Nyasaland News

Nyasaland News Follow us for well confirmed news, A true non biased Malawian paper,The news that you can trust. htt

Zikumveka kuti bwana  Moses kumkuyu athawa mdziko muno kuthawira ku UK komwe banja lawo limakhala.Kuthawaku kwachitika  ...
28/09/2025

Zikumveka kuti bwana Moses kumkuyu athawa mdziko muno kuthawira ku UK komwe banja lawo limakhala.

Kuthawaku kwachitika a MEC atangolengeza posachedwapa kuti a Peter Muntharika ndi omwe apambana pa chisankho cha u President kutikita a Lazarus Chakwera ndi mavoti osasimbika.

Ngakhale kuti chipani cha MCP chinaima pa chulu ndikumati chaberedwa mavoti ndi chipani Cha DPP Komabe izi sizinaphule kanthu kamba koti a Chakwera anavomereza msanga kugonja kwawo pachisankhochi ndikumufunira zabwino zonse Muntharika.

KUTHYOLO MKAZI WADULA MALICHE A MWAMUNA WAKE NDI MANOJacob Nyongo wochokera kwa Nthondo mudera la mfumu yaikulu ku Tenga...
27/09/2025

KUTHYOLO MKAZI WADULA MALICHE A MWAMUNA WAKE NDI MANO

Jacob Nyongo wochokera kwa Nthondo mudera la mfumu yaikulu ku Tengani m'boma la Nsanje wadulidwa maliseche ndi kazi wake kuthyolo.

Malingana ndi malipoti pankhaniyi, Jacob Nyongo anakwatira mkazi wa ku Thyolo dera la Mtambizi ndipo wamuchita chipongwe pomuvinira maliseche ake atasemphana chichewa mm'banja mwawo.

Pakadalipano pano, Nyongo ali pa chipatala cha Thekerani ndipo akufuna kuti amutumize ku chipatala cha Thyolo kuti akapitirize kulandira thandizo logwira mtima.

Izi zadzetsa mantha anthu aderali pomwe mkazi wake wa bamboyu wakwanisa kugwiritsa ntchito mano ake ndikuduliratu maliseche a njondayi atakangana zolimba pankhani zam'banja.

Ena akuganizira kuti mayiyu ndi wa chiwewe.

MICHAEL USI AKUTI NTHAWI IJA ANALI BUSY NDI KAMPENI KOMA PANO YEREKEZANI KUMUITANA INU A ACB kuzaperekera umboni paza mb...
27/09/2025

MICHAEL USI AKUTI NTHAWI IJA ANALI BUSY NDI KAMPENI KOMA PANO YEREKEZANI KUMUITANA INU A ACB kuzaperekera umboni paza mbava za mu MCP zomwe zinagwesa dziko kamba Kakuba ndalama zaboma, ndithu mamawa omwe akupezani kuzaperekera umboni kuti azazitchule mbavazo zimangidwe.

27/09/2025

AKUTI PALI CHIKONZERO CHOTI MUNTHARIKA APHEDWE PATSIKU LOMULUMBIRISA

Zonena nena zayambapotu, mwina musanyozere paja wa misala anaona nkhondo...

Zikumveka kuti azibambo awiriwa, Minister Stevie Wazisomo Muliya wasiya ntchito Ku Times 360 Malawi ndipo akukayamba Ku ...
27/09/2025

Zikumveka kuti azibambo awiriwa, Minister Stevie Wazisomo Muliya wasiya ntchito Ku Times 360 Malawi ndipo akukayamba Ku MBC ngati producer komanso présenter.

Izi zachitika atapambana ma interviews pakati apo, koma amadikira zisankho zichitike kuti atiuze.

Akakhala Brian Banda nde zikumvekanso kuti atha kusankhidwa ngati Director General watsopano wa MBC kutengera ndi momwe Bambo Kasakula ankalankhulira za a Professor Arthur Peter Mutharika boma lisanasinthe. Brian Banda anapatsidwa mwayi wopemphera kunyumba ya Prof APM kunyambadwe dzulo pamene amalankhula ndi mtundu wa Amalawi ndipo ambiri akuti ichi ndi chizindikiro choti zabwino zikubwera.

Mzake wapamtima  wa mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera  yemwe ndi Chris Chaima Banda walengeza kuti wat...
27/09/2025

Mzake wapamtima wa mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera yemwe ndi Chris Chaima Banda walengeza kuti watuluka muchipani cha Malawi Congress Party.

Chaima Banda wati wachita izi kamba koti ku MCP Kuli akuba ambiri omwe kuba kwake ndikoononga nako dziko.

Funso mkumati achaima aziwa liti kuti ku MCP kuli mbava zokha-zokha? Amalekeranji kunena izi MEC isanalengezera owina bwanji??

Chipani cha Democratic Progressive (DPP), chomwe changopambana kumene pachisankho cha mtsogoleri wa dziko lino, chachenj...
27/09/2025

Chipani cha Democratic Progressive (DPP), chomwe changopambana kumene pachisankho cha mtsogoleri wa dziko lino, chachenjeza kuti anthu omwe akhala akubisa chimanga mdziko muno, asauka akapusa.

Mneneri wa chipanicho Shadreck Namalomba wati chimangachi chiyamba kutsika mtengo posakhalitsapa chifukwa boma lionetsetsa kuti chimangachi chikupezeka ponseponse mdziko muno.

"Zimenezo nde titsindikedi. Chimanga mukusungacho ndibwino kuti muchigulitsiretu pano chifukwa pamsikapa, chitchipa kwambiri posachedwapa. Mapeto ake simupanga phindu kapena kuti chikuolerani m'nyumba," adatero Namalomba.

Anyamata awiri omwe pakadalipano sakudziwika mayina awo apezeka atafa mam'mawa uno pafupi ndi malo okwelera minibus zopi...
27/09/2025

Anyamata awiri omwe pakadalipano sakudziwika mayina awo apezeka atafa mam'mawa uno pafupi ndi malo okwelera minibus zopita mu Limbe omwe ndi oyandikana ndi nyumba za Blantyre Water Board komwe ndi kuseli kwa Kamuzu Stadium.

Anthuwa omwe matupi awo akuoneka ndi zilonda komanso magazi akuganiziridwa kuti achita chophedwa ndi anthu okwiya atagwidwa akuba zipangizo za khebo za lamya pamalo omwe ali pafupi ndi pamene afera pomwe paonetsa kuti anali atayamba kale kudula ma khebowa potengera kuti mmanja mwawo mukuonetsa atavala zozitetedzera (gloves) zomwe anavala munthawi yomwe amayamba kuchotsa zipangizozi.

Mdela la Gugulethu ku  Capetown mmalawi wina wamwamuna watisiya  ataomberedwa ndipo  oowomberayo wagwidwa ndi apolisi pa...
26/09/2025

Mdela la Gugulethu ku Capetown mmalawi wina wamwamuna watisiya ataomberedwa ndipo oowomberayo wagwidwa ndi apolisi pankhaniyi.

Mnyamatayu waomberedwa ndikumwalira akukhala kunyumba zamikhukhu komwe ngati siusamala Kumakhala zigawenga zoopsa kwambiri..

Mzimu wake ukause mumtendere.

AKAPONDA MGAGA AKUTI AMENYEDWA MAKOFI KUNYUMBA YABOMAYemwe anali Chief of the staff kunyumba yaboma a Chris Kapondamgaga...
26/09/2025

AKAPONDA MGAGA AKUTI AMENYEDWA MAKOFI KUNYUMBA YABOMA

Yemwe anali Chief of the staff kunyumba yaboma a Chris Kapondamgaga aulula kuti zulo alikitidwa makofi ndi ma bouncer a MCP ku meeting yomwe inachitika kunyumba yabomako.

Akaponda Mgaga akuzuzulidwa kuti ndiomwe athandizira kuti MCP ituluke m'boma pomamuuza president Lazarus Chakwera ziganizo zosakhala bwino pomwe kuchipani zimachitika zina.

Kunjaku akunamizana kuti Peter Mutharika anakachitira msonkhano wa atolankhani Lero kulilongwe.Abale Kodi msonkhanowu si...
26/09/2025

Kunjaku akunamizana kuti Peter Mutharika anakachitira msonkhano wa atolankhani Lero kulilongwe.

Abale Kodi msonkhanowu siunali ku Blantyre?

Kodi yemwe akumapereka ma information aboza kunjaku ndi ndani??

AKUTI WAZIBAYA PAMIMBA KAMBA KOTI WALEPHERA KUBERA MAVOTIMtsikanayu dzina lake ndi Beatrice mukunama. Mtsikanayu amagwir...
26/09/2025

AKUTI WAZIBAYA PAMIMBA KAMBA KOTI WALEPHERA KUBERA MAVOTI

Mtsikanayu dzina lake ndi Beatrice mukunama. Mtsikanayu amagwira ntchito ngati Namwino koma anatengedwa kukaonelera zisankho ku boma la Chikwawa.

Mtsikanayu anatumiza zosatira zomwe zinali zosiyana komaso zokondera chipani cha MCP. MEC inabweza zosatira zake kamba koti zasiyana ndi zaazake.

Ataona izi mtsikanayu anali ndimantha ndipo anatenga mpeni ndikuzibaya pamimba komaso pakhosi. Anthu ataona izi anathamangira naye kuchipatala kuti akapeze thandizo. Pakali pano alimoyo koma alimuululu oopsa.

Address

Opposite Chayamba Building, Along Victoria Avenue Street.
Blantyre
817.9

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nyasaland News posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nyasaland News:

Share