31/10/2025
Bungwe la Tikondane Trade Import and Export Association lachita mgwirizano ndi bungwe la Cotton Council of Malawi, pofuna kuthandizira alimi a Thonje, kufikira misika ya mbewuyi mosavuta.
Mtsogoleri wa bungwe la Tikondane, a John Khisimisi Tembo wati mwa mgwirizanowu, uthandizira kuti alimi adzitha kugulitsa mbewuyi, pa mitengo yabwino, komanso kufikira misika ya kunja kwa dziko lino.
Mabungwe awiriwa, achita mgwirizanowu lachinayi, pamenenso atsimikizira za kudzipereka kwawo pothandizira alimi kupeza ndalama za kunja, zomwe zimafunikira pa msika wa pakati pa dziko lino ndi maiko ena.
Pakadali pano, alimi a Thonje awalimbikitsa kukhala ma membala a mabungwe awiriwa, kuti athe kufikira thandizo pa ulimi wawo mosavuta.
Wolemba Daniel Zimba