Times 360 Malawi

Times 360 Malawi Times 360 Malawi, the online platform of the award-winning Times Group, Malawi’s only 360 media house
(369)

The Times Group has challenged itself since its humble beginnings in 1895 when it published the inaugural newspapers at Songani in Zomba. This is the only media giant and market leader in newspapers, radio, television, offset printing, courier, publishing, and advertising agency bagging a long list of media awards local and international through investigative and analytic journalism.

  Mtsogoleli wa dziko lino Peter Mutharika wasankha abusa Alexander Kambiri kukhala wachiwili kwa mlangizi wake pa nkhan...
10/01/2026



Mtsogoleli wa dziko lino Peter Mutharika wasankha abusa Alexander Kambiri kukhala wachiwili kwa mlangizi wake pa nkhani za chipembedzo.

Mu kalata yomwe mlembi wa mu ofesi ya President ndi nduna a Justin Saidi atulutsa lero, a Kambiri ayamba ntchito yawo lero.

A Kambiri ndi M’busa wa CCAP mu sinodi ya Nkhoma

A Timothy Khoviwah Ndiye mulangizi wa mkulu mu ofesiyi.

Nkhani

10/01/2026



Akonzi a kanema wotchedwa 'The Royal Dilemma' yemwe muli atengambali odziwika monga Joyce Chavula komanso Miracle Chinga ati kanemayu sakukopela kapena kutengela makanema akunja.

Mmodzi wa akonziwa Edwin Chonde wati nkhani ya kanemayu ikukhudza nkhani za maufumu omwe alinso mdziko muno.

Iwo ati sakutengela kanema zaku Nigeria monga ena akuganizira ponena kuti kanemayu akulunjika pa nkhani zachikhalidwe cha dziko lino.

A Chonde omwe akhala akutenga mbali mmakanema ambiri a mdziko muno anena izi lero pa msonkhano wa atolankhani omwe unachitika mu mzinda wa Lilongwe.

Kanemayu aonetsedwa koyamba pa 27 March 2026 mu mzinda wa Lilongwe.

Akonziwa alonjeza zoonetsaso kanemayu mzigawo zina za dziko lino monga Blantyre, Mzuzu komanso Zomba, asanamuponye pa YouTube.

A Chonde akufotokoza zambiri mkanemayu.

(Wolemba Jimmy Chazama)

10/01/2026

TIMES EXCLUSIVE | LUCY MTILATILA, DIRECTOR DEPARTMENT OF METEOROLOGICAL SERVICES & CLIMATE CHANGE | 10 JANUARY 2026

 Newly crowned Miss Malawi queen Thandie Chisi has said her crown is a tool for change.Chisi says she is using it to emp...
10/01/2026



Newly crowned Miss Malawi queen Thandie Chisi has said her crown is a tool for change.

Chisi says she is using it to empower young women in rural areas.

She made the remarks during a community event held at M’gona C in Lilongwe on Saturday.

Her group, Sustainable Fashion and Women Empowerment (SFWE), is recruiting for Cohort 4 of the Empower Her Now Program.

The program, which teaches tailoring, design and sustainable fashion, runs for six months.

“Many young women are willing to work but lack opportunities and practical skills,” Chisi said.

(Reported by Jimmy Chazama)

  Thupi la yemwe anakhalapo wachiwiri kwa sipikala wa nyumba ya malamulo, a Madalitso Kazombo, lafika ku Vikuyu Esiteti,...
10/01/2026




Thupi la yemwe anakhalapo wachiwiri kwa sipikala wa nyumba ya malamulo, a Madalitso Kazombo, lafika ku Vikuyu Esiteti, m'dera la mfumu yaikulu Kaomba m'bomali, komwe lilowe m'manda mawa, Lamulungu.

A Kazombo, anamwalira Lachinayi, pa 8 mwezi uno atadwala kwa ka nthawi kochepa nthenda ya Mphumu (Asthma).

Iwo anakhalapo phungu wa dera la kuvuma kwa boma la Kasungu kuyambira m'chaka cha 2014 mpaka 2025 ndipo anasankhidwa kukhala wachiwiri woyamba kwa sipikala wa nyumba ya malamulo m'chaka cha 2019 mpaka 2025.

A Kazombo, anabadwa pa 31 May, m'chaka cha 1979 ndipo asiya mkazi ndi ana atatu.

Wolemba: Nelson Gonjani.

10/01/2026

TIMES EVENING NEWS | 10 JANUARY 2026

  Minister of Transport and Public Works Jappie Mhango said lack of funding is one of the challenges that has slowed the...
10/01/2026



Minister of Transport and Public Works Jappie Mhango said lack of funding is one of the challenges that has slowed the completion of Rumphi- Nyika- Chitipa road in Rumphi district.

He made the remarks on Saturday after touring a 20 kilometer Bolero to Bembe stretch and Njakwa- Mphwaphwa -Livingstonia road in the district.

Mhango said the project which was launched in 2018 was expected to be completed within a year but failed to meet the deadline due to delayed payments to the contractor and fuel scarcity.

He has however said that government has not been able to meet the obligations overtime but stated that he will engage the ministry of finance to see how the matter that can be addressed .

He also added that his ministry through the Roads of Authority will be doing homework to ensure that Njakwa- Mphwaphwa stretch which was abandoned to be constructed.

Meanwhile Rumphi district council chairperson Alfred Butao said the road will ease problems of transportation of farm produce to and from various markets once it is completed.

Reported for Nertha Hara.

  The body of late Flames striker Esau Kanyenda will be laid to rest on February 4 in Manchester, United Kingdom, his fa...
10/01/2026



The body of late Flames striker Esau Kanyenda will be laid to rest on February 4 in Manchester, United Kingdom, his family has disclosed.

Organizing Chairperson of the funeral committee Velli Nyirongo confirmed the development today saying detailed funeral arrangements will be communicated later.

Kanyenda as Black Mamba is known succumbed to a liver cancer on December 2 2025.

Kanyenda had a distinguished career having played in South Africa and Russia.

Reported by Mphatso Malidadi

  Mmodzi wa ochita malonda m'boma la Kasungu, a Noah Suzgo Nhlane, walimbikitsa asungwana osewera masewera a mpira wa mi...
10/01/2026



Mmodzi wa ochita malonda m'boma la Kasungu, a Noah Suzgo Nhlane, walimbikitsa asungwana osewera masewera a mpira wa miyendo m'bomali kuti alimbikire maphunziro komanso kupewa m'chitidwe ogonana adakali achichipere.

A Nhlane, ayankhula izi pomwe amapereka mipira kwa ma timu a Creck Ladies komanso FC Liano, pa bwalo masewero la sukulu ya pulayimale ya Chithiba.

"Tikuwalimbikitsa asungwanawa kuti alimbikire sukulu komanso kupewa m'chitidwe ogonana adakali achipere kuti akwanilitse masomphenya awo ngati Temwa Chawinga komanso Tabitha Chawinga," atero a Nhlane.

Mmawu ake, wapampando wa masewera a mpira wa miyendo m'bomali, a Moffat Time, wayamikira a Nhlane kaamba kowalimbikitsa asungwanawa komanso popereka mipira ponena kuti zithandizira kuti asungwanawa azikhala otanganidwa ndi kuzikonzekeretsa za tsogolo lawo.

Pamapeto pa mwambowu, ma timuwa anapimana mphamvu ndipo timu ya Creck Ladies, ndiyomwe inapambana ndi zigoli zitatu kwa chilowere.

Wolemba: Nelson Gonjani.

 Ndalama zoposa K50 million ndi zomwe zagwiritsidwa ntchito kufikira pano kuti kanema wotchedwa 'The Royal Dilemma' athe...
10/01/2026



Ndalama zoposa K50 million ndi zomwe zagwiritsidwa ntchito kufikira pano kuti kanema wotchedwa 'The Royal Dilemma' atheke.

Izi zanenedwa lero pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe omwe cholinga chake chinali kulandira thandizo la ndalama zothandizira mwambo woonetsa kanemayu koyamba mu mzindawu omwe uliko pa 27 March 2026 ku BICC.

Ida Chicker Chabs yemwe alinso mkanemayu wapereka ndalama zokwana K5 million pamene a Aunt Dee's Garden apereka ndalama zokwana K500,000 ndi zinthu zina.

Kanemayu yemwe wajambulidwa ndi Isaac Misoya muli atengambali odziwika bwino monga Joyce Chavula, Edwin Chonde komanso Miracle Chinga.

(Wolemba Jimmy Chazama)

  Homeland Security Minister Peter Mukhito has reaffirmed government’s support for the financial empowerment of police o...
10/01/2026



Homeland Security Minister Peter Mukhito has reaffirmed government’s support for the financial empowerment of police officers through Malawi Police Sacco.

Mukhitho said this during his official visit to the National Police Headquarters at Area 30 in Lilongwe.

Speaking during the visit, Mukhito, who was accompanied by Deputy Minister of Homeland Security (Operations) Norman Paulosi Chisale, described Malawi Police Sacco as a key partner in improving the socio-economic wellbeing of police officers through savings mobilisation and access to affordable financial services.

In a demonstration of support, the minister donated K10 million to Malawi Police Sacco, commending the institution for promoting financial discipline, economic resilience and long-term empowerment among police officers and other civil servants.

Inspector General of Police Richard Luhanga described the minister’s support as a significant boost to the Sacco’s mission of improving the lives of its members.

Malawi Police Sacco Chief Executive Officer Ian Mwalungila welcomed the donation, describing it as a milestone for the institution.

“The donation is a clear vote of confidence in Malawi Police Sacco and our mission to empower members financially.

"It will strengthen our capacity to expand services, enhance member benefits, and deepen financial inclusion among police officers and other civil servants,” Mwalungila said.

  Akuluakulu ochokera ku ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino kudzera mu nthambi yoonetsetsa kuti masomphenya a boma akukwa...
10/01/2026



Akuluakulu ochokera ku ofesi ya mtsogoleri wa dziko lino kudzera mu nthambi yoonetsetsa kuti masomphenya a boma akukwaniritsidwa, alonjeza kuti athandiza kuti ndondomeko ya ulimi wa mthilira kunsi kwa mtsinje wa Shire ikwaniritsidwe.

Mmodzi wa akuluakulu ku nthambiyi a George Matipwiri, wafotokoza izi m'boma la Chikwawa pamene adakayendera mmene ikuyendera polojekitiyi komanso kumva kuchokera ku magulu a alimi amene apindule.

"Ndi cholinga cha mtsogoleri wa dziko lino kuti masomphenya ake akwaniritsidwe. Ndi chifukwa chake adakhazikitsa nthambiyi kuti izilondoloza zitukuko. Choncho tidabwera kuno kuti tizaone kotero kuti zimene taona tikafotokozera mtsogoleri wa dziko lino kuti ntchitoyi iyende bwino," iwo atero.

Mfumu Yaikulu Mulilima ya m'boma la Chikwawa idati ndi yokhumudwa ndi mmene yayendera polojekitiyi maka zaka zisanu zapitazi ponena kuti kufikira pano madzi sadayambebe kudutsa mu ngalande.

Pofika pano, malo okwana makilomita 43 mwa malo okwana makilomita 50 ndi amene amangako ngalande ya ulimi wa mthilira mu gawo loyamba la polojekitiyi.

Ngalande ya mthilira mu polojekitiyi ayimanga kuchoka ku Kapichira m'boma la Chikwawa kukafika ku Bangula m'boma la Nsanje.

Wolemba Isaac Salima

Address

Scott Road, Ginnery Corner, P/Bag 39
Blantyre
312200

Opening Hours

Monday 07:30 - 17:00
Tuesday 07:30 - 17:00
Wednesday 07:30 - 17:00
Thursday 07:30 - 17:00
Friday 07:30 - 17:00
Saturday 09:00 - 12:00

Telephone

+265887005791

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Times 360 Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Times 360 Malawi:

Share