Amazing Art Network

Amazing Art Network News| Arts | Entertainment |Storytelling | Graphic design |Digital media to inform, inspire, and empower. |Talent That Transforms Lives

Talent that Transforms Lives

14/03/2026

Good morning

11/02/2026
10/02/2026

Do it tired. Do it scared. Just don’t stop.

09/02/2026

No one sees the effort until the results appear. Stay committed anyway.

08/02/2026

God provides what we need for today. Tomorrow begins the same way, with Him.

07/02/2026

Seeing the destination is the easy part. Becoming the person who can reach it is the work.

ECHOES OF A STRANGER Kodi Joe achitenga chinthuchi?
07/02/2026

ECHOES OF A STRANGER
Kodi Joe achitenga chinthuchi?

ECHOES OF A STRANGERCHAPTER 4Lachisanu m’mawa ku ofesi kunkakhala busy nthawi zonse. Aliyense ankakhala otopa, ndiye kun...
07/02/2026

ECHOES OF A STRANGER
CHAPTER 4
Lachisanu m’mawa ku ofesi kunkakhala busy nthawi zonse. Aliyense ankakhala otopa, ndiye kunkachitika zinthu mofulumira kuti ntchito ithe mwachangu kenako tizipita ku weekend.
Koma ine ndinali nditapanikizika ndi kuyankha ma email ndiye kupezeka kwa kwa Joe mutsikuli kunkandipatsa mpishupishu.

“Melifa, send me the budget report before you leave okay?” Dr. Phiri analankhula uku akusuzumira mu office mwanga.
“Yeah no problem,” ndinatero, ndikuyesera kuti ndisaoneke wotopa monga momwe ndinkamvera.
Joe, yemwe anali atakhala desk yakutsogolo kwanga anandiyang’ana tsopano
“Can I help?”
“Osadandaula ndizosavuta kwenikweni,” ndinayankha mofulumira. Nanga ndani anamuwuza kuti ndinkafuna thandizo lake?

Anagwedeza mutu kenako nkumapitiliza ntchito yake.
Kunena zoona ndinkamva kuti nthawi zonse iyeyu amandiyang’ana. Zinali ngati ankadziwa bwino njira yondisokonezera maganizo anga ndiye ankachitira dala zonsezi.
Pofika 2:00 koloko masana, ofesi inali itatsala pang'ono kukhala yopanda anthu. Ngakhale Tadala anali atachoka kale. Ndipo adali atatumiza kale message yoti nane ndiweruke sizakwathu.

Ndinali nditatsala pang'ono kupakira zinthu kuti nditsatire malangizo akewa pamene foni yanga inalira. Anali Joe.
”Hey forgot to say you look cute today" ndidawerenga message yo.
Uyu ankafuna azipanga zondizunguza mutu. Nanga tsiku lonseli akandiuze ndikuweruka?

Ndidanamizila kumwetulira kwinaku ndikufuna ndizituluka mu office mu.
Ndikuti ndizituluka adandigwira nkono.
"Not here Joe" ndidatero ndikumuyang'ana mochenjeza.

Ndidamuona naye akupakira zinthu zake nkumanditsatira.
Ankafuna chani iyeyu? Zochitika zake zidali zitayamba kundiopsa.

Ndidayamba kuona kuti mwina kukumana naye mu minibus muja sidali ngozi. Kupezekaso kuntchito kwathu sidalinso ngozi.

Koma ngati sichoncho, cholinga chidali chani? Ndidapitirira kuyenda ndipo adanong'ona nkhutu mwanga.
"Can I drop you home?" Adatero.
Koma zoona? Akandisiye ine kunyumba pazifukwa ziti?
Sidali njira yofunira kukadziwa kwathu imeneyi?

"Vuto lako ndichani Joe?" Ndidamufusa ndikuima.
"Zongocheza chabe" adayankha akumwetulira.
Sindidamuyankhe, m'malo mwake ndiyamba kuyenda mpaka kufika pa car park.

Adathamangira kutsogolo kwanga kenako adatsekula pakamwa kuti ayambe kulankhula.
"Ayi Joe" ndidalankhula momudula mawu. Sindikadakwanitsa kumva zimene ankafuna alankhule.

Ndidayenda ndawala kumudutsa ndipo naye adalowera komwe adaimika galimoto lake.
Zimenezi zidandipangitsa kuganiza kwambiri Maka poti tsiku loyamba ikubwera kuntchito sadabwere pa galimoto lakeli.

Nditayenda pang'ono ndidamuona akundiyimira. Ndisaname iyeyu patsikuli adali chiphinjo.
“Kunja ndi kwa mvula. Tiye ndikakusiye kwanu” adatero.
Sankanama. Ndikadati ndiyende ndekha ndithudi ndikadanyowa. Ndinkangoyenera kumunvera.

Tidayenda chetechete ngati malilo opanda mpingo. Padalibe ankalankhula kapena kukhosomola. Phokoso lomwe linkamveka lidali la anthu awiri kupumira m'mwamba basi.

Nditangotsala pang'ono kufika kwathu ndidaona mayi anga akum'menya m'chimwene wanga. Ndidamuwuza Joe ayime mwachangu.
“Bwanji?” adafunsa.
“ndikufuna nditsikire pompano” ndidatero. Adadzuma chifukwa ngakhale mvula idali itasiya, kunja kudali kwa matope.

Ndikutuluka maso anga adaphana ndi mayi anga. Mwina ndikadadziwa sindikadatuluka.
"Bwanji mukumenya mwana choncho?" Ndidafusa.
"Mbuli yakoyi ikundipatsa busy wamva? Tikafika kunyumba uyilangize. Apo ayi muzingowononga ndalama”

Ndidadziwa nkhani yake, adali atalepheranso mayeso. Joe yemwe ankamva zonsezi adatulukaso mugalimoto muja.
“Ngati school ikuvuta, nditha kumamuthandiza. Ndidakhalapo mphunzitsi” adatero Joe.
“Oh? Mukupangitsa kuti Melifa ayambe kuzijudula masiku amenewa ndinu eti?” mayi anga adamuyankha Joe.

Zidandikwiyitsa. Joe ankaoneka kuti zamukomera ndipo ndidasowa choyankha. Kwinako sindinkamva kuti anthuwa ankambirana kuti chani.
Koma funso lomwe adafunsa Joe ndilomwe lidandibwezeletsa pamalowa.
“ndi mwana wako oyamba?" Adandifunsa.
“Chani?” ndidatutumuka nalo funsoli.
Ndikuti ndiziyankha nawo mayi anga adagundika kulankhula.
“ndiye kunyumba mufika liti apongozi?”

Ndidagwira kumutu. Zinthu zake zinkayenda mwachangu zedi.
Friday limeneri lidaononga weekend yanga.

Since when? Why? Melifa Kukhala amatero?
04/02/2026

Since when? Why? Melifa Kukhala amatero?

ECHOES OF A STRANGERCHAPTER 3“Hey, Melifa. Its Joe. Ndinasangalala kwambiri kugwira nawe ntchito lero. Have a lovely nig...
03/02/2026

ECHOES OF A STRANGER
CHAPTER 3
“Hey, Melifa. Its Joe. Ndinasangalala kwambiri kugwira nawe ntchito lero. Have a lovely night.”
Kodi anatenga kuti nambala yanga? Anatenga kwa bwana anga?
Maganizo anga ankathamanga ndi malingaliro osiyanasiyana, ndipo palibe ngakhale limodzi lomwe linali londilimbikitsa mtima.
Ndinayamba kulemba uthenga oti ndimuyankhe Joe. Ndimati kulemba kenako kufufuta. M’malo mwake, ndinayimbira Tadala.
“Tadala, Joe just sent me a text,” ndidatero ndipo naye adatutumuka.
“Zoona? Tadikira… wati Joe?!” Adafusa.
Ndidamuwerengera uthengawo, ndipo naye adayamba kundifusa.
“Eeh, choyamba, anatenga kuti nambala yako? Ndipo akufuna chiyani?”
“Sindikudziwa!” ndinayankha ndikuziponya pabedi. “Izi ndi zachilendo kwambiri. Nditani?”
“Muyankheni munthu” adananena ngati kuti munthawiyi chidali chinthu chosavuta kwambiri kuchita padziko lapansi.
“Ndiyankhe kuti chani? Zikomo? Naweso ugone bwino?”
Tadala anaseka. “Komatu Melifa…. Anyway, muwuzeni kuti ‘Zikomo, inunso’ mukhale pakatikati. Osamulola adziwe kuti akukusokoneza.”
Ndinapumira m’mwamba. “Chabwino. Bola zisathere pa Mikozi”
Ndinatumiza uthengawo ndipo nthawi yomweyo ndinafundira blanket langa kuti ndizigona.
Foni yanga inalira kachiwiri.
“Bwanji, ugona mochedwa?” Ndinang’ung’udza. Zachidziwikire adali ataona nthawi.
“Mawa ndi tsiku lalikulu. Ndikungoganiza kuti project iyenda bwanji”
“I feel the same way. Ndikuyembekezera kugwira nawe ntchito kachiwiri” anayankha.
Sindinayankhe. M’malo mwake, ndinazimitsa foni nkuyisiya pansi pa pilo yanga. Ndinkangofuna zindichoke.

M’mawa wotsatira ndinanyamuka kupita ku ofesi ndikumva ngati sindinagone ngakhale pang’ono. Joe anali atafika kale atakhala patebulo pake akulemba ngati kuti sanasokoneze moyo wanga usiku wonse wadzulo.
“Good morning, Melifa,” anatero akukweza maso ake ndi kumwetulira komwe nkati mwanga kunkandikwiyitsa koma pamaso ndinkasekelera.
“Morning” ndinalankhula ndikuzemba kuphana naye maso.
Patangopita mphindi zochepa Dr. Phiri analowa akuoneka osangalala kuposa masiku onse. Adali atabwerera kuchokera kunja msanga kuposa momwe tinkayembekezera.
“Mwamvanatu anthu inu” anatero, akuyang’ana ine ndi Joe.
“Simukunama bwana. “Melifa ndi munthu wabwino kwambiri.” Joe anayankha mwansaga
Ndinazikakamiza kumwetulira koma mkati mwanga sizidandisangalatse.

Tsikuli linatha mwachangu. Ma meeting apo ndi apo komanso kusintha projekiti. Joe anali waukadaulo monga nthawi zonse, koma nthawi iliyonse maso athu akakumana, ndimamva kugunda kwa mtima wanga.

Pa nthawi ya chakudya cha masana Tadala adandikoka.
“Anakutumiziranso uthenga?” anafunsa maso ake akuyang’ana komwe kudali Joe
“Inde” ndinavomereza. “Koma sindinayankhe text yake yachiwiri.”
“unachita bwino. Ofunika kumusiya choncho” Tadala adalankhula akugwedeza mutu wake.
Pofika kumapeto kwa tsikuli ndinali wokonzeka kupita kunyumba n’kuyiwala Joe kwathunthu. Koma pamene ndinkanyamula zinthu zanga anabweranso pa desk panga.
“Melifa. Ndimangofuna kudziwa ngati ungakonde titakamwa coffee mawa m’mawa. Adatero.

Ndinazengereza. Ankandifunira za ntchito kapena zina?
“No problem” ndinayankha.
“Just coffee right?”
Joe anangomwetulira. Yes, coffee basi.” Adatero ndikumapita

Usiku watsiku limeneri ndidachezera kuwerenga malata. Kodi vuto la Joe linali chiyani? Kodi ankangofuna ticheze, kapena panali china chopitirira pamenepo?
Posakhalitsa phone yanga inalira ndipo ndinatenga mokaika.
“Hey Melifa. Ndi Joe. Can’t wait for Coffee tomorrow. Good night.”
Ndinang’ung’udza. Munthu uyu anali okakamila.
“Zikomo. Goodnight too” ndidayankha.
Ndinazimitsa foni n’kuyisiyanso pansi pa pilo yanga. Koma pamene ndinkalowa tulo, lingaliro limodzi silidachoke.
Kodi Joe akufuna chiyani kwenikweni?

03/02/2026

a Melifa kutengeka....

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Amazing Art Network posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share