23/06/2026
Mayi Woyamba -Episode 2
Chipinda chochezera cha nyumbayi chinali chokongola kwambiri komanso chapamwamba. Pansi pake panali kapeti wofiira wokongola, ndipo makoma ake anali opakidwa utoto woyera wonyezimira. Makomawo anali oyera kwambiri moti Brian ankatha kuona chithunzi chake chikuwonekera pa iwo ngati galasi. Atangolowa m’chipindamo, anatenga mpweya wakuya ndipo mpweya wozizira wa makina oziziritsira mpweya unamupangitsa kumva bwino. Nyumba yonseyo inasonyeza chuma ndi mphamvu. Mayi Woyamba anasankha yekha nyumbayi, ndipo anthu ena sankaloledwa kulowamo. Inali nyumba yobisika yomwe inali m’dera lapamwamba la nyumba za m’likulu la boma.
Brian anaikonda kwambiri nyumba imeneyi, koma anadabwa kwambiri ndi zimene Mayi Woyambayu anamuuza atamulowetsa m’chipinda china cha nyumbayo.
“Brian , ndinakuitana kuno chifukwa ndakusowa kwa zaka zambiri. Chifukwa chimene ndinakusiyira nthawi imeneija n’chakuti sunali wokonzeka kukwatira ndipo sunali ndi ndalama zokwanira. Tsopano ndili ndi mphamvu ndi chuma, ndipo ndikufuna kuti tikhalenso pafupi ngati kale,” adatero Mayi Woyamba.
Brian anangokhala chete chifukwa anali wosokonezeka komanso wodabwa.
“Koma munandiuza kuti ndidzakhale mthandizi wanu wapadera. Munati ndidzagwira ntchito ku nyumba ya boma. Nanga bwanji mwandibweretsa kuno? Ntchito yomwe ndinabwera kudzagwira ili kuti?” anafunsa Brian.
“Brian usandikhumudwitse. Ndikufuna ukhale munthu amene ndingamudalire komanso kumamuyandikira nthawi zonse. Udzudzalandira ndalama zambiri, nyumba yabwino, galimoto komanso maubwino ena ambiri. Sindikufuna kuti udzavutike moyo wako wonse,” anayankha Mayi Woyamba.
“Musaiwale kuti ndine munthu wokwatira. Ndili ndi mkazi komanso mwana. Sindikufuna chilichonse chomwe chingabweretse mavuto m’banja langa kapena m’banja lanu,” adatero Brian.
Koma Mayi Woyamba sanasinthe maganizo ake.
“Sindikukupempha kuti usiye mkazi wako. Ndikungofuna kuti tizikhala pafupi. Mwamuna wanga amakhala wotanganidwa kwambiri ndi ntchito za boma ndipo nthawi zambiri samakhala ndi nthawi yokwanira. Ndikufuna munthu amene ndingamukhulupirire,” adatero.
Brian anamuyang’ana Mayi Woyambayu ndipo anaona kuti akadali wokongola monga momwe analili kale. Komabe, anadziwa kuti zimene ankafunazo zikanabweretsa mavuto ambiri.
“Ayi. Sindingachite zimenezo. Chonde, ndiwonetseni ntchito yeniyeni yomwe munandiyitanira. Sindinabwere kudzachita zimene mukunenazi,” adatero Brian.
Mayi Woyamba anaoneka kukwiya.
“Ndakuuza kale ntchito yomwe ndikufuna uzigwira. Ngati sukufuna kugwira , basi ndifufuza munthu wina amene angandithandize.”
“Ngati ndi choncho, ndiye pangani momwe mwaonera. Sindingachite zinthu zosagwirizana ndi zomwe ndimakhulupirira. Ndine wokwatira ndipo ndikufuna kukhala wokhulupirika ku banja langa,” anayankha .
Atayankhula zimenezo, anatuluka m’nyumbamo ndikubwerera kunyumba kwake. Mayi Woyamba anakhumudwa kwambiri ndipo anachoka pamalopo ali wokwiya.
Brian atafika kunyumba kuja , anauza mkazi wake zomwe zinachitika.
“Mayi Woyamba akunena kuti andichotsa ntchito,” adatero.
“Chani? Koma tangofika kumene! Nchifukwa chani akufuna kukuchotsa?” anafunsa Amina modabwa.
“Sindinakonde zimene akufuna kuti ndizichita.Ndi zosiyana kwambiri ndi ntchito yomwe anandilonjeza poyamba ija,” anayankha Brian.
“Koma Nchifukwa chani wakana? Ife takhala tikuvutika kwa nthawi yayitali. Kodi sungaganizireko za tsogolo la banja lathu? Ndalama zimenezi zitha kusintha moyo wathu. Mwana wathu athanso kubwerera kusukulu ndipo moyo wathu ungakhalenso wabwino,” adatero Amina mokwiya.
“Ndikumva zimene ukunena, koma sindingapange chilichonse chomwe chingawononge ulemu wanga kapena banja lathu,” anayankha Brian
Amina anakhala chete kwa kanthawi, koma ankawonekabe kuti sankakhutira ndi yankho la mwamuna wakelo.
Ikupitrira....
Kodi Brian apitirizabe kukana zomwe Mayi Woyamba akufuna? Kapena mavuto atsopano ayamba m’banja lakeli chifukwa cha chisankho chimene wapanga??
Like share and comment komanso follow Patricia 2 Frakeza