Mibawa TV

Mibawa TV Malawi's Entertainment Channel.
(412)

 TABWERA KUZATENGA UKATSWIRI WA REGION 5 - JEGWEMphunzitsi wa timu ya dziko lino yampira wamiyendo yosapyola zaka 20, Mi...
08/07/2025


TABWERA KUZATENGA UKATSWIRI WA REGION 5 - JEGWE

Mphunzitsi wa timu ya dziko lino yampira wamiyendo yosapyola zaka 20, Milias Pofera Jegwe wati cholinga chake ndikutenga ukatswiri wachikho cha Region 5.

Jegwe wayankhula izi atatha masewero omwe Flames yachisodzerayi yazigulira malo mundime ya matimu anayi itagojetsa Namibia ndi zigoli ziwiri zomwe zinabwera mu gawo la chiwiri la masewerowa.

Iye wati ngakhale panali zophinja zina monga kusakhala ndi nthawi yokwanila yakakonzekeledwe komanso kupita ndi osewera 17 kumpikisanowu malo mwa 20, sizinawoneke kwambiri kamba ka ubale wabwino omwe ulipo pakati pa osewera komanso aphunzitsi atimuyi.

Malawi yamaliza pa mwamba pa group A ndi mapointi wokwana 7, pomwe Angola, ili ndi mapointi 7 kufanana ndi Flames pa nambala yachiwiri koma ikutsalira ndi zigoli pamene eni bwalo Namibia ali nambala yachitatu ndi mapointi atatu ndipo Zimbabwe ndiyomwe ili pamapeto pomwe sinapeze chipambano chilichonse.

Olemba Peter Nyasulu,Lilongwe.

08/07/2025


EUTHINI MCP DISTRICT CHAIRMAN CONFIRMS FLAWED ELECTORAL COLLEGE PROCESS, UNDERMINES MCP DEFENSE

The political tensions surrounding the recent internal party processes in the Malawi Congress Party (MCP) have deepened, as the District Chairman for Euthini has come forward to confirm troubling irregularities in the formation of the Electoral College.

Echoing cross-examination statements in court, the Constituency Chairman Whightone Shaba and the District Chairman Mathews Shaba revealed that both officials were pressured into signing off on what he described as a "bogus Electoral College".

According to the duo, they got instructions from unidentified MCP member to approve the document without reviewing the list of names, under the assurance that they would be able to verify the details later.

"This was clearly an anomaly," says the District Chairman in court cross-examination statement, adding that they were only informed by Joseph Chavula three days later that the entire Electoral College was wrong.

He naratted that the delayed admission has raised serious concerns about the transparency and legitimacy of the process.

These revelations poke significant holes in the defense previously mounted by MCP officials, who had argued that the Electoral College process had followed proper protocol.

Call now to connect with business.

Lilongwe, this Friday, Khichini Hub, City Centre, opposite BICC. A new chapter begins as we setup an entertainment hub i...
08/07/2025

Lilongwe, this Friday, Khichini Hub, City Centre, opposite BICC. A new chapter begins as we setup an entertainment hub in the Capital City..

Mibawa Band in the house..

Zisakuphonyeni!!!!!Ngati muli  mu mzinda wa Lilongwe  ku mathero asabata ino Keturah uja nde  wafika ku Kapitolo komanso...
08/07/2025

Zisakuphonyeni!!!!!Ngati muli mu mzinda wa Lilongwe ku mathero asabata ino Keturah uja nde wafika ku Kapitolo komanso Teddy Makadi. Kodi mwagula kale Ticket ?

08/07/2025

Court Hearing of Eng. Vitumbiko AZ Mumba V Malawi Congress Party an another
Download Kanema M'manja NOW on play store to watch and catch-up all your favorite programs. https://play.google.com/store/apps/details...

08/07/2025

Mibawa Funeral Cover ndichani?

Zokonzekera chisankho zikuyenda bwanji
08/07/2025

Zokonzekera chisankho zikuyenda bwanji

 MAKINA OYEZERA TB NDI HIV ABEDWA PACHIPATALA CHA MACHINGAMakina awiri oyezera chifuwa chachikulu  komanso HIV (GeneXper...
08/07/2025


MAKINA OYEZERA TB NDI HIV ABEDWA PACHIPATALA CHA MACHINGA

Makina awiri oyezera chifuwa chachikulu komanso HIV (GeneXpert) apa chipatala chachikulu cha Machinga omwe onsewa pamodzi ndi a ndalama zokwana K60 miliyoni asowa.

M'neneri wa chipatalachi, Wongani Nyirenda, watsimikiza za kusowa kwa makinawa omwe wati asowa kucha kwa lero lachiwiri pa 8 July, 2025 ndipo apolisi akufufuza m'mene makinawa asowera.

Iye wati kusowa kwa makinawa kukhudza ntchito zoyeza matenda pa chipatalapa kaamba koti amathandizira kubweletsa zotsatira zingapo pakamodzi.

Mkulu wa mabungwe omwe si aboma ku Machinga a Belinda Chimombo ati ayesetsa kugwira ntchito ndi adindo a pachipatalachi ncholinga chofuna kupeza makinawa komanso kuti amene aba akapezeka aimbidwe milandu.

Olemba Charlie Ligomeka - Machinga

08/07/2025


Mulandu wa Eng. Vitumbiko Mumba V MCP and another ukupitilira ku bwalo lalikulu la milandu la Mzuzu High Court.

Pakanali pano a constituency chair a chipani cha MCP ku Mzimba Central a Wytone Shaba ndiomwe akuperekera umboni.

Mulanduwu pomwe unayimitsidwa masanawa, panja pa bwaloli panasonkhana khamu la anthu omwe akuoneka kuti ndi ambali ya a Mumba.

 AMANGIDWA KAMBA KOCHITA CHINYENGOApolisi mu mzinda wa Mzuzu amanga Owen Mkulichi ndi James Dulamoyo powaganizira kuti a...
08/07/2025


AMANGIDWA KAMBA KOCHITA CHINYENGO

Apolisi mu mzinda wa Mzuzu amanga Owen Mkulichi ndi James Dulamoyo powaganizira kuti anaba katundu ku malo a zam'sanguluso a Chisanga Complex Centre mwachinyengo.

Malingana ndi wachiwiri kwa m'neneri wa police ya Mzuzu Sub Ins. Cecilia Mfune, oganizilidwawa ndi ophunzira pa sukulu ija yaukachenjede mu nzinda wa Mzuzu.

A Mfune ati a Mkulichi ndi a Dulamoyo amakonza mapwando ku Chisanga Complex Centre ndipo iwo akhala akupita kumaloku ndi anzawo kuchokera mwezi wa May mpaka July chaka chino.

Oganizilidwawa ati amagwiritsa ntchito ma akaunti ojudula a National Bank kulipira zakudya ndi zakumwa ndipo oyang'anira zachuma ku Chisanga Complex Centre atachita kafukufuku anapeza kuti ndalama zokwana K4 miliyoni ndizomwe Oganizilidwawa sadalipire.

Eni malowa anatengela nkhaniyi ku police ya Luwinga ndipo apolisi amanga a Mkulichi ndi a Dulamoyo pa 7 July 2025.

A mfune ati anthuwa anavomera mlanduwu ndipo akaonekera kukhoti posachedwa kuti akayankhe mulandu wokhudza kuchita chinyengo.

Wolemba Salomy Chisi, Mzuzu.

 IDANA NDI OKONZEKA KUCHITA BWINO KU ZAMBIA Zatsimikizika kuti Chimwemwe Idana wapita ku timu ya Zanaco ya m'dziko la Za...
08/07/2025


IDANA NDI OKONZEKA KUCHITA BWINO KU ZAMBIA

Zatsimikizika kuti Chimwemwe Idana wapita ku timu ya Zanaco ya m'dziko la Zambia pa mgwirizano wa zaka ziwiri.

Yalengeza izi ndi timu'yi pamene osewera wakale wa timu ya Silver Strikers walengezedwa limodzi ndi ena okwana asanu ndi awiri ngati osewera atsopano ku timu ya Zanaco.

Poyankhula ndi Mibawa, Idana wati ndi okondwa kuti wapeza mwai osewera kunja kwa dziko lino.

"Ndine okondwa kuti ndasayinila mgwirizano ndi timu ya Zanaco, ndikhumbo la osewera aliyense kuti akasewere mpira kunja ndipo chiyembekezo changa ndi chabwino ndikuyenera kulimbikira ndikupangitsa timu yanga kuti izichita bwino," Anatero Idana

Idana anaonjezera kuti kupezeka kwa Chawanangwa Kaonga ndi Robert Saizi ku timu ya Zanaco kumuthandizila.

"Chawanangwa (Kaonga) ndi Saizi (Robert) kupezeka kwawo kundithandizila kwambiri posakhala ndi chilendo komanso ndi amene azindithandizila mu zina kuti ndizichita bwino," anaonjezera Idana.

Pakadali pano Idana wayamba kale kupanga zokonzekela ndi timu'yi.

Idana ndi osewera wachinayi ochokera mdziko muno amene azisewera mu ligi yayikulu yaku Zambia pamene mu ligi'yi mulinso Chifundo Mphasi amene anatenga ukatswiri ndi timu ya Power Dynamos chaka chatha.

Wolemba Duncan Kaonga, Blantyre.

Address

Blantyre

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 17:00
Saturday 09:00 - 17:00
Sunday 09:00 - 17:00

Telephone

00265999844266

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mibawa TV posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Mibawa TV:

Share