Nyasaland News

Nyasaland News Follow us for well confirmed news, A true non biased Malawian paper,The news that you can trust. htt

30/06/2025

CHENJERANI NDI MBAVA PAJONI

Pali akazi ena akumalawi omwe ali mdziko la South Africa akumaika post kuti aliku Malawi koma akufuna atabwera kujoni kungoti vuto alibe kofikira and ndalama ya transport ndiyoperewera.

Awa ndi akazi amene akumabwera ndiimeneyi koma chonsecho ali kale kujoni komweko.

zimene akupanga akumakuuza kuti chilichonse wapanga koma iweyo mwamuna umuonjezere transport kuti akabwera muzizasangalala kuchipinda.Akatero akumakumakupatsa nambala yaku Malawi mwamunawe iwe ndikumamutumizirako ndalama kuti akafika azafikire kwaiwe azakuchose ubatchala wazaka ndi zaka omwe wakulikita.

Mkaziyo aKumakhala zoti akunama and iye ali kujoni komweko.

Mkazi wakumalawi yemwe akukhala ku Cosmo city mziko la South Africa wachita izi akuti kubera amuna akumalawi ogona.

Abale sukusulani kujoniko..

27/06/2025

MAVUTO ENANSO:

Ku Lilongwe ku Area 49 New Shire A4 Street nyumba yayaka moto chaku madzulo omwe ano ndipo momwe zikuonekera katundu yemse waonongeka.

Chomwe chayambitsa motowu sichinadziwikebe mpaka pano.

27/06/2025

Bungwe la Malawi Law Society (MLS) ladzudzula apolisi a Malawi Police (MPS) ndi Malawi Defence Force (MDF) chifukwa chosachitapo kanthu pa zigawenga za zikwanje zomwe zidaukira anthu akuchita ziwonetsero mu mzinda wa Lilongwe dzulo Lachinayi.

Chikalata chomwe chasayinidwa ndi Purezidenti wa MLS Davis Mthakati Njobvu komanso mlembi wolemekezeka a Francis Ekari M’mame ati nkhanza zakhala zikuchitika mobwerezabwereza kwa anthu omwe akufuna kupanga zinthu malingana ndi ufulu wawo.

Ndemanga ya MLS yapemphanso mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera kuti achotse nduna ya chitetezo cha dziko Ezekiel Ching’oma.

“Sosaitiyi ikuona kuti malinga ndi ndime 153(4) ya malamulo oyendetsera dziko lino, nduna ndiyomwe ili ndi udindo wowonetsetsa kuti machitidwe ndi machitidwe wa apolisi a m’Malawi akugwirizana ndi malamulo oyendetsera dziko lino, udindo womwe nduna yalephera kuutsatira.

MLS yapemphanso Pulezidenti Chakwera kuti achotse mkulu wa apolisi m’dziko muno Merlyn Yolamu pa udindo wake chifukwa cholephera kuchita zinthu mwachilungamo komanso mopanda tsankho.

26/06/2025

MADEMO LERO AWONESA ZOTI MDZIKO MUNO KUTSOGOLOKU MUBUKA NKHONDO

Zomwe zachitika mu mzinda wa Lilongwe pamene apolisi komanso asilikali ankhondo amayang'anira anthu onyamula zikwanje a MCP akumenya mkulu amene amatsogolera ziwonetsero, Sylvester Namiwa komanso kusokoneza ziwonetserozi, zikutsutsana ndi zomwe akuluakulu a nthambi za chitetezo m'dziko muno analonjeza m'mbuyomu.

A Maxwell Mwachande omwe amayendetsa minibus mu mzinda wa Lilongwe ndipo anthu ena osadziwika bwino atentha minibus yawo yomwe anayimika pa community ground kumapanga zabizinesi yawo.

Malinga ndi kulankhula kwa a Mwachande anthu osadziwika bwino atentha minibusiyi kamba koti mtsogoleri wa zionetsero a Sylvester Namiwa anathawira mu basiyi anthu ena osadziwika bwino akufuna kuwakhapa ndi zikwanje.

Galimoto inanso ya 2 Toner yaotchedwa ndi anyamata azikwanjewa kumalo azionesereku omwe anatuluka kumaloku pa galimoto ya Toyota Fortuner.

Lolemba sabata lino, bungwe la MEC lidakumana ndi akuluakuluwa ku Mangochi komwe adalonjeza kuti awonetsetsa kuti aliyense ndi otetezedwa pamene dziko lino likukonzekera chisankho cha pa 16 September 2025.

Mkulu wa polisi, Merlyne Yolamu adati nthambi yake komanso ndi nthambi zina ndi zokonzeka kupereka chitetezo kwa aliyense mosakondera komanso mosasankha mbali.

"Tidali pa mkumano ndi nthambi zina zimene zimapereka chitetezo a MDF, Prison, Immigration komanso ayini akefe apolisi amene udindo wathu ndikupereka chitetezo cha mdziko. Tiri patsogolo pokhwimitsa chitetezo munyengo ino ya chisankho," iye adatero.

Izitu zadandawulitsa anthu mdziko muno ndipo ena mwa iwo, awonetsa kukhumudwa ndi kukula kwa mchitidwe wa anthu onyamula zikwanje, kwambiri ku Lilongwe, omwe akumalepheretsa kuchita ziwonetsero mumzindau.

A Namiwa amenyedwa koopsa pa maso pa asilikali ndi apolisi ndipo a Ayesa kupempha thandizo kuchokera kwa achitetezowa koma iwo amangoonerera Namiwa akumenyedwa ndi anyamata a MCP ati kamba kochita zionesero zokwana wamkulu wa mec Mayi Anabel John Tembo Mtalimanja.

Pa chisankho ichi ziko lisokonekera ili.

Padakali pano Dr Dalitso kabambe anapangitsa press briefing yodzudzula mchitidwe omwe wachitika ku ma demonstration ku Lilongwe,komwe nkulu otsogolera ziwonetselozo a Silvester Namiwa amenyedwa modetsa nkhawa ndi zigawenga za MCP pomwe a Police ndi asilikali (MDF) akuwonelera koma osachitapo kanthu.

26/06/2025

Ofesi ya kazembe wadziko la America mmalawi muno yatulusa chikalata chosonyeza chidwi chake pa ma demo omwe achitike lero kulilongwe, ku Blantyre ndi kumangochi mogwirizana.

Mademowa achitika lero pa 26 September 2025 pokakamiza mayi Anabel Mtalimanja yemwe ndi mwana wa Malemu John Tembo ndi bambo Andrew Mpesi kutula Maudindo awo pansi ku bungwe loyendesa zachisankho la MEC.

Mayi Anabel ndi bambo mpesi akuzuzulidwa ndi zina mwa mdzika za dziko lino kuti a kukakamira kugwiritsa ntchito makina a Smartmatic mu chisankho chomwe chili mkuzachi.

Amalawi ena mdziko muno akuti makina a Smartmatic asayandikire zisankho zapa 16 September zomwe zichitike mdziko muno chaka chino.

Nduna ya zamdziko ndi chitetezo cha dziko mdziko muno  bambo Ezekiel Peter  Ching'oma (MP) yaletsa nduna ya maboma ang'o...
25/06/2025

Nduna ya zamdziko ndi chitetezo cha dziko mdziko muno bambo Ezekiel Peter Ching'oma (MP) yaletsa nduna ya maboma ang'ono bambo Richard Chimwendo Banda ndi anthu ena onse mziko muno omwe amakonda kukhala busy kuvala ngati achitetezo mu zochitika zao kuti asazavalenso zovalazi,ndipo kuti akazapezeka akuswa lamuloli azaona zakuda.

Izi zikudza pomwe anthu ambiri mziko muno akangalika ndi kuvala ngati achitetezo mu misonkhano ya ndale pokonzekera chisankho chapa 16 September chaka chino.

Yemwe amafuna kupikisana nawo Pampando wa president pa 16 September pano bambo Chikomeni David Chirwa wati sapikisana na...
25/06/2025

Yemwe amafuna kupikisana nawo Pampando wa president pa 16 September pano bambo Chikomeni David Chirwa wati sapikisana nawonso Pampandou kamba koti alephera kupeza ndalama yonse yokwanira K10 Million yokapereka ku bungwe loyendesa zachisankho la Malawi Electoral Commission (MEC).

“Ndayesesa kuti ndipeze 10 Million yoti ndikalipire ku MEC koma zakanika pano ndivomeleze kuti zavuta ndizayesaso next time”.

A Chikomeni Chirwa omwe Anagundika ndi kuyenda ndawala komanso kupempha apempha ndalama kwa anthu akufuna kwabwini poyamba amati apeza ndalama zokwanira K10 Million ndipo amafunikira kuti azionjezere munthawi yomwe kunali mphekesera zoti ku MEC kuzafunika K20 Million ya anthu lofunika kupikisana Pampando wa president.

Kenako Zitaziwika kuti yomwe ikufunika ku MEC ndi K10 Million nawonso bambo Chikomeni anabwera poyera kuti apeza K5 Million yomwe amafuna aonjezere kuti ikwane K10 Million yokapereka ku MEC,.

Apa amalawi ena mziko muno anaima mitu ndikuyamba kufunsa a ngati mwa mkuluyu munali chilungamo.

Pano ndi uyu akuti basinso sapikisana azayesa ulendo wina, kusonyeza kuti mkuluyu cholinga chake kunali kungofuna kutolera ndalama yampamba kuti ayambire bizinesi basi osati opikisanazo, mwachidule mkuluyu ndikathyali.

Ku MCP u Running mate nawo wavuta ko uku, kaya atenga ko ndani? Mwa anthu awa ndiomwe sopano akuganiziridwa kuti mmodzi ...
25/06/2025

Ku MCP u Running mate nawo wavuta ko uku, kaya atenga ko ndani?

Mwa anthu awa ndiomwe sopano akuganiziridwa kuti mmodzi mwa iwo ndiyemwe atengedwe kuti ayende ndi Chakwera pa 16 September pano.

1,Atupere Muluzi.

2,Vitumbiko Mumba.

3,Kondwani Nankhumwa.

4.Cathren Gotani Hara.

Zokambirana zokhuza mgwirizano wazipani pakati pa MCP ndi UDF zikufika kumapeto tsopano.Zosatira muzimva posachedwapa.Ku...
25/06/2025

Zokambirana zokhuza mgwirizano wazipani pakati pa MCP ndi UDF zikufika kumapeto tsopano.

Zosatira muzimva posachedwapa.

Ku UDF masapota achipani ndi akulu akulu a Chipanicho sakufuna UDF kupanga mgwirizano ndi MCP, ndi Atupere muluzi yekha ndi bambo wake omwe Bakili muluzi omwe akufuna izi.

Ndi zakubanja izi olo mungakane bwanji kubanjako agwirizana zokutengerani komwe iwo akufuna osati komwe inu mukufuna ayi ndipo sakufunsaninso maganizo anu pa nkhaniyi.

Omsewa akuzuzula chipani cha DPP kuti chikuphangira Maudindo mu zokambirana zawo za mgwirizano.Izi zikuchitika pomwe ons...
25/06/2025

Omsewa akuzuzula chipani cha DPP kuti chikuphangira Maudindo mu zokambirana zawo za mgwirizano.

Izi zikuchitika pomwe onsewa akufuna kukhala wachiwiri (Running mate) wa Peter Muntharika pachisankho cha pa 16 September chomwe chili mkuzachi.

Abale, kungomuthandiza chabe Peter Muntharika, zitati za mgwirizano zatheka ndipo kuti alola zogawana ma udindo mofanana, pamenepa Muntharika atenge ndani ngati wachiwiri wake?

1,Dalitso Kabambe (UTM).

2,Atupere Muluzi (UDF).

3,Enoch Chihana(AFORD).

4,Joyce Banda(PP).

Avomereza kuti anangoziyamba koma  paokha sangazikwanise, K10 Million presidential nominations fee ija ku MEC anakonza.....
25/06/2025

Avomereza kuti anangoziyamba koma paokha sangazikwanise, K10 Million presidential nominations fee ija ku MEC anakonza...

Bambo Dickson Kashoti ndi amenewa, miyendo ngati ndodo za msungwi, koma akati anyoze andale ambali yotsutsa boma kumango...
25/06/2025

Bambo Dickson Kashoti ndi amenewa, miyendo ngati ndodo za msungwi, koma akati anyoze andale ambali yotsutsa boma kumangokhala ngati kuti iwo anabadwa molongosokatu.

Kwa amene mumawasatira zolemba zawo mukuwaziwa bwino-bwino kuti ndi mkulu oduka mutu kumalembedwe...

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Nyasaland News posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Business

Send a message to Nyasaland News:

Share