Blantyre Synod Radio

Blantyre Synod Radio Proclaiming The Gospel Of Our LORD JESUS CHRIST SOUTHERN REGION: 91.1FM
CENTRAL REGION : 100.3FM
NORTHERN REGION: 103.5FM
EASTERN REGION : 88.6FM

Bungwe la MANEB laulutsa zotsatira za mayeso a MSCE a chaka chino cha 2025 ndipo lati mwa ana 194,584 omwe analemba maye...
05/09/2025

Bungwe la MANEB laulutsa zotsatira za mayeso a MSCE a chaka chino cha 2025 ndipo lati mwa ana 194,584 omwe analemba mayeso'wa, ana 113,708 ndi amene akhonza mayeso'wa kuimira 58.44 pa 100 alionse.

Northern education division ndi imene yakhonzetsa bwino kuposa onse.

Ndipo sukulu za m'boma la Dedza zachita bwino kuposa ena, koma ma boma a Thyolo, Lilongwe, Chikwawa, Neno ndi Mwanza sizinakhonzetse bwino.

Sukulu za Dzukani Pvt, ndi Chiunda Community Secondary ana onse sanakhonze mayeso.

Robert chandilira
online

Unduna wa zamaphunziro pamodzi ndi bungwe loona za mayeso mdziko muno la Maneb lero masanawa akuyembekezeka kutulutsa zo...
05/09/2025

Unduna wa zamaphunziro pamodzi ndi bungwe loona za mayeso mdziko muno la Maneb lero masanawa akuyembekezeka kutulutsa zotsatira za mayeso a MSCE a chaka chino.

Mwambo'wu ukuyembekezeka kuyamba nthawi ya 2 koloko.

BSR online ikupatsirani zonse.

....

Milward Tobias m'modzi wa amene akupikisana nawo pa mpando wa m'tsogoleri wadziko lino oima payenkha  wati amalawi akuye...
05/09/2025

Milward Tobias m'modzi wa amene akupikisana nawo pa mpando wa m'tsogoleri wadziko lino oima payenkha wati amalawi akuyenera kudzamuvotera pa 16 September pano, kuti adzabwezeretse mphamvu ya ndalama ya dziko lino.

Tobias amayankhula izi lachisanu mumzinda wa Lilongwe pamene amatambasula zina mwa mfundo zimene adzatsatire ngati amalawi angamuvotere pazisankho zomwe zichitike pa 16 September.

Poyankhula ndi BSR online, Tobias walonjeza kudzaika adindo m'malo mosiyana siyana mogwirizana ndi kuthekera kwawo.

Tobias wati muzaka zisanu zoyambilira boma lake lidzatsegula ma fakitale asanu atsopano, komanso adzakonza ntchito zokopa alendo kuti dziko lino lidzitha kukopa alendo ambiri ochokera m'maiko ena kuti adzibwera m'dziko muno.

Malingana ndi Tobias, boma lake lidzakhazikitsa ndondomeko zapamwamba zokonza ntchito za migodi komanso adzaunikira migwirizano imene boma linapanga ndi makampani akunja kuti amalawi adzipindula mochuluka kuposa kale.

Robert chandilira
online...

Dziko la Malawi lizachititsa mpikisano wa masewero a mpira wamanja wa maiko a muno mu Africa (Africa Netball Cup), kuyam...
05/09/2025

Dziko la Malawi lizachititsa mpikisano wa masewero a mpira wamanja wa maiko a muno mu Africa (Africa Netball Cup), kuyambira pa 8 mpaka pa 14 December ku Griffin Saenda Sports Complex mu mzinda wa Lilongwe.

Izi zatsimikizika pa msonkhano wa atolankhani womwe bungwe la Netball Association of Malawi (NAM) mogwirizana ndi bungwe la Malawi National Council of Sports (MNCS), linachititsa ku Amaryllis Hotel mu mzinda wa Blantyre.

Mkulu woyan'ganira ntchito za bungwe la Malawi National Council of Sports, Henry Kamata, wati wayamikira bungwe la Netball Africa pokhulupilira dziko linobkuti lichititse mpikisanowu ndipo wati maiko onse omwe atenge nawo mbali mu mpikisanowu apatsidwa chisamaliro choyenera.

Yemwe akugwirizira ngati mtsogoleri wa bungwe la Netball Africa, Rabbecca Goagoses, wati bungwe lawo ndilokondwa kuona dziko la Malawi likuchititsa mpikisano umenewu kachiwiri ngati m'mene inachitira mu chaka cha 2012.

Timu ya mpira wamanja ya amuna yomwe yangokhazikitsidwa kumene m'dziko muno ikuyembezereka kuzasewera koyamba mu mpikisanowu.

Mpikisano umenewu uzachitika pa mutu woti kubweretsa umodzi, kumanga ndi kukweza ndipo matimu asanu ndi anayi a maiko amuno mu Africa akuyembekezereka kuzatenga nawo mbali.

Bungwe la Malawi Electoral Commission lati madela omwe sakhala ndi chisankho cha khansala kamba ka imfa ya anthu omwe am...
05/09/2025

Bungwe la Malawi Electoral Commission lati madela omwe sakhala ndi chisankho cha khansala kamba ka imfa ya anthu omwe amapikisa nawo pachisankhochi tsopano akwana anayi.

Maderawa ndi Chilobwe Ward ya ku Lilongwe Chilobwe Constituency, Msitu Ward ya ku Mchinji South Constituency, Mikongo Ward yaku Mangochi North East Constituency ndiku Luwinga Ward mdela la Mzuzu City North Constituency.

Ofalitsa nkhani zabungwe la MEC, Sangwani Mwafulirwa, wati malingana ndi lamulo, pamene munthu amene anavomelezedwa kupikisana nawo pa chisankho oyimira chipani wamwalira, chisankho chisanayambe, chisankho cha mdela limenelo chimayenela kuyimitsidwa.

Mwafulirwa wati malamulowa amati bungwe loyendetsa zisankho limayenela kulengeza kuti zonse zokonzekera chisankho mdela lomwe lakhudzidwa ziyambirenso mwatsopano.

Apolisi ya Lilongwe anjata mtsizina mtole wina  ochokera m'dziko la Ghana Boamah Owusu wa zaka 23 chifukwa chobera mzika...
04/09/2025

Apolisi ya Lilongwe anjata mtsizina mtole wina ochokera m'dziko la Ghana Boamah Owusu wa zaka 23 chifukwa chobera mzika ya mdziko la China yemwe ndi mwini wake wa kampani ya Purity Products kwa Njewa mumzinda wa Lilongwe ndalama zokwana 202.5 million kwacha.

Malingana ndi mneneri wa polisi ya Lilongwe, inspector Hastings Chigalu Maxwell Boamha Owusu analowa mdziko muno pa 1 September kudzela bwalo landege la Kamuzu ndipo anatumidwa ndi mzika ina yomwe sinadziwike padakali pano.

Chigalu wati Maxwell Boamah Owusu ananamiza mwini kampani ya Purity kuti amuthandiza kusitha ndalama za Malawi kupita ku yen yomwe ndindalama ya m'dziko la China zokwana 202.5 million kwacha koma anamubela .

Malingana ndi Chigalu apolisi ofufuza atagwira ntchito yawo, apeza kuti Maxwell Boamah Owusu anali m'gwirizano ndi anthu angapo auchigawenga omwe anamulonjeza kumupatsa 500 USD akakwanitsa kuba ndalama kwa anthu angapo.

Pakadali pano apolisi akwanitsa kupeza ndalama'zi zimene anali ataika kale m'ma bank ena am'dziko muno .

Robert chandilira
online....

Major General Paul Valentino Phiri mkulu wa asilikari a MDF wati asilikari am'dziko muno a  MDF ndiwokonzeka kuteteza ma...
03/09/2025

Major General Paul Valentino Phiri mkulu wa asilikari a MDF wati asilikari am'dziko muno a MDF ndiwokonzeka kuteteza malo onse kumene anthu akaponyere voti, kuteteza amalawi, komanso katundu yense amene adzagwiritsidwe ntchito patsiku loponya voti.

General Valentino Phiri walonjeza kuti MDF mogwirizana ndi mthambi zina zachitetezo agwira ntchito mosakondera chipani chili chonse .

Izi zanenedwa ku msonkhano otchedwa NECOF umene umabweretsa pamodzi nthambi zonse zokhudzidwa pachisankho omwe umachitikira mumzinda wa Lilongwe okonzedwa ndi bungwe loyendetsa zisankho la MEC.

Pamsonkhano'wu panafika mthumwi zochokera mzipani zomwe zikupikisana nawo pazisankho za chaka chino, amabungwe oima paokha komanso atsogoleri a mipingo.

Pamkumano'wu, wapampando wa bungwe la MEC Justice Annabel Mtalimanja watsimikizira amalawi kuti bungwe lawo lakonzeka kuti zisankho zidzakhale zamtendere komanso zovomelezeka.

Robert chandilira
online...

02/09/2025

Bungwe la Malawi Environmental Protection Authority (MEPA) lati ndi ndilokhumudwa ndi kuchepa kwa chiwelengero cha mitengo mdziko muno.

Izi zikutsatira kafukufuku yemwe nthambi yoona za nkhalango yapanga yemwe waonetsa kuti mitengo 60 pa 100 iliyonse ndi yomwe yapulumuka m'chaka chodzala mitengo cha 2023/2024.

Mkulu ophunzitsa zachilengwe ku bungwe la MEPA, Aubren Chirwa wati zotsatira za kafukufukuyu ndizokhumudwitsa potengera ndi kulimbika komwe kulipo pa ntchito yoteteza mitengo mdziko muno.

Chirwa wati mwa zina chiwelengerochi chatsika kamba kakusintha kwa kagwedwe ka mvula, komanso ngamba.

Iye watsindika kuti MEPA ipitiliza kugwira ntchito ndi nthambi zina zaboma monga nthambi yowona za nkhalango podzala mitengo mmadera komanso nkhalango zonse zimene zinawonongedwa.

Jones Chizenga

Ofalitsa nkhani n'chipani Cha MCP Dr Jessie Kabwira wati anthu ena amene akuwaganizira kuti ndi  achipani Cha Democratic...
02/09/2025

Ofalitsa nkhani n'chipani Cha MCP Dr Jessie Kabwira wati anthu ena amene akuwaganizira kuti ndi achipani Cha Democratic progressive (DPP) komanso AFORF amenya ndikulanda ndalama zokwana 17 million kwacha, mipira 200 kwa amene akufuna kudzaimira chipani Cha MCP pakati m'boma la kasungu Chikondi Kampachike.

Kabwira wati akuganizira kuti anthu'wo anatumidwa ndi a Enock Chihana m'tsogoleri wachipani cha AFORD.

Poyankhulapo amene akudzaimira chipani cha MCP pa mpando wa phungu kunyumba ya malamulo mdera la pakati m'boma la kasungu Chikondi Kampachike wati anthu'wo sanangowabera ndalama kokha komanso anawathira tsabola m'maso.

Pakadali pano, Shadreck Namalomba ofalitsa nkhani m'chipani cha DPP wati chipani chawo ndichamtendere ndipo sichingapange zimene chipani Cha MCP chikunena.

Namalomba wati chipani cha DPP sichinaike wochiimira kudera kumene chipani'chi chikunena pakati pa boma la Kasungu, ndipo ati chipani cha MCP chingofuna kuononga mbiri ya chipani Cha DPP koma sakwanitsa.

Robert chandilira
online....

Yemwe akufuna kudzaimira ngati phungu wa ku nyumba ya malamulo wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) ku de...
02/09/2025

Yemwe akufuna kudzaimira ngati phungu wa ku nyumba ya malamulo wa chipani cha United Transformation Movement (UTM) ku dera la Nguludi m'boma la Chiradzulu, Mwayi Lancy Mbewe, wati akudzipereka kwathuthu kuti achinyamata akhale odzidalira pa okha pa chuma kudera'li.

Mbewe walakhula izi lamulungu pa sukulu ya Nguludi Sekondale pamapeto amwambo wa ndime yotsiriza ya chikho cha mpira wamiyendo komanso wa manja chimene adakhazikitsa cha ndalama zokwana 6 million Kwacha.

Iye wati kupereka zochita komanso ma luso osiyanasiyana kwa achinyamata kungawathandize kupewa makhalidwe oipa amene akhoza kuononga tsogolo lao.

Mwazina, Mwayi Lancy Mbewe anati akulipilira ana amene anasiira Sukulu pa njira kuti apitilize maphunziro awo a Sekondale komanso ukachenjede.

Iye anaonjezeranso kunena kuti akuthandizanso achinyamata'wa ndi ngongole zopanda chiongola dzanja ngati njira imodzi yofuna kuti akhale odzidalira pa okha pa chuma ndi kusitha miyoyo yawo.

Timu ya Pa Mbumba Fc ndi yomwe yakhala akatswiri ampikisano'wo itagonjetsa Eleven Spanners Fc ndi chigoli chimodzi kwa chilowere ndipo mpira wa manja timu ya Banana Sisters inagonjetsa timu ya St Theresa Sisters ndi ma basiketi 24 kwa 3.

~ Piliran Chitekwe ~
....

Mzimayi wazaka 34, Yuniki Mwachande ali m'manja mwa polisi ya Lilongwe chifukwa chomuganizira kuti anaba zovala zamwana ...
01/09/2025

Mzimayi wazaka 34, Yuniki Mwachande ali m'manja mwa polisi ya Lilongwe chifukwa chomuganizira kuti anaba zovala zamwana ndi zakudya pamene bwana ake anali atachokapo.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Lilongwe, Sergeant Khumbo Nsanyiwa wati Mwachande amkagwira ntchito yapankhomo ku Area 3 mumzinda wa Lilongwe, koma anaganiza zakuba katundu ndi zovala zamwana wa bwana ake amene panthawiyi anali atachokapo.

Malingana ndi Sanyiwa, Mwachande atafunsidwa za kusowa kwa katundu'yu anakana kuti sakudziwapo kanthu, zimene zinapangitsa kuti bwana ake akanene ku polisi ya Lilongwe, ndipo apolisi atakafufuza kunyumba kwa mayi'yu kwa Chinsapo, anakapeza katundu osowayu.

Yuniki Mwachande akaonekera kubwalo la milandu posachedwa, komwe akayakhe mlandu wakuba.

Roberts chandilira
online...

Chimbale cha nyimbo zoonera choimbidwa ndi M'bawa CCAP Church Choir tsopano chakhazikitsidwa.Mwambo wokhazikitsa chimbal...
01/09/2025

Chimbale cha nyimbo zoonera choimbidwa ndi M'bawa CCAP Church Choir tsopano chakhazikitsidwa.

Mwambo wokhazikitsa chimbale chimenechi unachitika lamulungu ku St Michael and all Angels Multipurpose Hall mu mzinda wa Blantyre.

M'busa Johnson Damalekani ndi yemwe anatsogolera mwambo wopatula chimbalechi.

Mlendo olemekezeka pamwambowu ndiyemwe anali phungu wa dera la Mbayani Chemusa Magasa, Getrude Nankhumwa.

Oimba ena omwe anatumikila pa mwambowu ndi monga King James Phiri komanso Neligo Women's Choir mwaena.

~Dyson Phiri~

Address

The Station Manager Po Box 413
Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Blantyre Synod Radio posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Blantyre Synod Radio:

Share