27/12/2025
Shehe wamkulu, komanso odziwika bwino ku chipembedzo cha chisilamu, m'dziko la Nigeria, Ahmad Abubakar Manhud Gumi, wapempha Dzikolo, kuti lithetse mgwilizano wake wa pakati pa Asilikali a Dzikolo ndi Asilikali a Dziko la America.
Shehe Ahmad Abubakar Manhud Gumi, wapitiliza kufotokoza kuti kupezeka kwa Asilikali a Dziko la America, pa nthaka ya Dziko la Nigeria, ndi chiopsyezo ku Dzikolo.
Shehe Ahmad Abubakar Manhud Gumi, wati ngakhale chili chinthu chofunika kwambiri kuthana ndi zigawenga, malinga ndi malamulo a chipembedzo cha chisilamu, ntchito yothana ndi zigawenga, ikuyenera ikuchitika ndi Anthu olungama, osati Anthu omwe ali ndi magazi m'manja mwawo.
Shehe Ahmad Abubakar Manhud Gumi, wati zomwe lachita Dzikolo, ndi zinthu zolakwika kwambiri, kamba koti zigawenga sizimagwebana zinzake, kamba koti cholinga chake ndi kufuna kupeza zinthu zina.
Shehe Ahmad Abubakar Manhud Gumi, wati zomwe achita Asilikali a Dziko la America, ndi zinthu zomwe zibweletse magulu ena Anthu okhala ndi zida za nkhondo, ku Dziko la Nigeria.
(Olemba Grant Elisha Ngozo) 26/12/25