Blantyre Synod Radio

Blantyre Synod Radio Proclaiming The Gospel Of Our LORD JESUS CHRIST SOUTHERN REGION: 91.1FM
CENTRAL REGION : 100.3FM
NORTHERN REGION: 103.5FM
EASTERN REGION : 88.6FM

Phungu wanyumba ya malamulo wa Machinga East, Esther Jolobala wapambana pa mpando wa wachiwiri kwa wachiwiri wa sipikala...
29/10/2025

Phungu wanyumba ya malamulo wa Machinga East, Esther Jolobala wapambana pa mpando wa wachiwiri kwa wachiwiri wa sipikala wa nyumba ya malamulo .

Jolobala wapambana pampandowu aphungu ena amene amapikisana nawo atanena kuti asintha maganizo saimanawonso .

Aphungu ndi a Owen malijani phungu wa Nyumba ya malamulo m'dera la kum'mwera kwa boma la Mchinji komanso Abigail Selif Bongwe wa Zomba Likangala.

Mpando wa wachiwiri wa spikila wa nyumba ya malamulo wapita kwa a Gift Musowa amene ndi phungu wanyumba yamalamulo wa Mulanje Bale.

Zokambirana m'nyumbayi ziyamba lachisanu sabata ino, ndipo mtsogoleri wadziko lino , professor Arthur Peter Mutharika akuyembekezeka kudzatsegulira.

~Robert chandilira~
.

Aphungu anyumba ya malamulo asankha Sameer Suleman kukhala sipikala watsopano wa nyumba yamalamulo.Suleman yemwe ndi phu...
29/10/2025

Aphungu anyumba ya malamulo asankha Sameer Suleman kukhala sipikala watsopano wa nyumba yamalamulo.

Suleman yemwe ndi phungu wachipani cha DPP wapeza mavoti 135, pamene Peter Dimba wa chipani Cha MCP amene amapikasana nawo wapeza mavoti 85.

Aphungu ena omwe amapikasana nawo a Sandram Scott ndi Lasten Vigaro ochokeranso mchipani cha DPP sanapeze voti iliyonse.

Pakadali pano Sipikala watsopanoyu akulumbitsidwa pa mpandowu pa mwambo omwe akutsogolera ndi wachiwiri kwa mkulu wa mabwalo amilandu m'dziko muno Lovemore Chikopa.

~Robert Chandilira~

Chipani Cha Democratic progressive (DPP) chati  ana onse amene amalemba mayeso a MANEB monga std 8, JCE komanso MSCE sad...
29/10/2025

Chipani Cha Democratic progressive (DPP) chati ana onse amene amalemba mayeso a MANEB monga std 8, JCE komanso MSCE sadzilipiranso ndalama ya mayesowa kuyambira mwezi wa January Chaka Cha mawa msukulu zaboma komanso zoima pazokha.

Shadreck Namalomba yemwe ndi m'neneri wachipanichi wayankhula izi mum'zinda wa Lilongwe pamene amayankhula ndi atolankhani kunyumba yamalamulo.

Namalomba wati m'tsogoleri wadziko lino Professor Arthur Peter Mutharika ndiboma lake akwaniritsa mfundo zomwe analonjeza amalawi panthawi ya misonkhano yokopa anthu .

Malinga ndi Namalomba kuyambira mwezi wa January sukulu ya primary komanso secondary ikhala yaulere , ndipo ana sadzilipiranso ndalama ya mayeso a MANEB posatengera kuti akuchokera m'sukulu zaboma kapena zoima pazokha .

Iye watsimikizira amalawi kuti akhulupilire kuti boma la DPP likwanitsa zomwe linalonjeza manifesto yake.


~Robert Chandilira~

Mkulu oyang'anira alangizi azaumoyo pa Chipatala cha St Joseph Nguludi Mission, m'boma la Chiradzulu, a Thomas Julio Ban...
29/10/2025

Mkulu oyang'anira alangizi azaumoyo pa Chipatala cha St Joseph Nguludi Mission, m'boma la Chiradzulu, a Thomas Julio Banda ati ndi okhutira ndi momwe ntchito yobaya katemera wa Human PapillomaVirus ikuyendera.

Iye wati pakadali pano chiwerengero cha anthu obaitsa chapyola theka la mulingo umene adeyerekeza kuti afikile ndipo pali chiyembekezo choti pofika tsiku lotseka kubaya katemera'yu afikira atsikana ochuluka.

Banda walankhula izi lachiwiri pa sukulu ya pulaimale ya atsikana ya Nguludi pamene amapeleka katemerayu kwa atsikana oyambira zaka zisanu ndi zinayi 9 kulekela khumi, zisanu ndi zitatu 18, yemwe ndioteteza ku khansa ya khomo la chiberekero.

Pothilirapo ndemanga mphuzitsi wa mkuluyu Mercy Mwasiya, anati ntchito'yi yakhala yophweka kamba ka mkumano umene adachititsa ndi makolo a ophunzira powaunikira za ubwino olola ana awo kubaitsa katemera'yu.

Abgail Kanje ndi ophunzira pa Sukulu'yi ndipo anati ndiokondwa kukhala m'modzi mwa ophunzira amene abaitsa nawo katemera'yu ponena kuti athandizira kuti akhale ndi moyo wathanzi.

Khansa ya khomo la chiberekero ndi imodzi mwa khansa yomwe imapezeka kwambiri mwa atsikana komaso amayi m'dziko muno, ndipo ntchito yoyamba kubaya katemera'yu yomwe yayamba lolemba lapitali ikuyembezereka kutha lachisanu sabata ino.

~ Piliran Chitekwe ~
....

Chipani cha Malawi congres chapempha aphungu oima paokha komanso aphungu azipani zina kuti akavotere Peter Dimba pampand...
28/10/2025

Chipani cha Malawi congres chapempha aphungu oima paokha komanso aphungu azipani zina kuti akavotere Peter Dimba pampando wa sipikala wanyumba ya malamulo, komanso Chambulanyina Jere ngati wachiwiri wake.

Ofalitsa nkhani m'chipanichi Jessie Kabwira wauza atolankhani mu mzinda wa Lilongwe kuti nyumba yamalamulo ikufunika sipikala wanyumba ya malamulo amene alindi luso komanso maphunziro okwanira.

Kabwira wati ndi anthu ngati Dimba ndi amene angakwanitse kuti adzilimbikitsa boma la DPP zamalonjezo amene ananena munthawi ya misonkhano yokopa anthu.

Iye wati Dimba ali ndimaphunziro okwanira komanso anachitabwino kwambiri m'ma komiti akunyumba ya malamulo amene anatsogolerapo mnyumbayi .

Aphungu akunyumba ya malamulo akuyembekezeka kusankha sipikala komanso achiwiri ake mawa pa 29 October pamene akuyamba zokambilana zawo kuyambira pa 31 October.

~Robert Chandilira~

27/10/2025

*Kambani a Malawi*

Lolemba: 27/10/2025

*Hosts*: Blessings Kilowe & Jones Chizenga

Tiuzeni maganizo anu:

Unduna waza maphunziro kudzera ku nthambi yake yowunikira momwe maphunziro akuyendera mdziko muno ya Malawi Institute of Education (MIE) wakhazikitsa ndondomeko yatsopano ya momwe maphunziro akhale akuyendera.

Malingana ndi undunawu wati dondomeko yatsopano ikhale ikulunjika pokwanilitsa masophenya a 2063, mwazina zomwe zili mu ndondomeko yatsopanoyi muli magawo okhudza kulingalira kwakuya, kupereka mpata kwa ophunzira kugwiritsa ntchito nzeru zachibadwidwe komanso kuphunzira ndi momwe zithu zikusithira pa dziko la pansi.

Ndondomekoyi ikhale ndi magawo anayi yomwe ikuchedwa 1-6-6-3 yomwe kukhale chaka chozikonzekeretsa kenako ku Primary komanso Secondary zaka zisanu ndi chimodzi gawo lililonse kumaliza ndi maphunziro a ukachenjede omwe adzichitika kwa zaka zitatu.

Ndondomekoyi mwayilandira bwanji?

Call: 0885513399
SMS: 0885205184

M'busa wa mpingo wa Limbe CCAP Dr Hastings Abale Atha Phiri wayamikira ntchito za m'busa yemwe amamuthandizira mu utumik...
26/10/2025

M'busa wa mpingo wa Limbe CCAP Dr Hastings Abale Atha Phiri wayamikira ntchito za m'busa yemwe amamuthandizira mu utumikiwu a Chifundo Chibaya ngati munthu wa luso kwambiri zomwe wati ntchito zake zisowedwa pa mpingopa.


Poyankhula pa mwambo otsanzikana ndi abusa a Chibaya, Mbusa Abale Atha anati nt
abusa a Chibaya anali munthu odzipeleka pantchito yake, ofatsa komanso okhulupilika zomwe mpingo unazizolowera kwambiri.

M'busa Abale atha analimbikitsanso akhristu ampingowu kuti atengele khalidwe la mbusayu ndipo kuwalangiza kuti asafanizire zintchito za mbusayi ndi m'busa wina yemwe m'malo mwawo ponena kuti ntchito komanso mphatso zimasiyana mwa abusa.

M'mau ake m'busa Chifundo Chibaya anapempha akhristu pampingopa kuti akhale olimbika m'mapemphero ndicholinga choti apambane pa moyo wawo.

M'busa chibaya analandilidwa pa mpingowu pa 26 November m'chaka cha 2023 ndipo akukagwira ntchito ku sukulu ya sekondale ya mission ya Domasi komwe akakhale m'busa oyang'anila sukuluyi.

~Noel Mchenga~

Timu ya Mighty Wanderers yaswa mopanda chisoni FCB Nyasa Big Bullets mu masewero amu ligi ya TNM. Wanderers yawumbudza B...
26/10/2025

Timu ya Mighty Wanderers yaswa mopanda chisoni FCB Nyasa Big Bullets mu masewero amu ligi ya TNM.

Wanderers yawumbudza Bullets ndi zigoli zitatu kwa duu pa bwalo la Kamuzu mu mzinda wa Blantyre.

Adam Wallace anamwetsa chigoli choyamba cha timuyi pa mphindi 22 atachita kuchokera panja m'modzi mwa osewera a timuyi Wisdom Mpinganjira atabvulala.

Blessings Singini yemwe analowanso kuchokera panja ndiye anamwetsa zigoli zina ziwiri pa mphindi 76 ndi 83 zomwe zachititsa kuti timuyi imwemwetere chotere.

Polankhulapo, mphunzitsi wa timu ya Wanderers, Bob Mpulumutsi Mpinganjira, wati ndiwokondwa ndi chipambano chimenechi ndipo izi zawapatsa mangolomera pa masewero ena mtsogolo muno.

M'mawu ake, wophunzitsa timu ya Bullets Peter Mjojo Mponda, wati masiku sakoma onse ndipo wavomereza kugonja koma wati achita chilichonse chotheka kuti timuyi ichite bwino pa masewero ake ena m'masiku asanu ndi limodzi akubwerawa.

Zateremu, Wanderers yatolerera mapointi 48 pa masewero makumi awiri (20) omwe yasewera pamene Bullets ikutsogolabe mu ligiyi ndi mapointi 49 pa masewero okwana 21.

Matimu awiriwa akumananso lamulungu sabata ya mawa koma mu chikho cha FDH Bank.

Chithunzi: Bullets

~Emmanuel Harry~

Mpingo wa Luchenza CCAP mu Blantyre Synod wayika mwala wa maziko pomwe ukuyembekezeka kumanga manse ya moderator wa mpin...
26/10/2025

Mpingo wa Luchenza CCAP mu Blantyre Synod wayika mwala wa maziko pomwe ukuyembekezeka kumanga manse ya moderator wa mpingowu.

Mlendo olemekezeka pa mwambowu anali wachiwiri wa moderator wa Blantyre synod, M'busa Missie Kananji Spiki yemwe anati ntchito yomwe akhristu a Luncheza CCAP ayiyamba ndiyabwino kwambili kumpingo komanso utumiki.

M'busa Kananji walimbikitsa mipingo yamu Blantyre Synod yomwe ilibe ma manse kuti imange ndicholinga choti abusa adzikhala malo abwino.

M'mau ake moderator wa mpingo wa Luchenza CCAP, M'busa Alex Benson Maulana, wati ganizo lomanga manse linabwela potengela kuti manse yomwe ilipo pampingowu ndiyakale yomwenso inaonongeka zinthu zambiri.

Manse imene ikufuna kumangidwayi itenga ndalama zokwana pafupifupi 230 Million Kwacha.

~Lazia Blok~
BSRonline

25/10/2025

Unduna wazaumoyo mogwirizana ndi bungwe lowona za umoyo pa dziko lonse la World Health Organization WHO kuyambira pa 27 mwezi uno uyamba ntchito yopeleka katemera wa khansa ya khomo la chibelekero kwa atsikana a zaka 9 mpaka 18.

Ntchitoyi ikuyembekezeka kudzatha pa lachisanu pa 31 October.

Poyankhula pa msonkhano wa atolankhani mu mzinda wa Lilongwe, Mkulu owona za katemera ku bungwe la WHO Dr Dafrossa Lyima wati dziko la Malawi ndi lachiwiri pa maiko amene amayi akumwalira kwambiri chifukwa cha matenda a khansa padziko lonse.

Malinga ndi a Lyima, mwa amayi 2,300 amene amapezeka ndi nthendayi pachaka, amai okwana 1,600 ndi omwe amamwalira.

Iye wati ngati dziko lino silichitapo kanthu pofika 2030, pali chiyembekezo kuti chiwelengero cha amayi komanso atsikana okwana 22,545 adzapezeka ndi matendawa.

Matendawa akuti akukula kwambiri mdziko muno kamba pakati pa amai kamba ka mchitidwe oyamba zogonana akadali aang'ono komanso kusuta fodya.

Katemerayu aperekedwa m'sukulu zaboma komanso ndi sukulu zoima pazokha, m'misika ndi m'malo opangira malonda osiyanasiyana m'maboma onse a am'dziko lino.

~Robert Chandilira~
.

Mpingo wa Chigumula CCAP,  kudzera mu utumiki mvano, wapeleka katundu wa ndalama zokwana 3 million kwacha pa ndende ya T...
25/10/2025

Mpingo wa Chigumula CCAP, kudzera mu utumiki mvano, wapeleka katundu wa ndalama zokwana 3 million kwacha pa ndende ya Thyolo.

Wachiwiri kwa wapampando wa gulu la amayi amvano pa mpingowu, Angella Chimtokoma wati ndiokondwa ndi m'mene achezera ndi akaidi'wa.

Chimtokoma wati gulu lawo lili ndi malingaliro ofikila ndende zina komanso malo osiyanasiyana omwe akusowekera thandizo ngati lomweli.

M'mau ake moderator mpingowu, m'busa Dr. Austin Chimenya, wayamikira gululi pathandizo lomwe lapeleka.

Chimenya walimbikitsa mipingo ndi magulu ena kuti zikhala ndi udindo wothandiza anthu andende ndi ena omwe akusowa thandizo.

Katundu yemwe waperekedwa ndi monga Shuga, Zovala, makina osokera, Ufa, Soya pieces ndi wina.

~Noel Mchenga~

Phungu wadera la pakati m'boma la Ntcheu wati muzaka zisanu zimene akhale phungu waderali aonetsetsa kuti achinyamata m'...
24/10/2025

Phungu wadera la pakati m'boma la Ntcheu wati muzaka zisanu zimene akhale phungu waderali aonetsetsa kuti achinyamata m'derali apeze ngongole zoyambila ma bizinezi ang'onoang'ono komanso kuthandiza alimi kuti apeze zipangizo za ulimi zotsika mtengo.

Ng'oma wati akangolumbikitsidwa lolemba likubwerali, ayamba ndikubweretsa chakudya , komanso madzi aukhondo m'dera lake omwe akhala akuvuta kwa nthawi yaitali.

Phunguyu wati atengeraponso mwayi wa maphunziro aulere aku primary komanso secondary,polimbikitsa anthu a mderalake maka achinyamata kuti alimbikire sukulu komanso amanga midadada yophunziliramo kuti vuto la malo ophunziliramo lichepe .

Paul Ng'oma anapambana ngati phungu oima payekha pa zisankho zomwe zinachitika pa 16 September mwezi watha ndipo pano walowa chipani cholamula cha DPP.

~Robert Chandilira

Address

The Station Manager Po Box 413
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Blantyre Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Blantyre Synod Radio:

Share