25/07/2026
HERITAGE CARE FOUNDATION YAKHAZIKITSIDWA KU MANGOCHI
Anyamata awiri, Francis Mpezeni ndi Jonathan Khangaiwa, akhazikitsa bungwe lotchedwa Heritage Care Foundation, lomwe lakhazikitsidwa ndi cholinga chothandiza achikulire pa moyo wawo wa uzimu komanso wa kuthupi.
Poyambitsa ntchito za bungweli lero m'mudzi mwa Bauleni, m'boma la Mangochi, Heritage Care Foundation yathandiza anthu achikulire okwana 20 powapatsa zinthu zofunika pa moyo wawo wa tsiku ndi tsiku monga sopo, mchere komanso machesi.
Mmodzi mwa akuluakuku oyambitsa bungweli, Francis Mpezeni, wati cholinga cha Heritage Care Foundation ndi kuthandiza achikulire omwe nthawi zambiri amakumana ndi mavuto chifukwa chosowa zinthu zofunika pa moyo wawo komanso kuwalimbikitsa pa moyo wa chikhulupiriro.
"Takhazikitsa Heritage Care Foundation kuti likhale chiyambi cha ntchito yothandiza achikulire osati kuwapatsa zinthu zokha, komanso kuwalimbikitsa pa moyo wa uzimu kuti azikhala ndi chiyembekezo," watero Mpezeni.
Mmodzi mwa omwe alandira thandizoli, Sandy Hussein, yemwenso ndi mfumu ya mudzi wa Bauleni, wayamikira kwambiri ntchito yomwe Heritage Care Foundation yayambitsa.
Hussein walimbikitsanso Francis Mpezeni ndi Jonathan Khangaiwa kuti asataye mtima kapena kusiya ntchito yabwinoyi panjira, koma kuti apitirize kuthandiza achikulire chifukwa anthu ambiri okalamba amakumana ndi mavuto a kusowa kwa zinthu zofunikira pa moyo wawo wa tsiku ndi tsiku.
Anthu a m'derali akukhulupirira kuti Heritage Care Foundation ikhala chiyambi cha kusintha miyoyo ya achikulire ambiri m'boma la Mangochi komanso m'madera ena a dziko lino ngati ingathathandizidwe ndi anthu komaso mabungwe osiyanasiyana a mdziko muno ingakhale mayiko ena.