10/08/2026
Felix washoni yemwe ndi wapa mpando wa bungwe la atolankhani onse m'dziko muno wati Brian anali olimbikira pa ntchito ndipo osaopa wina aliyese.
Washoni wati atolankhani adzamusowa Brian kamba ka kulimbika ntchito kwake ndipo wapempha atolankhani m'dziko muno kuti atengele chitsanzo cha Brian pogwira ntchito mopanda matha.
Oyimila aku banja pastor James Ramsey Mbewe ati ndi odandala ndi imfa ya Brain ndipo ati Gogo Nanjaiko moyo wawo ukhala ovuta opanda Brian.
Popitiliza a Mbewe ati a Banda anabadwa m'chaka cha 1980 pa 8 August ndipo wasiya mkazi ndi ana okwana asanu ndi m'modzi ndipo wamwalira atadwala malungo.
Wolemba Agness Mpulula, Blantyre