Democratic Progressive Party DPP - Southern Region

Democratic Progressive Party DPP - Southern Region Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Democratic Progressive Party DPP - Southern Region, Broadcasting & media production company, Kirkaldy, Blantyre.

Noel Lipipa writes:Our message of national unity is shared across faiths.Just as the Bible teaches that a nation is like...
14/11/2025

Noel Lipipa writes:
Our message of national unity is shared across faiths.
Just as the Bible teaches that a nation is like one body made of many parts, Islam also carries the same wisdom.

The Prophet Muhammad (peace be upon him) taught that believers are like one body — “when one part suffers, the whole body feels the pain, and when one part is well, the whole body benefits”. (Sahih al-Bukhari 6011)

This is the spirit Malawi needs.
Different regions, different beliefs — but one nation, one people, one destiny.

Let us continue building a Malawi where every community feels seen, valued, and supported.

Voterani Eric Mofolo kuti akhale Mayor wa Mzinda wa Blantyre monga mwa masomphenya a Professor Arthur Peter Mutharika.
14/11/2025

Voterani Eric Mofolo kuti akhale Mayor wa Mzinda wa Blantyre monga mwa masomphenya a Professor Arthur Peter Mutharika.

13/11/2025

Hon. Mwayi Ndalama Chiradzulu Nyungwi Constituency kuyankhula mfundo ku nyumba ya malamulo.

ERIC MOFOLO AKUKWANIRA KUKHALA MFUMU YA MZINDA WA BLANTYRE.Chipani cha DPP chitawunguza potengera ndi munthu yemwe akufu...
13/11/2025

ERIC MOFOLO AKUKWANIRA KUKHALA MFUMU YA MZINDA WA BLANTYRE.
Chipani cha DPP chitawunguza potengera ndi munthu yemwe akufunika kuti akhale Mfumu ya Mzinda wa Blantyre chapeza kuti amene wakwanitsa ndondomeko zonse zofunikira ndi Eric Mofolo khansala wachipanichi oyimira dera la Mapanga Mzedi Ward.

Potengera ndi chikalata chomwe chipani cha DPP chinatulutsa kumapeto kwa mwezi wa November m'chaka chino cha 2025, munali ndondomeko zina zomwe zimawunikira masomphenya a munthu, maphunziro ake, kukhulupirika pa kagwiridwe kake ka ntchito, mbiri yake ndi zina zambiri potengera ndi munthu amene akhale mfumu ya mzindawu.

Pakadalipano chidwi cha Professor Arthur Peter Mutharika ndichoti akufuna kuyika anthu omwe angathandizire kuti masomphenya ake akhale otheka mwachangu potengera ndi mavuto omwe dziko la Malawi ladutsamo.

Ino ndi nthawi yomwe Professor Arthur Peter Mutharika akufuna kuti Mzinda wa Blantyre uyambe kulandira zosowa zake pakutsatira kubwereranso kwa maofesi aboma mu mzindawu.

Eric Mofolo ndi yankho kwa anthu amu Mzinda wa Blantyre ngati Mayor.
13/11/2025

Eric Mofolo ndi yankho kwa anthu amu Mzinda wa Blantyre ngati Mayor.

Eric Mofolo akuyenera kukhala Mayor wa Mzinda wa Blantyre ndipo akuluakulu achipani ndi ena amumzindawu avomereza zimene...
13/11/2025

Eric Mofolo akuyenera kukhala Mayor wa Mzinda wa Blantyre ndipo akuluakulu achipani ndi ena amumzindawu avomereza zimenezi.

Izi sizoti zangochitika ayi, koma mwa onse opikisana atafufuzidwa komanso pomva mfundo zawo ndi m'mene anthu amafunira mzinda wa Blantyre ukumawonekera, zawonetsa kuti Eric Mofolo akugwirizana ndi masomphenya a Professor Arthur Peter Mutharika.

MUKAVOTERA ERIC MOFOLO NGATI MAYOR WA MZINDA WA BLANTYRE NDIYE KUTI MWASANKHA CHITUKUKO.Kutumikira anthu kumafunika nzer...
13/11/2025

MUKAVOTERA ERIC MOFOLO NGATI MAYOR WA MZINDA WA BLANTYRE NDIYE KUTI MWASANKHA CHITUKUKO.
Kutumikira anthu kumafunika nzeru ndi luntha komanso mayitanidwe amumtima.

Eric Mofolo atawunikiridwa bwino zawonetsa kuti chidwi chake chofuna kukhala Mayor wa Mzinda wa Blantyre kupindulira anthu ambiri pa chipambano cha mzindawu angakhalenso dziko.

Masomphenya a Eric Mofolo akugwirizana ndendende ndizomwe Professor Arthur Peter Mutharika amafuna.

Mukavotera Eric Mofolo ndiye kuti mwasankha chipambano cha mzinda wa Blantyre komanso dziko la Malawi.

Sitingakambe za chitukuko cha Blantyre ngati munthu otumikira mzindawu alibe masomphenya.Aliyense amafuna pomwe amakhala...
13/11/2025

Sitingakambe za chitukuko cha Blantyre ngati munthu otumikira mzindawu alibe masomphenya.

Aliyense amafuna pomwe amakhala pali powoneka bwino ndipo izi zimabweretsa chimwemwe komanso anthu ozungulira deralo amakhumbira kumafikapo kamba koti malowo ndi owoneka bwino.

Mzinda wathu wa Blantyre kuti uzakhale otukuka pa chuma ndi mawonekedwe pakufunika munthu wa masomphenya abwino ngati Eric Mofolo.

Eric Mofolo ali ndi chidwi chozatukula mzinda wa Blantyre mutamupatsa mwayi okhala mfumu ya mzindawu (Mayor).

Mofolo ali ndi maphunziro abwino, wagwira ntchito zikuluzikulu m'maofesi aboma komanso ku mayiko akunja choncho wakonzekera kutumikira mzinda wa Blantyre mokomera aliyense potengeranso ndi masomphenya a Professor Arthur Peter Mutharika.

Mukavotera Eric Mofolo ndiye kuti mwasankha chitukuko cha mzinda wa Blantyre.

Lakwana lokha tsiku lokavotera Eric Mofolo kuti akhale Mayor wa Mzinda wa Blantyre amenenso akufunidwa ndi Professor Art...
12/11/2025

Lakwana lokha tsiku lokavotera Eric Mofolo kuti akhale Mayor wa Mzinda wa Blantyre amenenso akufunidwa ndi Professor Arthur Peter Mutharika.

Chipambano cha Blantyre City chafika!Eric Mofolo wazipereka kuti athandizire masomphenya a Professor Arthur Peter Muthar...
12/11/2025

Chipambano cha Blantyre City chafika!

Eric Mofolo wazipereka kuti athandizire masomphenya a Professor Arthur Peter Mutharika pokhala mayor ochita wa Mzinda wa Blantyre.

Zabwino zonse ma mpando wa Mfumu ya Mzinda wa Blantyre
12/11/2025

Zabwino zonse ma mpando wa Mfumu ya Mzinda wa Blantyre

BLANTYRE IRI NDI CHOKHUMBA PA MUNTHU YEMWE AKHALE MAYOR.Aliyense amakhala ndichokhumba ndipo ife ngati anthu timafuna ti...
11/11/2025

BLANTYRE IRI NDI CHOKHUMBA PA MUNTHU YEMWE AKHALE MAYOR.
Aliyense amakhala ndichokhumba ndipo ife ngati anthu timafuna tiri ndi zabwino pa moyo umene tikukhala angakhalenso kawonekedwe ka dziko lathu timafuna kali kabwino.

Chomwe munthu wachikulire amawona atakhala, pena kumakhala kovuta kuti wachichepere achiwone angakhale ali wotalika mu usinkhu.

Nzeru ipambana zonse ndipo chibwana chimalanda nachipweteketsa dziko kamba ka anthu opusa, osawona patali ndi okonda ndalama.

Padakalipano tikamati tikufuna zinthu zabwino timayang'anira kuti anthu akudera apindula bwanji ndi atsogoleri omwe tikuwafuna.

Kwanthawi yaitali mzinda wathu wa Blantyre wakhala usakuyenda bwino kamba kakulephera kwa atsogoleri anthu a mzindawu.

Nthawi yomwe Blantyre imalozeka inali nthawi ya a Noel Chalamanda yemwe anali Mayor wa Mzinda wa Blantyre mbuyomu ndipo atangochoka mzindawu wasanduka wabwinja.

Mayor wa mzindawu kuyambira kuyambira pano akufunika akhale wamaphumziro abwino, okhala ndi ukadaulo wa utsogoleri, oziwa kuchita ziganizo zabwino, oziwa kulemba ndi kuwerenga, oziwa kuyankhula chizungu chomveka bwino, akhale wambiri yabwino ndi zina zotero.

Izi ndizofunikira kwambiri kamba koti kukhala Mayor umayimirira anthu ndipo pamafunika kumalemba makalata olumikizana ndi akuluakulu ochita malonda, makampani, kukumana ndi nthumwi zochokera mayiko akunja ndikulumikizana momveka bwino pa chitukuko cha mzinda komanso dziko.

Eric Mofolo atapimidwa bwinobwino zawonetsa kuti akukwanira kukhala Mayor ndipo akuluakulu ambiri mu mzinda wa Blantyre ali okondwa kwambiri.

Eric Mofolo ndi munthu olimbikira kwambiri, wambiri yabwino, ophunzira bwino, wagwira ntchito ngati owerengesera ndalama m'mawofesi aboma kwa dzaka 10 komanso wakhalapo wapampando ku mabungwe omwe amayang'anira zakawerengeseredwe ka ndalama angakhalenso kutsogolera makampani osiyanasiyana monga wamkulu.

Chiyembekezo cha athu a mzinda wa Blantyre ndichachikulu ndipo yemwe akuyenera kukhala Mayor wa mzindawu akuyeneranso kukhala ndi masomphenya akulu otukula mzindawu osati okonda masewera.

Eric Mofolo sazakukhumudwitsani akakhala Mayor wa Mzinda wa Blantyre.

Address

Kirkaldy
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Democratic Progressive Party DPP - Southern Region posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Democratic Progressive Party DPP - Southern Region:

Share