
05/08/2025
Mbiri ya Zeze Kingston – Mlembi wa Nyimbo, Woyimba, Ndi Mtsogoleri wa Amapiano ku Malawi
Zeze Kingston, dzina lake lenileni Robert Ching’amba Junior, ndi m'modzi mwa oyimba otchuka kwambiri ku Malawi. Anabadwa pa 26 March 1993 ku Blantyre, koma adakulira ku Lilongwe, ndipo ndi m’modzi mwa anthu omwe akusintha kwambiri dziko la Malawi mu nyimbo zosakaniza za Afropop, Amapiano, Reggae, ndi Dancehall.
Zeze anayamba kuyimba ali mwana mu tchalitchi ndipo agogo ake ndi amene anamupatsa dzina lakuti Zeze chifukwa cha luso lake loimba. M’zaka za 2006 mpaka 2011, Zeze anali membala wa gulu lotchedwa Agwede, koma pambuyo pake anayamba kuyenda payekha.
Iye ali ndi digiri ya Drama ndi Sociology kuchokera ku Chancellor College ya University of Malawi. Kuwonjezera pa luso lake mu nyimbo, Zeze wakhala akugwira ntchito m'maboma, kusonyeza kuti ndi munthu wogwira ntchito molimbika.
Mu 2018, Zeze anapita ku South Africa kumene anakumana ndi nyimbo za Amapiano, zomwe zinamusintha kwambiri. Chifukwa cha kulimbikira kwake, mu 2023 adalowa mu “mainstream” ndikupeza kutchuka kwakukulu. Nyimbo zake monga “Shugga”, “Mvetsela”, “In My Zone”, ndi “For The Streets” zinakopa anthu ambiri.
Mu 2023, Zeze Kingston adapambana ma award awiri aakulu ku Maso Awards – Male Artist of the Year ndi Best Live Act. Adachitanso show yake yayikulu ku Blantyre yotchedwa “The Zeze Experience”, yomwe inali yodzaza ndi nyimbo, masewero, ndi chikondi.
Chimodzi mwa zinthu zapadera pa moyo wake, Zeze anakhazikitsa reality TV show yoyamba ku Malawi yotchedwa “The Kingstons”, yomwe ikutsatira moyo wake ndi wokondedwa wake.
Masiku ano, Zeze akugwira ntchito ndi oyimba akuluakulu monga Makhadzi, Heavy K, Ciza, Lady Du, ndi Tony Duardo, ndipo ali pa ulendo wowonetsa nyimbo zake mu mayi
TIKUBWELA NDI PAT2
ANTHANO ZAKASWILI
OSAYIWALA KUPANGA LIKE,SHARE COMMENT 🙏