
07/09/2025
Chigawenga, Babies, Max ndi Green Birds afika mu ndime ya matimu anayi ku Mbayani
Matimu a Chigawenga, Last Babies, Max United ndi Green Birds ndi omwe afika mu ndime ya matimu anayi amu chikho cha Lecherd Gwire Tikoma ku Mbayani mu mzinda wa Blantyre chomwe ndi cha ndalama zokwana K4 million atachita bwino pa masewero awo amu ndime ya matimu asanu ndi atatu.
Timu ya Chigawenga inagonjetsa King Power 4-2 pomwe Last Babies inagonjetsa 11 Devils 6-5 mu ndime ya ma penate pakuti mu mphindi 90 zinathera 1-1 loweruka.
Ndipo lachisanu, timu ya Max United inagweba timu ya Kabaza FC 3-2 pomwe Green Birds inalepherana 1-1 ndi Miracle Academy mu mphindi 90 kuti ikapambane 3-2 pa ma penate.
Ndime ya matimu anayi ikuyembekezeka kuseweredwa lachiwiri pa 9 September komanso lachitatu pa 10 September ndipo matimu ogonja adzakumana lachisanu polimbirana nambala yachitatu pomwe ndime yotsiriza izakhalako loweruka pa 13 September 2025.
Mayere amu ndime ya matimu anayi aliko lamulungu kummawa pomwe Komiti yoyendetsa mpira mu derali lichititse nthawi ya 8 koloko ku mmawa.
Opambana chikhochi adzatenga ndalama zokwana K1 million, Wachiwiri adzatenga K750,000, wachitatu adzatenga K500,000 pomwe yachinayi idzatenga K250,000.
Wolemba : Hastings Wadza Kasonga Jr