa taxi.
"Chonde nditengeni ku hotelo yapafupi," adauza driver wa taxi.
Driver anatsegula boot ya galimoto ndikumuthandiza Lindah kuyika katundu wake. Kenako analowa m'galimotomo ndipo anakhala pampando wakutsogolo. Pasanapite nthawi anafika ku hotelo yokongola.
"Ndikukhulupirira kuti si yokwera mtengo. Ndilibe ndalama zambiri. Ndikungofuna malo ogonamo usiku uno," adaganiza Lindah pamene amalowa m'hotelomo.
Anapita ku reception kukafunsa mtengo wa chipinda.
"K5,000 pa usiku umodzi," adatero receptionist.
Lindah analipira nthawi yomweyo. Ankadziwa kuti adzangogona usiku umodzi wokha chifukwa cholinga chake chinali kupeza nyumba yake mwamsanga m’mawa.
Atasonyezedwa chipinda chake, Lindah analowa mosangalala. Anakonza katundu wake kenako anapita kukasamba. Anaganiza zoyiwala mavuto onse kwa kanthawi. Atakhazikika bwino, anayitanitsa rice ndi nkhuku kuchokera ku canteen ya pa hoteloyo. Chakudyacho chinabwera ndipo anadya mosangalala kwambiri.
Kunyumba kwa azakhali ake sankadya bwino, ndipo sanazolowere kugwiritsa ntchito ndalama zake mopambanitsa pa chakudya. Koma usiku umenewu anaona kuti akuyenera kudya bwino.
"Sindingalole njala kundivutitsa. Ndiyenera kudya kuti mwana amene ali m'mimba mwanga nayenso apeze chakudya," adatero Lindah pomwe ankadya nkhuku yonse mpaka kuphwanya mafupa.
Atamaliza kudya, anagona pabedi ndikuyatsa foni yake yatsopano. Anatulutsa kabuku komwe analembamo nambala ya mayi ake ndipo anaimba.
"Moni amayi, madzulo abwino. Ndine Lindah . Iyi ndi nambala yanga . Ndagula foni, muisunge nambalayi" adatero.
Mayi ake anadabwa kumva kuti mwana wawo tsopano ali ndi foni.
"Ndani wakugulira foni? Kodi ndi azakhali ako?" anafunsa.
"Ndadzigulira ndekha amayi. Sindinabe foni kapena ndalama. Ndinagwira ntchito ndipo ndinasunga ndalama. Komanso sindilinso kwa azakhali anga. Andithamangitsa. Pakadali pano ndili mu hotelo," adatero Lindah .
Mayi ake anachita mantha.
"Eeh! Chachitika ndi chani? Wapalamula chani? Koma uli bwinobwno?" anafunsa mwachidwi.
"Ndili bwino amayi. Ndinapalamula chachikulu ndipo azakhali anaganiza zondithamangitsa. Sindikuwablema chifukwa mwina inenso ndikadachita chimodzimodzi,ndikadakhala mu nsapato yao"
"Cholakwacho ndi chani? Unaba ndalama zawo?" anafunsa mayi ake.
"Ayi amayi. Sindinabe chilichonse. Koma ndatenga pakati. Chomvetsa chisoni kwambiri n’chakuti mwamuna amene anandipatsa mimbayi anaikana ndipo anandisiya. Komanso wathawa. Azakhali sanathe kupirira zimenezi ndipo andithamangitsa."
Mayi ake anadabwa kwambiri.
"Watenga pakati? Lindah, ndikukhulupirira kuti ukunena nthabwala. Sunamalize ngakhale sekondale ndipo watenga kale pakati? Ukufuna kundichititsa manyazi?"
"Mimba si manyazi amayi. Ndanyamula mwana m'mimba mwanga osati nyama. Ndipo ndaganiza zosunga mwanayu. Ndikudziwa kuti kukhala mayi si kophweka, koma zimene zachitikazi sizingasinthidwenso. Ndikulakwa kutenga pakati ndisanakwatire, koma cholakwacho chachitika kale ndipo ndadzikhululukira. Tsopano ndikupempha kuti nanunso mundikhululukire.
Ndikudziwa mwakhumudwa ndipo mumafuna kuti ndidzakwatiwe kaye. Koma moyo si umayenda mofanana kwa aliyense. Sindikunyadira zolakwa zanga, koma sindidzasautsidwa nazo kwambiri chifukwa kudandaula sikuthetsa mavuto. Musadandaule amayi, ngakhale ndili ndi pakati, ndidzakupangitsanibe kundinyadira."
Mawu ake anakhudza mtima wa mayi ake ndipo analonjeza kuti adzamuthandiza.
"Koma ukutani kumeneko? Wagona masiku angati mu hotelo? Bwanji osabwerera kuno kumudzi? Ndiwe wamng'ono kwambiri. Kodi udzakwanitsa kulipira chilichonse ku Blantyre-ko?"
"Ndikhala bwino amayi. Ndinasunga ndalama kuchokera ku bizinesi yanga. Ndidzagwiritsa ntchito mwanzeru ndikuyamba moyo wanga."
Atanena zimenezo, Lindah anamaliza kuyankhula ndi mayi ake ndipo anagona tulo tamtendere ngati mwana.
Ikupitrira......
Like share andcomment Osaiwala kupanga follow Patricia 2 Frakeza
Lindah courageous girl..a girl with highself esteem🥳🥳🥳🥳🥳