SKY VIEWF Online

SKY VIEWF Online Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from SKY VIEWF Online, Broadcasting & media production company, Blantyre.

02/04/2024

Oweruza mlandu, Redson Kapindu, lero Lachiwiri nthawi ya 10 koloko m'mawa uno akuyembekezereka kupereka chigamulo ngati kuli koyenera kuti ma umboni ena okhudza mulandu wa wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr. Saulos Chilima abweretsedwe poyera ku bwaloli.

Oyimira mbali ya Chilima anapempha bwalo la milandu kuti akufuna nthambi ya Malawi Defence Force (MDF) ibweretse umboni osonyeza pomwe a Chilima adathandizira kuti a Zunneth Sattar alandire kontilakiti.

Koma, nthambi ya MDF inakana kupereka ma umboni-wa ponena kuti izi zitha kuyika pa chiopsezo chitetezo cha dziko lino.

Komabe oyimira mbali ya Chilima anafunitsitsabe kuti umboniwu ubweretsedwe ku bwaloli, zomwe zinapangitsa oweruza mulandu Justice Kapindu, kulamula MDF kuti imupatse umboniwo ndikuwuwunika m'chipinda chake ngati ulidi ndi kuthekera koyika pa chiopsezo chitetezo cha dziko lino.

A Chilima akuganiziridwa kuti analandira ndalama kuchokera kwa mponda-matiki Sattar ndi cholinga chofuna kuwathandizira kupeza ma kontirakiti mosavuta.

Wolemba:Che James Akwa Mandala

28/03/2024


Nyumba ya malamulo yavomeleza bilu yomwe idzilola dziko lino kulima chamba (local indian h**p) ndi cholinga chokweza ntchito za chuma mdziko lino.

Panthawi yomwe amavomeleza biluyi aphungu ena achipani cha DPP anatuluka mnyumbayi pofotokoza kuti phungu wadera lakumwera kwa boma la Lilongwe a Peter Dimba sanafikire nthambi zingapo zokhudzidwa.

Mtsogoleri wa zokambirana mnyumbayi a Richard Chimwendo Banda watsindika kuti cholinga cha biluyi sikuvomeleza kuti anthu adzisuta chamba koma kulima chambachi kuti dziko lino lidzipindula pa chu

22/03/2024

Phungu wa nyumba yamalamulo wadera lakumpoto chakum’mawa ku Blantyre, Fidson Chisesele, yemwe anali phungu oyima payenkha walowa chipani cha United Democratic Front (UDF).

Sipikala wanyumba yamalamulo Catherine Gotani Hara walengeza izi m’mawa uno mnyumbayi kuti phunguyu wapempha kuti amupatse malo mbali ya aphungu achipani cha UDF.

22/03/2024

President Yoweri Museveni has appointed his son Gen. Muhoozi Kainerugaba as the new Chief of Defence Forces (CDF),
He replaces Gen Wilson Mbasu Mbadi who has been appointed Minister of State for trade
Weeuh! Uganda is a Banana Republic.

22/03/2024

OCHITA MASEWERO OMWE ANALI KU AFRICA ALL GAMES KU GHANA, ALEPHERA KUPEZA MENDULO.

Timu ya ochita masewero osiyanasiyana yomwe inapita ku All Africa Games ku Accra, m'dziko la Ghana ifika kuno kumudzi opanda mendulo iliyonse potsatira kusachita bwino kumpikisanowu.

Ngakhale ochita masewero othamanga Asimenye Simwaka komanso Stern Lifa anafika mundime yamasemifainolo a 200 meters, onse analephera kuzigulira malo mundime yotsiliza kamba koti analephera kufika munthawi yomwe anapatsidwa.

Ochita masewero khumi ndi omwe anapita kumpikisanowu ndipo anatenga nawo gawo mumasewero monga;kusambira, judo, taekwondo, kuthamnga komanso nkhonya.

14/03/2024

MOZAMBIQUE

Anthu anayi(4) afa, Ndipo Munthu M'modzi wavulala, kamba ka Mvula ya mphamvu yomwe ikupitilira kugwa mosalekeza, yomwe ikutchedwa kuti Filipo, Mchigawo chotchedwa Inhambane, M'dziko la Mozambique.

Ndipo Malata asasuka pa Sukulu komanso Nyumba zambiri, Ndipo Galimoto zikulephera kudutsa M'miseu, Mapolo a mphamvu za Magetsi komanso Mathenifolo agwa pansi, zomwe zapangitsa kuti Anthu ambiri akhale opanda Magetsi komanso osayankhulana kudzera pa Thenifolo.

Ndipo Nzika za Dzikolo, zokhala Mzigawo za Maputo ndi Gaza, zachenjezedwa kuti zikhale zosamala kwambiri, kamba koti Mvula yotchedwa Filipo, ikhale ikowera ku Zigawozo Lero.

Komanso Mvula imeneyi padakali pano ikupitiliza kulowera ku Zigawo zina za Dziko la South Africa.

12/03/2024




President Lazarus Chakwera has commended the work that is being done under Marko Ifumbo Irrigation Scheme in Chitipa,saying it shows that it is indeed possible to have food security in the country through irrigation farming.

The President has since recommended that the area should have good storage facilities which will help to store yields from the irrigation scheme under better conditions for future use.

Chakwera also said with the kind of farming and value-addition that is being done, a good road is a must have in the area, so that the goods being produced can easily get to the markets.

12/03/2024




Mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera lero akulowera m'boma la Chitipa komwe akuyembekezeka kuyendera zitukuko zosiyanasiyana.

Mlembi mu ofesi ya mtsogoleri wa dziko ndi nduna zake a Colleen Zamba wati mwa zina a Chakwera ayendera malo a Meru Battalion, sikumu ya mthilira komanso msewu wa Chitipa Illomba kwa mfumu yaikulu Mwambulambya.

A Chakwera akuyembekezekanso kuyendera bwalo la zamasewero la Chitipa lomwe khonsolo ya m'bomali likumanga.

Dzulo, mtsogoleri wa dziko linoyu anali m'boma la Karonga kuyenderanso ntchito za chitukuko.

12/03/2024




Chipani cha UTM chati mgwirizano wawo ndi MCP pa yemwe akudzaimira mgwirizano wa Tonse mu chisankho chikudzachi sudasinthe ndipo ‘udakali chimodzimodzi’.

Mlembi wamkulu wa UTM, Patricia Kaliati, watiuza kuti adagawana zaka zisanu kwa otsogolera aliyense ndipo kuti mfundoyi sidachitike ndi atsogoleri a zipani ziwiri zokhazi ayi koma kuti otsatira ena adavomereza.

Malingana ndi Kaliati, mgwirizanowu ukudzaimiliridwa ndi mtsogoleri wa UTM, Saulos Chilima, pa chisankho cha chaka cha mawa popeza kuti mtsogoleri wa MCP, Lazarus Chakwera wachita kale mbali yake.

Izitu zikudza patapita sabata komiti yaikulu ya MCP itanena kuti odzaimila chipanichi mu chisankho chikudzayi ndi President Chakwera.

Poyankhurapo, katswiri pa ndale George Phiri wati kusainila mgwirizano kwa atsogoleri a mu mgwirizano wa Tonse kumaimila zipani zawo ndinso kuti MCP kusakha mtsogoleri wawo mu 2025 kukhoza kukhala mbali imodzi yokwaniritsa za mgwirizanowu.

12/03/2024




Education Minister Madalitso Kambauwa Wirima has told Parliament that the United States Government has indicated that it is unable to continue with construction of secondary schools under the Secondary Education Expansion for Development (Seed) project due to economic shocks which have rocked the entire world.

Kambauwa Wirima says the development means that two subsequent phases under the Seed Project will not be implemented.

So far, only 99 out of the 250 secondary schools that the US Government promised to construct in 2019 have been completed.

"Unfortunately and sadly, this having been said, my ministry and partners continue to mobilise resources for the expansion of secondary education across the country," Kambauwa Wirima said.

But Chiradzulu South lawmaker Joseph Mwanamvekha has alleged that MPs were told by the National Planning Commission yesterday that the reason for the US to discontinue the Seed Project was that of limited absorption capacity in the Ministry of Education.

But Leader of the House Richard Chimwendo Banda says lawmakers should believe the minister because she is saying this in the House of records.

09/03/2024

Unduna wazamalonda watseka mashopu anayi ogulitsa Shuga munzinda wa Lilongwe kaamba kopezeka akubisa komanso kugulitsa katunduyu pa mtengo okwera.

Kudzera m'chikalata chomwe chasayinidwa ndi mlembi wamkulu mu unduna-wu a Christina Zakeyo, mashopu-wa ndi a Romana Trading ndi ChouChou ku Area 2 (Bwalo Lanjovu) komanso Shalom ndi Simama General Dealers omwe ali ku Msungwi ku Area 25.

Iwo ati ntchitoyi ayigwira mothandizana ndi bungwe loona mpikisano pa malonda la CFTC pomwe anapeza mashopu ena akugulitsa belo la shuga yemwe amakhalamo makumi awiri (20) olemera 1 Kilogalamu akugulisidwa pa mtengo wa K69,000 m'malo mwa mtengo ovomelezeka wa K37,500.

Koma pakadali pano, mkulu wabungwe lomenyera ufulu wa anthu ogula la Consumers Association of Malawi (CAMA) a John Kapito ati ngakhale iyi ndi nkhani yabwino komabe boma lachedwa ndi ntchitoyi pomwe anthu akumva ululu pogula Shuga pamtengo okwera kwambiri.

Izi zikudza pamene m'madera ena m'dziko muno akugula paketi ya Shuga olemera 1 Kg pa mtengo wa K3,700.

06/03/2024

Address

Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when SKY VIEWF Online posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share