Eye of an Eagle Malawi

Eye of an Eagle Malawi 0 881 673 119

Ngati njira imodzi yolimbikitsa umodzi pakati pazipani zandale bungwe la atolankhani la Blantyre Press Club yapempha aku...
26/12/2024

Ngati njira imodzi yolimbikitsa umodzi pakati pazipani zandale bungwe la atolankhani la Blantyre Press Club yapempha akulu akulu azipani kuti akhazikike pofotokoza mfundo zawo osati kunyozana pomwe dziko la Malawi likupita kuchisankho chaka chamawa.

Tsogoleri wabungweri Luke Chimwaza wanena izi pomwe akonza msonkhano waukulu wapachaka omwe uchitike pa 27 December2024 m'boma la Mulanje.

"Ife atolankhani pokhala kamwa ya a Malawi tilindi udindo obweletsa pamodzi andale kuwafotokozera kuti a Malawi akufuna chitukuko osati kunyozana kotero akufunika azifotokoza m'mene azathetsere mavuto omwe anthu akukumana nawo osati kunyozana. Pa ichi tatiana azipani zosiyanasiyana kumsonkhanowu", atero a Chimwaza.

Mwambuwu ukuyembekezera kubweretsa pamodzi zipipani monga MCP, DPP, UDF, UTM, AFORD kungotchula zochepa chabe.

Mthumwi Kuchokera Ku MEC, NICE Trust Komanso Salima sugar zikhala nawonso pamsonkhanuwu.

Wolemba Happy Makhalira- Blantyre

16/10/2024

Zipani za Democratic progressive DPP, United Transformation Movement UTM ndi Alliance for Democracy AFORD ati mkulu wa bungwe loyendetsa chisankho la MEC a Anabel Mtalimanja atule pansi udindo ponena kuti akukayikitsa ngati agwire ntchito yokomera mzika za dziko lino pachisankho chikubwera chaka cha mawa.

Zipanizi zanena izi ma nsonkhono wa olemba nkhani omwe ukuchitikira ku Lilongwe.

Mwa ena omwe ali pansonkhanowu ndi mlembi wankulu wa UTM Dr Patricia Kaliyati, wachiwiri kwa tsogoleri wa AFORD Timothy Mtambo mlembi wamkulu wa DPP a Peter Mukhitho, a Bright Msaka, Shadrake Namalomba ndi ena.

Zipanizi zati bungwe la MEC lapanga hayala kampane ya Smartmatics yoti izagwire ntchito powerengera mavoti ngakhale kuti kampaneyi ilindimbiri yosokoneza zisankho m`mayiko ena.

Wolemba Happy Makhalira

  #Mtsogoleri wa chipani cha LEF wapeleka asiku 14 kwa mtsogoleri wadziko lino Dr Lazurus Chakwera kuti akhazikitse kafu...
12/10/2024

#

Mtsogoleri wa chipani cha LEF wapeleka asiku 14 kwa mtsogoleri wadziko lino Dr Lazurus Chakwera kuti akhazikitse kafukufuku ndikupeleka lipoti la ngozi yomwe inapha wachiwiri wakale wadziko lino malemu Dr Saulos Chilima.

Iwo ati ngati izi sizichitika mumasiku amenewo iwo pamodzi ndi chipani cha LEF apita ku nyumba ya malamulo kukatula nykhawa zawo.

Iwo ati ino sinthawi yopanga mantha ndipo a Malawi akuyenera kudzuka ndikususana ndikupondelezedwa.

Iwo ati yakwana nthawi tsopano kuti ndale za m`dziko muno zisinthe ndikuyamba kukomera mzika.

Wolemba Happy Makhalira

Mtsogoleri wa chipani cha LEF Dr David Mbewe tsopano ayamba kulankhula kuchikhamu cha anthu chomwe chafika pa bwalo la N...
12/10/2024

Mtsogoleri wa chipani cha LEF Dr David Mbewe tsopano ayamba kulankhula kuchikhamu cha anthu chomwe chafika pa bwalo la Nyambadwe primary School komwe chipanichi chikuchititsa msonkhano.

Uwu ndi msonkhano oyamba wachipanichi kuchokera pomwe chinalembetsedwa mu January Chaka Chino .

Wolemba Happy Makhalira _Blantyre

# #

Mtsogoleri wachipani cha Liberation for Economic Freedom Dr David Mbewe ndi mayi akunyumba mama Linda Mbewe afika pa bwa...
12/10/2024

Mtsogoleri wachipani cha Liberation for Economic Freedom Dr David Mbewe ndi mayi akunyumba mama Linda Mbewe afika pa bwalo la Nyambadwe primary School pomwe chipanichi chikuchititsa msonkhano.

Pabwaloli pafika anthu ochuluka omwe akufuna kunva zomwe Dr Mbewe akufuna kuwayankhula.

Wolemba Happy Makhalira_Blantyre
#

Woyimira anthu pa milandu Alexious Kamangira wakana kupepesa oweluza milandu Ku high court Ken Manda omwe amafuna Kuti a...
11/10/2024

Woyimira anthu pa milandu Alexious Kamangira wakana kupepesa oweluza milandu Ku high court Ken Manda omwe amafuna Kuti a Kamangira awapepese powaipisira mbiri.

A Ken Manda anafunsa a Kamangira Kuti awapepese ndi k250,000,000 komanso alembe uthenga owapepesa pa samba la Facebook ndipo a Kamangira atsindike Kuti zomwe akhala akulemba zokhuza a Manda ndizaboza.

Lawyer Alexious Kamangira wakhala akulemba Kuti judge Ken Manda ndiwakatangale ndipo amalandira ziphuphu Kuti azigamula milandu mokomera ena.

Koma poyankha pa pempho la a Manda lofuna kupepesedwa, layer Kamangira wati akasume ndipo iye sapepesa.

"Malinga ndikalata yofuna kupepesedwa yomwe munalemba m'malo mwa a Ken T Manda, chonde kasumeni", chatero chikalata chomwe a Kamangira alembera lawyer yemwe akuimira a Manda, Michael Goba Chipeta

Pakadalipano a Chipeta atenga chileso choketsa a Kamangira kulemba chilichonse chokhuza a Manda kufikira nkhaniyi itanvedwa ndi abwalo.

Mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera lero wafika mu mzinda wa Blantyre pomwe akuyembekezeraka kutsogolera masewer...
11/10/2024

Mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera lero wafika mu mzinda wa Blantyre pomwe akuyembekezeraka kutsogolera masewero a golf loweluka ku country club ku Limbe mu mzindawu.

akuwoneka mwa mphanvu ndi thanzi Dr Chakwera atera pa bwalo landenge la chileka chakum`mawaku pomwe analandilidwa ndi akulu akulu aboma komanso aku chipani cha Malawi Congress.

masewero a golf wa cholinga chake ndikutolera ndalama yothandizira ophunzira osowa m`sukulu za ukachenjede komanso kuthandizira anthu omwe anakhuzidwa ndi namondwe freddy.

#

Nthambi ya achinyamata muchipani cha Liberation for Economic Freedom LEF chomwe tsogoleri wake ndi Dr David Mbewe yati n...
05/09/2024

Nthambi ya achinyamata muchipani cha Liberation for Economic Freedom LEF chomwe tsogoleri wake ndi Dr David Mbewe yati nthawi yakwana Kuti achinyamata atengepo mbali potukula dziko lino.

Achinyamatawa anena izi lachitatu pomwe amachititsa msonkhano wa wolemba nkhani mu mzinda wa Blantyre.

Iwo ati ino sinthawi yoti achinyamata azigwiritsidwa ntchito ndi andale pobweretsa chisokozeno m'dziko.

Poyankhula pamsonkhanowu wachiwiri Kwa Mlembi wachipanichi Mayi Gloria Manjomo ati chipanichawo chayambapo kale kuthandiza achinyamata mdziko muno powapatsa mwayi wangongole zopanda chikole.

Iwo ati ndichipongwe chachikulu kudinda chikole kwamunthu yemwe wangomaliza maphunziro Ake ndipo akufuna ngongole Kuti ayambire business.

A Manjomo kenako apempha achinyamata mdziko muno kuzavotera Dr David Mbewe pansi pachipani cha LEF ponena Kuti Dr Mbewe ndi Bwenzi la achinyamata lomwe lakonzeka kukonza mavuto achinyamata mdziko muno.

Chipani cha Liberation For Economic Freedom LEF chakonza msonkhano omwe uchitike ku Nyambadwe primary School ground pa 28 September Chaka Chino ndipo mtsogoleri wachipanichi Dr David Mbewe akuyembekezereka kuzatsogolera msonkhanowu.

Wolemba Happy Makhalira _Blantyre
Chithunzi_Chisomo Phiri

Mpingo wa Living Word Evangelistic omwe mtsogoleri wake ndi Prophet David F. Mbewe lero ukuchititsa mwambo waukulu wa ma...
01/05/2024

Mpingo wa Living Word Evangelistic omwe mtsogoleri wake ndi Prophet David F. Mbewe lero ukuchititsa mwambo waukulu wa mapemphero otchedwa Shalom Day pa Desert ground Ku Bangwe mu mzinda wa Blantyre.

Mtsonkhanowu wabweretsa pamodzi anthu ochokera Madera osiyana Aiyana.

Modzi mwa anthu omwe afika kale pa Malo ano a Margret Singini ati akuyembekezera kukumana ndi mphamvu ya Mulungu pokutha pa mwambowu.

"Mulungu agenda pano Moti zadzikulu zake zichitikira anthu ake"atero mayo Singini.

Pakadalipano prophet Mbewe sanafike pa malopa.

Eye of an eagle Malawi ikhala ikukupatsilani zonse.

Wolemba Happy Makhalira_Desert ground Bangwe Blantyre.

07/03/2024

Shout out to our newest followers! Excited to have you onboard! Muhammad Matola, Painkiller Mkalimwana

Chipani cha Liberation For Economic Freefom( LEF) chomwe mtsogoleri wake ndi Dr David Mbewe chati ndichokhumudwa ndi mch...
24/02/2024

Chipani cha Liberation For Economic Freefom( LEF) chomwe mtsogoleri wake ndi Dr David Mbewe chati ndichokhumudwa ndi mchitidwe waupandu omwe anthu ena akuchitira otsatira zipani zosusa boma m'chigawo chapakati.

Iwo ati otsatira zipani zina mchigawochi akhala akukumana ndinkhaza monga kumenyedwa komaso kuonongeledwa katundu ndi anthu osaziwika pazifukwa zandale.

Mlembi wachipanichi mayi Georgina Limbikani Chunga anena izi kusatira zaupandu zimene anthu ena achitira otsatira chipani Cha Democratic Progressive DPP pa Mbowe ku Lilongwe pomwe otsatira DPP amasonkhana kuti ayambe m'dipiti omwe chipanichi chinakonza pofuna kumema anthu kuti akalembetse ziphatso za umzika kuti azakwanitse kuponya voti Chaka chamawa komaso kumema anthu akuti alowe chipani. .

Mayi Chunga ati aka sikoyamba kuti zaupanduzi zichitike pomwe pali malipotiso oti otsatira zipani za UDF komaso DPP anamenydwaso ku Dowa komaso ku Dedza.

Iwo ati mchitidwe waziwawa ndiosavomelezeka mu ulamuliro wa democracy omwe dziko lino linasankha.

Iwo apempha masapota azipani kukhala mololelana pomwe tikuwandikira nthawi ya zisankho.

Anthu oposa khumi ndiomwe agonekedwa pa chipatala Cha African Bible College (ACB) ku area 47 mumzinda wa Lilongwe.

Kupatula kumenya otsatira chipani Cha DPP anthu awupanduwa awonongatso galimoto zomwe zimayenera kugwilitsidwa ntchito pa m'dipitiwu.

Wolemba James Nkhoma Labana- Lilongwe

Address

Chimwankhunda
Blantyre

Telephone

+265881673119

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Eye of an Eagle Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share